< 2 Samuelsboken 22 >

1 Och David talade för Herranom denna visones ord, den tid då Herren hade hulpit honom ifrån alla hans fiendars hand, och ifrå Sauls hand;
Davide anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli.
2 Och sade: Herren är min klippa, och min borg, och min Frälsare.
Iye anati, “Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga.
3 Gud är min tröst, på honom vill jag trösta; min sköld och mine helsos horn; mitt beskärm, och min tillflykt, min Frälsare, du som mig hjelper ifrån orätt.
Mulungu wanga ndiye thanthwe langa, mʼmene ndimathawiramo, chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa. Iye ndi linga langa, pothawirapo panga ndi mpulumutsi wanga. Munandipulumutsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
4 Jag vill lofva och åkalla Herran, så blifver jag ifrå mina fiendar förlossad.
“Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
5 Ty dödsens förderf hade omhvärft mig; och Belials bäcker hade förskräckt mig.
“Mafunde a imfa anandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
6 Helvetes band omhvärfde mig; och dödsens snaror öfverföllo mig. (Sheol h7585)
Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol h7585)
7 När jag bedröfvad är, vill jag åkalla Herran, och ropa till min Gud, så hörer han mina röst utaf sitt tempel; och mitt rop kommer för honom i hans öron.
“Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinapemphera kwa Mulungu wanga. Iye ali mʼnyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika mʼmakutu ake.
8 Jorden bäfvade och skalf; himmelens grundvalar hafva sig rört, och gifvit sig, då han var vred.
“Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, maziko a miyamba anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
9 Rök gick upp utaf hans näso, och förtärande eld utaf hans mun; så att det ljungade deraf.
Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
10 Himmelen böjde han, och steg neder; och mörker var under hans fötter.
Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
11 Och han steg på Cherub, och flög, och syntes på vädrens vingar.
Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
12 Hans tjäll kringom honom var mörker, och svart tjockt moln.
Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, mitambo yakuda ya mlengalenga.
13 Af skenet för honom brann det med ljungande.
Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera makala amoto alawilawi.
14 Herren dundrade af himmelen; och den Högste lät utgå sitt dunder.
Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
15 Han sköt sina pilar, och förströdde dem; han lät ljunga, och förskräckte dem.
Iye anaponya mivi yake, nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
16 Då såg man vattnet uppvälla; och jordenes grund vardt blottad genom Herrans straff, och genom hans näsos anda och blåst.
Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera, ndipo maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwake.
17 Han sände utaf höjdene, och hemtade mig, och drog mig utu stor vatten.
“Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
18 Han frälste mig ifrå mina starka fiendar; ifrå mina hatare, som mig för mägtige voro;
Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga amene anali amphamvu kuposa ine.
19 De mig öfverföllo i mine olyckos tid; och Herren är min tröst vorden.
Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
20 Han hafver utfört mig på rymdena. Han tog mig ut; förty han hade lust till mig.
Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
21 Herren gör väl vid mig efter mina rättfärdighet; han betalar mig efter mina händers renhet.
“Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
22 Ty jag håller Herrans vägar, och är icke ogudaktig vorden emot min Gud.
Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso pa Mulungu wanga.
23 Förty alla hans rätter hafver jag för ögon; och hans bud kastar jag icke ifrå mig.
Malamulo ake onse ali pamaso panga, sindinasiye malangizo ake.
24 Men jag är utan vank för honom, och bevarar mig för synd.
Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
25 Derföre vedergäller mig Herren efter min rättfärdighet; efter min renhet för hans ögon.
Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi makhalidwe anga abwino pamaso pake.
26 Med de heliga äst du helig; med de fromma äst du from.
“Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu, kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
27 Med de rena äst du ren; och vid de afvoga ställer du dig afvog.
Kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa anthu achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
28 Ty du hjelper det elända folk; och med din ögon förnedrar du de höga.
Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma maso anu amatsutsana ndi odzikuza ndipo mumawatsitsa.
29 Ty du, Herre, äst min lykta; Herren upplyser mitt mörker.
Inu Yehova, ndinu nyale yanga; Yehova wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
30 Förty med dig kan jag nederslå krigsfolk; och genom min Gud springa öfver muren.
Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo, ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
31 Guds vägar äro utan brist; Herrans tal är genomluttradt; han är en sköld allom dem som hoppas till honom.
“Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa iye.
32 Ty hvilken är en Gud, utan Herren? Och hvilken är en tröst, utan vår Gud?
Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
33 Gud styrker mig med kraft, och visar mig en väg utan brist.
Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
34 Han gör mina fötter lika som hjortars; och sätter mig uppå mina höjder.
Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
35 Han lärer mina händer strida, och drifver mina armars kopparbåga.
Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
36 Och du gifver mig dine helsos sköld; och när du förnedrar mig, gör du mig storan.
Inu mundipatsa ine chishango chanu cha chigonjetso; mumawerama kuti mundikweze.
37 Du gör rum för mig till att gå, att mina fötter icke slinta.
Inu mwalimbitsa njira yanga kuti ndiyende bwino, kuti mapazi anga asaterereke.
38 Jag vill jaga efter mina fiendar, och förgöra dem; och vill icke omvända, tilldess jag gör en ända med dem.
“Ine ndinathamangitsa adani anga ndi kuwakantha; sindinabwerere mpaka iwo atawonongedwa.
39 Jag vill förgöra dem, och nederslå dem, och de skola icke stå mig emot; de måste falla under mina fötter.
Ndinawakantha kotheratu, ndipo sanathe kudzukanso; Iwo anagwera pansi pa mapazi anga.
40 Du kan omgjorda mig med kraft till strid; du kan kasta dem under mig, som sätta sig upp emot mig.
Inu munandipatsa ine mphamvu yochitira nkhondo; munagwaditsa adani anga pa mapazi anga.
41 Du gifver mig mina fiendar på flyktena, att jag må förstöra dem som mig hata.
Inu muchititsa kuti adani anga atembenuke ndi kuthawa; ndipo ndinawononga adani anga.
42 De ropa, men der är ingen hjelpare; till Herran, men han svarar dem intet.
Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova, koma sanawayankhe.
43 Jag skall sönderstöta dem såsom stoft på jordene; såsom träck uppå gatone skall jag göra dem till mull, och förströ dem.
Ine ndinawaperesa ngati fumbi la pa dziko lapansi; ndinawasinja ndipo ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
44 Du hjelper mig ifrå det trätosamma folket; och bevarar mig till ett hufvud öfver Hedningarna. Det folk, som jag intet kände, skall tjena mig.
“Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa mitundu ya anthu; Inu mwandisunga kuti ndikhale mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
45 De främmande barn försaka mig; men desse lyda mig med hörsam öron.
Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine, amandigonjera.
46 De främmande barn äro försmäktade, och brytas i sina bojor.
Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
47 Herren lefver, och lofvad vare min tröst; och varde upphöjd Gud, mine helsos tröst.
“Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa. Akuzike Mulungu, Thanthwe, Mpulumutsi wanga!
48 Gud, som gifver mig hämnden, och kastar folk under mig;
Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amayika anthu a mitundu yonse pansi pa ulamuliro wanga,
49 Han förer mig ut ifrå mina fiendar, och ifrå dem, som sätta sig emot mig, upphöjer du mig; och ifrå vrångvisa män frälsar du mig.
amene amandimasula mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
50 Derföre vill jag tacka dig, Herre, ibland Hedningarna, och dino Namne lofsjunga;
Choncho ine ndidzakutamandani Inu Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
51 Den der stor salighet bevisar sinom Konung; och gör väl med David sinom smorda, och med hans säd i evig tid.
“Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake, amaonetsa kukoma mtima kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.”

< 2 Samuelsboken 22 >