< 2 Samuelsboken 19 >

1 Och det vardt bådadt Joab: Si, Konungen gråter, och beklagar sig om Absalom.
Yowabu anawuzidwa kuti, “Mfumu ikulira maliro a Abisalomu.”
2 Och vardt i den dagen en sorg af segren i hela folkena; förty folket hade i den dagen hört, att Konungen var bedröfvad om sin son.
Ndipo kwa asilikali onse chipambano cha tsiku limenelo chinasandulika maliro, chifukwa tsiku limenelo anthu anamva kuti mfumu ili pa chisoni chachikulu chifukwa cha mwana wake.
3 Och folket drog sig bort i den dagen, så att det icke kom i staden, lika som ett folk drager sig bort, som till blygd kommet är, när det i strid flytt hafver.
Ankhondo analowa mu mzinda mwakachetechete tsiku limenelo ngati momwe amalowera anthu mwamanyazi chifukwa athawa ku nkhondo.
4 Men Konungen förskylde sitt ansigte, och ropade högt: Ack! min son Absalom! Absalom, min son, min son!
Mfumu inaphimba nkhope yake ndipo inalira mofuwula, “Iwe mwana wanga Abisalomu! Iwe Abisalomu, mwana wanga, mwana wanga!”
5 Så gick Joab in uti huset till Konungen, och sade: Du hafver i dag till blygd gjort alla dina tjenare, som i dag undsatt hafva dina, dina söners, dina döttrars, dina hustrurs och dina frillors själar;
Kenaka Yowabu analowa mʼnyumba ya mfumu nafika kwa mfumuyo ndipo anati, “Lero mwachititsa manyazi asilikali anu onse, amene apulumutsa moyo wanu ndiponso moyo wa ana anu aamuna ndi aakazi, kudzanso moyo wa akazi anu ndi wa azikazi anu.
6 Så att du hafver dem kär som dig hata, och hatar dem som dig kär hafva; ty du låter dig märka i dag, att dig ligger ingen magt uppå höfvitsmännerna och tjenarena; utan jag märker i dag väl, att om allenast Absalom lefde dig, och vi alle i dag döde vore, det skulle dig tycka så godt vara.
Inu mumakonda amene amadana nanu ndipo mumadana ndi amene amakukondani. Inuyo mwaonetsa lero poyera kuti simusamala za atsogoleri anu a nkhondo ndi asilikali awo. Ine ndikuona kuti inu mukanakondwera ngati Abisalomu akanakhala ndi moyo lero, tonsefe titafa.
7 Så statt nu upp, och gack ut, och tala vänliga med dina tjenare; ty jag svär dig vid Herran: Om du icke går ut, blifver icke en man qvar när dig öfver denna nattena; det skall vara dig värre, än allt det onda som öfver dig kommet är, ifrå din ungdom allt intill nu.
Tsopano pitani mukawalimbikitse asilikali anu. Ine ndikulumbira mwa Yehova kuti ngati inu simupita palibe munthu amene adzatsale ali ndi inu polowa dzuwa. Ichi chidzakhala choyipa kwambiri kuposa zovuta zonse zimene zinakugwerani kuyambira muli mnyamata mpaka lero.”
8 Då stod Konungen upp, och satte sig i porten, och allo folkena vardt sagdt: Si, Konungen sitter i portenom. Så kom allt folket för Konungen; men Israel var flydd, hvar och en i sin hyddo.
Kotero mfumu inanyamuka ndipo inakhala pa mpando wake pa chipata. Pamene asilikali anawuzidwa kuti, “Mfumu yakhala pa chipata,” onse anabwera kwa iye. Nthawi imeneyi nʼkuti Aisraeli atathawira ku nyumba zawo.
9 Och allt folket kifvade tillhopa i alla Israels slägter, och sade: Konungen hafver hulpit oss utu våra fiendars hand, och förlossat oss utu de Philisteers hand, och hafver måst fly utaf landena för Absalom.
Pakati pa mafuko onse a Israeli, anthu amakangana ndipo amati, “Mfumu inatipulumutsa mʼmanja mwa adani anthu. Iye ndi amene anatilanditsa mʼdzanja la Afilisti. Koma tsopano wathawa mʼdziko muno chifukwa cha Abisalomu.
10 Så är Absalom död blifven i stridene, den vi öfver oss smort hade; hvi ären I nu så stilla, att I icke hemten Konungen igen?
Ndipo Abisalomu amene ife tinamudzoza kuti atilamulire wafa pa nkhondo. Tsono nʼchifukwa chiyani simukunena kanthu za kubweretsanso mfumu?”
11 Och Konungen sände till Zadok och AbJathar Presterna, och lät säga dem: Taler med de äldsta i Juda, och säger: Hvi viljen I vara de siste, till att hemta Konungen hem i sitt hus igen? Ty hela Israels tal var kommet för Konungen i hans hus.
Mfumu Davide inatumiza uthenga uwu kwa ansembe Zadoki ndi Abiatara, “Funsani akuluakulu a Yuda, ‘Nʼchifukwa chiyani inu mukukhala otsiriza kuyitana mfumu ku nyumba yake yaufumu, pakuti zimene zikunenedwa mu Israeli yense zamveka kwa mfumu ndi onse amene akukhala nayo.
12 I ären mine bröder, mitt ben, och mitt kött; hvi viljen I då vara de siste, till att hemta Konungen igen?
Inu ndinu abale anga enieni, mafupa anga ndi mnofu wanga. Nʼchifukwa chiyani inuyo mukukhala otsiriza kubweretsa mfumu?’
13 Och till Amasa säger: Äst du icke mitt ben, och mitt kött? Gud göre mig det och det, om du icke skall blifva härhöfvitsman för mig, så länge du lefver, i Joabs stad.
Ndipo munene kwa Amasa, ‘Kodi iwe si mʼbale wanga weniweni? Mulungu andilange, andilange kwambiri ngati kuyambira tsopano sukhala mtsogoleri wa ankhondo anga kulowa mʼmalo mwa Yowabu.’”
14 Och han bevekte alla Juda mäns hjerta, såsom ens mans; och de sände till Konungen: Kom igen, du och alle dine tjenare.
Davide anakopa mitima ya anthu onse a Yuda ndipo anthuwo anakhala ngati munthu mmodzi. Iwo anatumiza mawu kwa mfumu, “Bwererani inu ndi anthu anu onse.”
15 Så kom då Konungen igen. Och som han kom till Jordan, voro Juda män komne till Gilgal, till att draga neder emot Konungen, att de skulle föra Konungen öfver Jordan.
Kotero mfumu inabwerera ndipo inakafika mpaka ku Yorodani. Tsono anthu a ku Yuda anabwera ku Giligala kuti akakumane ndi mfumu ndi kumuwolotsa Yorodani.
16 Och Simei, Gera son, Jemini sons, som i Bahurim bodde, hastade sig, och drog neder med Juda män emot Konung David.
Simei mwana wa Gera, wa fuko la Benjamini wa ku Bahurimu, anabwera mofulumira pamodzi ndi Ayuda kudzakumana ndi mfumu Davide.
17 Och med honom voro tusende män af BenJamin; desslikes ock Ziba, den tjenaren af Sauls hus, med hans femton söner, och tjugu tjenare, och de skyndade sig öfver Jordan;
Iyeyo anali ndi anthu 1,000 a fuko la Benjamini pamodzi ndi Ziba, wantchito wa banja la Sauli ndi ana ake aamuna khumi ndi asanu ndi antchito ake makumi awiri. Iwo anathamangira ku Yorodani kumene kunali mfumu.
18 Och beredde färjona för Konungenom, att de skulle föra Konungens tjenare öfver, och göra det honom till vilja var. Och Simei, Gera son, föll neder för Konungen, då han for öfver Jordan;
Iwo anawoloka mtsinje kukatenga banja lonse la mfumu ndi kuchita zonse zimene mfumuyo imafuna. Pamene Simei mwana wa Gera anawoloka Yorodani, anagwa pansi chafufumimba pamaso pa mfumu,
19 Och sade till Konungen: Min Herre, tillräkna mig icke den missgerning, och kom icke ihåg, att din tjenare förtörnade dig den dagen, då min herre Konungen gick utu Jerusalem, och Konungen lägge ett icke på hjertat;
ndipo anati, “Mbuye wanga musaganizire za kulakwa kwanga. Musakumbukire zolakwa zimene mtumiki wanu anakuchitirani tsiku limene mbuye wanga mfumu mumachoka mu Yerusalemu. Mfumu musazikumbukirenso zimenezi.
20 Ty din tjenare känner, att jag syndat hafver. Och si, jag är i dag den förste kommen utaf Josephs hus, att jag skulle draga neder emot min herra Konungen.
Pakuti ine mtumiki wanu ndazindikira kuti ndachimwa. Koma lero ndabwera ngati woyamba wa nyumba ya Yosefe yonse kudzakumana nanu mbuye wanga mfumu.”
21 Men Abisai, ZeruJa son, svarade, och sade: Och skulle icke Simei derföre dö, som bannade Herrans smorda?
Ndipo Abisai mwana wa Zeruya anati, “Kodi Simei saphedwa chifukwa cha ichi? Iye anatukwana wodzozedwa wa Yehova.”
22 David sade: Hvad hafver jag beställa med eder, I ZeruJa barn, att I viljen i dag varda mig till Satan? Skulle i dag någor dö i Israel? Menar du att jag icke vet, att jag i dag är vorden Konung öfver Israel?
Davide anayankha kuti, “Kodi inu ana a Zeruya, ndikuchitireni chiyani? Lero lino iwe wakhala mdani wanga! Kodi wina aphedwe lero mu Israeli? Kodi ine sindikudziwa kuti lero ndine mfumu mu Israeli?”
23 Och Konungen sade till Simei: Du skall icke dö; och Konungen svor honom.
Ndipo mfumu inati kwa Simei, “Iwe Simei suphedwa.” Ndipo mfumuyo inalonjeza ndi lumbiro.
24 Kom också MephiBoseth, Sauls son, neder emot Konungen, och hade intet ryktat sina fötter, eller sitt skägg, eller tvagit sin kläder, ifrå den dagen Konungen bortgången var, intill den dagen då han kom med frid.
Mefiboseti, mdzukulu wa Sauli, nayenso anabwera kudzakumana ndi mfumu. Kuyambira tsiku limene mfumu inachoka mpaka tsiku limene inabwerera mu mtendere, iye sanasambe mapazi kaya kumeta ndevu kapena kuchapa zovala zake.
25 Då han nu till Jerusalem kom, till att möta Konungenom, sade Konungen till honom: Hvi for du icke med mig, MephiBoseth?
Pamene anafika kuchokera ku Yerusalemu kudzakumana ndi mfumu, mfumu inamufunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani sunapite nane Mefiboseti?”
26 Och han sade: Min herre Konung, min tjenare gjorde orätt emot mig; ty din tjenare tänkte: Jag vill sadla en åsna, och stiga deruppå, och rida till min herra Konungen; förty din tjenare är ofärdig.
Iye anayankha kuti, “Mbuye wanga mfumu, pakuti ine wantchito wanu ndine wolumala. Ndinati, ‘Andikonzere chishalo cha bulu wanga ndipo ndidzakwera kuti ndipite ndi mfumu.’ Koma Ziba wantchito wanga anandilakwitsa.
27 Dertill hafver han ock beklagat din tjenare för min herra Konungenom; men min herre Konungen är såsom en Guds Ängel, och må göra hvad honom täckes.
Ndipo wayankhula zosinjirira za ine mtumiki wanu kwa inu mbuye wanga mfumu. Mbuye wanga mfumu ali ngati mngelo wa Mulungu ndipo chitani chimene chikukomerani.
28 Ty allt mins faders hus hafver icke varit utan till döden skyldigt för minom herra Konungenom; så hafver du dock satt din tjenare ibland dem, som äta öfver ditt bord; hvad rätt hafver jag mer, eller hvad kan jag mer ropa till Konungen?
Zidzukulu zonse za agogo anga sizinayenera chilichonse koma imfa kuchokera kwa inu mbuye wanga mfumu, koma inu munapereka malo kwa mtumiki wanu pakati pa amene amadya pa tebulo lanu. Tsono ine ndili ndi chiyaninso kuti ndipitirize kudandaula kwa mfumu?”
29 Konungen sade till honom: Hvad talar du mer härom? Jag hafver sagt det, du och Ziba skifter åkren med hvarannan.
Mfumu inayankha kuti, “Uneneranji zambiri? Ine ndikulamula kuti iwe ndi Ziba mugawane minda.”
30 MephiBoseth sade till Konungen: Han må tagan allsamman, efter min herre Konungen med frid hemkommen är.
Mefiboseti anati kwa mfumu, “Muloleni atenge zonse, pakuti tsopano mbuye wanga mwafika kwanu mu mtendere.”
31 Och Barsillai, den Gileaditen, kom neder ifrå Roglim, och for öfver Jordan för Konungen, på det han skulle ledsaga honom öfver Jordan.
Barizilai Mgiliyadi anabweranso kuchokera ku Rogelimu kudzawoloka Yorodani ndi mfumu ndi kumuperekeza kuchokera kumeneko.
32 Och Barsillai var fast gammal, väl åttatio år; han hade försörjt Konungen, medan han var i Mahanaim; ty han var en ganska väldig man.
Tsono Barizilai anali wokalamba kwambiri, wa zaka makumi asanu ndi atatu. Iye ndi amene anapereka zinthu kwa mfumu pamene anali ku Mahanaimu pakuti anali wolemera kwambiri.
33 Och Konungen sade till Barsillai: Du skall draga fram med mig; jag vill försörja dig med mig i Jerusalem.
Mfumu inati kwa Barizilai, “Woloka nane ndipo ukakhale ndi ine mu Yerusalemu ndipo ineyo ndidzakusamalira.”
34 Men Barsillai sade till Konungen: Hvad är det jag ännu hafver till att lefva, att jag ännu skulle draga upp med Konungenom till Jerusalem?
Barizilai anayankha mfumu kuti, “Kodi zakhala zaka zingati zoti ndikhale ndi moyo, kuti ndipite ku Yerusalemu ndi mfumu?
35 Jag är i dag åttatio år gammal; huru skulle jag känna hvad godt eller ondt är? Eller smaka hvad jag äter eller dricker? Eller höra hvad de sångare eller sångerskor sjunga? Hvi skulle din tjenare ytterligare besvära min herra Konungen?
Ine tsopano ndili ndi zaka 80. Kodi ndingathe kusiyanitsa pakati pa chabwino ndi choyipa? Kodi mtumiki wanu angathe kuzindikira kukoma kwa zimene akudya ndi kumwa? Kodi ndingathe kumva kuyimba kwa amuna ndi akazi? Nʼchifukwa chiyani wantchito wanu akakhale ngati katundu kwa mbuye wanga mfumu?
36 Din tjenare skall något litet fara med Konungenom öfver Jordan; hvi skulle Konungen göra mig en sådana vedergällning?
Koma ine mtumiki wanu ndingoyenda pangʼono kuti ndiwoloke Yorodani pamodzi ndi mfumu. Amfumu mungandipatsirenji mphotho yotere?
37 Låt din tjenare vända om igen, att jag må dö i minom stad, och varda begrafven i mins faders och mine moders grift. Si, der är din tjenare Chimham, den låt draga öfver med min herra Konungen; och gör honom hvad dig täckes.
Muloleni, mtumiki wanu abwerere, kuti ndikafere kwathu pafupi ndi manda a abambo ndi amayi anga. Koma nayu mtumiki wanu Kimuhamu. Muloleni iye awoloke nanu mbuye wanga mfumu. Mumuchitire chilichonse chimene chikukomereni!”
38 Konungen sade: Chimham skall draga öfver med mig, och jag vill göra honom hvad dig är till vilja; och allt det du bedes af mig, det vill jag göra dig.
Mfumu inati, “Kimuhamu adzawoloka ndi ine, ndipo ndidzamuchitira iye chilichonse chimene chidzakondweretsa iwe. Ndipo chilichonse chimene udzandipempha ine ndidzakuchitira.”
39 Och då allt folket var kommet öfver Jordan, och Konungen desslikes, kysste Konungen Barsillai, och välsignade honom; och han vände om igen till sitt rum.
Kotero anthu onse anawoloka Yorodani ndipo kenaka mfumu inawoloka. Mfumu inapsompsona Barizilai ndi kumupatsa madalitso ndipo Barizilaiyo anabwerera kwawo.
40 Och Konungen drog öfver till Gilgal, och Chimham for med honom; och allt Juda folk hade fört Konungen öfver; men Israels folk var icke utan hälften der.
Pamene mfumu inawolokera ku Giligala, Kimuhamu anawoloka naye. Ankhondo onse a Yuda ndi theka la ankhondo a Israeli onse anaperekeza mfumu.
41 Och si, då kommo alle Israels män till Konungen, och sade till honom: Hvi hafva våre bröder, Juda män, stulit dig, och hafva fört Konungen och hans hus öfver Jordan, och alla Davids män med honom?
Kenaka Aisraeli onse amabwera kwa mfumu nʼkumati kwa iye, “Nʼchifukwa chiyani abale athu, anthu a ku Ayuda, anakubani mfumu, nawoloka nanu Yorodani inu ndi banja lanu, pamodzi ndi anthu ake onse?”
42 Då svarade de af Juda dem af Israel: Konungen är oss när åkommen; hvi ären I der vrede före? Menen I, att vi af Konungenom kost och skänker fått hafve?
Ayuda onse anayankha Aisraeli kuti, “Ife timachita zimenezi chifukwa mfumu ndi mʼbale wathu. Nʼchifukwa chiyani inu mwapsa mtima ndi zimenezi? Kodi ife tinadya chakudya chilichonse cha mfumu? Kodi chilipo chimene ife tatenga kukhala chathu?”
43 Så svarade då de af Israel dem af Juda, och sade: Vi hafve tio sinom mer, med Konungenom, med David också, än I; hvi hafver du då så ringa aktat mig, att vi icke måtte hafva varit de förste, till att hemta vår Konung? Men de af Juda talade hårdare, än de män af Israel.
Aisraeli anayankha Ayuda kuti, “Ife ndi magawo khumi mwa mfumu imeneyi, ndipo kuwonjezera apo, ife tili ndi zinthu zambiri mwa Davide kuposa inu. Tsono nʼchifukwa chiyani mukutichita chipongwe? Kodi ife si amene tinayamba kunena za kubweretsa mfumu yathu?” Koma anthu a Yuda anayankha mwaukali kwambiri kupambana anthu a ku Israeli.

< 2 Samuelsboken 19 >