< 2 Samuelsboken 17 >
1 Och Achitophel sade till Absalom: Jag vill utvälja mig tolftusend män, och stå upp till att fara efter David i denna nattene;
Ahitofele anati kwa Abisalomu, “Mundilole ndisankhe asilikali 12,000, ndinyamuke usiku womwe uno kuti ndithamangire Davide.
2 Och vill öfverfalla honom, medan han trött och mödd är. När jag nu förskräcker honom, så att allt folket, som när honom är, flyr, vill jag slå Konungen allena;
Ndipo ndikamuthira nkhondo atatopa ndiponso atataya mtima. Ndikamuchititsa mantha ndipo anthu onse amene ali naye akathawa. Ine ndikakantha mfumu yokhayo,
3 Och draga allt folket till dig igen. När då hvar man till dig dragen är, såsom du begärar, så blifver allt folket i frid.
ndipo anthu onse ndidzabwera nawo kwa inu, ngati mkwati amene akubwerera kwa mwamuna wake. Imfa ya munthu mmodzi yekha idzakhalitsa anthu onse pa mtendere.”
4 Detta tycktes Absalom vara godt, och allom äldstom i Israel.
Malangizo awa anaoneka abwino kwa Abisalomu ndi kwa akuluakulu onse a Israeli.
5 Men Absalom sade: Käre, låt oss ock kalla Husai den Architen, och höra hvad han säger derom.
Koma Abisalomu anati, “Muyitanenso Husai Mwariki kuti timve zimene iye adzanena.”
6 Och då Husai kom in till Absalom, sade Absalom till honom: Sådant hafver Achitophel sagt; säg du, skole vi göra så, eller ej?
Husai atabwera kwa iye, Abisalomu anati, “Ahitofele wapereka malangizo ake. Kodi tichite zimene wanena? Ngati sichoncho, tiwuze maganizo ako.”
7 Då sade Husai till Absalom: Det är intet godt råd, som Achitophel i denna gången gifvit hafver.
Husai anayankha Abisalomu kuti, “Malangizo amene Ahitofele wapereka si abwino pa nthawi ino.
8 Och Husai sade ytterligare: Du känner väl din fader, och hans män, att de äro starke och illsinnade såsom en björn, hvilkom ungarna äro ifråtagne i markene. Dertill är din fader en stridsman, och varder sig intet försummandes med folkena.
Inu mukudziwa bwino abambo anu ali ndi ankhondo awo. Iwo ndi anthu ankhondo komanso ndi woopsa ngati chimbalangondo chimene chalandidwa ana ake. Kuwonjezera apa abambo anu ndi katswiri wa nkhondo. Iwo sanagone pamodzi ndi asilikali awo.
9 Si, han hafver tilläfventyrs nu förvarat sig någorstäds i en kulo, eller annorstäds. Om det nu skedde, att det ginge icke väl i första gången, och uppkomme ett rykte, och sades: Det är skedt en slagtning på det folk, som Absalom efterföljer,
Onani, ngakhale tsopano lino abisala mʼphanga lina ku malo ena ake. Ngati iwo atayamba kuthira nkhondo asilikali anu, aliyense amene adzamve zimenezi adzati, ‘Gulu lalikulu lankhondo lotsatira Abisalomu laphedwa.’
10 Så varder hvar och en förtviflad, den dock eljest dugelig är, och hafver ett hjerta såsom ett lejon; ty hela Israel vet, att din fader är stark, och dugelige män de som när honom äro.
Tsono ngakhale msilikali wolimba mtima kwambiri, amene mtima wake uli ngati wa mkango, adzagwidwa ndi mantha aakulu pakuti Aisraeli akudziwa kuti abambo anu ndi ankhondo ndipo kuti iwo amene ali nawo ndi anthu olimba mtima.
11 Men det råder jag, att du församlar dig hela Israel, ifrå Dan intill BerSeba, många såsom sanden i hafvet; och din person drage ibland dem;
“Kotero ine ndikukulangizani kuti: Aisraeli onse, kuchokera ku Dani mpaka ku Beeriseba; ochuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja, asonkhane kwa inu ndipo muwatsogolera kupita ku nkhondo.
12 Så vilje vi öfverfalla honom på hvad rum vi finne honom, och vilje komma öfver honom, såsom daggen faller på jordena, att vi icke låte blifva en qvar, af honom och alla hans män.
Ndipo ife tidzapita kukamuthira nkhondo kulikonse kumene tikamupeze, ndipo ife tikamuthira nkhondo ngati mame pa nthaka. Palibe amene adzakhale wamoyo kaya iye kapena ankhondo ake.
13 Om han församlar sig in uti någon stad, så skall hela Israel kasta linor kringom samma stad, och rycka honom i strömmen, att der skall icke finnas en sten igen af.
Iye akakathawira mu mzinda, Aisraeli onse adzabweretsa zingwe ku mzindawo, ndipo ife tidzawugwetsera ku chigwa mpaka sipadzapezeka ngakhale kachidutswa.”
14 Då sade Absalom, och hvar och en i Israel: Husai den Architens råd är bättre, än Achitophels råd. Men Herren skickade det så, att det goda Achitophels råd skulle varda förhindradt, på det att Herren skulle låta komma en olycko på Absalom.
Abisalomu ndi ankhondo ena onse a Israeli anati, “Malangizo a Husai Mwariki ndi abwino kuposa a Ahitofele.” Pakuti Yehova anatsimikiza kutsutsa malangizo onse abwino a Ahitofele ndi cholinga choti zimuvute Abisalomu.
15 Och Husai sade till Zadok och AbJathar Presterna: Så och så hafver Achitophel rådt Absalom och dem äldstom i Israel; men jag hafver så och så rådt.
Husai anawuza ansembe Zadoki ndi Abiatara kuti, “Ahitofele analangiza Abisalomu ndi akuluakulu a Israeli zakuti, koma ine ndawalangiza kuchita zakutizakuti.
16 Så sänder nu med hast åstad, och båder David, och säger: Blif icke öfver nattena på slättmarkene i öknene; utan drag deröfver snarliga, att Konungen icke varder uppsluken, och allt folket, som med honom är.
Tsopano tumizani wamthenga msangamsanga kuti akamuwuze Davide kuti, ‘Musakagone powolokera Yorodani ku chipululu koma mukawoloke. Mukapanda kutero, mfumu ndi anthu onse amene ali naye adzaphedwa.’”
17 Men Jonathan och Ahimaaz stodo vid den brunnen Rogel; och en tjenstepiga gick bort, och sade dem det; och de gingo åstad, och sade det Konung David; förty de torde icke låta sig se, så att de kommo in i staden.
Yonatani ndi Ahimaazi amakhala ku Eni Rogeli. Tsono wantchito wamkazi ndiye amapita kukawawuza ndipo iwo amayenera kupita kukamuwuza mfumu Davide, pakuti iwowo sankayenera kuonekera polowa mu mzinda.
18 Men en dräng fick se dem, och sade det för Absalom. Då gingo de både med hast sin väg, och kommo uti ens mans hus i Bahurim; han hade en brunn i sinom gård, der stego de in.
Koma mnyamata wina anawaona ndipo anakawuza Abisalomu. Kotero anthu awiriwo anachoka mofulumira ndipo anapita ku nyumba ya munthu wina ku Bahurimu. Iye anali ndi chitsime ku mpanda kwake ndipo iwo analowamo.
19 Och qvinnan tog och bredde ett öfvertäckelse öfver brunnshålet, och slog der gryn uppå, så att man kunde det intet märka.
Mkazi wake anatenga chophimba ndipo anachiyika pamwamba pa chitsimecho nawazapo tirigu. Palibe amene anadziwa chilichonse za izi.
20 Då nu Absaloms tjenare kommo till qvinnona i huset, sade de: Hvar är Ahimaaz och Jonathan? Qvinnan sade till dem: De gingo öfver vattubäcken. Och då de sökte, och funno intet, gingo de tillbaka igen till Jerusalem.
Anthu a Abisalomu atafika kwa mkaziyo pa nyumbapo anafunsa kuti, “Kodi Ahimaazi ndi Yonatani ali kuti?” Mkaziyo anawayankha kuti, “Awoloka mtsinje.” Anthuwo anafunafuna koma sanapeze munthu, kotero anabwerera ku Yerusalemu.
21 Och då de voro bortgångne, stego de upp utu brunnen, och gingo sina färde; och underviste det Konung David, och sade till David: Står upp, och går med hast öfver älfvena; ty så och så hafver Achitophel gifvit råd emot eder.
Anthu aja atapita, awiriwo anatuluka mʼchitsimemo ndipo anapita kukawuza mfumu Davide nati kwa iye, “Nyamukani, muwoloke mtsinje msangamsanga. Ahitofele wapereka malangizo akutiakuti kutsutsana nanu.”
22 Då stod David upp, och allt folket, som när honom var, och gingo öfver Jordan, tilldess morgon ljust vardt; och icke en fattades, som icke var kommen öfver Jordan.
Kotero Davide ndi anthu onse amene anali nawo ananyamuka ndi kuwoloka Yorodani. Pofika mmamawa, panalibe munthu amene anatsala asanawoloke Yorodani!
23 Då Achitophel såg, att hans råd icke hade framgång, sadlade han sin åsna, och stod upp, och for hem i sin stad, och skickade om sitt hus, och hängde sig, och blef död, och vardt begrafven i sins faders graf.
Ahitofele ataona kuti malangizo ake sanatsatidwe, iye anakwera bulu wake napita ku mzinda wa kwawo ku nyumba yake. Iye anakonza mʼnyumba mwakemo ndi kudzimangirira. Kotero anafa nayikidwa mʼmanda a abambo ake.
24 Och David kom till Mahanaim; och Absalom drog öfver Jordan, och alle Israels män med honom.
Davide anapita ku Mahanaimu, ndipo Abisalomu anawoloka Yorodani pamodzi ndi ankhondo ena onse a Israeli.
25 Och Absalom hade satt Amasa i Joabs stad öfver hären; och Amasa var ens mans son, som het Jithra, en Israelit, hvilken låg när Abigail, Nahas dotter, ZeruJa syster, Joabs moder.
Abisalomu anasankha Amasa kukhala mkulu wa ankhondo mʼmalo mwa Yowabu. Amasa anali mwana wa munthu wotchedwa Itira Mwisraeli amene anakwatira Abigayeli mwana wa Nahasi mlongo wake wa Zeruya, amayi ake a Yowabu.
26 Men Israel och Absalom lägrade sig i Gilead.
Aisraeli ndi Abisalomu anamanga zithando mʼdziko la Giliyadi.
27 Då David var kommen till Mahanaim, kommo der Sobi, Nahas son, af Rabba Ammons barnas, och Machir, Ammiels son af Lodebar, och Barsillai, en Gileadit af Rogelim;
Davide atafika ku Mahanaimu, Sobi mwana wa Nahasi wochokera ku Raba ku dziko la Amoni ndi Makiri mwana wa Amieli wochokera ku Lodebara, ndi Barizilai Mgiliyadi wochokera ku Rogelimu
28 Och förde sängkläder, bäcken, lerkäril, hvete, bjugg, mjöl, torkad ax, bönor, linse, gryn,
anabweretsa zofunda, mabeseni ndi miphika. Iwo anabweretsanso kwa Davide ndi anthu ake zakudya izi: tirigu ndi barele, ufa ndi tirigu wokazinga, nyemba ndi mphodza,
29 Hannog, smör, får, och nötaostar till David, och till folket, som med honom var, till spisning; ty de tänkte, folket varder hungrigt, trött och törstigt i öknene.
uchi ndi chambiko, nkhosa ndi mafuta olimba a mkaka wangʼombe. Pakuti anati, “Anthuwa ali ndi njala ndipo atopa, alinso ndi ludzu muno mʼchipululu.”