< 2 Samuelsboken 16 >
1 Och som David något litet var nedergången af berget, si, då mötte honom Ziba, MephiBoseths tjenare, med ett par sadlade åsnar; deruppå voro tuhundrad bröd, och hundrade stycke russin, och hundrade stycke fikon, och en lägel vin.
Davide atapitirira pangʼono pamwamba pa phiri, anakumana ndi Ziba mtumiki wa Mefiboseti akudikira kuti akumane naye. Iye anali ndi abulu a chishalo pa msana ndipo ananyamula malofu a buledi 200, ntchintchi 100 za mphesa zowuma, zipatso za pa nthawi yachilimwe 100 ndi thumba la vinyo.
2 Då sade Konungen till Ziba: Hvad vill du göra härmed? Ziba sade: Åsnorna skola vara för Konungens husfolk, att de derpå rida; och bröden och fikonen för tjenarena, att de måga äta, och vinet till att dricka, när de varda trötte i öknene.
Mfumu inafunsa Ziba kuti, “Nʼchifukwa chiyani wabweretsa izi?” Ziba anayankha kuti, “Abuluwa ndi oti anthu a mʼbanja mwanu akwerepo, buledi ndi zipatso ndi za anthu anu kuti adye, ndipo vinyoyo ndi woti atsitsimutse anthu amene atope mʼchipululu.”
3 Konungen sade: Hvar är dins herras son? Ziba sade till Konungen: Si, han blef i Jerusalem; ty han sade: I dag varder Israels hus mig igengifvandes mins faders rike.
Kenaka mfumu inafunsa kuti, “Kodi chidzukulu cha mbuye wako chili kuti?” Ziba anati kwa iye, “Watsalira ku Yerusalemu chifukwa akuganiza kuti, ‘Lero Aisraeli andibwezera ufumu wa agogo anga.’”
4 Konungen sade till Ziba: Si, allt det MephiBoseth hafver, skall vara ditt. Ziba sade med tillbedjande: Låt mig finna nåd för dig, min herre Konung.
Ndipo mfumu inati kwa Ziba, “Zonse zimene zinali za Mefiboseti ndi zako tsopano.” Ziba anati, “Ine modzichepetsa ndikukugwandirani, mbuye wanga mfumu, kuti ndipeze chisomo pamaso panu.”
5 Då nu Konung David kom till Bahurim, si, då gick der en man utaf Sauls hus slägt, han het Simei, Gera son; han gick ut och bannades;
Mfumu Davide itayandikira Bahurimu, munthu wochokera ku fuko limodzi ndi banja la Sauli anabwera kuchokera mʼmenemo. Dzina lake linali Simei, mwana wa Gera ndipo amatukwana pamene amabwera.
6 Och kastade stenar åt David, och åt alla Konung Davids tjenare; ty allt folk och alle de väldige voro vid hans högra, och vid hans venstra sido.
Iye amagenda Davide miyala ndi akuluakulu onse a mfumu, ngakhale kuti ankhondo onse ndi oteteza Davide anali ali kumanzere ndi kumanja kwake.
7 Och sade Simei, då han bannades: Härut, härut, du blodhund, du Belials man!
Potukwana, Simeiyo amati, “Choka iwe, choka iwe, munthu wopha anthu, munthu wachabechabe iwe!
8 Herren hafver vedergullit dig allt Sauls hus blod, att du äst vorden Konung i hans stad; nu hafver Herren gifvit riket i din sons Absaloms hand; och si, nu tränger dig din olycka; ty du äst en blodhund.
Yehova wakubwezera chifukwa cha magazi onse amene unakhetsa pa nyumba ya Sauli, yemwe iwe ukulamulira mʼmalo mwake. Yehova wapereka ufumu kwa mwana wako Abisalomu. Ndipo ona mathero ako ndi amenewa chifukwa ndiwe munthu wopha anthu!”
9 Men Abisai, ZeruJa son, sade till Konungen: Skall denne döde hunden banna min herra Konungen? Jag vill gå bort, och hugga hufvudet af honom.
Ndipo Abisai mwana wa Zeruya anati kwa mfumu, “Nʼchifukwa chiyani galu wakufa uyu akutukwana mbuye wanga mfumu? Ndiloleni ndipite kuti ndikadule mutu wake.”
10 Konungen sade: I ZeruJa barn, hvad hafver jag skaffa med eder? Låt honom banna, ty Herren hafver budit honom banna David. Ho kan nu säga, hvi gör du så?
Koma mfumu inati, “Inu ana a Zeruya, kodi ndikuchitireni chiyani? Ngati iye akutukwana chifukwa Yehova wamuwuza kuti, ‘Tukwana Davide,’ angafunse ndani kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ukuchita zimenezi?’”
11 Och David sade till Abisai, och till alla sina tjenare: Si, min son, som af mitt lif kommen är, går mig efter mitt lif; hvi ock icke nu Jemini son? Låt honom betämma, att han bannar; ty Herren hafver så budit honom.
Tsono Davide anati kwa Abisai ndi akuluakulu ake onse, “Mwana wanga wobereka ndekha akufuna kundipha. Nanji tsono munthu wa fuko la Benjamini uyu! Musiyeni; mulekeni atukwane pakuti Yehova wachita kumuwuza kuti atero.
12 Må hända, att Herren ser till mina bedröfvelse, och Herren löner mig med godo dessa bannor, som jag lider i dag.
Mwina Yehova adzaona mazunzo anga ndipo adzandibwezera zabwino chifukwa cha kutukwanidwa kumene ndikulandira lero.”
13 Alltså gick David med sitt folk framåt vägen; men Simei gick ut med bergssidone jemte vid honom, och bannades, och kastade stenar till honom, och hof jord.
Kotero Davide ndi anthu ake anapitirira kuyenda mu msewu pamene Simei amayenda mʼmbali mwa phiri moyangʼanana naye akutukwana ndi kuponya miyala pamene amayenda nʼkumamutsiranso dothi.
14 Och Konungen kom derin, och allt folket, som med honom var, trötte; och vederqvickte sig der.
Mfumu ndi anthu ake onse anafika kumene amapita atatopa kwambiri. Ndipo kumeneko anapumula.
15 Men Absalom och allt folket, Israels män, kommo till Jerusalem, och Achitophel med honom.
Pa nthawi imeneyi Abisalomu ndi Aisraeli ena onse anabwera ku Yerusalemu, Ahitofele anali naye.
16 Då nu Husai den Architen, Davids vän, kom in till Absalom, sade han till Absalom: Till lycko, herre Konung, till lycko, herre Konung.
Tsono Husai Mwariki bwenzi la Davide anapita kwa Abisalomu ndipo anati kwa iye, “Ikhale ndi moyo wautali mfumu! Ikhale ndi moyo wautali mfumu!”
17 Absalom sade till Husai: Är detta din barmhertighet emot din vän? Hvi hafver du icke farit ut med dinom vän?
Abisalomu anafunsa Husai, “Kodi ichi ndi chikondi chimene ukumuonetsa bwenzi lako? Nʼchifukwa chiyani sunapite ndi bwenzi lako?”
18 Husai sade till Absalom: Icke så, utan den som Herren utväljer, och detta folk, och hvar man i Israel, honom vill jag tillhöra, och när honom blifva.
Husai anati kwa Abisalomu, “Ayi, ndidzakhala wake wa amene Yehova wamusankha, wosankhidwa ndi anthu awa ndi anthu onse a Israeli, ndipo ndidzakhala wake nthawi zonse.
19 Och sedan, hvem skulle jag tjena? Skulle jag icke tjena hans son? Såsom jag hafver tjent dinom fader, så vill jag ock tjena dig.
Kodi ndidzatumikiranso yani? Kodi sinditumikira mwana wa mfumu? Monga momwe ndinatumikira abambo anu, kotero ndidzatumikiranso inu.”
20 Och Absalom sade till Achitophel: Gifver råd, hvad skole vi göra?
Abisalomu anati kwa Ahitofele, “Tiwuze malangizo ako. Kodi tichite chiyani?”
21 Achitophel sade till Absalom: Lägg dig när dins faders frillor, som han hafver låtit qvara blifva till att bevara huset, så får hele Israel höra, att du hafver gjort din fader illa luktande, och alles deras hand, som när dig äro, blifver styrkt.
Ahitofele anayankha kuti, “Mugone ndi azikazi a abambo anu amene awasiya kuti asamalire nyumba yaufumu. Aisraeli onse adzamva kuti mwachitira abambo anu chinthu chonyansa kotheratu ndipo anthu onse amene ali ndi iwe adzalimbikitsidwa.”
22 Då gjorde de till Absalom ett tjäll uppå taket; och Absalom belåg sins faders frillor för all Israels ögon.
Choncho anamangira tenti Abisalomu pa denga la nyumba ndipo iye anagona ndi azikazi a abambo ake Aisraeli onse akuona.
23 På den tiden, då Achitophel gaf ett råd, var det såsom man hade frågat Gud om någon ting; alltså var all Achitophels rådslag, både när David, och så när Absalom.
Tsono masiku amenewo malangizo amene Ahitofele amapereka anali ngati mawu ochokera kwa Mulungu. Umu ndi mmene Davide ndi Abisalomu amalandirira malangizo onse a Ahitofele.