< 2 Samuelsboken 14 >

1 Men Joab, ZeruJa son, förmärkte att Konungens hjerta var vändt till Absalom.
Yowabu mwana wa Zeruya anadziwa kuti maganizo a mfumu ali pa Abisalomu.
2 Och han sände bort till Thekoa, och lät hämta dädan ena kloka qvinno, och sade till henne: Jämra dig, och drag sorgkläder uppå, och smörj dig icke med oljo; utan ställ dig såsom en qvinna, den en lång tid hafver haft sorg öfver någon dödan;
Kotero Yowabu anatuma munthu wina kupita ku Tekowa ndi kukatengako mkazi wanzeru. Yowabu anati kwa mkaziyo, “Ukhale ngati namfedwa. Uvale zovala zaumasiye ndipo usadzole mafuta ena aliwonse. Ukhale ngati mkazi amene wakhala akulira masiku ambiri.
3 Och skall gå in till Konungen, och tala så och så med honom. Och Joab gaf henne in hvad hon säga skulle.
Kenaka upite kwa mfumu ndipo ukayankhule mawu awa.” Ndipo Yowabu anamuwuza mawu oti akanene.
4 Och då Qvinnan af Thekoa ville tala med Konungenom, föll hon på sitt anlete neder på jordena, och tillbad, och sade: Hjelp mig, Konung.
Mkazi wochokera ku Tekowa uja atapita kwa mfumu anadzigwetsa pansi, napereka ulemu kwa mfumu nati, “Thandizeni mfumu!”
5 Konungen sade till henne: Hvad är dig? Hon sade: Jag är en enka, en qvinna som sorg hafver, och min man är död;
Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi chikukusautsa iwe nʼchiyani?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine mkazi wamasiye, mwamuna wanga anamwalira.
6 Och din tjenarinna hade två söner; de kifvade tillhopa på markene; och efter der var ingen, som dem förtagat kunde, slog den ene den andra, och drap honom.
Ine wantchito wanu ndinali ndi ana aamuna awiri. Iwo anayamba kumenyana mʼmunda, ndipo panalibe woti awaleretse. Wina anakantha mnzakeyo mpaka kumupha.
7 Och si, nu reser sig upp hela slägten emot dina tjenarinno, och säga: Få hit den som slog sin broder ihjäl, att vi måge dräpa honom för hans broders själ, den han dräpit hafver, och göra dig arfvingalösa; och de vilja utsläcka mina gnisto, som ännu qvar är, att minom man intet namn och ingen återlefva blifva skall på jordene.
Tsono banja lonse landiwukira ine, wantchito wanu. Iwo akuti, ‘Utipatse mwana amene anakantha mʼbale wakeyo kuti timuphe chifukwa cha moyo wa mʼbale wake amene anaphedwayo. Ife tidzaphanso mlowamʼmalo.’ Anthuwo adzapha mwana wanga amene wanditsalira, ndipo dzina la mwamuna wanga silidzakumbukika pakuti sipadzakhalanso mwana pa banja lathu.”
8 Konungen sade till qvinnona: Gack hem, jag vill bjuda för dig.
Mfumu inati kwa mkaziyo, “Pitani ku nyumba kwanu ndipo ine ndidzalamula mʼmalo mwanu.”
9 Och qvinnan af Thekoa sade till Konungen: Min herre Konung, missgerningen vare uppå mig, och uppå mins faders hus; men Konungen och hans stol vare oskyldig.
Koma mkazi wochokera ku Tekowayo anati kwa mfumu, “Mbuye wanga mfumu, kulakwa kukhale pa ine ndi banja la abambo anga ndipo mfumu ndi mpando wanu waufumu mukhale osalakwa.”
10 Konungen sade: Den som emot dig talar, honom haf till mig, så skall han intet mer röra dig.
Mfumu inayankha kuti, “Ngati wina aliyense anene kanthu kwa iwe, umubweretse kwa ine, ndipo sadzakuvutitsanso.”
11 Hon sade: Konungen tänke på Herran din Gud, att de blodhämnare icke varda för månge till att förderfva, och att min son icke förgörs. Han sade: Så sant som Herren lefver, skall icke ett hår falla på jordene af dinom son.
Mkaziyo anati, “Mfumu ipemphe kwa Yehova Mulungu wake kuti aletse wobwezera imfa asaphenso wina kuti mwana wanga asawonongedwe.” Mfumu inati, “Pali Yehova wamoyo ngakhale tsitsi limodzi la pamutu pa mwana wako silidzathotholedwa.”
12 Och qvinnan sade: Låt dina tjenarinno något säga minom herra Konungenom. Han sade: Säg.
Kenaka mkaziyo anati, “Lolani kuti wantchito wanu ayankhule mawu kwa inu mbuye wanga mfumu.” Iye anayankha kuti, “Yankhula.”
13 Qvinnan sade: Hvi hafver du ett sådant tänkt emot Guds folk, att Konungen detta sagt hafver, att han skall komma sig i skuld, och icke låta igentaga sin fördrefna?
Mkaziyo anati, “Nʼchiyani tsono chimene mwaganiza kuchitira zimenezi anthu a Mulungu? Pamene mfumu yanena izi, kodi sikudzitsutsa yokha, pakuti mfumu sinayitanitse mwana amene anamupirikitsa?
14 Ty vi dö döden, och förlöpe såsom vatten i jordena, det man icke uppehåller; och Gud vill icke taga lifvet bort, utan betänker sig, att det fördrefna icke också skall fördrifvet varda af honom.
Koma poti madzi akatayika sawoleka, ndiye tonsefe tiyenera kufa ndithu. Koma Mulungu safuna kuti moyo wa munthu utayike kotero anakonza njira yakuti wopirikitsidwayo asakhale wotayikiratu.
15 Så är jag nu kommen, till att tala med min herra Konungen dessa ord; ty folket hafver förskräckt mig; ty din tjenarinna tänkte: Jag skall tala med Konungenom; kanhända, att han gör det hans tjenarinna säger.
“Tsopano ine ndabwera kudzanena izi kwa inu mbuye wanga mfumu chifukwa anthu andichititsa mantha. Mdzakazi wanu anaganiza kuti, ‘Ndikayankhula kwa mfumu, mwina adzachita zimene mdzakazi wake adzamupempha.
16 Ty han skall väl höra sina tjenarinno, att han hjelper mig ifrån allas deras hand, som mig, samt med minom son, ifrå Guds arf förgöra vilja.
Mwina mfumu idzavomereza kupulumutsa mdzakazi wake mʼdzanja la munthu amene akufuna kupha ine pamodzi ndi mwana wanga kutichotsa pa cholowa chimene Mulungu anatipatsa.’
17 Och din tjenarinna tänkte: Mins herras Konungens ord skall vara mig en tröst; ty min herre Konungen är såsom en Guds Ängel, så att han kan höra godt och ondt; derföre varder ock Herren din Gud med dig blifvandes.
“Ndipo tsopano mtumiki wanu akuti, ‘Lolani mawu a mbuye wanga mfumu abweretse mpumulo kwa ine, pakuti mbuye wanga mfumu ali ngati mngelo wa Mulungu pozindikira chabwino ndi choyipa. Yehova Mulungu wanu akhale nanu.’”
18 Konungen svarade, och sade till qvinnona: Ljug icke för mig i det jag frågar dig. Qvinnan sade: Min herre Konungen tale.
Kenaka mfumu inati kwa mkaziyo, “Usandibisire chilichonse pondiyankha chimene ndidzakufunsa.” Mkaziyo anati, “Mbuye wanga mfumu yankhulani.”
19 Konungen sade: Är icke Joabs hand med dig i allo desso? Qvinnan svarade, och sade: Så sant som din själ lefver, min herre Konung, det är ingen annan, antingen på högra handen eller den venstra, utan såsom min herre Konungen sagt hafver; ty din tjenare Joab hafver detta så budit mig, och han hafver allt detta dine tjenarinno ingifvit.
Mfumu inafunsa kuti, “Kodi zimenezi sukuchita motsogozedwa ndi Yowabu?” Mkaziyo anayankha kuti, “Pali inu wamoyo, mbuye wanga mfumu, palibe munthu angakhotere kumanja kapena kumanzere pa chilichonse chimene mbuye wanga mfumu mwanena. Inde, ndi mtumiki wanu Yowabu amene wandilangiza ine kuchita zimenezi ndipo ndi amene anandipatsa mawu onsewa woti ine mtumiki wanu ndiyankhule.
20 Att jag skulle så vända denna sakena, det hafver din tjenare Joab gjort; men min herre är vis såsom en Guds Ängels vishet, så att han allt vet på jordene.
Mtumiki wanu Yowabu anachita zimenezi kuti asinthe mmene zinthu zilili lero. Mbuye wanga muli ndi nzeru ngati za mngelo wa Mulungu. Mumadziwa zonse zimene zikuchitika mʼdziko.”
21 Då sade Konungen till Joab: Si, jag hafver detta gjort; så gack nu bort, och haf pilten Absalom hem igen.
Mfumu inati kwa Yowabu, “Chabwino, ine ndichita zimenezi. Pita kamutenge Abisalomuyo.”
22 Då föll Joab på sitt ansigte till jordena, och tillbad, och tackade Konungenom, och sade: I dag förmärker din tjenare, att jag hafver funnit nåd för din ögon, min herre Konung, att Konungen gör hvad hans tjenare säger.
Yowabu anawerama pansi kupereka ulemu kwa mfumu. Yowabuyo anati, “Lero mtumiki wanu wadziwa kuti wapeza chifundo pamaso panu, mbuye wanga mfumu, chifukwa mwavomera pempho lakeli.”
23 Så stod då Joab upp, och for till Gesur, och hade Absalom till Jerusalem.
Choncho Yowabu anapita ku Gesuri ndipo anamubweretsa Abisalomu ku Yerusalemu.
24 Men Konungen sade: Låt honom gå i sitt hus igen, och icke se mitt ansigte. Och så kom då Absalom igen i sitt hus, och såg intet Konungens ansigte.
Koma mfumu inati, “Iye apite ku nyumba yake; asaone nkhope yanga.” Kotero Abisalomu anapita ku nyumba yake ndipo sanakumane ndi mfumu.
25 Och i hela Israel var icke en man så dägelig och så prislig som Absalom; ifrå hans fotabjelle upp till hans hjessa var ingen brist på honom.
Mʼdziko lonse la Israeli munalibe munthu amene anayamikidwa chifukwa cha maonekedwe ake wokongola ngati Abisalomu. Kuyambira kumutu mpaka ku mapazi ake, analibe chilema.
26 Och när han skar sitt hår af; det skedde gemenliga hvart år, ty det var honom för tungt, så att man måste det afskära; så vog hans hufvudhår tuhundrade siklar, efter Konungsvigt.
Nthawi ina iliyonse akamameta tsitsi lake, ankameta pamene layamba kumulemera. Akatero amaliyeza, ndipo limalemera makilogalamu awiri pa sikelo yaufumu.
27 Och Absalom vordo födde tre söner, och en dotter; hon het Thamar, och var en dägelig qvinna.
Abisalomu anali ndi ana aamuna atatu ndi wamkazi mmodzi. Mwana wamkazi dzina lake linali Tamara, ndipo anali mkazi wokongola kwambiri.
28 Alltså blef Absalom i tu år i Jerusalem, att han Konungens ansigte intet såg.
Abisalomu anakhala zaka ziwiri mu Yerusalemu osaonekera kwa mfumu.
29 Och Absalom sände efter Joab, att han skulle sända honom till Konungen; och han ville icke komma till honom. Han sände annan gången, likväl ville han icke komma,
Kenaka Abisalomu anatumiza mawu kwa Yowabu, kumutuma kuti apite kwa mfumu, koma Yowabu anakana kubwera. Kotero anatumizanso mawu kachiwiri, koma Yowabu anakananso.
30 Då sade han till sina tjenare: Ser det stycket af Joabs åker bredevid min, och han hafver der bjugg uppå; så går bort, och sticker eld deruppå. Så stucko Absaloms tjenare eld på det stycket.
Tsono Abisalomu anati kwa antchito ake, “Taonani, munda wa Yowabu uli pafupi ndi wanga ndipo muli barele mʼmenemo. Pitani mukawutenthe mundawo.” Ndipo antchito a Abisalomu anawutentha mundawo.
31 Då stod Joab upp, och kom till Absalom i huset, och sade till honom: Hvi hafva dine tjenare stuckit eld på mitt stycke?
Ndipo Yowabu anapita ku nyumba ya Abisalomu ndipo anati kwa iye, “Nʼchifukwa chiyani antchito ako atentha munda wanga?”
32 Absalom sade till Joab: Si, jag sände efter dig, och lät säga dig: Kom till mig, att jag må sända dig till Konungen, och låta säga: Hvi kom jag ifrå Gesur? Det vore mig bättre, att jag ännu vore der. Så låt mig nu få se Konungens ansigte; är ock någon missgerning i mig, så dräp mig.
Abisalomu anati kwa Yowabu, “Taona, ine ndinatumiza mawu kwa iwe ndipo ndinati, ‘Bwera kuno kuti ndikutume kwa mfumu kukafunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ine ndinabwera kuchokera ku Gesuri? Zikanakhala bwino ndikanakhala komweko!’ Tsono pano ndikufuna kuonana ndi mfumu, ndipo ngati ndili olakwa mfumuyo indiphe.’”
33 Och Joab gick in till Konungen, och sade det honom; och han kallade Absalom, att han kom in till Konungen; och han tillbad på sitt ansigte neder till jordena för Konungenom; och Konungen kysste Absalom.
Choncho Yowabu anapita kwa mfumu ndipo anayiwuza zimenezi. Ndipo mfumu inamuyitanitsa Abisalomu, ndipo analowa nawerama kugunditsa nkhope yake pansi pamaso pa mfumu. Tsono mfumu inapsompsona Abisalomu.

< 2 Samuelsboken 14 >