< 2 Samuelsboken 12 >

1 Och Herren sände Nathan till David. När han kom till honom, sade han till honom: Det voro två män uti en stad; den ene rik, den andre fattig.
Tsono Yehova anatumiza Natani kwa Davide. Atafika kwa Davide anati, “Panali anthu awiri mʼmizinda ina, wina wolemera ndi wina wosauka.
2 Den rike hade ganska mycken får och fä;
Munthu wolemerayo anali ndi nkhosa ndi ngʼombe zambiri,
3 Men den fattige icke utan ett litet får, hans endesta, hvilket han köpt hade, och uppfödde det, att det uppväxte när honom, och bredovid hans barn. Det åt af hans beta, och drack af hans drickekar, och sof i hans famn, och han höll det såsom ena dotter.
koma wosaukayo analibe chilichonse kupatula kankhosa kamodzi kakakazi kamene anakagula. Iye anakasunga ndipo kanakula naye pamodzi ndi ana ake. Kamadya chakudya chake, kamamwera chikho chake ndipo kamagona mʼmanja mwake. Kanali ngati mwana wamkazi kwa iyeyo.
4 Men då till den rika mannen kom en gäst, nändes han icke taga af sin får och fä, till att tillreda något åt den gästen, som till honom kommen var; och tog den fattiga mannens får, och redde det till för den mannen, som till honom kommen var.
“Ndipo mlendo anafika kwa munthu wolemera uja, koma munthu wolemerayo sanafune kutenga imodzi mwa nkhosa kapena ngʼombe zake kuti akonzere chakudya mlendo amene anafika kwa iye. Mʼmalo mwake anatenga mwana wankhosa wamkazi wa munthu wosauka uja nakonzera chakudya mlendo uja amene anabwera kwa iye.”
5 Då förgrymmade sig David med stora vrede emot den mannen, och sade till Nathan: Så sant som Herren lefver, den mannen är dödsens barn, som detta gjort hafver.
Davide anapsa mtima kwambiri chifukwa cha munthuyo ndipo anati kwa Natani, “Pali Yehova, munthu amene anachita zimenezi ayenera kufa basi!
6 Dertill skall han betala fåret fyradubbelt igen, efter han sådant gjort hafver, och icke hade det fördrag.
Iye ayenera kulipira mwana wankhosa wamkaziyo kanayi, chifukwa anachita chinthu chimenechi ndipo analibe chifundo.”
7 Då sade Nathan till David: Du äst den mannen. Så säger Herren Israels Gud: Jag hafver smort dig till en Konung öfver Israel, och hafver frälst dig utu Sauls hand;
Kenaka Natani anati kwa Davide, “Munthuyo ndinu! Yehova, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakudzoza kukhala mfumu ya Israeli, ndipo ndinakupulumutsa mʼdzanja la Sauli.
8 Och hafver gifvit dig dins herras hus; dertill hans hustrur i din famn, och hafver gifvit dig Israels hus och Juda; och är det icke nog, vill jag ännu det och det göra dig dertill.
Ndinakupatsanso banja la mbuye wako ndiponso akazi a mbuye wako mʼmanja mwako. Ine ndinakupatsanso banja la Israeli ndi Yuda. Ndipo ngati zinthu zonse izi zinali zochepa, Ine ndikanakupatsa zambiri.
9 Hvi hafver du då föraktat Herrans ord, att du sådant ondt för hans ögon göra skulle? Uria den Hetheen hafver du slagit med svärd; hans hustru hafver du tagit dig till hustru; men honom hafver du dräpit med Ammons barnas svärd.
Nʼchifukwa chiyani unanyoza mawu a Yehova pochita chimene chili choyipa pamaso pake? Iwe unakantha Uriya Mhiti ndi lupanga ndipo unatenga mkazi wake kukhala wako. Uriyayo unamupha ndi lupanga la Aamoni.
10 Nu, så skall icke svärd återvända af ditt hus till evig tid; efter du hafver föraktat mig, och Uria den Hetheens hustru tagit, att hon skall vara din hustru.
Ndipo tsopano lupanga silidzachoka pa nyumba yako, chifukwa unandinyoza ine ndi kutenga mkazi wa Uriya Mhiti kukhala wako.’
11 Detta säger Herren: Si, jag skall uppväcka ondt öfver dig, utaf ditt eget hus, och skall taga dina hustrur för din ögon, och skall gifva dinom nästa, att han skall ligga när dina hustrur om ljusa dagen.
“Yehova akuti, ‘Ine ndidzabweretsa tsoka pa iwe lochokera mʼbanja lako. Ndidzatenga akazi ako iwe ukuona ndi kuwapereka kwa wina amene ali pafupi nawe, ndipo iye adzagona ndi akazi ako masanasana Aisraeli onse akuona.
12 Ty du hafver gjort det hemliga; men jag vill detta göra för hela Israel, på ljusa dagen.
Iwe unachita zimenezi mwamseri koma Ine ndidzachita izi masanasana Aisraeli onse akuona.’”
13 Då sade David till Nathan: Jag hafver syndat emot Herranom. Nathan sade till David: Så hafver ock Herren tagit din synd bort; du skall icke dö.
Kenaka Davide anati kwa Natani, “Ine ndachimwira Yehova.” Natani anayankha kuti, “Yehova wachotsa tchimo lanu. Simufa ayi.
14 Men efter du hafver med detta ärendet kommit Herrans fiendar till att förhäda, skall den sonen, som dig födder är, döden dö.
Komabe, popeza pochita zimenezi mwachititsa kuti adani a Yehova amunyoze, mwana amene akubalireniyo adzafa.”
15 Och Nathan gick hem i sitt hus. Men Herren slog barnet, som Uria hustru David födt hade, så att det vardt dödssjukt.
Natani atapita kwawo, Yehova anakantha mwana amene mkazi wa Uriya anabereka ndipo anayamba kudwala.
16 Och David bad Gud om barnet, och fastade, och gick in, och låg öfver natt ena på jordene.
Davide anapempherera mwanayo kwa Mulungu. Iye anasala chakudya ndipo analowa mʼnyumba mwake nagona pansi usiku wonse.
17 Då stodo upp de äldste i hans hus, och ville rätta honom upp af jordene; men han ville icke, och åt icke heller med dem.
Akuluakulu a banja lake anayima pambali pake kuti amudzutse, koma iye anakana, ndipo sanadye chakudya chilichonse pamodzi ndi iwo.
18 På sjunde dagenom blef barnet dödt; och Davids tjenare torde icke säga honom att barnet var dödt; ty de tänkte: Si, då barnet ännu var lefvandes, talade vi med honom, och han hörde vår röst intet; huru mycket mer skall det göra honom ondt, om vi säge: Barnet är dödt?
Mwana anamwalira pa tsiku lachisanu ndi chiwiri. Antchito a Davide anaopa kumuwuza kuti mwanayo wamwalira, popeza ankaganiza kuti, “Pamene mwanayu anali ndi moyo, ife tinayankhula Davide koma sanatimvere. Nanga tingamuwuze bwanji kuti mwana wamwalira? Mwina atha kudzipweteka.”
19 Och David fick se att hans tjenare talade i mjugg, och förmärkte att barnet var dödt, och sade till sina tjenare: Är barnet dödt? De sade: Ja.
Davide anaona kuti antchito ake amanongʼonezana pakati pawo ndipo anazindikira kuti mwanayo wamwalira. Iye anafunsa kuti, “Kodi mwanayo wamwalira?” Iwo anayankha kuti, “Inde wamwalira.”
20 Då stod David upp af jordene, och tvådde sig, och smorde sig, och lade annor kläder uppå, och gick in uti Herrans hus, och tillbad; och då han kom hem igen i sitt hus, lät han komma mat upp för sig, och åt.
Ndipo Davide anayimirira. Anakasamba nadzola mafuta ndi kusintha zovala zake. Pambuyo pake anapita ku nyumba ya Yehova kukapembedza. Kenaka anapita ku nyumba kwake ndipo atapempha chakudya anamupatsa nadya.
21 Då sade hans tjenare till honom: Hvad är det för ett ting, som du gör? Då barnet lefde, fastade du, och gret; men nu, sedan det dödt är, står du upp, och äter!
Antchito ake anamufunsa kuti, “Chifukwa chiyani mukuchita zinthu motere? Pamene mwana anali ndi moyo, munkasala chakudya ndi kulira, koma tsopano pamene mwana wamwalira inu mukudzuka ndi kudya!”
22 Han sade: För barnets skull fastade jag, och gret, då det lefde; ty jag tänkte: Ho vet, om Herren varder mig nådelig, så att barnet må blifva vid lif.
Iye anayankha kuti, “Pamene mwana anali ndi moyo ine ndinkasala zakudya ndi kulira. Ine ndinkaganiza kuti, ‘Akudziwa ndani? Yehova atha kundikomera mtima kuti mwanayo akhale ndi moyo.’
23 Men nu, sedan det dödt är, hvad skulle jag fasta? Kan jag ock hemta honom igen? Jag går väl till honom, men han kommer intet till mig igen.
Koma tsopano wamwalira ndisaliranji chakudya? Kodi ndingathe kumubwezanso? Ine ndidzapita kumene kuli iyeko, koma iye sadzabwerera kwa ine.”
24 Och då David hade hugsvalat sina hustru BathSeba, gick han in till henne, och sof när henne; och hon födde en son, den kallade han Salomo; och Herren älskade honom.
Ndipo Davide anatonthoza mkazi wake Batiseba, napita kwa iye ndi kugona naye. Iye anabereka mwana wamwamuna, ndipo anamutcha dzina lake Solomoni. Yehova ankamukonda iye.
25 Och han fick honom under Nathans hand, Prophetens; han kallade honom JedidJa, för Herrans skull.
Ndipo chifukwa chakuti Yehova ankamukonda iyeyo, Yehovayo anatumiza mawu kwa mneneri Natani kuti akamutchule Yedidiya.
26 Så stridde nu Joab emot Rabba Ammons barnas, och vann den Konungsliga staden;
Pa nthawi imeneyi Yowabu anamenyana ndi Raba ku Amoni ndipo analanda nsanja yaufumu.
27 Och sände båd till David, och lät säga honom: Jag hafver stridt emot Rabba, och hafver ock vunnit vattustaden.
Ndipo Yowabu anatumiza amithenga kwa Davide kukanena kuti, “Ine ndamenyana ndi Raba ndipo ndatenga zitsime zake za madzi.
28 Så tag nu tillhopa det folk, som qvart är, och belägg staden, och vinn honom; på det att jag icke vinner honom, och får der namnet af.
Ndipo tsopano sonkhanitsani asilikali onse ndipo muzungulire mzindawo ndi kuwulanda.”
29 Alltså tog David allt folket tillhopa, och drog åstad, och stridde emot Rabba, och vann honom;
Kotero Davide anasonkhanitsa ankhondo onse ndipo anapita ku Raba kukawuthira nkhondo ndi kuwulanda.
30 Och tog deras Konungs krono utaf hans hufvud, hvilken hade i vigt en centener guld, och ädla stenar; och den vardt satt David på hans hufvud; och förde ganska mycket rof utu staden.
Davide anachotsa chipewa chaufumu pamutu pa mfumu yawo ndipo Davide anavala chipewacho. Chipewacho chinkalemera makilogalamu asanu agolide, ndiponso chinali ndi miyala yokongola. Iye anatenga katundu wambiri kuchokera mu mzindawo,
31 Och folket derinne förde han ut, och lade dem under jernsågar och taggar, och jernkilar, och brände dem upp uti tegelugnar; så gjorde han alla Ammons barnas städer. Så vände då David och allt folket om igen till Jerusalem.
ndipo anatulutsa anthu amene anali mʼmenemo, nawayika kuti azigwira ntchito ya macheka, yosula makasu ndi nkhwangwa, ndiponso yowomba njerwa. Davide anachita izi ndi mizinda yonse ya Aamoni. Kenaka iye pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo anabwerera ku Yerusalemu.

< 2 Samuelsboken 12 >