< 2 Kungaboken 4 >
1 Och en qvinna utaf de Propheters söners hustrur ropade till Elisa, och sade: Din tjenare, min man, är död blefven; så vetst du, att han din tjenare fruktade Herran; nu kommer den han skyldig var, och vill taga båda mina söner till trälar.
Mkazi wa mmodzi mwa ana a aneneri anafuwula kwa Elisa kuti, “Mtumiki wanu, mwamuna wanga wamwalira ndipo inu mukudziwa kuti ankaopa Yehova. Koma tsopano munthu amene mwamuna wanga anakongolako zinthu zake, akubwera kudzatenga ana anga awiri aamuna kuti akhale akapolo ake.”
2 Elisa sade till henne: Hvad skall jag göra dig? Säg mig, hvad hafver du i huset? Hon sade: Din tjenarinna hafver intet i huset, utan ena kruko med oljo.
Elisa anayankha mayiyo kuti, “Kodi ufuna ndikuchitire chiyani? Tandiwuza uli ndi chiyani mʼnyumba mwako?” Mayiyo anayankha kuti, “Mdzakazi wanu alibe kanthu kalikonse koma timafuta pangʼono chabe.”
3 Han sade: Gack bort, och beds af alla dina grannhustrur tom käril, väl mång;
Elisa anati, “Pita kabwereke mitsuko yonse yopanda kanthu kwa anzako. Usakabwereke mitsuko yochepa.
4 Och gack in, och slut dörrena igen efter dig, med dina söner, och gjut i all kärilen; och när du hafver fyllt dem, så tag bort dem.
Kenaka ukalowe mʼnyumba mwako ndi kudzitsekera iwe ndi ana ako. Mukakatero mukakhuthulire mafuta mʼmitsuko yonseyo, ndipo mtsuko uliwonse ukadzaza muzikawuyika pambali.”
5 Hon gick bort, och slöt dörrena igen efter sig, samt med sina söner; de båro kärilen fram till henne, och hon göt uti.
Mayi uja anachoka kwa Elisa nakadzitsekera ndi ana ake. Anthu anabweretsa mitsuko kwa iye ndipo ankathiramo mafuta.
6 Och då kärilen voro full, sade hon till sin son: Hemta mig ännu ett kärile. Han sade till henne: Här är intet kärile mer. Så stadnade oljan.
Mitsuko yonse itadzaza, mayiyo anawuza mwana wake kuti, “Bweretsa mtsuko wina.” Koma iye anayankha kuti, “Mitsuko yonse yatha.” Pamenepo mafuta analeka kutuluka.
7 Och hon gick bort, och sade det Guds mannenom. Han sade: Gack bort, sälj oljona, och betala dem du skyldig äst; men du och dine söner, lefver utaf det andra, som öfver är.
Mayiyo anapita nakamuwuza munthu wa Mulungu amene anamuyankha kuti, “Pita, kagulitse mafutawo ndipo ukabweze ngongole ija. Ndalama zotsalazo zikakhale zako ndi ana ako.”
8 Och det begaf sig på en tid, att Elisa gick till Sunem. Der var en rik qvinna, och hon höll honom uppe, så att han fick sig der mat. Och som han ofta färdades derigenom, gick han ju in till henne, och åt när henne.
Tsiku lina Elisa anapita ku Sunemu. Kumeneko kunkakhala mayi wina wachuma amene anawumiriza Elisa kuti adye chakudya. Choncho nthawi iliyonse imene Elisa amadutsa kumeneko, ankayima ndi kudya.
9 Och hon sade till sin man: Si, jag förmärker, att denne Guds mannen är helig, som alltid går här fram.
Mayiyo anawuza mwamuna wake kuti, “Taonani, ine ndikudziwa kuti munthu amene amadutsa pano nthawi zambiriyu ndi munthu woyera wa Mulungu.
10 Låt oss göra en liten brädesal, och sätta derin en säng, bord, stol, och ljusastaka; på det att, när han till oss kommer, må han der blifva.
Tiyeni timumangire kachipinda kakangʼono pa denga la nyumbayi ndi kumuyikiramo bedi ndi tebulo, mpando ndi nyale. Akabwera kuno azikhala mʼmenemo.”
11 Så hände det sig på en tid, att han kom ditin, och lade sig i salen, och sof derinne;
Tsiku lina pamene Elisa anafika ku Sunemu, iye anakalowa mʼchipinda chake chija nagona mʼmenemo.
12 Och sade till sin tjenare Gehasi: Kalla den Sunamitiskona. Och då han hade kallat henne, gick hon fram för honom.
Iye anati kwa mtumiki wake Gehazi, “Muyitane Msunemuyu.” Ndipo anapita kukamuyitana mayiyo, ndipo anabwera nayima pamaso pa Elisa.
13 Han sade till honom; Säg henne: Si, du hafver gjort oss alla denna tjenstena; hvad skall jag göra dig? Hafver du något värf till Konungen, eller till härhöfvitsmannen? Hon sade: Jag bor ibland mitt folk.
Elisa anati kwa Gehazi, “Muwuze mayiyo kuti, ‘Wavutika potichitira zonsezi. Nanga tsopano ifeyo tikuchitire chiyani? Kodi ukufuna kuti tikadziwitse mfumu kapena mtsogoleri wa ankhondo zimene watichitirazi?’” Mayiyo anayankha kuti, “Ine ndimakhala mwamtendere pakati pa abale anga.”
14 Han sade: Hvad skall man då göra henne? Gehasi sade: Ack! hon hafver ingen son, och hennes man är gammal.
Elisa anafunsanso Gehazi kuti, “Kodi tingamuchitire chiyani?” Gehazi anati, “Ndithu, mayiyu alibe mwana ndipo mwamuna wake ndi wokalamba.”
15 Han sade: Kalla henne. Och då han hade kallat henne, kom hon i dörrena.
Pamenepo Elisa anati, “Muyitane.” Choncho Gehazi anamuyitana, ndipo iye anabwera nayima pa khomo.
16 Och han sade: På denna tiden, när frukten kan lefva, skall du hafva en son i famnen. Hon sade: Ack! nej, min Herre, du Guds man, ljug icke för dine tjenarinno.
Elisa anati kwa mayiyo, “Nthawi ngati yomwe ino chaka chamawa, udzakhala utanyamula mwana wamwamuna mʼmanja mwako.” Mayiyo anatsutsa zimenezi nanena kuti, “Ayi mbuye wanga. Inu munthu wa Mulungu, musanamize mdzakazi wanu!”
17 Och qvinnan vardt hafvandes, och födde en son, på samma tiden då frukten lefva kunde, såsom Elisa hade sagt henne.
Koma mayi uja anakhala woyembekezera, ndipo chaka chotsatiracho, nthawi ngati yomweyo anabereka mwana wamwamuna monga momwe Elisa anamuwuzira.
18 Då pilten vardt stor, hände sig, att han gick ut till sin fader, till skördemännerna;
Mwana uja anakula, ndipo tsiku lina anapita kwa abambo ake amene anali ndi anthu odula tirigu.
19 Och sade till sin fader: Ack! mitt hufvud, mitt hufvud. Han sade till sin tjenare: Haf honom bort till sina moder.
Mwanayo anafuwula kwa abambo ake kuti, “Mayo! Mutu wanga ine! Mayo! Mutu wanga ine!” Abambo akewo anawuza wantchito wake kuti, “Munyamule ndi kukamupereka kwa amayi ake.”
20 Och han tog honom, och hade honom till hans moder. Och hon satte honom i sitt sköte allt intill middagen; då blef han död.
Wantchito uja atamunyamula ndi kumupereka kwa amayi ake. Mwanayo anakhala pa miyendo ya amayi akeyo mpaka masana, ndipo pambuyo pake anamwalira.
21 Och hon gick upp, och lade honom på Guds mansens säng, slöt till, och gick ut;
Mayiyo ananyamula mwanayo nakamugoneka pa bedi la munthu wa Mulungu uja. Kenaka anatseka chitseko iye nʼkuchokapo.
22 Och kallade sin man, och sade: Sänd mig en af tjenarena, och ena åsninno; jag vill till Guds mannen, och komma igen.
Iye anayitanitsa mwamuna wake namuwuza kuti, “Tumizireni wantchito mmodzi ndi bulu mmodzi kuti ndipite mofulumira kwa munthu wa Mulungu nʼkubwererako.”
23 Han sade: Hvi vill du till honom? Är dock i dag icke nymånad eller Sabbath. Hon sade: Väl.
Mwamuna wakeyo anafunsa kuti, “Chifukwa chiyani ukupita kwa iyeyo lero? Lero si tsiku la Chikondwerero cha Mwezi Watsopano kapena tsiku la Sabata.” Mayiyo anayankha kuti, “Zonse zili bwino.”
24 Och hon sadlade åsninnona, och sade till tjenaren: Drif uppå, och låt oss icke töfva med ridandet, såsom jag säger dig.
Mayiyo anamangirira chishalo pa bulu ndipo anawuza wantchito wake kuti, “Yendetsa bulu mofulumira. Usachepetse liwiro pokhapokha nditakuwuza.”
25 Alltså drog hon åstad, och kom till Guds mannen på Carmels berg. Som nu Guds mannen såg henne komma, sade han till sin tjenare Gehasi: Si, den Sunamitiskan är der;
Choncho ananyamuka nakafika kwa munthu wa Mulungu uja ku Phiri la Karimeli. Munthu wa Mulungu ataona mayiyo patali, anawuza mtumiki wake Gehazi kuti, “Taona! Msunemu uyo!
26 Så löp nu emot henne, och fråga henne, om henne, och hennes man, och son väl går. Hon sade: Väl.
Thamanga msanga ukakumane naye ndipo ukamufunse kuti, ‘Kodi muli bwino? Kodi mwamuna wanu ali bwino? Kodi mwana wanu ali bwino?’” Mayiyo anayankha kuti, “Zonse zili bwino.”
27 Men då hon uppkom till Guds mannen på berget, fick hon honom om hans fötter. Och Gehasi gick fram, och ville drifva henne bort; men Guds mannen sade: Låt blifva henne; förty hennes själ är bedröfvad; och Herren hafver mig det fördolt, och icke låtit mig det förstå.
Atafika kwa munthu wa Mulunguyo pa phiripo, mayiyo anagwira mapazi a Elisa. Gehazi anabwera kuti amukankhe, koma munthu wa Mulungu anati, “Musiye! Iyeyu ali pa mavuto aakulu, koma Yehova wandibisira zimenezi ndipo sanandiwuze chifukwa chake.”
28 Hon sade: När hafver jag bedts en son af min herra? Sade jag icke, att du icke skulle bespotta mig?
Tsono mayiyo anati, “Mbuye wanga, kodi ine ndinakupemphani mwana? Kodi sindinakuwuzeni kuti musandinamize?”
29 Han sade till Gehasi: Begjorda dina länder, och tag min staf i dina hand, och gack åstad; om någor möter dig, så helsa honom intet; och om någor helsar dig, så svara honom intet; och lägg min staf på piltens anlete.
Elisa anawuza Gehazi kuti, “Manga lamba mʼchiwuno mwako, tenga ndodo yanga mʼdzanja lako ndipo thamanga. Ngati ukumana ndi munthu wina aliyense, usamupatse moni, ndipo ngati wina akupatsa moni, usayankhe. Ukagoneke ndodo yanga pa nkhope ya mwanayo.”
30 Men piltens moder sade: Så sant som Herren lefver, och din själ, jag släpper dig icke. Då stod han upp, och följde henne.
Koma mayi wake wa mwana uja anati, “Pali Yehova wamoyo ndiponso pali inu nomwe, ineyo sindidzakusiyani.” Choncho Elisa ananyamuka natsatira mayiyo.
31 Men Gehasi var allaredo gången framför dem, och lade stafven på piltens anlete; men der var hvarken röst eller sinne. Och han gick tillbaka igen emot honom, och bådade honom, och sade: Pilten är icke uppväckt.
Gehazi anatsogola nakagoneka ndodoyo pa nkhope ya mwanayo, koma sipanamveke mawu kapena kugwedezeka kuonetsa kuti ali moyo. Choncho Gehazi anabwerera kukakumana ndi Elisa ndipo anamuwuza kuti, “Mwanayo sanatsitsimuke.”
32 Och då Elisa kom i huset, si, då låg pilten död på hans säng.
Ndipo Elisa atafika ku nyumbako, taonani, mwanayo anali wakufa atamugoneka pa bedi lake.
33 Och han gick in, och slöt igen dörrena om sig båda, och bad till Herran;
Elisa analowa mʼnyumbamo natseka chitseko. Anali awiri okha mʼchipindamo ndipo iye anapemphera kwa Yehova.
34 Och steg upp, och lade sig öfver pilten, och lade sin mun på piltens mun, och sin ögon på hans ögon, och sina händer på hans händer, och räckte sig så ut öfver honom, så att piltens kropp vardt varm.
Kenaka anakwera pa bedi ndi kumugonera mwanayo, pakamwa pake panakhudzana ndi pakamwa pa mwanayo, maso ake anakhudzana ndi maso a mwanayo, ndipo manja ake anakhudzana ndi manja a mwanayo. Pamene ankadzitambalitsa yekha pa mwanayo, thupi la mwanayo linayamba kufunda.
35 Men han stod åter upp, och gick en gång hit och dit i huset, och steg upp, och räckte sig ut öfver honom. Då prustade pilten sju resor; sedan lät pilten ögonen upp.
Elisa anatembenuka nayenda uku ndi uku kamodzi mʼchipindamo ndipo kenaka anakweranso pa bedi nagoneranso mwanayo. Mwanayo anayetsemula kasanu ndi kawiri ndipo anatsekula maso ake.
36 Och han kallade Gehasi, och sade: Kalla Sunamitiskona. Och då han hade kallat henne, kom hon in till honom. Han sade: Tag här din son.
Elisa anayitana Gehazi ndipo anati, “Muyitane Msunemuyo.” Ndipo anaterodi. Mayiyo atabwera, Elisa anati, “Tenga mwana wako.”
37 Då kom hon, och föll till hans fötter, och tillbad på jordena; och tog sin son, och gick ut.
Mayiyo analowa, nagwada pa mapazi a Elisa, naweramitsa mutu wake pansi. Kenaka ananyamula mwana wake natuluka.
38 Då Elisa kom igen till Gilgal, vardt dyr tid i landena, och de Propheters söner bodde för honom. Och han sade till sin tjenare: Sätt fram en stor gryto, och koka ett mos för Propheternas söner.
Elisa anabwerera ku Giligala ndipo ku dera limenelo kunali njala. Elisa akukumana ndi ana a aneneri, anati kwa mtumiki wake, “Ika mʼphika waukulu pa moto ndipo uwaphikire chakudya anthu awa.”
39 Så gick en ut på markena till att hemta krydde; och han fann en kurbitsstjelk, och hemte deraf vildkurbits sitt kläde fullt. Och då han kom, skar han det i grytona till moset; förty de kände det icke.
Mmodzi mwa ana aneneriwo anapita kuthengo kukafuna ndiwo ndipo anakapeza mpesa wakuthengo. Iye anathyolako zipatso zake nadzaza nsalu yake. Atabwerera, anazidula zipatsozo naziyika mu mʼphika, ngakhale kuti panalibe amene ankazidziwa.
40 Och då de gåfvo det upp för männerna till att äta, och de åto af moset, ropade de, och sade: O! Guds man, döden i grytone; ty de kunde icke ätat.
Anawapakulira anthu chakudyacho, koma atayamba kudya, anthuwo anafuwula kuti, “Inu munthu wa Mulungu muli imfa mu mʼphikamu!” Ndipo sakanatha kudya chakudyacho.
41 Han sade: Hafver hit mjöl; och han kastade det i grytona, och sade: Gif upp för folket, att de måga äta. Så var det intet bittert i grytone.
Elisa anati, “Bweretsani ufa.” Iye anathira ufa mu mʼphikamo ndipo anati, “Perekani chakudyachi kwa anthu kuti adye.” Ndipo mu mʼphikamo munalibenso zoopsa.
42 Och en man kom ifrå BaalSalisa, och bar Guds mannenom förstlingsbröd, nämliga tjugu bjuggbröd, och ny säd i sin kjortel. Men han sade: Gif det folkena, att de äta.
Munthu wina wochokera ku Baala-Salisa anabwera atamutengera munthu wa Mulungu malofu a barele makumi awiri opangidwa kuchokera ku zokolola zoyamba kucha, pamodzinso ndi ngala zatsopano za tirigu. Elisa anati kwa munthuyo, “Apatse anthu kuti adye.”
43 Hans tjenare sade: Hvad kan det slå framför hundrade män? Han sade: Gif det folkena, att de måga äta; förty så säger Herren: De skola äta, och skall ändå öfverblifva.
Mtumiki wake anafunsa kuti, “Kodi ndikachigawe motani chakudyachi kwa anthu 100?” Koma Elisa anamuwuzanso kuti, “Apatse anthu adye. Pakuti izi ndi zimene Yehova akunena kuti, ‘Iwo adzadya chakudyachi ndipo china chidzatsalako.’”
44 Och han lade det fram för dem, så att de åto; och blef ändå öfver, efter Herrans ord.
Tsono iye anachipereka kwa anthuwo ndipo anadya china nʼkutsalako, molingana ndi mawu a Yehova.