< 2 Kungaboken 3 >

1 Joram, Achabs son, vardt Konung öfver Israel i Samarien, uti adertonde årena Josaphats, Juda Konungs; och regerade i tolf år;
Yoramu mwana wa Ahabu anakhala mfumu ya Israeli ku Samariya mʼchaka cha 18 cha Yehosafati mfumu ya ku Yuda ndipo analamulira zaka khumi ndi ziwiri.
2 Och gjorde det ondt varför Herranom, dock icke såsom hans fader och hans moder; ty han kastade bort Baals stöder, som hans fader hade göra låtit.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova koma sizinafanane ndi zimene anachita abambo ndi amayi ake. Iye anachotsa fano la mwala la Baala limene abambo ake anapanga.
3 Men han blef vid Jerobeams, Nebats sons, synder, hvilken kom Israel till att synda; och trädde intet derifrå.
Komabe anawumirira kuchita machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli ndipo sanafune kuwaleka.
4 Men Mesa, de Moabiters Konung, hade mång får, och han skattade Israels Konunge ull af hundradetusend lamb, och af hundradetusend vädrar.
Tsono Mesa, mfumu ya ku Mowabu ankaweta nkhosa, ndipo iye ankayenera kumapereka kwa mfumu ya ku Israeli chaka ndi chaka ana ankhosa onenepa okwanira 100,000 pamodzi ndi ubweya wankhosa 100,000 zazimuna.
5 Då nu Achab var död, föll de Moabiters Konung af ifrån Israels Konung.
Koma atamwalira Ahabu, mfumu ya ku Mowabu inawukira mfumu ya ku Israeli.
6 Då drog ut på den tiden Konung Joram af Samarien, och skickade hela Israel;
Choncho nthawi imeneyi mfumu Yoramu inatuluka mu Samariya ndi kukasonkhanitsa Aisraeli onse.
7 Och sände bort till Josaphat, Juda Konung, och lät säga honom: De Moabiters Konung är affallen ifrå mig. Kom med mig till att strida emot de Moabiter. Han sade: Jag vill uppkomma; jag är såsom du, och mitt folk såsom ditt folk, och mine hästar såsom dine hästar;
Yoramu anatumizanso uthenga uwu kwa Yehosafati mfumu ya ku Yuda: “Mfumu ya ku Mowabu yandiwukira. Kodi ungapite nane kukamenyana ndi Mowabu?” Iye anayankha kuti, “Ine ndidzapita nawe. Iwe ndi ine ndife anthu amodzi, anthu anga ali ngati anthu ako, akavalo anga ali ngati akavalo ako.”
8 Och sade: Hvilken vägen vilje vi draga ditupp? Han sade: Den vägen igenom Edoms öken.
Yehosafati anafunsa kuti, “Kodi tidzera njira iti popita ku nkhondoko?” Yoramu anayankha kuti, “Tidzera ku Chipululu cha Edomu.”
9 Alltså drogo åstad Israels Konung, Juda Konung, och Edoms Konung. Och som de omkringdragit hade sju dagsresor, hade hären, och de öker, som med dem voro, intet vatten.
Choncho mfumu ya ku Israeli inanyamuka pamodzi ndi mfumu ya ku Yuda ndi ya ku Edomu. Ndipo atayenda mozungulira mʼchipululu kwa masiku asanu ndi awiri, asilikali analibe madzi woti amwe kapena kumwetsa nyama zawo zosenza katundu.
10 Då sade Israels Konung: Ack, ve! Herren hafver dessa tre Konungar församlat, på det han skall gifva dem uti de Moabiters händer.
Mfumu inafuwula kuti, “Nʼchiyani chomwe chikutichitikira! Kodi Yehova wasonkhanitsa mafumu atatu pamodzi kuti atipereke mʼmanja mwa Amowabu?”
11 Men Josaphat sade: Är här ingen Herrans Prophet, att vi måge genom honom fråga Herran? Då svarade en ibland Israels Konungs tjenare, och sade: Här är Elisa, Saphats son, hvilken göt vatten på Elia händer.
Koma mfumu Yehosafati inafunsa kuti, “Kodi kuno kulibe mneneri wa Yehova woti tingakafunse kwa Yehova kudzera mwa iyeyo?” Mtsogoleri wa ankhondo wa mfumu ya ku Israeli anayankha kuti, “Alipo, Elisa mwana wa Safati. Iye anali mtumiki wa Eliya.”
12 Josaphat sade: Herrans ord är när honom. Alltså drogo neder till honom Israels Konung, och Josaphat, och Edoms Konung.
Yehosafati anati, “Yehova amayankhula kudzera mwa iye.” Choncho mfumu ya ku Israeli pamodzi ndi Yehosafati ndiponso mfumu ya ku Edomu anapita kwa Elisa.
13 Då sade Elisa till Israels Konung: Hvad hafver du med mig skaffa? Gack bort till dins faders Propheter, och till dine moders Propheter. Israels Konung sade till honom: Nej; ty Herren hafver församlat dessa tre Konungar, på det han skall gifva dem uti de Moabiters händer.
Elisa ananena kwa mfumu ya ku Israeli kuti, “Pali ubale wanji pakati pa inu ndi ine? Pitani kwa aneneri a abambo ndi amayi anu.” Mfumu ya ku Israeli inayankha kuti, “Ayi, pakuti ndi Yehova amene anatisonkhanitsa ife mafumu atatu pamodzi kuti atipereke mʼmanja mwa Amowabu.”
14 Elisa sade: Så sant som Herren Zebaoth lefver, för hvilkom jag står, om jag icke ansåge Josaphat, Juda Konung, jag ville icke anse dig eller akta dig.
Elisa anati, “Pali Yehova Wamphamvuzonse amene ndimamutumikira, pakanapanda kuti ndimamuchitira ulemu Yehosafati mfumu ya ku Yuda, sindikanakulabadirani kapena kukuyangʼanani nʼkomwe.
15 Så låter nu en spelman komma hit. Och då spelmannen spelade på strängerna, kom Herrans hand öfver honom;
Koma tsopano ndiyitanireni munthu wodziwa kuyimba bwino zeze.” Munthuyo akuyimba zeze, mphamvu ya Yehova inafika pa Elisa,
16 Och han sade: Detta säger Herren: Görer grafver vid denna bäcken här och der.
ndipo anati, “Yehova akuti, ‘Kumbani ngalande mʼchigwa chonse.’
17 Förty så säger Herren: I skolen intet väder eller regn se; likväl skall bäcken varda full med vatten, så att I, och edart folk, och edra öker skola få dricka.
Pakuti Yehova akunena kuti, ‘Simudzaona mphepo kapena mvula, komabe chigwa ichi chopanda madzi chidzadzaza ndi madzi, ndipo inu mudzamwa pamodzi ndi ngʼombe zanu ndiponso nyama zanu zonse.’
18 Dertill är detta en ringa ting för Herranom; han skall ock gifva de Moabiter i edra händer;
Izi ndi zosavuta pamaso pa Yehova. Ndipo adzaperekanso Amowabu mʼmanja mwanu.
19 Så att I skolen slå alla fasta städer, och alla utvalda städer, och skolen omkullhugga all god trä, och skolen förstoppa alla vattubrunnar, och skolen förderfva alla goda åkrar med stenar.
Mudzagonjetsa mizinda yawo yonse yotetezedwa ndiponso mizinda yawo ikuluikulu. Mudzagwetsa mtengo wabwino uliwonse, mudzatseka akasupe onse amadzi, ndiponso mudzawononga minda yawo yonse yachonde poponyamo miyala.”
20 Om morgonen, då man spisoffer offrade, si, då kom ett vatten på den vägen ifrån Edom, och fyllde landet med vatten.
Mmawa mwake, nthawi yopereka nsembe ili pafupi, anangoona madzi akutuluka kuchokera ku Edomu, ndipo malo onse anadzaza ndi madzi.
21 Då nu de Moabiter hörde, att Konungarna drogo upp till att strida emot dem, kallade de tillhopa alla, som vuxne voro att bära vapen, och derutöfver, och drogo intill gränson.
Tsono nʼkuti Amowabu onse atamva kuti mafumu abwera kudzachita nawo nkhondo. Kotero, anayitana munthu aliyense, wamkulu ndi wamngʼono amene ankatha kugwira chida chankhondo ndipo anakayima ku malire a dziko lawo.
22 Och som de om morgonen bittida uppstode, och solen uppgick öfver vattnet, tyckte de Moabiter, att vattnet emot dem var rödt såsom blod;
Amowabu atadzuka mmamawa, dzuwa likuwala pa madziwo, anaona madziwo akuoneka wofiira ngati magazi patsogolo pawo.
23 Och de sade: Det är blod; Konungarna hafva slagits inbördes med svärd, och den ene hafver slagit den andra. Nu Moab, statt upp, och tag byte.
Ndipo iwo anati, “Taonani magazi! Mafumu aja amenyana okhaokha ndipo aphana. Amowabu, tsopano ndi nthawi yofunkha!”
24 Men då de kommo till Israels lägre, reste Israel upp, och slog de Moabiter, och de flydde för dem; men de kommo in, och slogo Moab;
Koma Amowabu atafika ku misasa ya Israeli, Aisraeli ananyamuka ndi kumenyana nawo mpaka anathawa. Ndipo Aisraeli analowa mʼdzikolo ndi kupha Amowabu.
25 Bröto städerna neder, och hvar och en kastade sin sten på alla goda åkrar, och uppfyllde dem, och förstoppade alla vattubrunnar, och fällde all god trä, tilldess att allenast stenarna i tegelmuren qvare blefvo; och de kringhvärfde staden med slungor, och slogo honom.
Aisraeli anagumula mizinda yawo ndipo munthu aliyense anaponya mwala pa munda uliwonse wachonde mpaka utadzaza ndi miyala. Iwo anatseka akasupe onse amadzi ndiponso anadula mtengo wabwino uliwonse. Mzinda wa Kiri Hareseti wokha ndiye unatsala wotetezedwa koma anthu oponya miyala anawuzungulira nawuthiranso nkhondo.
26 Då de Moabiters Konung såg att striden vardt honom för stark, tog han sjuhundrade män till sig, som svärd utdrogo, till att slå ut emot Edoms Konung; men de kunde icke.
Mfumu ya ku Mowabu itaona kuti nkhondo ikumulaka, inatenga anthu 700 a malupanga kuti athawe modutsa mfumu ya ku Edomu, koma inalephera.
27 Då tog han sin första son, som i hans stad skulle Konung vordit, och offrade honom till ett bränneoffer på muren. Då kom en stor vrede öfver Israel; så att de drogo ifrå honom, och vände till landet igen.
Choncho inatenga mwana wake wamwamuna woyamba kubadwa, amene akanalowa ufumu mʼmalo mwake, ndi kumupereka nsembe pa khoma la mzinda. Zimenezi zinachititsa kuti mkwiyo ndi ukali wa Amowabu ukule kwambiri pa Aisraeli ndipo Aisraeliwo anathawa nabwerera ku dziko la kwawo.

< 2 Kungaboken 3 >