< 2 Kungaboken 22 >
1 Josia var åtta åra gammal, då han vardt Konung, och regerade ett och tretio år i Jerusalem; hans moder het Jedida, Adaja dotter, af Bozkath.
Yosiya anakhala mfumu ali ndi zaka zisanu ndi zitatu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 31. Amayi ake anali Yedida mwana wa Adaiya wochokera ku Bozikati.
2 Han gjorde det godt var för Herranom, och vandrade i allom sins faders Davids väg, och böjde hvarken på högra sidona, eller på den venstra.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova ndipo anayenda mʼnjira zonse za Davide kholo lake, osatembenukira kumanja kapena kumanzere.
3 Uti adertonde årena Konungs Josia, sände Konungen Saphan, Azalia son, Mesullams sons, skrifvaren, bort uti Herrans hus, och sade:
Mʼchaka cha 18 cha ufumu wake, Mfumu Yosiya anatuma mlembi wa nyumba ya mfumu, Safani, mwana wa Azariya, mwana wa Mesulamu, ku Nyumba ya Yehova. Iye anati,
4 Gack upp till öfversta Presten Hilkia, att man må få honom de penningar, som till Herrans hus införde äro, och dörravaktarena församlat hafva af folkena;
“Pita kwa mkulu wa ansembe Hilikiya ndipo ukamuwuze kuti awerenge ndalama zimene anthu abwera nazo ku Nyumba ya Yehova, zimene alonda a pa khomo anasonkhanitsa kwa anthu.
5 Att de måga gifva dem arbetarena, som beställde äro i Herrans hus, och gifva dem som arbeta på Herrans hus, och bota det som förfallet är i husena;
Ndalamazo azipereke kwa anthu amene asankhidwa kuti ayangʼanire ntchito ya Nyumba ya Yehova. Ndipo anthu amenewa azilipira antchito amene akukonzanso Nyumba ya Yehova,
6 Nämliga timbermannom, byggningsmannom, murmästarom, och dem som trä och huggen sten köpa skola, till husets förbättring;
amisiri a matabwa, amisiri omanga ndi amisiri a miyala. Iwo akagulenso matabwa ndi miyala yosemedwa kuti akonzere Nyumba ya Yehova.
7 Dock så, att man ingen räkenskap skulle taga af dem för de penningar, som under deras hand antvardade vordo; utan de skulle handla dermed på sina tro.
Koma anthu amene apatsidwa ndalama zolipira antchito okonza Nyumbayo asawafunse za kagwiritsidwe ntchito ka ndalamazo, popeza ndi anthu wokhulupirika.”
8 Och öfverste Presten Hilkia sade till skrifvaren Saphan: Jag hafver funnit lagbokena uti Herrans hus; och Hilkia fick Saphan bokena, att han skulle den läsa.
Mkulu wa ansembe Hilikiya anawuza Safani, mlembiyo kuti, “Ndapeza Buku la Malamulo mʼNyumba ya Yehova.” Anapereka bukulo kwa Safani amene analiwerenga.
9 Och skrifvaren Saphan bar henne till Konungen, och bådade honom igen, och sade: Dine tjenare hafva tillhopahemtat de penningar, som i husena funne voro, och hafva utgifvit dem arbetarena, som beställde äro i Herrans hus.
Ndipo Safani mlembi uja, anapita nakafotokozera mfumu kuti, “Atumiki anu apereka ndalama zija zinali mʼNyumba ya Yehova kwa anthu amene akugwira ntchito ndi kuyangʼanira ntchito yokonza Nyumba ya Yehova.”
10 Och förtäljde skrifvaren Saphan Konungenom, och sade: Hilkia Presten fick mig ena bok; och Saphan las henne för Konungenom.
Kenaka Safani mlembiyo, anafotokozera mfumu kuti, “Wansembe Hilikiya wandipatsa buku.” Ndipo Safani analiwerenga pamaso pa mfumu.
11 Då Konungen hörde orden i lagbokene, ref han sin kläder sönder.
Mfumu itamva mawu a mʼBuku la Malamulo, inangʼamba zovala zake.
12 Och Konungen böd Hilkia Prestenom, och Ahikam, Saphans sone, och Achbor, Michaja sone, och Saphan skrifvarenom, och Asaja, Konungens tjenare, och sade:
Iyo inalamula wansembe Hilikiya, Ahikamu mwana wa Safani, Akibo mwana wa Mikaya, Safani mlembi uja ndi Asaiya mtumiki wa mfumu, kuti,
13 Går bort, och fråger Herran, för mig, för folket, och för hela Juda, om denna bokenes ord, som funnen är; ty det är en stor Herrans vrede, som är upptänd öfver oss; derföre, att våre fäder icke lydt hafva denna bokenes ord, att de måtte gjort allt det derutinnan skrifvet är.
“Pitani mukafunse Yehova mʼmalo mwanga ndi mʼmalo mwa anthu onse a mʼdziko la Yuda, za zomwe zalembedwa mʼbuku limene lapezekali. Mkwiyo wa Yehova ndi waukulu kwambiri pa ife ndipo watiyakira chifukwa makolo athu sanamvere mawu a buku ili. Iwo sanachite molingana ndi zonse zimene zalembedwa mʼmenemu zokhudza ife.”
14 Då gingo åstad Hilkia Presten, Ahikam, Achbor, Saphan och Asaja, till den Prophetissan Hulda, Sallums hustru, Thikva sons, Harhas sons, klädavaktarens; och hon bodde i Jerusalem i dem andra delenom, och de talade med henne.
Choncho Hilikiya wansembe, Ahikamu, Akibo, Safani ndi Asaiya anapita kukayankhula ndi Hulida, mneneri wamkazi, mkazi wa Salumu mwana wa Tikiva, mwana wa Harihasi, wosunga zovala zaufumu. Mneneri wamkaziyu ankakhala mu Yerusalemu, ku chigawo chachiwiri cha mzindawo.
15 Men hon sade till dem: Detta säger Herren Israels Gud: Säger dem månne, som eder till mig sändt hafver:
Ndipo iye anawawuza kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti: Kamuwuzeni munthu amene wakutumani kwa ine kuti,
16 Så säger Herren: Si, jag skall låta komma olycko öfver detta rum, och dess inbyggare, efter all lagsens ord, som Juda Konung hafver läsa låtit.
‘Ichi ndi chimene Yehova akunena: Taonani, ndidzabweretsa mavuto pa malo ano ndi pa anthu ake, molingana ndi zonse zimene zalembedwa mʼbuku limene mfumu ya Yuda yawerenga.
17 Derföre, att de hafva öfvergifvit mig, och rökt andra gudar, förtörnande mig med allt deras handaverk; derföre skall min vrede upptändas emot detta rum, och skall icke utsläckt varda.
Chifukwa anthuwo andisiya Ine ndi kumafukiza lubani kwa milungu ina nandikwiyitsa ndi mafano onse amene manja awo anapanga, mkwiyo wanga udzayaka pa malo ano ndipo sudzazimitsidwa.’
18 Men Juda Konunge, som eder utsändt hafver till att fråga Herran, skolen I så säga: Så säger Herren Israels Gud:
Koma mfumu ya Yuda imene inakutumani kuti mudzafunse kwa Yehova kayiwuzeni kuti, ‘Ichi ndi chimene Yehova Mulungu wa Israeli akunena molingana ndi mawu amene unamva:
19 Derföre, att ditt hjerta hafver bevekt sig, af de ord, som, du hört hafver, och hafver ödmjukat dig för Herranom, då du hörde hvad jag sagt hade emot detta rum, och dess inbyggare, att de skulle varda till en förödelse och förbannelse, och hafver rifvit din kläder sönder, och hafver gråtit för mig, så hafver jag ock hört det, säger Herren.
Chifukwa unasweka mtima ndi kudzichepetsa wekha pamaso pa Yehova, pamene unamva zomwe zinayankhulidwa zotsutsana ndi malo ano ndi anthu ake, kuti adzakhala otembereredwa nasanduka bwinja, ndiponso chifukwa unangʼamba zovala ndi kulira pamaso panga, ndamva pemphero lako, akutero Yehova.
20 Derföre vill jag samka dig till dina fäder, att du skall samkas i grafvena med frid, och din ögon icke se skola alla denna olyckona, som jag öfver detta rum föra skall. Och de sade Konungenom det igen.
Choncho taona, Ine ndidzakutenga kupita kwa makolo ako ndipo udzayikidwa mʼmanda mwako mwamtendere. Maso ako sadzaona mavuto onse amene ndidzabweretse pamalo pano.’” Ndipo anthu aja anabwerera nakafotokoza mawu amenewa kwa mfumu.