< 2 Kungaboken 19 >
1 Då Konung Hiskia det hörde, ref han sin kläder, och drog en säck uppå sig, och gick in uti Herrans hus;
Mfumu Hezekiya atamva zimenezi, anangʼamba zovala zake navala chiguduli ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova.
2 Och sände Eliakim hofmästaren, och Sebna skrifvaren, samt med de äldsta Presterna, klädda i säcker, till Propheten Esaia, Amos son.
Iye anatuma Eliyakimu, woyangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo ndi ansembe akuluakulu, onse atavala ziguduli, kwa mneneri Yesaya mwana wa Amozi.
3 Och de sade till honom: Så säger Hiskia: Denne dagen är en bedröfvelses, bannors och förhädelses dag; barnen äro komne till födslon; men ingen magt är till att föda.
Iwo anamuwuza kuti, “Hezekiya akunena kuti, ‘Lero ndi tsiku lamavuto, lachilango ndi lamanyazi. Ife lero tili ngati mayi woyembekezera amene pofika nthawi yoti achire akupezeka kuti alibe mphamvu zoberekera.
4 Om tilläfventyrs Herren din Gud ville höra all RabSake ord, hvilken hans Herre, Konungen i Assyrien, utsändt hafver, till att tala förhädelse emot lefvandes Gud; och till att bannas med de ord, som Herren din Gud hört hafver; så upphäf nu din bön för dem som ännu igenlefde äro.
Mwina Yehova Mulungu wanu adzamva mawu onse a Rabusake amene mbuye wake, mfumu ya ku Asiriya anamutuma kudzanyoza Mulungu wamoyo, ndipo Mulunguyo adzamulanga chifukwa cha mawu amene Yehova Mulungu wanu wamva. Choncho pemphererani anthu otsala amene akanali ndi moyo.’”
5 Och Konungens Hiskia tjenare kommo till Esaia.
Akuluakulu a Mfumu Hezekiya atafika kwa Yesaya,
6 Då sade Esaia till dem: Så säger edrom herra: Detta säger Herren: Frukta dig intet för de ord, som du hört hafver, der Konungens tjenare af Assyrien mig med förhädt hafva.
Yesaya anawawuza kuti, “Kawuzeni mbuye wanu kuti, ‘Yehova akunena kuti: Usachite mantha ndi zimene wamva, mawu amene nthumwi za mfumu ya ku Asiriya zandinyoza nawo Ine.
7 Si, jag vill gifva honom en anda, att han skall få höra ett rykte, och draga tillbaka igen i sitt land; och jag vill fälla honom med svärd i hans land.
Tamverani! Ine ndidzayika mwa mfumuyo mzimu wina kotero kuti akadzamva mphekesera ya nkhondo, adzabwerera ku dziko lake ndipo Ine ndidzachititsa kuti aphedwe ndi lupanga kwawo komweko.’”
8 Och då RabSake kom igen, fann han Konungen af Assyrien stridandes emot Libna; förty han hade hört, att han var dragen ifrå Lachis.
Rabusake atamva kuti mfumu ya ku Asiriya yachoka ku Lakisi, iye anabwerera mʼmbuyo ndipo anakapeza mfumu ikuchita nkhondo ndi mzinda wa Libina.
9 Och han fick höra om Thirhaka, Konungen i Ethiopien: Si, han är utdragen till att strida emot dig. Då vände han om, och sände båd till Hiskia, och lät säga honom:
Nthawi imeneyi Senakeribu analandira uthenga wakuti Tirihaka, mfumu ya ku Kusi, akubwera kudzachita naye nkhondo. Choncho iye anatumanso amithenga kwa Hezekiya ndi mawu awa:
10 Detta säger Hiskia, Juda Konung: Låt icke din Gud bedraga dig, på hvilken du dig förlåter, och säger: Jerusalem varder icke gifvet uti Konungens hand i Assyrien.
“Kawuzeni Hezekiya mfumu ya Yuda kuti: Usalole kuti Mulungu amene ukumudalira akupusitse ponena kuti, ‘Yerusalemu sadzaperekedwa mʼmanja mwa mfumu ya ku Asiriya.’
11 Si, du hafver hört, hvad Konungarna i Assyrien gjort hafva allom landom, och gifvit dem tillspillo; och du skulle nu friad varda?
Ndithu iwe unamva chimene mafumu a Asiriya anachita ku mayiko ena onse, kuti anawawononga kotheratu. Ndipo kodi iwe nʼkupulumuka?
12 Hafva ock Hedningarnas gudar friat dem, hvilka mine fäder förderfvat hafva; Gosan, Haran, Reseph, och Edens barn, som i Thelassar voro?
Kodi milungu ya mitundu imene makolo anga anayigonjetsa, milungu ya anthu a ku Gozani, Harani, Rezefi ndi Aedeni amene anali ku Teli Asara, inawapulumutsa?
13 Hvar är Konungen i Hamath, Konungen i Arphad, Konungen i den staden Sepharvaim, Hena och Iva?
Kodi mafumu a Hamati, Aripadi ndi mafumu a mizinda ya Sefaravaimu, Hena ndi Iva, ali kuti?”
14 Då Hiskia hade anammat brefvet af båden, och läsit det, gick han upp i Herrans hus, och upplät det för Herranom;
Hezekiya analandira kalata kwa amithenga aja nayiwerenga. Pomwepo anapita ku Nyumba ya Yehova nayika kalatayo pamaso pa Yehova.
15 Och bad inför Herranom, och sade: Herre Israels Gud, som sitter öfver Cherubim, du äst allena Gud i all rike på jorden; du hafver gjort himmel och jord.
Ndipo Hezekiya anapemphera kwa Yehova nati, “Inu Yehova Mulungu wa Israeli, Inu amene mumakhala pa Akerubi, Inu nokha ndinu Mulungu wolamulira maufumu onse a dziko lapansi. Inu munalenga kumwamba ndi dziko lapansi.
16 Herre, böj din öron, och hör; Herre, upplåt din ögon och se; och hör Sanheribs ord, den hitsändt hafver, till att tala hädelse emot lefvandes Gud.
Inu Yehova, tcherani khutu lanu ndipo mumve Yehova tsekulani maso anu ndipo muone, imvani mawu onse amene Senakeribu watumiza kunyoza Inu Mulungu wamoyo.
17 Det är sant, Herre, Konungarna i Assyrien hafva med svärd förlagt Hedningarna, och deras land;
“Inu Yehova, nʼzoonadi kuti mafumu a Asiriya anawononga mitundu iyi ndi mayiko awo.
18 Och hafva kastat deras gudar i elden; ty de voro icke gudar, utan menniskors handaverk, stock och sten; derföre hafva de förlagt dem.
Iwo anaponya milungu yawo pa moto ndi kuyiwononga pakuti sinali milungu koma mitengo ndi miyala chabe, yopangidwa ndi anthu.
19 Men nu, Herre vår Gud, hjelp oss utu hans hand, på det all rike på jordene skola förstå, att du, Herre, allena äst Gud.
Ndipo tsopano Inu Yehova Mulungu wathu, tipulumutseni ndithu mʼdzanja lake, kuti maufumu onse a dziko lapansi adziwe kuti Inu nokha, Inu Yehova, ndinu Mulungu.”
20 Så sände Esaia, Amos son, till Hiskia, och lät säga honom: Detta säger Herren Israels Gud: Hvad du af mig bedit hafver om Sanherib, Konungen i Assyrien, det hafver jag hört.
Ndipo Yesaya mwana wa Amozi anatumiza uthenga kwa Hezekiya wakuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndamva pemphero lako lonena za Senakeribu mfumu ya ku Asiriya.’”
21 Detta är det Herren emot honom talat hafver: Jungfrun, dottren Zion, föraktar dig, och bespottar dig; dottren Jerusalem rister hufvudet efter dig.
Mawu amene Yehova wayankhula wotsutsana naye ndi awa: “Namwali wa Ziyoni akukunyoza ndi kukuseka iwe. Mwana wamkazi wa Yerusalemu akupukusa mutu wake kumbuyo kwako.
22 Hvem hafver du försmädat och förhädt? Öfver hvem hafver du upphöjt dina röst? Du hafver upphäfvit dina ögon emot den Heliga i Israel.
Kodi iweyo wanyoza ndi kuchitira chipongwe yani? Kodi ndani amene wamufuwulira mawu ako ndi kumuyangʼana monyada? Wachitiratu izi Woyera wa Israeli!
23 Du hafver genom din sändningabåd försmädat Herran, och sagt: Jag hafver genom mina många vagnar stigit upp på bergshöjderna, uppå Libanons sido; jag hafver afhuggit dess höga ceder, och utvalda furor, och är kommen intill yttersta herberget, i hans Carmels skog.
Kudzera mwa amithenga ako wonyoza Ambuye. Ndipo wanena kuti, ‘Ndi magaleta ochuluka ndinakwera mapiri ataliatali, pa msonga za mapiri a Lebanoni. Ndigwetsa mitengo yake ya mkungudza yayitali kwambiri, mitengo yake ya payini yabwino kwambiri. Ndalowanso mʼkati mwake mwenimweni, mwa nkhalango yake yowirira kwambiri.
24 Jag hafver grafvit, och utdruckit de främmande vatten, och hafver med mitt fotabjelle uttorkat all förvarad vatten.
Ndakumba zitsime ku mayiko achilendo ndipo ndinamwa madzi a kumeneko. Ndi mapazi anga ndawumitsa mitsinje yonse ya ku Igupto.’”
25 Men hafver du icke hört, att jag detta långt tillförene gjort hafver, och af begynnelsen hafver jag beredt det? Men nu hafver jag det komma låtit, att faste städer skulle förfalla till en öde stenhop.
“‘Kodi sunamvepo? Zimenezi ndinazikhazikitsa kalekale. Ndinazikonzeratu masiku amakedzana; tsopano ndachita kuti zichitikedi, iwe kwako kunali kungosandutsa mizinda yotetezedwa kukhala milu ya miyala.
26 Och de som deruti bodde, skulle varda vanmägtige, och rädas och skämmas, och varda såsom örter på markene, och som gröna gräset till hö på taken, hvilket förtorkas förr än det moget varder.
Anthu a kumeneko ndi opanda mphamvu, athedwa nzeru ndipo ali ndi manyazi. Ali ngati mbewu za mʼmunda, ngati udzu wanthete, ali ngati udzu womera pa denga, umene umawuma usanakule nʼkomwe.’”
27 Jag vet din boning, din utgång och ingång; och att du rasar emot mig.
“‘Koma Ine ndimadziwa kukhala kwako, kutuluka kwako ndi kulowa kwako, ndi mkwiyo wako pa Ine.
28 Så efter du rasar emot mig, och ditt högmod är uppkommet för min öron, så skall jag sätta en ring i dina näso, och ett bett i din mun, och skall föra dig den vägen hem igen, som du hit kommen äst.
Chifukwa chakuti wandikwiyira ndipo ndamva za mwano wako, ndidzakola mphuno yako ndi mbedza ndi kuyika chitsulo changa mʼkamwa mwako, ndipo ndidzakubweza pokudzeretsa njira yomwe unadzera pobwera.’
29 Och detta skall vara dig ett tecken: Uti detta år ät hvad som förtrampadt är; uti de andro årena hvad sjelft växer; uti tredje årena sår och uppskärer, och planterer vingårdar, och äter deras frukt.
“Koma iwe Hezekiya, chizindikiro chako chidzakhala ichi: “Chaka chino mudzadya tirigu wamphulumukwa, ndipo chaka chamawa mudzadya tirigu wongodzimerera. Koma chaka chachitatu mudzadzala ndi kukolola, mudzawoka mphesa ndipo mudzadya zipatso zake.
30 Och Juda hus, som frälst och igenblifvet är, skall ännu rota sig nedantill, och bära frukt ofvantill.
Anthu a nyumba ya Yuda amene adzatsale adzazika mizu ndi kubereka zipatso.
31 Ty utaf Jerusalem varda utgångande de som igenblefne äro; och utaf Zions berg de som undsluppne äro; Herrans Zebaoths nit varder detta görandes.
Pakuti ku Yerusalemu kudzachokera anthu otsala, ndi ku phiri la Ziyoni kudzachokera gulu la anthu opulumuka.” “Changu cha Yehova Wamphamvuzonse chidzachita zimenezi.
32 Derföre säger Herren om Konungen i Assyrien alltså: Han skall icke komma i denna staden, och ingen pil skjuta der in, och ingen sköld föra der före, och ingen vall uppkasta der omkring;
“Choncho chimene Yehova akunena za mfumu ya ku Asiriya ndi ichi: “‘Iye sadzalowa mu mzinda umenewu kapena kuponyamo muvi. Sadzayandikira mzindawu ndi zishango zake kapena kumanga nthumbira ya nkhondo.
33 Utan han skall draga den vägen tillbaka igen, som han kommen är, och skall intet komma i denna staden; Herren hafver det sagt.
Adzabwerera potsata njira imene anadzera pobwera; sadzalowa mu mzinda umenewu, akutero Yehova.
34 Och jag skall beskärma denna staden, så att jag honom hjelpa vill för mina skull, och för Davids min tjenares skull.
Ndidzateteza mzinda umenewu kuwupulumutsa, chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha Davide mtumiki wanga.’”
35 På den samma nattena for Herrans Ängel ut, och slog i de Assyriers lägre hundradetusend, och fem och åttatio tusend män; och då de om morgonen bittida uppstodo, si, då låg allt fullt med döda kroppar.
Usiku umenewo mngelo wa Yehova anapita ku misasa ya ku Asiriya ndi kupha ankhondo 185,000. Ndipo pamene anthu anadzuka mmawa, taonani, mitembo inali ngundangunda!
36 Alltså bröt Sanherib, Konungen af Assyrien, upp, drog sina färde, och vände om, och blef i Nineve.
Choncho Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anapasula misasa ndi kuchoka. Anabwerera ku Ninive nakakhala kumeneko.
37 Och då han tillbad i Nisrochs sins guds hus, slogo honom hans söner med svärd, Adrammelech och SarEzer, och undflydde in uti det landet Ararat; och hans son EsarHaddon vardt Konung i hans stad.
Tsiku lina, pamene Senakeribu ankapembedza mʼnyumba ya Nisiroki mulungu wake, ana ake Adirameleki ndi Sarezeri anamupha ndi lupanga ndipo anathawira ku dziko la Ararati. Tsono Esrahadoni, mwana wake, analowa ufumu mʼmalo mwake.