< 2 Kungaboken 14 >

1 Uti andro årena Joas, Joahas sons, Israels Konungs, vardt Amazia Konung, Joas, Juda. Konungs, son.
Mʼchaka chachiwiri cha Yehowasi mwana wa Yowahazi mfumu ya Israeli, Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
2 Fem och tjugu åra gammal var han, då han vardt Konung; och regerade nio och tjugu år i Jerusalem; hans moder het Joaddan af Jerusalem.
Iye anali ndi zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 29. Amayi ake anali Yehoyadini wa ku Yerusalemu.
3 Och han gjorde det Herranom väl behagade; dock icke såsom hans fader David, utan såsom hans fader Joas gjort hade, så gjorde han ock.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, koma osafanana ndi zomwe anachita Davide kholo lake. Iye anatsatira zochita zonse za Yowasi abambo ake.
4 Ty höjderna vordo icke aflagda; utan folket offrade och rökte ännu på höjderna.
Komabe sanachotse malo opembedzerapo mafano. Anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
5 Då han nu var mägtig vorden i riket, slog han sina tjenare, som Konungen hans fader dräpit hade.
Atakhazikika mu ufumu wake, Amaziya anapha atumiki ake amene anapha abambo ake, mfumu ija.
6 Men dråparenas barn drap han icke; såsom ock skrifvet är i Mose lagbok, der Herren budit hade, och sagt: Fäderna skola icke dö för barnens skull, och barnen skola icke dö för fädernas skull; utan hvar och en skall dö för sina synd.
Komatu iye sanaphe ana a anthu amene anapha abambo ake potsatira zomwe zinalembedwa mʼbuku la Malamulo a Mose. Mʼmenemo Yehova analamula kuti, “Makolo asaphedwe chifukwa cha ana awo, ndipo ana asaphedwe chifukwa cha makolo awo, koma aliyense ayenera kufa chifukwa cha zolakwa zake.”
7 Han slog desslikes de Edomeer i saltdalenom, tiotusend, och vann den staden Sela med strid; och kallade honom Joktheel, allt intill denna dag.
Iye ndiye amene anapha Aedomu 10,000 mʼchigwa cha Mchere nalanda mzinda wa Sela pa nkhondo ndipo anawutcha Yokiteeli, dzina lake ndi lomwelo mpaka lero lino.
8 Då sände Amazia båd till Joas, Joahas son, Jehu sons, Israels Konung, och lät säga honom: Kom hit, och låt oss se hvarannan.
Tsono Amaziya anatuma amithenga kwa Yehowasi mwana wa Yehowahazi, mwana wa Yehu mfumu ya Israeli ndi kumuopseza kuti, “Bwera tidzaonane maso ndi maso.”
9 Men Joas, Israels Konung, sände till Amazia, Juda Konung, och lät säga honom: Törnebusken, som i Libanon är, sände till cedreträt i Libanon, och sade: Gif dina dotter minom son till hustru; men vilddjuret på markene i Libanon lopp öfver törnebuskan, och förtrampade honom,
Koma Yehowasi mfumu ya Israeli anabweza mawu kwa Amaziya mfumu ya Yuda kuti, “Mtengo wa minga wa ku Lebanoni unatumiza uthenga kwa mkungudza wa ku Lebanoni. ‘Patse mwana wako wamkazi kuti ndimukwatire.’ Kenaka chirombo cha ku Lebanoni chinabwera ndi kupondaponda mtengo wa mingawo.
10 Du hafver slagit de Edomeer, deraf förhäfver sig ditt hjerta; behåll den prisen, och blif hemma; hvi söker du efter olycko, att du må falla, och Juda med dig?
Inde iwe wagonjetsa Edomu ndipo tsopano wayamba kudzikuza. Dzitamandire chifukwa cha kupambana kwako, koma khala kwanu konko! Nʼchifukwa chiyani ukuyamba dala mavuto amene adzakuwononga pamodzi ndi Yuda?”
11 Men Amazia hörde honom intet. Så drog Joas, Israels Konung, upp; och de besågo hvarannan, han och Amazia, Juda Konung, i BethSemes, som i Juda ligger.
Koma Amaziya sanamvere zimenezi. Choncho Yehowasi mfumu ya Israeli anakamuthira nkhondo. Yehowasi ndi Amaziya anakumana maso ndi maso ku Beti-Semesi mʼdziko la Yuda.
12 Men Juda vardt slagen för Israel, så att hvar och en flydde i sina hyddo.
Israeli anagonjetsa Yuda ndipo munthu aliyense anathawira kwawo.
13 Och Joas, Israels Konung, grep Amazia, Juda Konung, Joas son, Ahasia sons, i BethSemes; och kom till Jerusalem, och ref omkull, murarna i, Jerusalem, ifrån Ephraims port, allt intill hörnporten, fyrahundrad alnar långt.
Yehowasi mfumu ya Israeli anagwira Amaziya mfumu ya Yuda, mwana wa Yowasi, mwana wa Ahaziya ku Beti-Semesi. Ndipo anapita ku Yerusalemu nakagwetsa khoma la Yerusalemu kuyambira ku Chipata cha Efereimu mpaka ku Chipata Chapangodya, gawo lotalika mamita 180.
14 Och tog allt det guld och silfver, och tyg, som funnet vardt i Herrans hus, och i Konungshusens fatebur, dertill barnen, till pant; och drog åter till Samarien.
Iye anatenga golide ndi siliva yense pamodzi ndi ziwiya zonse zimene zinali mʼNyumba ya Yehova ndi zimene zinali mosungira chuma cha nyumba ya mfumu. Iye anagwiranso anthu nabwerera ku Samariya.
15 Hvad nu mer af Joas sägande är, det han gjort hafver, och hans magt, och huru han med Amazia, Juda Konung, stridde, si, det är skrifvet uti Israels Konungars Chrönico.
Ntchito zina za Yehowasi ndi zonse zimene anachita, kuwonjezera za nkhondo yake ndi Amaziya mfumu ya Yuda, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
16 Och Joas afsomnade med sina fader, och vardt begrafven i Samarien ibland Israels Konungar; och hans son Jerobeam vardt Konung i hans stad.
Yehowasi anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu Samariya pamodzi ndi mafumu a Israeli. Ndipo mwana wake Yeroboamu analowa ufumu mʼmalo mwake.
17 Men Amazia. Joas son, Juda Konungs, lefde efter Joas död, Joahas sons, Israels Konungs, i femton år.
Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anakhala zaka khumi ndi zisanu atamwalira Yehowasi mwana wa Yehowahazi mfumu ya Israeli.
18 Hvad nu mer af Amazia sägandes är, det är skrifvet uti Juda Konungars Chrönico.
Ntchito zina za Amaziya, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
19 Och de gjorde ett förbund emot honom i Jerusalem; men han flydde till Lachis. Och de sände efter honom till Lachis, och dråpo honom der.
Anthu anapangana zomuchita chiwembu mu Yerusalemu ndipo Amaziya anathawira ku Lakisi, koma anatumiza anthu ku Lakisiko nakamuphera komweko.
20 Och de förde honom dädan på hästar; och han vardt begrafven i Jerusalem, när sina fäder uti Davids stad.
Anabwera naye ku pa kavalo ku Yerusalemu ndi kumuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide.
21 Och hela Juda folk togo Asaria, uti lians sextonde äre, och gjorde honom till Konung i hans faders Amazia stad.
Ndipo anthu onse a ku Yuda anatenga Azariya, amene anali ndi zaka 16 namulonga ufumu mʼmalo mwa abambo ake Amaziya.
22 Han byggde Elath, och fick det igen under Juda, sedan Konungen med hans fäder afsomnad var.
Azariya anamanga mzinda wa Elati ndi kuwubwezeretsa ku Yuda, Amaziya atamwalira.
23 Uti femtonde årena Amazia, Joas sons, Juda Konungs, vardt Jerobeam, Joas son, Konung öfver Israel i Samarien, ett och fyratio år,
Mʼchaka cha khumi ndi chisanu cha Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda, Yeroboamu mwana wa Yehowasi mfumu ya Israeli analowa ufumu ku Samariya ndipo analamulira za 41.
24 Och gjorde det ondt varför Herranom, och öfvergaf icke alla Jerobeams, Nebats sons, synder, den Israel kom till att synda.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova ndipo sanasiye machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
25 Men han tog igen Israels gränsor, ifrå Hamath allt intill hafvet, som ligger i hedmarkene, efter Herrans Israels Guds ord, som han sagt hade genom, sin tjenare Propheten Jona, Amitthai son, som var af GathHepher.
Iye ndi amene anabwezeretsanso malire a Israeli kuyambira ku Lebo Hamati mpaka ku Nyanja ya Araba, molingana ndi zimene ananena Yehova Mulungu wa Israeli, kudzera mwa mtumiki wake Yona mwana wa Amitai, mneneri wochokera ku Gati-Heferi.
26 Ty Herren såg till Israels svåra jämmer, så att ock de innelyckte och igenlefde förgingos; och ingen hjelpare var i Israel.
Pakuti Yehova anaona masautso a Israeli amene anali owawa kwambiri, panalibe kapolo kapena mfulu ngakhale wina aliyense amene akanathandiza Israeli.
27 Och Herren hade icke sagt, att han ville utskrapa Israels namn under himmelen; utan halp dem genom Jerobeam, Joas son.
Pakuti Yehova anali asananene zofafaniza ufumu wa Israeli pa dziko lapansi, Iye anawapulumutsa kudzera mʼdzanja la Yeroboamu mwana wa Yowasi.
28 Hvad nu mer af Jerobeam sägandes är, och allt det han gjort hafver, och hans magt, huru han stridt hafver, och huru han igenfick Damascon och Hamath till Juda i Israel, si, det är skrifvet i Israels Konungars Chrönico.
Ntchito zina za Yeroboamu ndi zonse zimene anachita, za kupambana kwake pa nkhondo, za mmene anagonjetsera Damasiko ndi Hamati, imene inali mizinda ya Yuda, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
29 Och Jerobeam afsomnade med sina fäder, Israels Konungar; och hans son Zacharia vardt Konung i hans stad.
Yeroboamu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi mafumu a Israeli. Ndipo Zekariya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Kungaboken 14 >