< 2 Kungaboken 11 >

1 Men Athalja, Ahasia moder, då hon såg, att hennes son var död, stod hon upp, och förgjorde all Konungslig säd.
Ataliya amayi ake a Ahaziya ataona kuti mwana wawo wafa, ananyamuka nakawononga banja lonse la mfumu.
2 Men Joseba, Konung Jorams dotter, Ahasia syster, tog Joas, Ahasia son, och stal honom ifrå Konungsbarnen, som dräpne vordo, med hans ammo i sängkammarenom, och hon förgömde honom för Athalja, så att han icke vardt dräpen.
Koma Yehoseba, mwana wamkazi wa Mfumu Yehoramu, mlongo wake wa Ahaziya, anatenga Yowasi mwana wa Ahaziya, namusunga kutali ndi ana a mfumu amene ankati awaphewo. Anamuyika iye pamodzi ndi mlezi wake mʼchipinda chogona chamʼkati kubisira Ataliya kotero iye sanaphedwe.
3 Och han vardt undstungen med henne i Herrans hus i sex år; och Athalja var rådandes i landena.
Mwanayo anakhala mobisala pamodzi ndi mlezi wake mʼnyumba ya Yehova kwa zaka zisanu ndi chimodzi pamene Ataliya ankalamulira dzikolo.
4 Uti sjunde årena sände Presten Jojada bort, och tog till sig de öfversta öfver hundrade, med höfvitsmännerna och drabanterna, och lät komma dem till sig i Herrans hus, och gjorde ett förbund med dem, och tog en ed af dem i Herrans hus, och viste dem Konungens son;
Koma mʼchaka chachisanu ndi chiwiri, Yehoyada anatumiza mawu kukayitana atsogoleri olamulira asilikali 100 olondera mfumu ndiponso alonda olonda nyumba yaufumu ndipo anabwera nawo mʼNyumba ya Yehova. Iye anapangana nawo pangano ndipo anawalumbiritsa mʼnyumba ya Yehova. Kenaka anawaonetsa mwana wamwamuna wa mfumu uja.
5 Och böd dem, och sade: Detta är det I göra skolen; tredjeparten af eder, hvilkens skifte om Sabbathsdagen uppå går, skolen hålla vakt i Konungshusena;
Yehoyada anawalamulira kuti, “Chimene muti muchite ndi ichi: Inu magulu atatu amene muti mudzakhale pa ntchito tsiku la Sabata, gulu loyamba lidzalondera nyumba ya mfumu,
6 Och en tredjepart skall vara vid den porten Sur; och en tredjepart skall vara vid den porten, som är bak drabanterna; och skolen hålla vakt för Massa hus.
gulu lachiwiri lidzalondera Chipata cha Suri, ndipo gulu lachitatu lidzalondera chipata cha kumbuyo kwa asilikali amene amasinthana polondera nyumbayo.
7 Men två parter af eder allom, I som om Sabbathsdagen afgån, skolen vakta i Herrans hus när Konungen;
Ndipo inu amene muli mʼmagulu ena awiri amene simugwira ntchito pa tsiku la Sabata, nonse mudzalondere mfumu ku nyumbayo.
8 Och skolen ställa eder rundt omkring Konungen, och hvar och en med sine värjo i handene; och ho som kommer in emellan väggarna, han skall dö; så att I ären när Konungen, då han ut och in går.
Mudzakhale mozungulira mfumuyo, munthu aliyense ali ndi chida mʼmanja mwake. Wina aliyense amene adzakuyandikireni adzayenera kuphedwa. Muzikhala pafupi ndi mfumu kulikonse kumene ikupita.”
9 Och de öfverste öfver hundrade gjorde allt det Presten Jojada dem budit hade; och togo sina män till sig, som på Sabbathsdagen uppå gingo, med de som på Sabbathsdagen af gingo, och kommo till Presten Jojada.
Atsogoleri olamulira asilikali 100 aja anachitadi zonse monga analamulira wansembe Yehoyada. Aliyense anatenga anthu ake, iwo amene amakagwira ntchito pa tsiku la Sabata ndi amene amapita kukapuma ndipo anabwera kwa wansembe Yehoyada.
10 Och Presten fick höfvitsmännerna spetsar, och sköldar, som hade varit Konung Davids, och voro i Herrans hus.
Ndipo wansembeyo anawapatsa asilikaliwo mikondo ndi zishango zimene zinali za mfumu Davide ndipo zinali mʼNyumba ya Yehova.
11 Och drabanterna stodo omkring Konungen, hvar och en med sine värjo i handene; ifrå husens hörn på högra sidone, allt intill det hörnet på den venstra, intill altaret, och till huset.
Alondawo, aliyense ali ndi chida mʼmanja mwake, anayima mozungulira mfumu, pafupi ndi guwa lansembe ndi nyumbayo, kuchokera mbali ya kummwera mpaka mbali ya kumpoto kwa nyumbayo.
12 Och han lät Konungens son komma fram, och satte ena krono på honom, och tog vittnesbördet, och gjorde honom till Konung, och voro glade, och klappade händerna tillhopa, och sade: Lycka ske Konungenom!
Yehoyada anatulutsa mwana wa mfumuyo namuveka chipewa chaufumu ndipo anamupatsa Buku la Chipangano ndi kumuyika kukhala mfumu. Iwo anamudzoza ndipo anthu anamuwombera mʼmanja akufuwula kuti, “Mfumu ikhale ndi moyo wautali!”
13 Och då Athalja fick höra ropet af folket, som lopp dertill, kom hon ut till folket i Herrans hus;
Ataliya atamva phokoso limene alonda ndi anthuwo amachita, anapita ku Nyumba ya Yehova kumene kunali anthuwo.
14 Och såg till, si, då stod Konungen invid stodena, såsom sedvänja var, och sångare och trummetare när Konungenom; och allt folket i landena var gladt, och blåste med trummeter. Då ref Athalja sin kläder, och sade: Uppror, uppror.
Iye anayangʼana naona mfumu itayima pa chipilala, potsata mwambo waufumu. Atsogoleri a asilikali ndi oyimba malipenga anali pafupi ndi mfumuyo, ndipo anthu onse a mʼderalo ankasangalala ndi kuyimba malipenga. Pamenepo Ataliya anangʼamba mkanjo wake nafuwula kuti, “Kuwukira! Kuwukira!”
15 Men Presten Jojada böd de öfversta öfver hundrade, som voro satte öfver hären, och sade till dem: Hafver henne utu huset i gården; och om någor följer henne, han dräpes med svärd; ty Presten hade sagt, att hon icke skulle dö i Herrans hus.
Wansembe Yehoyada analamula atsogoleri a asilikali 100 amene amayangʼanira asilikaliwo kuti, “Mutulutseni ameneyo pakati panu ndipo muphe ndi lupanga aliyense amene adzamutsata.” Pakuti nʼkuti wansembeyo atanena kuti, “Ataliyayo asaphedwere mʼNyumba ya Yehova.”
16 Och de båro händerna på henne, och hon gick in på den vägen, som hästarna till Konungshuset gå, och vardt der dräpen.
Choncho anamugwira pamene amafika pa malo amene akavalo amalowera ku nyumba ya mfumu ndipo anamuphera pamenepo.
17 Så gjorde Jojada ett förbund emellan Herran, och Konungen, och folket, att de skulle vara Herrans folk; desslikes ock emellan Konungen och folket.
Tsono Yehoyada anachititsa pangano pakati pa Yehova ndi mfumu ndi anthu kuti adzakhala anthu a Yehova. Iye anachititsanso pangano pakati pa mfumu ndi anthu.
18 Då gick allt folket i landena in uti Baals hus, och bröto hans altare ned; och sönderslogo hans beläte allt grant, och Matthan, Baals Prest, slogo de ihjäl inför altaret; och Presten beställde ämbeten uti Herrans hus;
Anthu onse a mʼdzikomo anapita ku nyumba ya Baala nakayigwetsa. Iwo anaphwanya kotheratu maguwa ansembe ndi mafano ake ndipo anapha Matani wansembe wa Baala patsogolo pa maguwa pomwepo. Pamenepo wansembe Yehoyada anasankha oyangʼanira Nyumba ya Yehova.
19 Och tog de öfversta öfver hundrade, och de höfvitsmän och de drabanter, och allt folket i landena, och förde Konungen ned ifrå Herrans hus, och kommo den vägen ifrå drabantaporten intill Konungshuset; och han satte sig på Konungsstolen.
Iye anatenga atsogoleri a asilikali 100 aja, alonda olonda nyumba yaufumu pamodzi ndi anthu onse a mʼdzikomo ndipo onse pamodzi anayitulutsa mfumu mʼNyumba ya Yehova ndi kukalowa ku nyumba yaufumu podzera pa chipata cha alonda. Ndipo mfumuyo inakhala pa mpando wake waufumu.
20 Och allt folket i landet var gladt, och staden vardt stilla. Men Athalja dråpo de med svärd i Konungshuset.
Choncho anthu onse a mʼdzikomo anasangalala. Ndipo mu mzindamo munakhala bata chifukwa Ataliya nʼkuti ataphedwa ndi lupanga ku nyumba ya mfumu.
21 Och Joas var sju år gammal, då han vardt Konung.
Yowasi anali wa zaka zisanu ndi ziwiri pamene anayamba kulamulira.

< 2 Kungaboken 11 >