< 2 Kungaboken 10 >

1 Och Achab hade sjutio söner i Samarien; och Jehu skref bref, och sände till Samarien till de öfversta i Israels stad, till de äldsta, och Achabs förmyndare, hvilket så lydde:
Tsono Ahabu anali ndi ana aamuna 70 a ku Samariya. Ndipo Yehu analemba makalata nawatumiza ku Samariya kwa atsogoleri a mu mzinda wa Yezireeli, kwa akuluakulu ndiponso kwa amene ankalera ana a Ahabu, nati,
2 När detta bref kommer till eder, när hvilkom edars herras söner äro, hans vagnar, hästar, faste städer och rustning;
“Inu mukangolandira kalatayi, popeza ana a mbuye wanu ali ndi inu ndiponso muli ndi magaleta ndi akavalo, mzinda wotetezedwa ndi zida zankhondo,
3 Så ser till, hvilken bäst och likast är ibland edars herras söner, och sätter honom på hans faders stol, och strider för edars herras hus.
sankhani mwana wa mbuye wanu amene ndi wooneka bwino ndiponso woyenera, mulowetseni ufumu wa abambo ake. Kenaka muchite nkhondo kuteteza nyumba ya mbuye wanu.”
4 Men de fruktade sig ganska fast, och sade: Si, två Konungar hafva icke blifvit ståndande för honom; huru skulle vi då stå?
Koma anthuwo anachita mantha kwambiri ndipo anati, “Taonani, mafumu awiri sanathe kulimbana naye, nanga ife tingathe bwanji?”
5 Och de som voro öfver huset, och öfver staden, och de äldste, och förmyndarena, sände bort till Jehu, och läto säga honom: Vi äre dine tjenare, vi vilje göra allt det du säger oss; vi vilje ingen göra till Konung; gör hvad dig täckes.
Choncho woyangʼanira nyumba ya mfumu, bwanamkubwa wa mzinda, akuluakulu ena ndiponso olera anawo anatumiza uthenga uwu kwa Yehu: “Ife ndife atumiki anu ndipo tidzachita chilichonse chomwe mutiwuze. Sitidzasankha munthu wina aliyense kukhala mfumu ndipo chitani chimene mukuganiza kuti nʼchabwino kwa inu.”
6 Då skref han ett annat bref till dem; det lydde alltså: Ären I mine, och lyden mine röst, så tager hufvuden af de män edars herras söner, och förer dem i morgon bittida till mig i Jisreel. Och Konungssönerna voro sjutio män, och de ypperste i staden uppfödde dem.
Ndipo Yehu anawalembera kalata yachiwiri yonena kuti, “Ngati inu muli mbali yanga ndi kuti mudzandimvera, mudule mitu ya ana a mbuye wanu ndipo mubwere nayo kwa ine ku Yezireeli mawa nthawi ngati yomwe ino.” Tsono ana a mfumu onse 70 anali pamodzi ndi akuluakulu a mu mzindamo, amene ankawalera.
7 Då nu brefvet kom till dem, togo de Konungssönerna, och dråpo sjutio män, och lade deras hufvud i korgar, och sände dem till honom i Jisreel.
Kalatayo itafika, anthuwo anatenga ana a mfumu 70 aja ndi kuwapha onse. Anayika mitu yawo mʼmadengu ndi kuyitumiza ku Yezireeli kwa Yehu.
8 Och då bådet kom, och bådade honom det, och sade: De hafva fört hit Konungssönernas hufvud; sade han: Lägger dem i två hopar för stadsporten, intill morgons.
Mthenga uja atafika, anamuwuza Yehu kuti, “Abweretsa mitu ya ana a mfumu.” Ndipo Yehu analamula kuti, “Unjikani mituyo mʼmilu iwiri pa chipata cha mzinda ndipo ikhale pamenepo mpaka mmawa.”
9 Och om morgonen, när han utgick, trädde han dit, och sade till allt folket: Ären I rättvise? Si, hafver jag gjort ett förbund emot min herra, och dräpit honom; ho hafver då slagit alla dessa?
Mmawa mwake Yehu anatuluka. Iye anayimirira pamaso pa anthu onse ndipo anati, “Inu ndinu osalakwa. Ndine amene ndinachita chiwembu mbuye wanu ndi kumupha, koma kodi wapha anthu onsewa ndani?
10 Så må I ju se, att intet Herrans ord är på jordena fallet, som Herren talat hafver emot Achabs hus; och Herren hafver gjort såsom han talat hafver genom sin tjenare Elia.
Koma dziwani tsono, kuti mawu amene Yehova anayankhula kunena za banja la Ahabu sadzapita padera. Yehova wachita chimene analonjeza kudzera mwa mtumiki wake Eliya.”
11 Alltså slog Jehu alla dem som qvare voro af Achabs hus i Jisreel, alla hans yppersta, hans vänner, och hans Prester, tilldess icke en var qvar;
Choncho Yehu anapha onse amene anatsala a mʼbanja la Ahabu ku Yezireeli, pamodzinso ndi akuluakulu ake onse, abwenzi ake ndiponso ansembe ake, sanasiyeko ndi mmodzi yemwe wamoyo.
12 Och stod upp, och drog bort till Samarien. Men i vägen var ett herdahus.
Kenaka Yehu ananyamuka kupita ku Samariya. Atafika pa malo otchedwa Beti-Ekedi wa abusa,
13 Der råkade Jehu vid Ahasia, Juda Konungs, bröder, och sade: Ho ären I? De sade: Vi äre Ahasia bröder, och drage ned till att helsa Konungens barn, och Drottningenes barn.
Yehu anakumana ndi abale ena a Ahaziya mfumu ya Yuda nawafunsa kuti, “Kodi ndinu yani?” Iwo anayankha kuti, “Ndife abale ake a Ahaziya, ndipo tabwera kulonjera banja la mfumu ndi ana a mfumukazi.”
14 Han sade: Griper dem lefvande. Och de grepo dem lefvande, och dråpo dem vid brunnen när herdahuset, två och fyratio män; och lät icke en af dem slippa.
Yehu analamula kuti, “Atengeni amoyo!” Choncho anawatenga amoyo ndipo anakawaphera ku chitsime cha ku malo otchedwa Beti-Ekedi wa abusa; anthu onse 42. Iye sanasiyepo ndi mmodzi yemwe wamoyo.
15 Och då han drog dädan, fann han Jonadab, Rechabs son, den honom mötte, och helsade honom, och sade till honom: Är ditt hjerta rätt, såsom mitt hjerta med dino hjerta? Jonadab sade: Ja. Är det så, sade han, så räck mig dina hand. Och han räckte honom sina hand; och han lät honom sitta uppe när sig på vagnen;
Yehu atachoka kumeneko anakumana ndi Yehonadabu mwana wa Rekabu, amene amabwera kudzakumana naye. Yehu anamulonjera nati kwa iye, “Kodi mtima wako uli bwino monga momwe mtima wanga ugwirizana nawo mtima wako?” Yehonadabu anayankha kuti, “Inde ndikugwirizana nawe.” Yehu anati, “Ngati ndi choncho, gwire dzanja.” Ndipo iye anaterodi, ndipo Yehu anamugwira dzanja namulowetsa mʼgaleta lake.
16 Och sade: Kom med mig, och se mitt nit om Herran. Och de förde honom med honom på hans vagn.
Yehu anati, “Tiye kuno uwone mmene ndikudziperekera kwa Yehova.” Ndipo anayenda naye mʼgaleta mwake.
17 Då han kom till Samarien, slog han allt det som qvart var af Achab i Samarien, tilldess han förgjorde honom, efter Herrans ord, som han till Elia talat hade.
Yehu atafika ku Samariya, anapha onse amene anatsala a mʼbanja la Ahabu ku Samariya; anawawonongeratu potsata mawu a Yehova amene anayankhula kudzera mwa Eliya.
18 Och Jehu församlade allt folket, och lät säga till dem: Achab hafver fögo tjent Baal; Jehu vill bättre tjena honom.
Ndipo Yehu anasonkhanitsa anthu onse pamodzi nawawuza kuti, “Ahabu ankatumikira Baala pangʼono chabe; Yehu adzamutumikira kwambiri.
19 Så låt nu kalla alla Baals Propheter, alla hans tjenare, och alla hans Prester, till mig, så att ingen är borto; förty jag hafver ett stort offer till att göra Baal; hvilken borto är, den skall icke lefva. Men Jehu gjorde detta med listighet, att han måtte förgöra Baals tjenare.
Tsopano itanani aneneri a Baala onse, atumiki ake onse ndi ansembe ake onse. Pasapezeke ndi mmodzi yemwe wotsala chifukwa ine ndidzapereka nsembe yayikulu kwa Baala. Aliyense amene alephere kubwera adzaphedwa.” Koma Yehu anachita zimenezi mwachinyengo ndi cholinga choti awononge atumiki onse a Baala.
20 Och Jehu sade: Helger Baal ena högtid, och låter den utropa.
Yehu anati, “Itanitsani msonkhano wodzalemekeza Baala.” Ndipo analengeza za msonkhanowo.
21 Och sände Jehu i hela Israel, och lät komma alla Baals tjenare, så att ingen qvar var, som icke kom. Och de kommo i Baals hus; så att Baals hus vardt fullt i all rum.
Pamenepo Yehu anatumiza mawu ku dziko lonse la Israeli ndipo atumiki onse a Baala anabwera; palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala. Iwo anadzaza nyumba ya Baala. Nyumbayo inadzaziratu kuchokera ku khoma lina mpaka ku khoma lina.
22 Då sade han till dem, som voro öfver klädehuset: Bärer ut kläder för alla Baals tjenare. Och de båro kläder ut.
Ndipo Yehu anawuza munthu wosunga mikanjo kuti, “Bweretsa mikanjo yokwanira atumiki onse a Baala.” Ndipo iye anabweretsa mikanjoyo.
23 Och Jehu gick in uti Baals hus med Jonadab, Rechabs son, och sade till Baals tjenare: Ransaker, och ser till, att ingen Herrans tjenare är ibland eder, utan Baals tjenare allena.
Kenaka Yehu ndi Yehonadabu mwana wa Rekabu analowa mʼnyumba ya Baala. Yehu anawawuza atumiki a Baala kuti, “Yangʼanitsitsani ndipo muone kuti muno musapezeke atumiki a Yehova, koma mukhale atumiki okhawo a Baala.”
24 Och som de kommo in till att göra offer och bränneoffer, beställde Jehu sig åttatio män utanföre, och sade: Ho som släpper någon af männerna, som jag får under edra händer, hans själ skall vara för hans själ.
Choncho Yehu analowa kukapereka nsembe zina ndi nsembe zopsereza. Nthawi iyi nʼkuti Yehu atayika anthu 80 kunja kwa nyumbayo ndi chenjezo lakuti, “Ngati wina aliyense wa inu adzathawitsa wina aliyense wa anthu amene ndayika kuti muziwayangʼanira, munthu woteroyo adzaphedwa.”
25 När nu bränneoffret fullkomnadt var, sade Jehu till drabanterna och höfvitsmännerna: Går in, och slår dem allasamman; låter ingen komma derut. Och de slogo dem med svärdsegg, och drabanterna och höfvitsmännerna hofvo dem bort. Och de gingo till Baals hus stad;
Yehu atangotsiriza kupereka nsembe yopsereza, analamula alonda ndi akulu a ankhondo kuti, “Lowani ndipo mukawaphe ndipo musalole kuti wina athawe.” Choncho iwo anawapha ndi lupanga. Alonda ndi akulu a ankhondo anaponya mitembo ya anthuwo panja ndipo anakalowa mʼkati mwenimweni mwa nyumba ya Baala.
26 Och togo ut de stodar i Baals hus, och brände dem upp;
Iwo anakatulutsa mwala wopatulika umene unali mʼnyumba ya Baala ndipo anawutentha.
27 Och slogo sönder Baals stodar, samt med Baals hus; och gjorde der ett hemligt hus af, allt intill denna dag.
Anawononga mwala wopatulika wa Baala ndi kugwetsa nyumba ya Baala, ndipo anthu anayisandutsa chimbudzi mpaka lero lino.
28 Alltså förgjorde Jehu Baal utur Israel.
Motero Yehu anawononga Baala mu Israeli.
29 Men ifrå Jerobeams, Nebats sons, synder, den Israel kom till att synda, gick Jehu icke, och öfvergaf icke de guldkalfvar i BethEl och i Dan.
Koma Yehuyo sanaleke machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati amene anachimwitsa nawo Israeli kupembedza mafano a golide a ana angʼombe ku Beteli ndi ku Dani.
30 Och Herren sade till Jehu: Derföre, att du hafver viljog varit till att göra min vilja, och hafver gjort på Achabs hus allt det i mino hjerta var, skola dina söner sitta dig på Israel stol intill fjerde led.
Yehova anati kwa Yehu, “Chifukwa wachita bwino pokwaniritsa kuchita zabwino pamaso panga ndipo wachitira banja la Ahabu zonse zimene zinali mʼmaganizo anga, zidzukulu zako zidzakhala pa mpando waufumu wa Israeli mpaka mʼbado wachinayi.”
31 Dock höll icke Jehu, att han i Herrans Israels Guds lag vandrade af allo hjerta; ty han trädde icke ifrå Jerobeams synder, som kom Israel till att synda.
Komatu Yehu sanasamalire kusunga lamulo la Yehova Mulungu wa Israeli ndi mtima wake wonse. Iyeyo sanaleke machimo a Yeroboamu amene anachimwitsa nawo Israeli.
32 På den tiden begynte Herren ledas vid Israel; ty Hasael slog dem i alla Israels gränsor;
Masiku amenewo Yehova anayamba kuchepetsa dziko la Israeli. Hazaeli anagonjetsa Aisraeli,
33 Ifrå Jordan österut, och hela Gilead, de Gaditers, Rubeniters, och Manassiters land, ifrån Aroer, som ligger när den bäcken vid Arnon; och Gilead, och Basan.
kuyambira kummawa kwa Yorodani, dziko lonse la Giliyadi (chigawo cha Gadi, Rubeni ndi Manase), kuchokera ku Aroeri pafupi ndi chigwa cha Arinoni kudutsa Giliyadi mpaka ku Basani.
34 Hvad nu mer af Jehu sägande är, och allt det han gjort hafver, och all hans magt, si, det är skrifvet uti Israels Konungars Chrönico.
Ntchito zina za Yehu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?
35 Och Jehu afsomnade med sina fäder; och de begrofvo honom i Samarien; och Joahas hans son vardt Konung i hans stad.
Yehu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake ku Samariya. Ndipo Yehowahazi mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
36 Men tiden, som Jehu öfver Israel regerade i Samarien, är åtta och tjugu år.
Yehu analamulira Aisraeli ku Samariya zaka 28.

< 2 Kungaboken 10 >