< 2 Krönikeboken 31 >

1 Då detta alltså uträttadt var, drogo ut alle de Israeliter, som i Juda städer funne voro, och bröto ned stoderna, och höggo bort lundarna, och bröto ned höjderna och altaren, i hela Juda, BenJamin, Ephraim och Manasse, tilldess de gjorde en ända på dem. Och Israels barn drogo alle till sina ägor i sina städer igen.
Zonse zitatha, Aisraeli onse amene anali kumeneko anapita ku mizinda ya ku Yuda, nakaphwanya miyala yachipembedzo ndi kudula mitengo ya mafano a Asera. Iwo anakawononga malo achipembedzo ndi maguwa ansembe amene anali mʼdziko lonse la Yuda, Benjamini, Efereimu ndi Manase. Atawononga zonsezi, Aisraeli anabwerera ku mizinda yawo ndi ku malo awo.
2 Men Jehiskia ställde Presterna och Leviterna uti deras ordning, hvar och en efter sitt ämbete, både Prester och Leviter, till bränneoffer och tackoffer, att de skulle tjena, tacka och lofva, i portarna åt Herrans lägre.
Hezekiya anakhazikitsa magulu a ansembe ndi Alevi, gulu lililonse monga mwa ntchito zawo ngati ansembe kapena Alevi, kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano, kutumikira, kuyamikira ndi kuyimba matamando pa zipata za ku malo okhala Yehova.
3 Och Konungen gaf sin del af sina håfvor till bränneoffer, om morgon och om afton, och till bränneoffer om Sabbatherna, och nymånadom, och högtidom, efter som skrifvet står i Herrans lag.
Kuchokera pa chuma chake, mfumu inapereka nsembe zopsereza za mmawa ndi madzulo ndiponso nsembe zopsereza za pa Chikondwerero cha Masabata, Chikondwerero cha Mwezi Watsopano ndipo inakhazikitsa zikondwerero monga zinalembedwera mʼmalamulo a Yehova.
4 Och han sade till folket, som i Jerusalem bodde, att de skulle gifva Presterna och Leviterna delar, att de måtte desto bättre akta på Herrans lag.
Iyo inalamula anthu amene amakhala mu Yerusalemu kupereka gawo lawo kwa ansembe ndi Alevi kuti iwowo adzipereke ku malamulo a Yehova.
5 Och då det talet kom ut, gåfvo Israels barn mycken förstling af säd, vin, oljo, hannog och allahanda årsväxt på markene; och allahanda tiond förde de in, ganska mycket.
Lamuloli atangolilengeza, Aisraeli anapereka mowolowamanja zipatso zoyamba kucha za tirigu, vinyo watsopano, mafuta ndi uchi ndi zonse zomwe nthaka yawo inabereka. Anabweretsa zochuluka kwambiri, chakhumi cha chilichonse.
6 Förde också Israels barn och Juda, som i Juda städer bodde, tiond fram af fä och får, och tiond af det helgada som de Herranom sinom Gud helgat hade, och lade en hop här, och en hop der.
Aisraeli ndi Ayuda amene amakhala mʼmizinda ya Yuda anabweretsanso chakhumi cha ngʼombe zawo ndi nkhosa ndi chakhumi cha zinthu zoyera zoperekedwa kwa Yehova Mulungu wawo, ndipo anaziyika mʼmilumilu.
7 Uti tredje månadenom begynte de att lägga hoparna, och i sjunde månadenom lyktade de det.
Anayamba kuchita izi mwezi wachitatu ndipo anatsiriza mwezi wachisanu ndi chiwiri.
8 Och då Jehiskia med de öfversta ingingo, och sågo hoparna, lofvade de Herran, och hans folk Israel;
Hezekiya ndi akuluakulu ake atabwera ndi kuona miluyo, anatamanda Yehova ndi kudalitsa anthu ake, Aisraeli.
9 Och Jehiskia frågade Presterna och Leviterna om hoparna.
Hezekiya anafunsa ansembe ndi Alevi za miluyi;
10 Och Asaria Presten, den ypperste i Zadoks hus, sade till honom: Ifrå den tid man begynte införa häfoffret i Herrans hus, hafve vi ätit och äre mätte vordne, och här är ännu mycket qvart; förty Herren hafver välsignat sitt folk; derföre är denne hopen öfverblefven.
ndipo Azariya, mkulu wa ansembe, ochokera ku banja la Zadoki anayankha kuti, “Kuyambira pamene anthu anayamba kubweretsa zopereka zawo ku Nyumba ya Yehova ife takhala ndi zokwanira kudya ndi zina zambiri zosunga, chifukwa Yehova wadalitsa anthu ake, ndipo mulu umenewu ndiye zotsala.”
11 Då befallde Konungen, att de skulle reda till kistor i Herrans hus; och de tillredde dem;
Hezekiya analamula kuti akonze zipinda zosungiramo za mʼNyumba ya Yehova, ndipo izi zinachitika.
12 Och lade derin häfoffret, tionden, och det helgada, på sina tro. Och öfver det samma var skickad Chanania den Leviten, och Simei hans broder den andre;
Ndipo iwo mokhulupirika anabweretsa zopereka, chakhumi ndi mphatso zopatulika. Konaniya Mlevi ndiye amayangʼanira zinthu zimenezi ndipo mʼbale wake Simei ndiye anali wachiwiri wake.
13 Och Jehiel, Asasia, Nahath, Asahel, Jerimoth, Josabad, Eliel, Jismacha, Mahath och Benaja, förskickade af Chanania och Simei hans broders hand, efter Konungens Jehiskia befallning. Men Asaria var öfverste i Guds hus.
Yehieli, Azaziya, Nahati, Asaheli, Yerimoti, Yozabadi, Elieli, Isimakiya, Mahati ndi Benaya anali oyangʼanira motsogozedwa ndi Konaniya ndi Simei, mʼbale wake. Iwowa anasankhidwa ndi mfumu Hezekiya ndi Azariya mkulu woyangʼanira Nyumba ya Mulungu.
14 Och Kore, Jimna son, den Leviten, den dörravaktaren östantill, var öfver de friviljoga Guds gåfvor, som Herranom till häfoffer gifna vordo, och öfver det aldrahelgasta.
Kore mwana wa Imuna Mlevi, mlonda wa Chipata Chakummawa, amayangʼanira zopereka zaufulu kwa Mulungu, ankagawa zopereka za kwa Yehova ndiponso mphatso zopatulika.
15 Och under hans hand voro Eden, Minjamin, Jesua, Semaja, Amaria och Sechania, uti Presternas städer, på sina tro; att de skulle gifva sina bröder efter deras ordning, dem minsta såsom dem största;
Edeni, Miniyamini, Yesuwa, Semaya, Amariya, Sekaniya amamuthandiza mokhulupirika mʼmizinda yonse a ansembe kugawira kwa ansembe anzawo monga mwa magulu awo, aakulu ndi aangʼono omwe.
16 Desslikes dem som för manspersoner räknade vordo, tre åra gamle, och derutöfver, ibland alla dem som uti Herrans hus gingo, hvar på sin dag till sitt ämbete, och i sine vakt efter sitt skifte;
Kuwonjezera apa, amagawira ana aamuna a zaka zitatu kapena kupitirira amene mayina awo anali mʼmbiri ya mibado yawo, amene adzalowe mʼNyumba ya Yehova kugwira ntchito za tsiku ndi tsiku za magulu awo, molingana ndi udindo ndi magulu awo.
17 Sammalunda dem som för Prester räknade vordo, i deras fäders hus, och Leviterna, ifrå tjugu år och derutöfver, i deras vakt efter deras skifte;
Ndipo anazigawa kwa ansembe amene analembetsa mayina awo mwa mbiri ya mabanja awo, chimodzimodzinso Alevi amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirira molingana ndi udindo wawo ndi magulu awo.
18 Dertill dem som räknade vordo ibland deras barn, hustrur, söner och döttrar, i hela menighetene; förty de helgade på sina tro det helgada.
Iwo anaphatikizanso ana onse aangʼono, akazi ndiponso ana aamuna ndi ana aakazi a gulu lonse amene analembedwa mʼmbiri ya mibado yawo iyi, pakuti anakhulupirika pa kudzipatula okha.
19 Voro också män vid namn nämnde ibland Aarons barn, Presterna uppå förstädernes mark, i alla städer, att de skulle del gifva alla manspersoner ibland Presterna, och allom dem som ibland Leviterna räknade vordo.
Kunena za ansembe, zidzukulu za Aaroni, amene amakhala mʼminda yozungulira mizinda yawo kapena mzinda wina uliwonse, anthu anasankhidwa mowatchula mayina kuti azipereka magawo kwa munthu wamwamuna aliyense pakati pawo ndiponso kwa onse amene analembedwa mʼmbiri ya mibado ya Alevi.
20 Alltså gjorde Jehiskia i hela Juda, och gjorde det godt, rätt och sant var för Herranom sinom Gud.
Izi ndi zimene Hezekiya anachita mu Yuda monse, kuchita zabwino, zolungama ndi zokhulupirika pamaso pa Yehova Mulungu wake.
21 Och i all handel, som han tog sig före med Guds hus tjenste, efter lagen och buden, till att söka sin Gud, det gjorde han af allt hjerta; derföre gick han det ock väl igenom.
Pa chilichonse chimene anachita pa ntchito ya Nyumba ya Mulungu ndi pa kumvera malangizo ndi malamulo, iye anafunafuna Mulungu wake ndipo anagwira ntchito ndi mtima wake wonse. Ndipo zinthu zimamuyendera bwino.

< 2 Krönikeboken 31 >