< 2 Krönikeboken 25 >
1 Fem och tjugu åra gammal var Amazia, då han Konung vardt, och regerade nio och tjugu år i Jerusalem; hans moder het Joaddan af Jerusalem.
Amaziya anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 29. Dzina la amayi ake linali Yehoyadini wa ku Yerusalemu.
2 Och han gjorde det Herranom väl behagade, dock icke af allt hjerta.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, koma osati ndi mtima wonse.
3 Då nu hans rike stadfäst var, drap han sina tjenare, som hans fader Konungen slagit hade;
Pamene mphamvu zonse zaufumu zinali mʼmanja mwake, iye anapha akuluakulu amene anapha abambo ake, mfumu ija.
4 Men deras barn drap han intet; förty det står så skrifvet i lagen i Mose bok, der Herren bjuder och säger: Fäderna skola icke dö för barnen, och icke barnen för fäderna; utan hvar och en skall för sina synd dö.
Komabe iye sanaphe ana awo koma anatsatira zolembedwa mʼbuku la Mose, mʼmene Yehova analamula kuti, “Makolo sadzaphedwa chifukwa cha ana awo kapena ana kuphedwa chifukwa cha makolo awo. Aliyense adzafera machimo ake.”
5 Och Amazia församlade Juda, och satte dem efter fädershusen, efter öfverstarna öfver tusende och öfver hundrade, i hela Juda och BenJamin; och talde dem allt ifrå tjugu år, och derutöfver, och fann dem trehundradtusend utvalda, som i här draga kunde, som spjut och sköld föra kunde.
Amaziya anasonkhanitsa anthu a ku Yuda ndipo anawapatsa zochita molingana ndi mabanja awo kukhala anthu olamulira 1,000, ndi olamulira 100 pa Ayuda onse ndi Benjamini. Ndipo iye anawerenga amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo napeza kuti analipo amuna 300,000 okonzeka kugwira ntchito ya usilikali, okhoza kugwiritsa ntchito mkondo ndi chishango.
6 Dertill besoldade han utaf Israel hundradtusend starka krigsmän, för hundrade centener silfver.
Iye analembanso ntchito anthu odziwa nkhondo 100,000 ochokera ku Israeli pa mtengo wa makilogalamu 3,400 a siliva.
7 Men en Guds man kom till honom, och sade: Konung, låt icke Israels här komma med dig; förty Herren är icke med Israel, eller med all Ephraims barn.
Koma munthu wa Mulungu anabwera kwa iye ndipo anati, “Inu mfumu, asilikali awa ochokera ku Israeli asapite ndi inu, pakuti Yehova sali ndi Israeli kapena ndi aliyense wa anthu a Efereimu.
8 Ty om du kommer till att bevisa dina dristighet i stridene, så låter Gud dig falla för dina fiendar; förty när Gudi står magten till att hjelpa, och till att stjelpa.
Ngakhale mupite ndi kuchita nkhondo molimba mtima, Mulungu adzakugonjetsani pamaso pa adani anu, pakuti Mulungu ali ndi mphamvu yothandiza kapena kugonjetsa.”
9 Amazia sade till Guds mannen: Hvad skall man då göra med de hundrade centener, som jag hafver gifvit de krigsmän af Israel? Guds mannen sade: Herren hafver väl mer än det är, som han dig gifva kan.
Amaziya anafunsa munthu wa Mulungu kuti, “Koma nanga za makilogalamu aja a siliva amene ndapereka kwa asilikali a Israeli?” Munthu wa Mulungu anayankha kuti, “Yehova atha kukupatsani zambiri kuposa zimenezo.”
10 Då skiljde Amazia de krigsmän ifrå, som till honom af Ephraim komne voro, så att de gingo till deras rum igen. Då förgrymmade deras vrede sig svårliga emot Juda, och drogo hem igen illa tillfrids.
Choncho Amaziya anachotsa asilikali amene anabwera kwa iye kuchokera ku Efereimu ndipo anawatumiza kwawo. Iwo anakwiyira anthu a ku Yuda ndipo anapita kwawo atapsa mtima kwambiri.
11 Men Amazia var tröst, och förde sitt folk ut, och drog ut i saltdalen, och slog af Seirs barn tiotusend.
Ndipo Amaziya analimba mtima ndipo anatsogolera gulu lake lankhondo ku Chigwa cha Mchere, kumene anapha anthu 10,000 a ku Seiri.
12 Och Juda barn fångade af dem tiotusend lefvande; dem förde de uppå en bergsklint, och störte dem utför bergsklinten, att de alle sönderkrossades.
Gulu la ankhondo la Yuda linagwiranso anthu amoyo 10,000, napita nawo pamwamba pa thanthwe ndipo anawaponya pansi kotero kuti onse ananyenyeka.
13 Men de krigsmän, som Amazia hade ifrå sig sändt, så att de icke drogo med hans folk till stridena, lade sig neder i Juda städer, allt ifrå Samarien intill BethHoron, och slogo af dem tretusend, och togo mycket rof.
Pa nthawi imeneyi asilikali amene Amaziya anawabweza ndipo sanawalole kuti achite nawo nkhondo, anakathira nkhondo mizinda ya Yuda kuyambira ku Samariya mpaka ku Beti-Horoni. Iwo anapha anthu 3,000 ndipo anafunkha katundu wambiri.
14 Och då Amazia igenkom af de Edomeers slagtning, hade han med sig Seirs barnas afgudar, och satte dem sig till gudar, och tillbad dem, och rökte för dem.
Amaziya atabwerera kuja anakapha Aedomu, anabweretsa milungu ya anthu a ku Seiri. Ndipo anayika kuti ikhale milungu yake, ankayipembedza ndi kupereka nsembe zopsereza.
15 Då förgrymmade sig Herrans vrede öfver Amazia, och sände en Prophet till honom. Han sade till honom: Hvi söker du dess folks gudar, som sitt folk intet undsätta kunde ifrå dine hand?
Yehova anakwiyira Amaziya, ndipo anamutumizira mneneri amene anati, “Nʼchifukwa chiyani mukupembedza milungu ya anthu awa, imene sinathe kupulumutsa anthu ake mʼdzanja lanu?”
16 Och då han talade med honom, sade han till honom: Hafver man gjort dig till Konungens råd? Vänd igen; hvi vill du varda slagen? Då vände Propheten igen, och sade: Jag förmärker väl, att Gud hafver i sinnet förderfva dig, efter du detta gjort hafver, och hörer intet mitt råd.
Iye ali kuyankhula, mfumu inati, “Kodi ife takusankha iwe kuti ukhale mlangizi wa mfumu? Khala chete! Ufuna kuphedweranji?” Choncho mneneriyo analeka koma anati, “Ine ndikudziwa kuti Mulungu watsimikiza kukuwonongani chifukwa mwachita izi ndipo simunamvere uphungu wanga.”
17 Och Amazia, Juda Konung, var till råds, och sände bort till Joas, Joahas son, Jehu sons, Israels Konung, och lät säga honom: Kom, låt oss bese hvarannan.
Amaziya mfumu ya ku Yuda, atafunsa alangizi ake, anatumiza mawu awa kwa Yowasi mwana wa Yehowahazi mwana wa Yehu, mfumu ya Israeli: “Bwera udzakumane nane maso ndi maso.”
18 Men Joas, Israels Konung, sände till Amazia, Juda Konung, och lät säga honom: Törnebusken i Libanon sände till cedreträt i Libanon, och lät säga honom: Gif dina dotter minom son till hustru; men vilddjuren i Libanon lupo öfver törnebuskan, och trampade honom neder.
Koma Yowasi mfumu ya Israeli inayankha Amaziya mfumu ya Yuda kuti, “Nthawi ina kamtengo kaminga ka ku Lebanoni kanatumiza mawu kwa mkungudza wa ku Lebanoni kuti, ‘Pereka mwana wako wamkazi kwa mwana wanga kuti amukwatire!’ Koma chirombo cha ku Lebanoni chinabwera ndi kupondaponda mtengo wa minga uja.
19 Du menar: Si, jag hafver slagit de Edomeer, der förhäfver sig ditt hjerta utaf, och berömmer sig. Nu sitt hemma; hvi söker du efter olycko, att du må falla, och Juda med dig?
Iwe ukuti wagonjetsa Edomu, ndipo tsopano ukudzikuza ndi kudzitamandira, koma khala kwanu komweko! Nʼchifukwa chiyani ukufuna mavuto ndi kudzichititsa kuti ugwe pamodzinso ndi Yuda?”
20 Men Amazia hörde det intet; förty det skedde af Gudi, på det att de skulle varda gifne i fiendahand; derföre, att de de Edomeers gudar sökt hade.
Komabe Amaziya sanamvere pakuti ndi Mulungu amene anakonzeratu kuti awapereke kwa Yehowasi, chifukwa iwo amapembedza milungu ya ku Edomu.
21 Då drog Joas, Israels Konung, upp, och de besågo hvarannan, han och Amazia, Juda Konung, i BethSemes, som i Juda ligger.
Kotero Yowasi mfumu ya Israeli inakamuthira nkhondo. Iye ndi Amaziya anayangʼanana maso ndi maso ku Beti-Semesi ku Yuda.
22 Men Juda vardt slagen för Israel, och flydde, hvar och en i sina hyddor.
Yuda anagonjetsedwa ndi Israeli ndipo munthu aliyense anathawira kwawo.
23 Och Joas, Israels Konung, grep Amazia, Joas son, Joahas sons, Juda Konung, i BethSemes, och förde honom till Jerusalem, och bröt muren neder i Jerusalem, allt ifrån Ephraims port intill hörnporten, fyrahundrade alnar långt.
Yehowahazi mfumu ya Israeli inagwira Amaziya mfumu ya Yuda, mwana wa Yowasi, mwana wa Ahaziya ku Beti-Semesi. Yehowasi anabwera naye ku Yerusalemu ndipo anagwetsa khoma la Yerusalemu kuyambira pa Chipata cha Efereimu mpaka ku Chipata Chapangodya, khoma lotalika mamita 180.
24 Och allt det guld och silfver, och all käril, som för handene voro i Guds hus när ObedEdom, och i fataburenom i Konungshusena, och barnen, tog han till pant med sig till Samarien.
Iye anatenga golide ndi siliva yense ndi zida zonse zimene zimapezeka mʼNyumba ya Mulungu zimene ankazisamalira Obedi-Edomu, pamodzinso ndi chuma cha mʼnyumba yaufumu ndipo anatenga anthu ngati chikole.
25 Och Amazia, Joas son, Juda Konung, lefde efter Joas, Joahas sons, Israels Konungs, död i femton år.
Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anakhala ndi moyo kwa zaka khumi ndi zisanu atamwalira Yehowasi mwana wa Yehowahazi mfumu ya Israeli.
26 Hvad nu mer af Amazia sägande är, både det första och det sista, si, det är skrifvet uti Juda och Israels Konungars bok.
Ntchito zina za mfumu Amaziya, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli?
27 Och ifrå den tiden, att Amazia trädde ifrå Herranom, gjorde de ett förbund emot honom i Jerusalem; men han flydde till Lachis. Då sände de efter honom till Lachis, och dråpo honom der;
Kuyambira nthawi imene Amaziya analeka kutsatira Yehova anthu anamukonzera chiwembu mu Yerusalemu ndipo anathawira ku Lakisi, koma adaniwo anatumiza anthu ku Lakisiko ndipo anamupha komweko.
28 Och förde honom med hästar, och begrofvo honom när sina fäder uti Juda stad.
Iwo anabwera naye ali pa kavalo ndipo anayikidwa mʼmanda ndi makolo ake mu mzinda wa Yuda.