< 2 Krönikeboken 20 >

1 Derefter kommo Moabs barn, Ammons barn, och med dem de af Ammonim, till att strida emot Josaphat.
Zitatha izi, Amowabu ndi Aamoni pamodzi ndi Ameuni ena anabwera kudzachita nkhondo ndi Yehosafati.
2 Och man kom, och bådade det Josaphat, och sade: Emot dig kommer ett mägta stort tal ifrå hinsidon hafvet, af Syrien, och si, de äro i HazezonThamar, det är EnGedi.
Anthu ena anabwera kudzamuwuza Yehosafati kuti, “Gulu lalikulu kwambiri lankhondo likubwera kudzachita nanu nkhondo lochokera ku Edomu, ku mbali ina ya Nyanja. Gululi lafika kale ku Hazazoni Tamara” (ndiye kuti Eni-Gedi).
3 Men Josaphat fruktade sig, och ställde sitt ansigte till att söka Herran, och lät utropa en fasto i hela Juda.
Ndi mantha, Yehosafati anaganiza zofunsira kwa Yehova, ndipo analengeza kuti Ayuda onse asale zakudya.
4 Och Juda kom tillhopa, till att söka Herran; kommo ock utaf alla Juda städer till att söka Herran.
Anthu a ku Yuda anabwera pamodzi kudzafuna thandizo kwa Yehova, ndipo anabweradi kuchokera ku mzinda uliwonse wa mu Yuda kudzafunafuna Yehova.
5 Och Josaphat trädde in i menigheten af Juda och Jerusalem, uti Herrans hus inför nya gården;
Yehosafati anayimirira pakati pa msonkhano wa Yuda ndi Yerusalemu, pa Nyumba ya Yehova patsogolo pa bwalo latsopano
6 Och sade: Herre, våra fäders Gud, äst icke du Gud i himmelen, och råder öfver all Hedningarnas rike? Och i dine hand är kraft och magt, och ingen är, som emot dig stå kan.
ndipo anati: “Inu Yehova, Mulungu wa makolo athu, kodi Inu sindinu Mulungu amene muli kumwamba? Inu mumalamulira maufumu onse a mitundu ya anthu. Mphamvu ndi nyonga zili mʼmanja mwanu, ndipo palibe amene angalimbane nanu.
7 Hafver du, vår Gud, icke fördrifvit detta lands inbyggare för dino folke Israel, och hafver gifvit det Abrahams dins väns säd till evig tid;
Inu Mulungu wathu, kodi simunathamangitse nzika za dziko lino pamaso pa anthu anu Aisraeli ndipo munalipereka kwa zidzukulu za Abrahamu bwenzi lanu kwamuyaya?
8 Så att de hafva bott deruti, och byggt dig derinne till ditt Namn en helgedom, och sagt:
Iwo akhala mʼdzikolo ndipo anamangira Dzina lanu malo opatulika, nʼkumati,
9 Om något ondt, svärd, straff, pestilentie, eller hård tid öfver oss komme, skulle vi stå för detta hus inför dig; förty ditt Namn är i desso huse; och ropa till dig i våra nöd, så ville du höra dertill och hjelpa?
‘Ngati tsoka litigwera kaya ndi lupanga lachiweruzo, kapena mliri, kapenanso njala, ife tidzayima pamaso panu patsogolo pa Nyumba ya Mulungu ino imene imatchedwa ndi Dzina lanu ndipo tidzalirira kwa inu mʼmasautso athu, ndipo Inu mudzatimvera ndi kutipulumutsa.’
10 Nu si, Ammons barn, Moab, och de af Seirs berg, öfver hvilka du icke lät Israels barn draga, då de foro utur Egypti land, utan de måste vika af ifrå dem, och icke förderfva dem;
“Koma tsopano pano pali anthu ochokera ku Amoni, Mowabu ndi Phiri la Seiri amene dziko lawo Inu simunawalole Aisraeli kuti alithire nkhondo pamene amabwera kuchokera ku Igupto. Kotero anatembenuka ndi kuwaleka ndipo sanawawononge.
11 Och si, de låta oss det umgälla, och komma till att utdrifva oss utu ditt arf, som du oss gifvit hafver.
Taonani, mmene akutibwezera ife pobwera kudzatithamangitsa mʼdziko limene inu munatipatsa ngati cholowa chathu.
12 Vår Gud, vill du icke döma dem? Ty i oss är ingen magt emot denna stora hopen, som emot oss kommer; vi vete icke hvad vi göra skole, utan vår ögon se till dig.
Inu Mulungu wathu, kodi simuwaweruza? Pakuti ife tilibe mphamvu zolimbana ndi gulu lalikulu lankhondo limene likutithira nkhondoli. Ife sitikudziwa choti tichite, koma maso athu ali pa Inu.”
13 Och hele Juda stod för Herranom med sin barn, hustrur och söner.
Anthu onse a Yuda, pamodzi ndi akazi awo ndi ana ndi makanda, anayima chilili pamaso pa Yehova.
14 Men öfver Jahasiel, Sacharia son, Benaja sons, Jehiels sons, Matthania sons, den Leviten utaf Assaphs barn, kom Herrans Ande midt i menighetene;
Ndipo Mzimu wa Yehova unabwera pa Yahazieli mwana wa Zekariya, mwana wa Benaya, mwana wa Yeiyeli, mwana wa Mataniya Mlevi, chidzukulu cha Asafu, atayimirira mu msonkhano.
15 Och sade: Akter härtill, hele Juda, och I Jerusalems inbyggare, och Konung Josaphat; så säger Herren till eder: I skolen icke frukta eder, eller gifva eder för denna stora hopenom; ty det striden icke I, utan Gud.
Iye anati, “Tamverani mfumu Yehosafati ndi onse amene amakhala mu Yuda ndi Yerusalemu! Zimene Yehova akunena kwa inu ndi izi: ‘Musaope kapena kutaya mtima chifukwa cha gulu lalikulu lankhondo ili. Pakuti nkhondoyi si yanu, koma ya Mulungu.
16 I morgon skolen I draga ned till dem; och si, de draga upp till Ziz, och I skolen råka dem vid bäcken, för öknene Jeruel.
Mawa mupite mukamenyane nawo. Adzakhala akubwera mokweza kudzera Njira ya Zizi, ndipo mukawapeza kumapeto kwa chigwa cha ku chipululu cha Yeruweli.
17 Förty I skolen intet strida i denna sakene; allenast träder fram, och står, och ser Herrans salighet, den med eder är; Juda och Jerusalem, frukter eder intet, och gifver eder icke; i morgon drager ut emot dem. Herren är med eder.
Sikudzafunika kuti Inu mumenyane nawo pa nkhondo imeneyi. Inu mukhale pa malo anu; imani molimba ndipo onani chipulumutso chimene Yehova adzakupatsani, Inu Yuda ndi Yerusalemu. Musaope, musataye mtima. Pitani kuti mukakumane nawo mawa, ndipo Yehova adzakhala nanu.’”
18 Då böjde sig Josaphat med sitt ansigte till jordena, och hela Juda och Jerusalems inbyggare föllo neder för Herranom, och tillbådo Herran.
Yehosafati anaweramitsa nkhope yake ndi kugunda pansi, ndiponso anthu onse a Yuda ndi Yerusalemu anagwa pansi ndi kulambira Yehova.
19 Och Leviterna utaf de Kehathiters barn, och utaf de Korinters barn, stodo upp till att lofva Herran Israels Gud med höga röst åt himmelen.
Kenaka Alevi ena ochokera ku mabanja a Kohati ndi Kora anayimirira ndipo anatamanda Yehova Mulungu wa Israeli ndi mawu ofuwula kwambiri.
20 Och de voro bittida uppe om morgonen, och drogo ut till den öknen Thekoa. Och då de utdrogo, stod Josaphat och sade: Hörer härtill, Juda, och I Jerusalems inbyggare: Tror uppå Herran edar Gud, så varden I trygge; och tror hans Propheter, så sker eder lycka.
Mmamawa, ananyamuka kupita ku chipululu cha Tekowa. Akunyamuka, Yehosafati anayimirira ndipo anati, “Tandimverani ine anthu a Yuda ndi Yerusalemu! Khalani ndi chikhulupiriro mwa Yehova Mulungu wanu ndipo mudzatchinjirizidwa, khalani ndi chikhulupiriro mwa aneneri ake ndipo mudzapambana.”
21 Och han underviste folket, och satte sångare för Herranom, och dem som lofva skulle i heligom skrud, och gå för väpnade hären, och säga: Tacker Herranom, ty hans barmhertighet varar evinnerliga.
Atafunsira kwa anthu, Yehosafati anasankha anthu oti ayimbire Yehova ndi kumutamanda chifukwa cha ulemerero wa chiyero chake pamene amapita ali patsogolo pa gulu la ankhondo, akunena kuti: “Yamikani Yehova pakuti chikondi chake ndi chosatha.”
22 Och då de begynte till att tacka och lofva, lät Herren bakhären, som emot Juda kommen var, komma in på Ammons barn, Moab, och dem af Seirs berg; och de slogo dem.
Atangoyamba kuyimba ndi kutamanda, Yehova anapereka mʼmanja mwawo anthu a ku Amoni ndi a ku Mowabu ndiponso a ku Phiri la Seiri amene amalimbana ndi Yuda, ndipo anagonjetsedwa.
23 Då stodo Ammons barn och Moab emot dem af Seirs berg, till att förspilla och nederlägga dem; och då de hade gjort ända på dem af Seirs berg, halp den ene dem andra, att de ock förderfvade sig.
Anthu a ku Amoni ndi a ku Mowabu anawukira anthu ochokera ku Phiri la Seiri, ndipo anawawononga ndi kuwatheratu. Atatsiriza kuwapha anthu ochokera ku Seiri anamenyana wina ndi mnzake mpaka kuwonongana.
24 Men då Juda kom till Mizpe vid öknen, vände de sig emot hopen; och si, då lågo de döde kroppar på jordene, så att ingen undsluppen var.
Anthu a ku Yuda atafika pa malo oyangʼanana ndi chipululu ndi kuona kumene kunali gulu lalikulu lankhondo, iwo anangoona mitembo yokhayokha itagona pansi ndipo palibe amene anathawa.
25 Och Josaphat kom med sitt folk till att byta deras rof, och funno ibland dem myckna ägodelar och kläder, och kostelig tyg; och skinnade dem, så att de icke mer kunde föra, och utbytte rofvet i tre dagar; ty det var ganska mycket.
Choncho Yehosafati ndi anthu ake anapita kukafunkha, ndipo pakati pawo anapeza katundu wambiri ndi zovala ndiponso zinthu zina zamtengowapatali kuposa zomwe akanatha kunyamula. Kunali katundu wambiri kotero kuti zinawatengera masiku atatu kuti amutenge.
26 På fjerde dagenom kommo de tillhopa uti lofsdalenom; förty der lofvade de Herran; deraf heter det rummet lofsdal, allt intill denna dag.
Tsiku lachinayi anasonkhana ku chigwa cha Beraka kumene anatamanda Yehova. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa chigwa cha Beraka mpaka lero.
27 Alltså vände hvar och en af Juda och Jerusalem tillbaka igen, och Josaphat för dem, så att de drogo till Jerusalem med fröjd; ty Herren hade gifvit dem en glädje öfver deras fiendar;
Tsono motsogozedwa ndi Yehosafati, anthu onse a Yuda ndi Yerusalemu anabwerera ku Yerusalemu mokondwera pakuti Yehova anawagonjetsera adani awo.
28 Och drogo in uti Jerusalem med psaltare, harpor och trummeter, till Herrans hus.
Iwo analowa mu Yerusalemu ndipo anapita ku Nyumba ya Mulungu akuyimba azeze, apangwe ndi malipenga.
29 Och Guds fruktan kom öfver all rike i landen, då de hörde, att Herren hade stridt emot Israels fiendar.
Kuopsa kwa Mulungu kunali pa maufumu onse a mayiko amene anamva mmene Yehova anamenyera adani a Aisraeli.
30 Alltså vardt Josaphats rike stilla; och Gud gaf honom ro allt omkring.
Ndipo ufumu wa Yehosafati unali pa mtendere pakuti Mulungu wake anamupatsa mpumulo ku mbali zonse.
31 Och Josaphat regerade öfver Juda; och var fem och tretio år gammal, då han Konung vardt, och regerade fem och tjugu år i Jerusalem. Hans moder het Asuba, Silhi dotter.
Choncho Yehosafati analamulira Yuda. Iye anali wa zaka 35 pamene anakhala mfumu ya Yuda ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 25. Dzina la amayi ake linali Azuba mwana wa Sili.
32 Och han vandrade uti sins faders Asa väg, och gick intet derifrå, att han ju gjorde det Herranom väl täcktes;
Iye ankayenda mʼnjira za Asa abambo ake ndipo sanapatuke pa zimenezi pakuti anachita zolungama pamaso pa Yehova.
33 Undantagno, att de höjder icke borttagne vordo; förty folket hade ännu icke skickat sitt hjerta till deras fäders Gud.
Komabe malo opembedzerapo mafano sanachotsedwe ndipo anthu sanaperekebe mitima yawo kwa Mulungu wa makolo awo.
34 Hvad nu mer af Josaphat sägande är, både det första och det sista, si, det är skrifvet i Jehu gerningar, Hanani sons, hvilka han upptecknat hafver uti Israels Konungars bok.
Zochitika zina zokhudza ufumu wa Yehosafati, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la Yehu mwana wa Hanani, zomwe zikupezeka mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
35 Derefter förenade sig Josaphat, Juda Konung, med Ahasia, Israels Konung, hvilken ogudaktig var med sitt väsende.
Zitapita izi, Yehosafati mfumu ya Yuda inachita mgwirizano ndi Ahaziya mfumu ya Israeli, amene anachita zoyipa kwambiri.
36 Och han samfällde sig med honom till att göra skepp, att de skulle fara till sjös; och skeppen gjorde de i EzionGeber.
Iye anagwirizana ndi Ahaziya kuti apange sitima zapamadzi zochitira malonda. Atazipanga zimenezi ku Ezioni-Geberi,
37 Men Elieser, Dodava son af Maresa, spådde emot Josaphat, och sade: Derföre, att du hafver förenat dig med Ahasia, hafver Herren omintetgjort din verk. Och skeppen vordo sönderslagne, och kunde intet till sjös fara.
Eliezara mwana wa Dodavahu wa ku Maresa ananenera motsutsana ndi Yehosafati ndipo anati, “Chifukwa chakuti wachita mgwirizano ndi Ahaziya, Yehova adzawononga zimene mwapangazo!” Sitima za pamadzizo zinawonongeka ndipo sizinapite nʼkomwe kumene zimakachita malonda.

< 2 Krönikeboken 20 >