< 2 Krönikeboken 17 >

1 Och hans son Josaphat vardt Konung i hans stad, och vardt mägtig emot Israel;
Yehosafati mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake ndipo anadzilimbitsa pofuna kulimbana ndi Israeli.
2 Och lade krigsfolk uti alla Juda fasta städer, och satte befallningsmän i Juda land, och i Ephraims städer, som hans fader Asa vunnit hade.
Iye anayika magulu a asilikali mʼmizinda yonse yotetezedwa ya Yuda, ndipo anamanga maboma mu Yuda ndi mʼmizinda yonse ya Efereimu imene Asa abambo ake analanda.
3 Och Herren var med Josaphat; ty han vandrade i de förra Davids sins faders vägar, och sökte icke Baalim;
Yehova anali ndi Yehosafati chifukwa mʼzaka zoyambirira anatsatira makhalidwe a Davide abambo ake. Iye sanafunsire kwa Abaala.
4 Utan sins faders Gud, och vandrade i hans bud, och icke efter Israels gerningar.
Koma anafunafuna Mulungu wa abambo ake ndipo anatsatira malamulo ake osati zochita za Israeli.
5 Derföre stadfäste Herren honom riket; och hele Juda gaf Josaphat skänker; och han hade rikedomar och härlighet ganska mycket.
Yehova anakhazikitsa kolimba ufumuwo mʼmanja mwake ndipo Ayuda onse anabweretsa mphatso kwa Yehosafati, kotero kuti anali ndi chuma ndi ulemu wambiri.
6 Och då hans hjerta dristigt vardt i Herrans vägar, hof han också bort höjderna och lundarna utu Juda.
Mtima wake anawupereka kutsatira Yehova, kuwonjezera apo, anachotsa malo onse achipembedzo ndi mafano a Asera mu Yuda.
7 Uti tredje årena sins rikes sände han sina Förstar, Benhail, Obadia, Zacharia, Nethaneel och Michaja, att de skulle lära i Juda städer;
Mʼchaka chachitatu cha ufumu wake, iye anatuma akuluakulu ake Beni-Haili, Obadiya, Zekariya, Netaneli ndi Mikaya kukaphunzitsa mʼmizinda ya Yuda.
8 Och med dem de Leviter, Semaja, Nethania, Sebadja, Asahel, Semiramoth, Jonathan, Adonia, Tobia och TobAdonia; och med dem Presterna, Elisama och Joram.
Pamodzi ndi iwo panali Alevi ena: Semaya, Netaniya, Zebadiya, Asaheli, Semiramoti, Yonatani, Adoniya, Tobiya ndi Tobu-Adoniya ndiponso ansembe Elisama ndi Yehoramu.
9 Och de lärde i Juda, och hade Herrans lagbok med sig, och foro omkring i alla Juda städer, och lärde folket.
Iwo anaphunzitsa mu Yuda monse atatenga Buku la Malamulo a Yehova iwo anayenda mʼmizinda yonse ya ku Yuda ndipo anaphunzitsa anthu.
10 Och Herrans fruktan kom öfver all rike i de land, som lågo omkring Juda, så att de intet stridde emot Josaphat.
Kuopsa kwa Yehova kunali pa maufumu onse a mayiko oyandikana ndi Yuda, kotero kuti sanachite nkhondo ndi Yehosafati.
11 Och de Philisteer förde Josaphat skänker, en hop silfver; och de Araber förde honom sjutusend och sjuhundrad vädrar, och sjutusend och sjuhundrad bockar.
Afilisti ena anabweretsa kwa Yehosafati mphatso ndi siliva ngati msonkho, ndipo Aarabu anabweretsa ziweto: nkhosa zazimuna 7,700 ndi mbuzi 7,700.
12 Alltså växte Josaphat till, och vardt ju större och större; och han byggde i Juda slott och kornstäder.
Mphamvu za Yehosafati zinkakulirakulira. Iye anamanga malo otetezedwa ndi mizinda yosungiramo chuma mu Yuda
13 Och hade mycket till skaffa i Juda städer; och voro stridsamme och väldige män i Jerusalem.
ndipo anali ndi katundu wambiri mʼmizinda ya Yuda. Iye anayikanso asilikali odziwa bwino nkhondo mu Yerusalemu.
14 Och detta var ordningen ibland deras fäders hus, som i Juda Öfverstar voro öfver tusende: Adna den öfversten, och med honom voro trehundradetusend väldige män.
Chiwerengero chawo potsata mabanja awo chinali chotere: kuchokera ku Yuda, atsogoleri a magulu 1,000; mtsogoleri Adina, anali ndi anthu 300,000 odziwa nkhondo;
15 Näst honom var Johanan den öfversten, och med honom voro tuhundrade och åttatio tusend.
otsatana naye, mtsogoleri Yehohanani, anali ndi anthu 280,000;
16 Dernäst Amasia, Sichri son, den Herrans friviljoge, och med honom voro tuhundradetusend väldige män.
otsatana naye, Amasiya mwana wa Zikiri amene anadzipereka yekha kutumikira Yehova, anali ndi anthu 200,000.
17 Af BenJamins barn var Eljada en väldig man, och med honom voro tuhundradetusend, som med bågar och sköld färdige voro.
Kuchokera ku Benjamini: Eliada, msilikali wolimba mtima, anali ndi anthu 200,000 amene anali ndi mauta ndi zishango;
18 Efter honom var Josabad, och med honom voro hundrade och åttatio tusend färdige män till strid.
otsatana naye, Yehozabadi, anali ndi anthu 180,000 okonzekera nkhondo.
19 Desse vaktade alle på Konungen, förutan de som Konungen lagt hade uti de fasta städer i hela Juda.
Awa ndi anthu amene ankatumikira mfumu osawerengera amene anawayika mʼmizinda yotetezedwa mʼdziko lonse la Yuda.

< 2 Krönikeboken 17 >