< 2 Krönikeboken 15 >

1 Och uppå Asaria, Obeds son, kom Guds Ande.
Mzimu wa Mulungu unabwera pa Azariya mwana wa Odedi.
2 Han gick ut emot Asa, och sade till honom: Hörer härtill, Asa, och hele Juda och BenJamin; Herren är med eder, efter I ären med honom; och när I söken honom, låter han sig af eder finna; om I ock öfvergifven honom, så öfvergifver han ock eder.
Iye anapita kukakumana ndi Asa ndipo anati kwa iye, “Tandimverani, inu Asa ndi Ayuda onse ndi Benjamini. Yehova ali ndi inu, inunso mukakhala naye. Ngati inu mumufunafuna Iye mudzamupeza, koma ngati mumusiya, Iye adzakusiyani.
3 Men det skall vara många dagar i Israel, att der skall ingen rätter Gud vara; ingen Prest, som lärer; ingen lag.
Kwa nthawi yayitali Israeli anali wopanda Mulungu weniweni, wopanda wansembe wophunzitsa ndi wopanda malamulo.
4 Och när de omvända sig i sine nöd till Herran Israels Gud, och söka honom, så skall han låta sig finna.
Koma pamene anali pa mavuto anatembenukira kwa Yehova, Mulungu wa Israeli ndi kufunafuna Iye, ndipo anamupeza.
5 På den tiden varder icke väl gångandes dem som ut och in gå; förty det varder ett stort buller öfver alla de som bo på jordene.
Masiku amenewo sikunali kwabwino kuyenda ulendo, pakuti anthu onse okhala mʼdziko anali pa mavuto aakulu.
6 Ty det ena folket skall slå det andra, och en stad den andra; förty Gud skall förskräcka dem med allahanda ångest.
Mtundu umodzi umakanthidwa ndi mtundu wina ndipo mzinda wina umakanthidwa ndi mzinda wina, pakuti Mulungu amawasautsa ndi mazunzo a mtundu uliwonse.
7 Men I varer tröste, och drager icke edra händer ifrå; ty edart verk hafver sin lön.
Koma inu, khalani amphamvu ndipo musataye mtima, pakuti mudzalandira mphotho ya ntchito yanu.”
8 Då Asa hörde dessa orden, och Obeds den Prophetens Prophetia, vardt han tröst, och kastade bort de styggelser utu hela Juda land och BenJamin, och utu städerna, som han vunnit hade på Ephraims berg, och förnyade Herrans altare, som för Herrans förhus stod;
Asa atamva mawu awa ndiponso uneneri wa Azariya mwana wa Odedi, analimba mtima. Iye anachotsa mafano onse onyansa mʼdziko lonse la Yuda ndi Benjamini ndi mʼmizinda yonse imene analanda a ku mapiri a Efereimu. Iye anakonzetsa guwa lansembe la Yehova limene linali kutsogolo kwa khonde la Nyumba ya Mulungu.
9 Och församlade hela Juda och BenJamin, och främlingarna när dem utaf Ephraim, Manasse och Simeon; förty till honom föllo månge af Israel, som de sågo att Herren hans Gud med honom var.
Kenaka anasonkhanitsa anthu onse a ku Yuda ndi Benjamini ndiponso anthu ochokera ku Efereimu, Manase ndi Simeoni amene ankakhala pakati pawo, pakuti gulu lalikulu linabwera kwa iye kuchokera ku Israeli litaona kuti anali ndi Yehova Mulungu wake.
10 Och de församlade sig till Jerusalem i tredje månadenom, i femtonde årena Asa rikes;
Iwo anasonkhana mu Yerusalemu mwezi wachitatu wa chaka cha 15 cha ulamuliro wa Asa.
11 Och offrade på den dagen Herranom utaf rofvet, som de hemtat hade, sjuhundrad nöt, och sjutusend får.
Pa nthawi imeneyi anapereka nsembe kwa Yehova, ngʼombe 700 ndiponso nkhosa ndi mbuzi 7,000 zochokera pa zolanda ku nkhondo zimene anabweretsa.
12 Och de trädde uti förbundet, att de skulle söka Herran deras fäders Gud, af allt hjerta, och af allo själ;
Iwo anachita pangano loti azifunafuna Yehova, Mulungu wa makolo awo, ndi mtima ndi moyo wawo wonse.
13 Och hvilken som icke sökte Herran Israels Gud, han skulle dö, både liten och stor, både man och qvinna.
Aliyense wosafunafuna Yehova Mulungu wa Israeli aziphedwa, kaya ndi wamngʼono kapena wamkulu, mwamuna kapena mkazi.
14 Och de svoro Herranom med höga röst, med rop, med trummeter och basuner.
Iwo analumbira kwa Yehova, mokweza mawu, akuyimba malipenga ndi mbetete.
15 Och hele Juda fröjdade sig öfver eden; ty de hade svorit af allt hjerta, och de sökte honom af allom vilja, och han lät sig af dem finna; och Herren gaf dem ro allt omkring.
Anthu onse a ku Yuda anakondwera pa kulumbirako chifukwa analumbira ndi mtima wawo wonse. Iwo anafunafuna Mulungu mwachidwi, ndipo anamupeza Iye. Kotero Yehova anawapatsa mpumulo mbali zonse.
16 Ock satte Konung Asa sina moder Maacha af ämbetet, för det hon stiktat hade uti Miplezeths lund; och Asa utrotade hennes Miplezeth, och sönderslog honom, och uppbrände honom vid Kidrons bäck.
Mfumu Asa anachotsanso Maaka agogo ake pa udindo wa amayi a mfumu chifukwa anapanga fano lonyansa la Asera. Asa anagwetsa fanolo, naliswa ndipo kenaka anakaliwotcha ku chigwa cha Kidroni.
17 Men höjderna vordo icke bortlagda utur Israel; dock var Asa hjerta rättsinnigt, så länge han lefde.
Ngakhale kuti sanachotse malo opembedzerako mafano mu Israeli, mtima wa Asa unali wodzipereka kwathunthu kwa Yehova, masiku onse a moyo wake.
18 Och han lät komma in uti Guds hus hvad hans fader helgat hade, och hvad han helgat hade, silfver, guld och käril.
Iye anabweretsanso mʼNyumba ya Mulungu zipangizo zasiliva, golide ndi ziwiya zina zimene iyeyo ndi abambo ake anazipatula.
19 Och intet örlig var allt intill femte och tretionde året Asa rikes.
Panalibenso nkhondo mpaka chaka cha 35 cha ufumu wa Asa.

< 2 Krönikeboken 15 >