< 2 Krönikeboken 13 >
1 Uti adertonde årena Konungs Jerobeams vardt Abia Konung i Juda;
Mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yeroboamu, Abiya analowa ufumu wa Yuda,
2 Och regerade tre år i Jerusalem; hans moder het Michaja, Uriels dotter, af Gibea. Och en strid hof sig upp emellan Abia och Jerobeam.
ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka zitatu. Dzina la amayi ake linali Maaka mwana wa Urieli wa ku Gibeya. Koma panali nkhondo pakati pa Abiya ndi Yeroboamu.
3 Och Abia gjorde redo till strid med fyrahundradtusend unga män, starka till strid; men Jerobeam gjorde redo till att strida emot dem med åttahundradtusend starka unga män.
Abiya anapita ku nkhondo ndi asilikali odziwa bwino nkhondo 400,000, ndipo Yeroboamu anandandalitsa ankhondo, asilikali 800,000 odziwa bwino nkhondo, osankhidwa ndi amphamvu, woti amenyane naye.
4 Och Abia steg upp på Zemaraims berg, som ligger på Ephraims berg, och sade: Hörer härtill, Jerobeam, och hele Israel!
Abiya anayima pa phiri la Zemaraimu, mʼdziko lamapiri la Efereimu, ndipo anati, “Yeroboamu ndi Aisraeli onse, tandimverani!
5 Veten I icke, att Herren Israels Gud hafver gifvit David Israels Konungarike till evig tid; honom och hans söner ett saltförbund?
Kodi inu simukudziwa kuti Yehova, Mulungu wa Israeli, wapereka ufumu wa Israeli kwa Davide ndi zidzukulu zake mpaka muyaya ndiponso pangano la mchere?
6 Men Jerobeam, Nebats son, Salomos tjenare, Davids sons, kastade sig upp, och satte sig emot sin herra;
Komabe Yeroboamu mwana wa Nebati, mtumiki wa Solomoni mwana wa Davide, anawukira mbuye wake.
7 Och till honom hafva gifvit sig lösaktige män och Belials barn, och hafva förstärkt sig emot Rehabeam, Salomos son; förty Rehabeam var ung, och af blödigt hjerta, så att han icke varde sig för honom.
Ndipo anthu ena achabechabe anasonkhana kwa iye ndipo anatsutsana ndi Rehobowamu mwana wa Solomoni pamene anali wamngʼono ndi wosalimba mtima ndi wopanda mphamvu kuti athe kulimbana nawo.
8 Nu menen I vilja sätta eder emot Herrans rike, ibland Davids söner; efter I ären en stor hop, och hafven gyldene kalfvar, som Jerobeam eder för gudar gjort hafver.
“Ndipo tsopano inu mwakonzekera kutsutsana ndi ufumu wa Yehova, umene uli mʼmanja mwa zidzukulu za Davide. Inu ndithu mulipo ankhondo ambirimbiri ndipo muli ndi ana angʼombe agolide amene Yeroboamu anapanga kuti akhale milungu yanu.
9 Hafven I icke fördrifvit Herrans Prester, Aarons söner, och Leviterna; och hafven gjort eder egna Prester, såsom folken i landen? Den som kommer till att fylla sina hand med en ung stut och sju vädrar, den varder Prest till dem som icke äro gudar.
Koma kodi inu simunathamangitse ansembe a Yehova, ana a Aaroni ndiponso Alevi ndi kudzisankhira ansembe anuanu monga anthu ena amachitira? Aliyense amene amabwera kuti adzipatule atatenga mwana wangʼombe wamwamuna ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri amakhala wansembe wa zinthu zimene sizili milungu.
10 Men med oss är Herren vår Gud, den vi icke öfvergifve, och Presterna, som Herranom tjena, Aarons barn, och Leviterna i deras sysslor;
“Koma kunena za ife, Yehova ndiye Mulungu wathu, ndipo sitinamusiye. Ansembe amene amatumikira Yehova ndi ana a Aaroni ndipo amathandizidwa ndi Alevi.
11 Och upptända Herranom bränneoffer, hvar morgon och hvar afton, dertill det goda rökverket, och tillreda bröden på det rena bordet, och den gyldene stakan med sina lampor, så att de varda upptände hvar afton; ty vi behålle Herrans vår Guds vakt; men I hafven öfvergifvit honom.
Mmawa uliwonse ndi madzulo aliwonse amapereka nsembe zopsereza ndi kufukiza lubani kwa Yehova. Iwo amayika buledi pa tebulo loyeretsedwa monga mwa mwambo ndipo amayatsa nyale pa zoyikapo nyale zagolide madzulo aliwonse. Ife timachita zofuna za Yehova Mulungu wathu. Koma inu mwamusiya.
12 Si, med oss är Gud i spetsen, och hans Prester och trummeterna till att trummeta; så att man skall trummeta emot eder; I Israels barn, strider icke emot Herran edra fäders Gud; ty det varder eder icke väl bekommandes.
Mulungu ali nafe pakuti ndiye mtsogoleri wathu. Ansembe ake atanyamula malipenga, adzayimba mfuwu wankhondo kulimbana nanu. Inu Aisraeli musalimbane ndi Yehova, Mulungu wa makolo anu, pakuti simungathe kupambana.”
13 Men Jerobeam gjorde en bakhär, att han måtte komma bakuppå dem; så att desse voro frammanför Juda, och bakhären efter dem.
Tsono Yeroboamu anali atatumiza asilikali kumbuyo mowazungulira, kotero kuti iye ali kutsogolo kwa anthu a ku Yuda, anthu owabisalira anali kumbuyo kwawo.
14 Då nu Juda vände sig om, si, då var strid både för och efter. Då ropade de till Herran, och Presterna trummetade med trummeter;
Asilikali a Yuda anatembenuka ndipo anaona kuti nkhondo imachitikira kutsogolo ndi kumbuyo. Ndipo iwo anafuwulira Yehova. Ansembe anayimba malipenga awo
15 Och hvar man i Juda skriade. Och då hvar man i Juda skriade, plågade Gud Jerobeam och hela Israel för Abia och Juda.
ndipo asilikali a Yuda anafuwula mawu ankhondo. Atafuwula mawu ankhondowo, Mulungu anagonjetsa Yeroboamu pamodzi ndi Aisraeli onse pamaso pa Abiya ndi Yuda.
16 Och Israels barn flydde för Juda; och Gud gaf dem i deras händer.
Aisraeli anathawa Ayuda. Ndipo Mulungu anawapereka mʼmanja mwawo.
17 Och Abia med sitt folk gjorde en stor slagtning på dem; och föllo af Israel slagne femhundradtusend unge män.
Abiya pamodzi ndi anthu ake anapha anthu ambiri, kotero kuti Aisraeli 500,000 odziwa bwino nkhondo anaphedwa.
18 Alltså vordo Israels barn nedertryckte i den tiden; och Juda barn vordo tröste; förty de förläto sig på Herran deras fäders Gud.
Ankhondo a Israeli anagonjetsedwa pa nthawi imeneyi, ndipo ankhondo a Yuda anapambana chifukwa anadalira Yehova, Mulungu wa makolo awo.
19 Och Abia jagade efter Jerobeam, och vann honom städer af, BethEl med dess döttrar, Jesana med dess döttrar, och Ephron med dess döttrar;
Abiya anathamangitsa Yeroboamu ndipo anamulanda mizinda ya Beteli, Yesana, ndi Efroni pamodzi ndi midzi yawo yozungulira.
20 Så att Jerobeam kom intet mer till magt, så länge Abia lefde. Och Herren plågade honom, så att han blef död.
Yeroboamu sanapezenso mphamvu nthawi ya Abiya. Ndipo Yehova anamukantha nafa.
21 Då nu Abia vardt förstärkt, tog han fjorton hustrur, och födde två och tjugu söner och sexton döttrar.
Koma Abiya mphamvu zake zinakula. Iye anakwatira akazi 14 ndipo anali ndi ana aamuna 22 ndi ana aakazi 16.
22 Hvad nu mer af Abia sägande är, och om hans vägar, och hans gerningar, det är skrifvet uti den Prophetens Iddo Historia.
Zina ndi zina zokhudza Abiya, zimene anachita ndi zimene anayankhula, zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mneneri Ido.