< 2 Krönikeboken 1 >

1 Och Salomo, Davids son, vardt i sitt rike förstärkt, och Herren hans Gud var med honom, och gjorde honom ju större och större.
Solomoni mwana wa Davide anakhazikika molimbika mu ufumu wake, pakuti Yehova Mulungu wake anali naye ndipo anamukweza kwambiri.
2 Och Salomo talade med hela Israel, med de öfverstar öfver tusend och hundrade, med domare och alla Förstar i Israel, med de öfversta fäder;
Tsono Solomoni anayankhula kwa Aisraeli onse, olamulira a anthu 1,000, olamulira a anthu 100, oweruza ndiponso kwa atsogoleri onse a Israeli ndi atsogoleri amabanja.
3 Att de skulle gå, Salomo och hela menigheten med honom, bort till den höjden, som i Gibeon var; ty der var Guds vittnesbörds tabernakel, som Mose Herrans tjenare gjort hade i öknene.
Solomoni pamodzi ndi gulu lonse la anthu anapita ku malo ofunika kwambiri pachipembedzo ku Gibiyoni. Tenti ya msonkhano ya Mulungu inali kumeneko, imene Mose mtumiki wa Yehova anayipanga mʼchipululu muja.
4 Ty Guds ark hade David uppfört ifrå KiriathJearim, dit han för honom tillredt hade; förty han hade honom uppslagit ett tabernakel i Jerusalem.
Davide anabweretsa Bokosi la Mulungu kuchokera ku Kiriyati Yearimu, ndi kulikhazika kumalo kumene analikonzera popeza analimangira tenti mu Yerusalemu.
5 Men det kopparaltaret som Bezaleel, Uri son, Hurs sons, gjort hade, var der för Herrans tabernakel; och Salomo och menigheten plägade söka det.
Koma guwa lansembe lamkuwa limene Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri analipanga linali ku Gibiyoni kutsogolo kwa tenti ya Yehova. Kotero kuti Solomoni ndi gulu lonse anakapembedza kumeneko.
6 Och Salomo offrade för Herranom på kopparaltaret, som der för dörrene af vittnesbördsens tabernakel stod, tusende bränneoffer.
Solomoni anapita pamene panali guwa lansembe lamkuwa pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano ndipo anapereka nsembe zopsereza 1,000.
7 I samma nattene syntes Gud Salomo, och sade till honom: Bed, hvad skall jag gifva dig?
Usiku umenewo Mulungu anaonekera kwa Solomoni ndipo anati kwa iye, “Pempha chilichonse chimene ukufuna ndipo ndidzakupatsa.”
8 Och Salomo sade till Gud: Du hafver gjort stora barmhertighet med minom fader David, och hafver gjort mig till Konung i hans stad.
Solomoni anayankha Mulungu kuti, “Inu munaonetsa kukoma mtima kwakukulu kwa Davide abambo anga ndipo mwayika ine kukhala mfumu mʼmalo mwake.
9 Så låt nu, Herre Gud, din ord varda sann till min fader David; ty du hafver gjort mig till Konung öfver ett folk, det så mycket är som stoftet på jordene.
Tsopano Inu Yehova Mulungu, lolani kuti lonjezo lanu kwa abambo anga Davide likwaniritsidwe, pakuti mwandiyika kukhala mfumu ya anthu anu amene ndi ochuluka ngati fumbi la pa dziko lapansi.
10 Så gif mig nu vishet och förstånd, att jag för detta folket må gå ut och in; ty ho förmår döma detta ditt myckna folk?
Mundipatse nzeru ndi luntha zolamulira anthu awa, pakuti ndani amene angathe kulamulira anthu anu ochulukawa?”
11 Då sade Gud till Salomo: Efter du hafver detta i sinnet, och hafver icke bedit om rikedomar, eller ägodelar, eller om härlighet, eller om dina fiendars själar, eller om långt lif; utan hafver bedit om visdom och förstånd, att du må döma mitt folk, der jag dig en Konung öfver gjort hafver;
Mulungu anati kwa Solomoni, “Popeza izi ndi zokhumba za mtima wako ndipo sunapemphe katundu, chuma kapena ulemu, kapena imfa ya adani ako, ndiponso poti sunapemphe moyo wautali koma nzeru ndi luntha kuti ulamulire anthu anga amene Ine ndakuyika kukhala mfumu yawo,
12 Så vare dig visdom och förstånd gifvet; dertill vill jag ock gifva dig rikedomar, ägodelar och härlighet, så att din like ibland Konungarna för dig icke varit hafver, ej heller varda skall efter dig.
Ine ndidzakupatsa nzeru ndi chidziwitso. Ndipo ndidzakupatsanso katundu, chuma ndi ulemu, zinthu zoti palibe mfumu imene inali nazo iwe usanakhalepo ndipo palibe wina amene adzakhale nazo iweyo ukadzafa.”
13 Alltså kom Salomo ifrå höjdene, som i Gibeon var, till Jerusalem, ifrå vittnesbördsens tabernakel, och regerade öfver Israel.
Kotero Solomoni anabwerera ku Yerusalemu kuchoka kumalo opembedzerako a ku Gibiyoni, ku tenti ya msonkhano ndipo analamulira Israeli.
14 Och Salomo församlade sig vagnar och resenärar, så att han åstadkom tusende och fyrahundrade vagnar, och tolftusend resenärar, och lät dem uti vagnsstäderna, och när Konungenom i Jerusalem.
Solomoni anasonkhanitsa magaleta ndi akavalo; anali ndi magaleta 1,400 ndi akavalo 12,000, amene anawayika mʼmizinda yosungira magaleta ndipo ena anali ndi iye mu Yerusalemu.
15 Och Konungen gjorde, att silfver och guld var i Jerusalem så mycket som stenar; och cedreträ så mycket som mulbärsträ i dalarna.
Mfumu inasandutsa siliva ndi golide kukhala ngati miyala wamba mu Yerusalemu. Inasandutsanso mkungudza kukhala wochuluka ngati mitengo ya mkuyu ya ku zigwa.
16 Och man förde Salomo hästar utur Egypten, och allahanda varor. Och Konungens köpmän köpte samma varor;
Solomoni amagula akavalo ku Igupto ndi Kuwe pakuti anthu amalonda a mfumu amakawagula ku Kuwe.
17 Och förde dem utur Egypten, hvar vagn för sexhundrad silfpenningar, och hvar häst för hundrade och femtio; alltså förde man dem ock till alla de Hetheers Konungar, och till de Konungar i Syrien, genom deras hand.
Anthu ankagula galeta ku Igupto pa mtengo wa masekeli asiliva 600 ndipo kavalo pa mtengo wa ndalama zasiliva 150. Iwo ankazigulitsanso kwa mafumu onse a Ahiti ndi a Aramu.

< 2 Krönikeboken 1 >