< 1 Samuelsboken 11 >

1 Så for Nahas, den Ammoniten, upp, och belade Jabes i Gilead. Och alle män i Jabes sade till Nahas: Gör ett förbund med oss, så vilje vi tjena dig.
Nahasi, Mwamoni anapita ndi kuzungulira mzinda wa Yabesi Giliyadi. Tsono anthu onse a ku Yabesi anapempha Nahasiyo kuti, “Muchite nafe pangano, ndipo tidzakutumikirani.”
2 Men Nahas, den Ammoniten, svarade dem: I så måtto vill jag göra ett förbund med eder, att jag stinger ut högra ögat på eder alla, och sätter eder till en försmädelse i hela Israel.
Koma Nahasi Mwamoni uja anayankha kuti, “Ndidzachita nanu pangano pokhapokha nditakolowola diso lakumanja la aliyense wa inu kuti ndichititse manyazi Aisraeli onse.”
3 Då sade till honom alle äldste i Jabes: Gif oss sju dagar, att vi måge sända bådskap i alla Israels gränsor; är då ingen hjelp, så vilje vi gå ut till dig.
Akuluakulu a mzinda wa Yabesi anati kwa iye, “Utipatse masiku asanu ndi awiri kuti titumize uthenga mu Israeli monse. Ngati sipapezeka wodzatipulumutsa, ndiye ife tidzadzipereka kwa iwe.”
4 Så kommo bådskapen till Gibea Sauls, och sade detta för folkens öron. Då hof allt folket sina röst upp, och gret.
Amithenga aja atafika kwawo kwa Sauli ku Gibeya ndi kufotokoza nkhaniyi kwa anthu onse, iwo analira motaya mtima.
5 Och si, då kom Saul utaf markene, gångandes bakefter sitt fä, och sade: Hvad skadar folkena, att det gråter? Då förtäljde de honom de mäns ord af Jabes.
Pa nthawiyo nʼkuti Sauli akubwera kuchokera ku munda, ali pambuyo pa ngʼombe zake za ntchito ndipo anafunsa. “Nʼchiyani chawavuta anthuwa kuti azilira motere?” Ndipo anamufotokozera zomwe anthu a mu mzinda wa Yabesi ananena.
6 Då kom Guds Ande öfver honom, när han dessa orden hörde, och hans vrede förgrymmade sig svårliga.
Sauli atamva mawu awo, Mzimu wa Mulungu unabwera pa iye mwa mphamvu ndipo anakwiya kwambiri.
7 Och han tog ett par oxar, och styckade dem, och sände i alla Israels gränsor med bådskap, och lät säga: Den som icke utdrager efter Saul och Samuel, hans oxar skall man så göra. Så föll Herrans fruktan öfver folket, att de utdrogo såsom en man.
Tsono anatenga ngʼombe ziwiri za ntchito, nazidula nthulinthuli. Ndipo anatumiza amithenga ndi nthulizo dziko lonse la Israeli ndi mawu akuti, “Umo ndi mmene adzachite ndi ngʼombe ya aliyense amene satsata Sauli ndi Samueli.” Ndipo anthu anachita mantha aakulu motero kuti onse ananyamuka ndi mtima umodzi.
8 Och man räknade dem i Besek; och Israels barn voro tre resor hundradetusend män; och Juda barn tretiotusend.
Pamenepo Sauli anawasonkhanitsa ku Bezeki nawawerenga, ndipo Aisraeli analipo 300,000, Ayuda analipo 30,000.
9 Och de sade till bådskapen, som komne voro: Säger de män i Jabes i Gilead: I morgon skolen I få hjelp, när solen är som hetast. Då desse bådskapen kommo, och förkunnade det de män i Jabes, vordo de glade.
Tsono Sauli anawuza amithenga ochokera ku Yabesi aja kuti, “Mukawawuze anthu a ku Yabesi Giliyadi kuti mawa nthawi ya masana adzapulumutsidwa.” Pamene amithengawo anapita ndi kukafotokoza nkhani imeneyi kwa anthu a ku Yabesi, iwo anasangalala kwambiri.
10 Och de män i Jabes sade: I morgon vilje vi gå ut till eder, att I mågen göra oss allt det eder täckes.
Choncho anthu a ku Yabesi anawuza Nahasi kuti, “Mawa tidzadzipereka kwa inu ndipo inu mudzachite nafe chilichonse chokukomerani.”
11 Den andra morgonen skickade Saul folket i tre hopar, och de kommo i lägret i morgonväktene, och slogo de Ammoniter allt intill dagen vardt som hetast. Och de som öfverblefvo, vordo så förskingrade, att icke två blefvo tillhopa.
Tsono mmawa mwake Sauli anagawa anthuwo mʼmagulu atatu. Mmamawa kusanache iwo analowa mʼmisasa ya Aamoni ndi kuwapha mpaka masana. Amene anapulumuka anabalalika, aliyense kwakekwake.
12 Då sade folket till Samuel: Hvar äro de, som sade: Skall Saul råda öfver oss? Låt de män komma här fram, att vi måge dräpa dem.
Kenaka anthu anafunsa Samueli kuti, “Kodi ndani aja ankanena kuti, ‘Kodi Sauli nʼkutilamulira ife?’ Bwera nawoni kuno kuti tidzawaphe.”
13 Saul sade: På denna dagen skall ingen dö; ty Herren hafver i dag gjort salighet i Israel.
Koma Sauli anati, “Palibe amene ati aphedwe lero, pakuti lero lino Yehova wagwira ntchito yopulumutsa Israeli.”
14 Samuel sade till folket: Kommer, låter oss gå till Gilgal, och der förnya Konungariket.
Ndipo Samueli anati kwa anthuwo, “Tiyeni tipite ku Giligala kuti tikatsimikizenso kuti Sauli ndi mfumu yathu.”
15 Så drog allt folket till Gilgal, och gjorde der Saul till Konung för Herranom i Gilgal, och offrade tackoffer inför Herranom. Och Saul med alla Israels män fröjdade sig der ganska storliga.
Choncho anthu onse anapita ku Giligala ndipo kumeneko Samueli anakalonga Sauli ufumu pamaso pa Yehova. Pambuyo pake anthu anapereka nsembe zachiyanjano pamaso pa Yehova, ndipo Sauli ndi Aisraeli onse anachita chikondwerero chachikulu.

< 1 Samuelsboken 11 >