< 1 Samuelsboken 1 >

1 Det var en man af Ramathaim Zophim, af Ephraims berg; han het ElKana, Jerohams son, Elihu sons, Thohu sons, Zuphs sons, hvilken en Ephrateer var.
Panali munthu wina wochokera ku Ramataimu, Mzofimu wa ku dziko la mapiri la Efereimu. Iyeyu dzina lake anali Elikana ndipo anali mwana wa Yerohamu, mwana wa Elihu, mwana wa Tohu, mwana wa Zufu wa fuko la Efereimu.
2 Och han hade två hustrur, den ena het Hanna, den andra Peninna; men Peninna hade barn, och Hanna hade inga barn.
Iye anali ndi akazi awiri, Hana ndi Penina. Penina anali ndi ana, koma Hana analibe.
3 Den samme mannen gick upp ifrå sin stad i sinom tid, att han skulle tillbedja och offra Herranom Zebaoth i Silo: och dersammastäds voro Herrans Prester Hophni och Pinehas, både Eli söner.
Chaka ndi chaka Elikana ankachoka ku mudzi kwawo kupita ku Silo kukapembedza ndi kukapereka nsembe kwa Yehova Wamphamvuzonse. Ku Siloko kunali ana awiri a Eli, Hofini ndi Finehasi amene anali ansembe a Yehova.
4 Då nu en dag kom, att ElKana offrade, gaf han sine hustru Peninna, och alla hennes söner och döttrar, stycker;
Tsiku lopereka nsembe likafika Elikana amapereka magawo a nsembeyo kwa mkazi wake Penina ndi kwa ana ake onse aamuna ndi aakazi.
5 Men Hanna gaf han ett stycke sörjandes; ty han hade Hanna kär; men Herren hade igenlyckt hennes lif.
Ngakhale ankamukonda Hana, koma ankamupatsa gawo limodzi popeza Yehova sanamupatse ana.
6 Och hennes haterska gjorde henne harmt, och kastade henne före hennes ofruktsamhet, att Herren hade igenlyckt hennes lif.
Tsono popeza Yehova sanamupatse Hana ana, mkazi mnzakeyo ankamuyamba dala ndi cholinga chomukwiyitsa.
7 Så gjorde hon hvart år, när de gingo upp till Herrans hus, och gjorde henne alltså harmt; men hon gret, och åt intet.
Izi zimachitika chaka ndi chaka. Hana ankati akamapita ku Nyumba ya Yehova mkazi mnzakeyo ankamunyogodola. Choncho Hana ankangokhalira kulira osafuna ndi kudya komwe.
8 Och ElKana hennes man sade till henne: Hanna, hvi gråter du? Och hvi äter du icke? Och för hvad sak är ditt hjerta så illa tillfrids? Är jag dig icke bättre än tio söner?
Tsono mwamuna wake Elikana ankamufunsa kuti, “Hana ukulira chifukwa chiyani? Wakhumudwa ndi chiyani kuti sukufuna ndi kudya komwe? Kodi ine kwa iwe sindili woposa ana aamuna khumi?”
9 Då stod Hanna upp, sedan hon ätit och druckit hade i Silo; och Presten Eli satt på en stol utanför dörrene af Herrans tempel.
Tsiku lina atatha kudya ndi kumwa ku Silo kuja, Hana anayimirira kukapemphera. Nthawiyi nʼkuti wansembe Eli atakhala pa mpando pa khomo la Nyumba ya Yehova.
10 Och hon var full med hjertans bedröfvelse; och hon bad till Herran, och gret;
Hana anavutika mʼmoyo mwake, ndipo anapemphera kwa Yehova akulira kwambiri.
11 Och lofvade ett löfte, och sade: Herre Zebaoth, om du ville se till dina tjenarinnos jämmer, och tänka på mig, och icke förgäta dina tjenarinno, utan gifva dina tjenarinno en son, så vill jag gifva honom Herranom, så länge han lefver, och ingen rakoknif skall komma på hans hufvud.
Ndipo iye analumbira kuti, “Inu Yehova Wamphamvuzonse, ngati muyangʼana kusauka kwa mtumiki wanune, ndi kuyankha pemphero langa osandiyiwala ine mtumiki wanu pondipatsa mwana wamwamuna, ine ndidzamupereka mwanayo kwa inu Yehova masiku onse a moyo wake. Lumo silidzapita pa mutu pake.”
12 Och som hon länge bad för Herranom, gaf Eli akt på hennes mun.
Akupemphera choncho kwa Yehova, Eli ankamuyangʼana pakamwa.
13 Ty Hanna talade i sitt hjerta, allenast hennes läppar rörde sig, men hennes röst hördes intet. Då mente Eli, att hon var drucken;
Hana ankapemphera chamumtima ndipo milomo yake inkangogwedera koma mawu ake samamveka. Choncho Eli anaganiza kuti anali ataledzera.
14 Och sade till henne: Huru länge vill du vara drucken? Låt vinet gå af dig.
Ndipo anamufunsa Hana kuti, “Kodi mukhala chiledzerere mpaka liti? Pitani, ayambe wakuchokani vinyo mwamwayo.”
15 Men Hanna svarade och sade: Nej, min Herre, jag är en bedröfvad qvinna; vin och starka drycker hafver jag icke druckit, utan hafver utgjutit mitt hjerta för Herranom.
Koma Hana anayankha kuti, “Sichoncho mbuye wanga. Ndakhala ndikumukhuthulira Yehova chisoni changa. Sindinamwe vinyo kapena chakumwa choledzeretsa chilichonse, popeza nthawi yonseyi ndakhala ndikupereka kwa Yehova nkhawa yayikulu ndi mavuto anga.
16 Räkna dock icke dina tjenarinno såsom en Belials dotter; ty jag hafver utaf mitt svåra bekymmer och sorg talat allt härtill.
Musaganize kuti mtumiki wanu ndi kukhala mkazi wachabechabe. Ine ndakhala ndi kupereka nkhawa yanga yayikulu ndi zowawa zanga.”
17 Eli svarade, och sade: Gack i frid; Israels Gud gifve dig dina bön, den du af honom bedit hafver.
Eli anayankha, “Pitani mu mtendere, ndipo Mulungu wa Israeli akupatseni zimene mwamupemphazo.”
18 Hon sade: Låt dina tjenarinno finna nåd för din ögon. Så gick qvinnan sin väg och åt, och såg icke mer så sorgeliga ut.
Hana anati, “Mundikomerebe mtima mtumiki wanune.” Kenaka anachoka nakadya, ndipo sanaonekenso wachisoni.
19 Och om morgonen voro de bittida uppe; och då de tillbedit hade för Herranom, vände de om, och gingo hem igen till Ramath. Och ElKana kände sina hustru Hanna. Och Herren tänkte på henne.
Elikana ndi banja lake anadzuka mmawa mwake nakapemphera pamaso pa Yehova. Pambuyo pake anabwerera kwawo ku Rama. Elikana anakhala pamodzi ndi mkazi wake, ndipo Yehova anamukumbuka Hanayo.
20 Och då någre dagar voro framlidne, vardt hon hafvandes, och födde en son, och kallade honom Samuel, sägandes: Ty jag hafver bedit honom af Herranom.
Motero Hana anakhala ndi pakati ndipo anabereka mwana wamwamuna. Anamutcha dzina lake Samueli, popeza anati, “Ndinachita kumupempha kwa Yehova.”
21 Och då mannen ElKana for upp med hela sitt hus, till att offra Herranom offer efter sedvänjon och sitt löfte;
Elikana ndi banja lake lonse anapita kukapereka nsembe ya pa chaka kwa Yehova ndi kukakwaniritsa malonjezo ake.
22 For Hanna intet med upp; utan sade till sin man: Jag vill icke fara upp, tilldess barnet är afvanat; då vill jag hafva honom med, att han må hafvas fram för Herran, och blifva der sedan evigliga.
Koma Hana sanapite nawo popeza anawuza mwamuna wake kuti, “Mwanayu akadzaleka kuyamwa, ndidzapita naye ndi kukamupereka pamaso pa Yehova ndipo adzakhala kumeneko moyo wake wonse.”
23 ElKana hennes man sade till henne: Gör såsom dig täckes; blif, tilldess du hafver afvant honom; Herren stadfäste det han sagt hafver. Så blef då qvinnan, och däggde sin son, intilldess hon vande honom af.
Elikana mwamuna wake anamuwuza kuti, “Chita chimene chakukomera. Tsala kuno mpaka utamusiyitsa kuyamwa, Yehova yekha akwaniritse mawu ake.” Choncho mkaziyo anatsala ku nyumba ndi kusamalira mwana wake mpaka atamuletsa kuyamwa.
24 Och så hade hon honom upp, sedan hon honom afvant hade, med tre stutar, med ett epha mjöl, och med en flasko vin, och hade honom in i Herrans hus i Silo; och pilten var ännu ung.
Atamuletsa kuyamwa, Hana anatenga mwanayo ali wachichepere, ndikupita naye ku nyumba ya Yehova ku Silo. Anatenga ngʼombe yamphongo ya zaka zitatu, ufa wa makilogalamu khumi, ndi thumba lachikopa la vinyo.
25 Och de slagtade stuten, och hade pilten fram för Eli.
Tsono anapha ngʼombe yamphongo ija ndi kupereka mwana uja kwa Eli.
26 Och hon sade: Ack! min Herre, så visst som din själ lefver, min Herre, jag är den qvinnan, som här när dig stod, och bad Herran;
Ndipo Hana anati kwa Eli, “Mbuye wanga, ine ndikunenetsadi pamaso panu kuti ndine mkazi uja amene anayima pamaso panu ndi kumapemphera kwa Yehova.
27 Då jag bad om denna pilten. Nu hafver Herren gifvit mig den bönena, som jag bad af honom.
Ndinapempha mwana uyu, ndipo Yehova wandipatsa chimene ndinamupempha.
28 Derföre gifver jag honom Herranom igen evigliga, efter han af Herranom beden är. Och de tillbådo der Herran.
Ndiye tsopano ine ndikumupereka kwa Yehova. Pa moyo wake wonse adzakhala wa Yehova.” Ndipo onse anapembedza Yehova kumeneko.

< 1 Samuelsboken 1 >