< 1 Kungaboken 22 >

1 Och gingo tre år om, att intet örlig var emellan de Syrer och Israel.
Kwa zaka zitatu panalibe nkhondo pakati pa Aramu ndi Israeli.
2 I tredje årena drog Josaphat, Juda Konung, ned till Israels Konung.
Koma pa chaka chachitatu, Yehosafati mfumu ya ku Yuda anapita kukacheza ndi mfumu ya ku Israeli.
3 Och Israels Konung sade till sina tjenare: Veten I icke, att Ramoth i Gilead är vårt, och vi sitte stilla, och tage det icke igen utu Konungens hand i Syrien?
Mfumu ya ku Israeli nʼkuti itawuza atumiki ake kuti, “Kodi inu simukudziwa kuti Ramoti Giliyadi ndi dera lathu ndipo ife palibe chimene tikuchita kuti tilitenge deralo mʼmanja mwa mfumu ya Aramu?”
4 Och sade till Josaphat: Vill du draga med mig i strid emot Ramoth i Gilead? Josaphat sade till Israels Konung: Jag vill vara såsom du, och mitt folk såsom ditt folk, och mina hästar såsom dina hästar.
Tsono iye anafunsa Yehosafati kuti, “Kodi udzapita nane ku nkhondo ku Ramoti Giliyadi?” Yehosafati anayankha mfumu ya ku Israeli kuti, “Ine ndili monga inu, anthu anga monga anthu anu, akavalo anga monga akavalo anu.”
5 Och Josaphat sade till Israels Konung: Fråga dock i dag om Herrans ord.
Koma Yehosafati anawuzanso mfumu ya ku Israeli kuti, “Poyamba mupemphe nzeru kwa Yehova.”
6 Då församlade Israels Konung Propheter vid fyrahundrad män, och sade till dem: Skall jag draga till Ramoth i Gilead till strid, eller skall jag låta bestå det? De sade: Drag ditupp; Herren varder det gifvandes i Konungens hand.
Choncho mfumu ya Israeli inasonkhanitsa pamodzi aneneri okwanira 400, ndipo inawafunsa kuti, “Kodi ndipite kukathira nkhondo Ramoti Giliyadi, kapena ndileke?” Iwo anayankha kuti, “Pitani, pakuti Ambuye waupereka mzindawo mʼmanja mwa mfumu.”
7 Men Josaphat sade: Är här nu ingen Herrans Prophet mer, att vi måge, fråga af honom?
Koma Yehosafati anafunsa kuti, “Kodi kuno kulibenso mneneri wina wa Yehova kumene ife tingakafunsireko nzeru?”
8 Israels Konung sade till Josaphat: Der är ännu en man, Micha, Jimla son, af hvilkom vi måge fråga Herran; men jag är vred på honom, ty han spår mig intet godt, utan allt ondt. Josaphat sade: Konungen tale icke så.
Mfumu ya ku Israeli inayankha Yehosafati kuti, “Alipo munthu mmodzi amene ife tingakafunsire kwa Yehova, koma ndimadana naye chifukwa iyeyo samanenera kanthu kalikonse kabwino ka ine, koma zoyipa nthawi zonse. Dzina lake ndi Mikaya mwana wa Imula.” Yehosafati anayankha kuti, “Mfumu musatero.”
9 Då kallade Israels Konung en kamererare, och sade: Haf med hast Micha, Jimla son, hit.
Choncho mfumu ya Israeli inayitana mmodzi mwa atumiki ake ndipo inati, “Kayitane Mikaya mwana wa Imula msangamsanga.”
10 Och Israels Konung, och Josaphat, Juda Konung, såto hvardera på sinom stol, klädde i Konungslig kläder, på platsen för portenom af Samarien; och alle Propheterna spådde för dem.
Atavala mikanjo yawo yaufumu, mfumu ya ku Israeli ndi Yehosafati mfumu ya ku Yuda anakhala pa mipando yawo yaufumu pabwalo lopondera tirigu pafupi ndi chipata cha Samariya, pamodzi ndi aneneri onse akunenera pamaso pawo.
11 Och Zedekia, Chenaana son, hade gjort sig jernhorn, och sade: Detta säger Herren: Härmed skall du stöta de Syrer, tilldess du gör ända på dem.
Tsono Zedekiya mwana wa Kenaana nʼkuti atapanga nyanga zachitsulo ndipo iye ananenera kuti, “Yehova akuti, ‘Ndi nyanga izi, inu mudzagunda nazo Aaramu mpaka iwo atawonongeka.’”
12 Och alle Propheterna spådde sammalunda, och sade: Drag upp till Ramoth i Gilead, och far lyckosamliga; Herren varder det gifvandes i Konungens hand.
Aneneri ena onse ananenera zomwezonso. Iwo anati, “Kathireni nkhondo Ramoti Giliyadi ndipo mukapambana, pakuti Yehova adzawupereka mzindawo mʼdzanja la mfumu.”
13 Och bådet, som bortgånget var till att kalla Micha, sade till honom: Si, Propheternas tal är endrägteliga godt för Konungenom; så låt nu ditt tal ock vara såsom deras tal, och tala det godt är.
Wamthenga amene anapita kukayitana Mikaya anamuwuza kuti, “Taonani, aneneri onse monga munthu mmodzi akunenera za kupambana kwa mfumu. Mawu anunso akhale ogwirizana ndi mawu awo, ndipo mukayankhule zabwino.”
14 Micha sade: Så sant som Herren lefver, jag skall tala det som Herren mig sägandes varder.
Koma Mikaya anati, “Pali Yehova wamoyo, ine ndikawawuza zokhazo zimene Yehova akandiwuze.”
15 Och då han kom till Konungen, sade Konungen till honom: Micha, skole vi draga till Ramoth i Gilead till att strida, eller skole vi låta det bestå? Han sade till honom: Ja, drag ditupp, och far lyckosamliga. Herren varder det gifvandes i Konungens hand.
Atafika, Ahabu anamufunsa kuti, “Mikaya, kodi tipite kukathira nkhondo Ramoti Giliyadi, kapena tileke?” Iye anayankha kuti, “Pitani ndipo mukapambana, pakuti Yehova adzawupereka mzindawo mʼdzanja la mfumu.”
16 Konungen sade åter till honom: Jag besvär dig, att du icke annat säger mig än sanningen, i Herrans Namn.
Ahabu anati kwa iye, “Kodi ndikulumbiritse kangati kuti undiwuze zoona zokhazokha mʼdzina la Yehova?”
17 Han sade: Jag såg hela Israel förströdd på bergen såsom får, de ingen herdan hafva; och Herren sade: Hafva desse ingen herra? Hvar och en vände om hem igen med frid.
Pamenepo Mikaya anayankha kuti, “Ndinaona Aisraeli onse atamwazikana pa mapiri ngati nkhosa zopanda mʼbusa, ndipo Yehova anati, ‘Anthu awa alibe mbuye wawo. Aliyense apite kwawo mwamtendere.’”
18 Då sade Israels Konung till Josaphat: Hafver jag icke sagt dig, att han intet godt spår mig, utan allt ondt?
Mfumu ya ku Israeli inati kwa Yehosafati, “Kodi ine sindinakuwuzeni kuti ameneyu samanenera kanthu kalikonse kabwino ka ine, koma zoyipa zokhazokha?”
19 Han sade: Derföre hör nu Herrans ord: Jag såg Herran sitta på sinom stol; och allan himmelska hären stå der när honom, på hans högra sido, och hans venstra.
Mikaya anapitiriza kuyankhula nati, “Tsono imvani mawu a Yehova: Ine ndinaona Yehova atakhala pa mpando wake waufumu, gulu lonse la kumwamba litayima ku dzanja lake lamanja ndi ku dzanja lake lamanzere.
20 Och Herren sade: Ho vill komma Achab i det sinnet, att han drager upp, och faller i Ramoth i Gilead? Och en sade det, och den andre det.
Ndipo Yehova anati, ‘Kodi ndani amene akamukope Ahabu kuti akathire nkhondo Ramoti Giliyadi, nʼkukafera komweko?’” “Wina anapereka maganizo ena ndipo winanso maganizo ena.
21 Då gick en ande ut, och steg fram för Herran, och sade: Jag vill komma honom i det sinnet. Herren sade till honom: Hvarmed?
Potsirizira, mzimu wina unabwera ndi kuyima pamaso pa Yehova ndipo unati, ‘Ine ndidzamukopa.’”
22 Han sade: Jag vill utgå, och vill vara en falsk ande uti alla hans Propheters mun. Han sade: Du skall komma honom i det sinnet, och få framgång; gack åstad, och gör alltså.
Yehova anafunsa kuti, “Ukamukopa bwanji?” Mzimuwo unati, “Ndidzapita ndi kukakhala mzimu wabodza pakamwa pa aneneri ake onse.” Yehova anati, “‘Iwe udzamukopadi. Pita kachite zomwezo.’
23 Nu se, Herren hafver gifvit en falsk anda uti alla dessa dina Propheters mun; och Herren hafver talat ondt öfver dig.
“Ndipo tsopano taonani, Yehova wayika mzimu wabodza mʼkamwa mwa aneneri anu onsewa. Yehova waneneratu kuti mukaona mavuto.”
24 Då gick Zedekia fram, Chenaana son, och slog Micha vid kindbenet, och sade: Huru? Hafver då Herrans Ande öfvergifvit mig, och talat med dig?
Pamenepo Zedekiya mwana wa Kenaana anapita pafupi namenya Mikaya patsaya. Iye anafunsa Mikaya kuti, “Kodi mzimu wa Yehova unadzera njira iti pamene umatuluka mwa ine kuti uziyankhula ndi iwe?”
25 Micha sade: Du skall få set på den dagen, då du går utu den ena kammaren uti den andra, att du må förgömma dig.
Mikaya anayankha kuti, “Udzaona pa tsiku limene uzikalowa mʼchipinda chamʼkati kuti ukabisale.”
26 Israels Konung sade: Tag Micha, och låt honom blifva när Amon borgamästaren, och när Joas, Konungens son;
Pamenepo mfumu ya ku Israeli inalamula kuti, “Mugwireni Mikaya ndipo mubwerere naye kwa Amoni mkulu wa mzinda, ndi kwa Yowasi mwana wa mfumu
27 Och säg: Detta säger Konungen: Sätter denna i fängsle, och spiser honom med bedröfvelses bröd och vatten, tilldess jag kommer igen med frid.
ndipo mukanene kuti, ‘Chimene mfumu ikunena ndi ichi; Muyikeni mʼndende munthu uyu ndipo musamupatse chakudya china koma buledi ndi madzi pangʼono mpaka nditabwerera mwamtendere.’”
28 Micha sade: Kommer du med frid igen, så hafver icke Herren talat genom mig. Och sade: Hörer häruppå, allt folk.
Mikaya ananena kuti, “Ngati mudzabwerera mwamtendere, Yehova sanayankhule kudzera mwa ine.” Ndipo iye anapitiriza kunena kuti, “Gwiritsitsani mawu angawa, anthu inu nonse!”
29 Alltså drog Israels Konung och Josaphat, Juda Konung, upp till Ramoth i Gilead.
Choncho mfumu ya ku Israeli ndi Yehosafati mfumu ya ku Yuda anapita ku Ramoti Giliyadi.
30 Och Israels Konung sade till Josaphat: Jag vill förkläda mig, och komma i stridena; men du klädd i din egna kläder. Israels Konung förklädde sig, och drog i stridena.
Mfumu ya ku Israeli inawuza Yehosafati kuti, “Ine ndidzalowa mu nkhondoyi modzibisa, koma inu muvale zovala zanu zaufumu.” Choncho mfumu ya ku Israeli inadzibisa ndi kupita ku nkhondo.
31 Men Konungen i Syrien böd sina öfverstar öfver hans vagnar, som voro två och tretio, och sade: I skolen icke strida antingen emot små eller stora, utan emot Israels Konung allena.
Tsono mfumu ya ku Aramu nʼkuti italamulira anthu ake 32 olamulira magaleta kuti, “Musamenyane ndi wina aliyense, wamngʼono kapena wamkulu, koma mfumu ya ku Israeli.”
32 Och då de öfverste sågo Josaphats vagnar, mente de att det hade varit Israels Konung, och föllo till honom med stridene; men Josaphat ropade.
Olamulira magaleta ataona Yehosafati, ankaganiza kuti, “Ndithu iyi ndiye mfumu ya ku Israeli.” Choncho anabwerera kukamenyana naye, koma Yehosafati atafuwula,
33 Då nu då öfverste för vagnarna sågo, att det var icke Israels Konung, vände de tillbaka igen ifrå honom.
olamulira akavalo anaona kuti sanali mfumu ya ku Israeli ndipo analeka kumuthamangitsa.
34 Och en man bände sin båga hårdt, och sköt Israels Konung emellan magan och lungorna. Och han sade till sin foroman: Vänd dina hand, och för mig utu hären; ty jag är sår.
Koma munthu wina anaponya muvi wake mwachiponyeponye ndi kulasa mfumu ya ku Israeli polumikizira malaya ake odzitetezera. Mfumu inawuza woyendetsa galeta lake kuti, “Tembenuka ndipo undichotse pa nkhondo pano pakuti ndalasidwa.”
35 Och striden vardt svår i den dagen. Och Konungen stod uppå vagnen emot de Syrer, och om aftonen blef han död; och blodet flöt utaf såret midt i vagnen.
Nkhondo inakula kwambiri tsiku limenelo, ndipo mfumu inakhala tsonga mʼgaleta lake moyangʼanana ndi Aaramu. Magazi ake ankayenderera pansi kuchokera mʼgaleta, ndipo pa nthawi ya madzulo inamwalira.
36 Och man lät utropa i hären, då solen gick neder, och säga: Hvar och en gånge i sin stad, och i sitt land.
Pamene dzuwa linkalowa, kunamveka mfuwu wa nkhondo kuti, “Munthu aliyense apite ku mzinda wa kwawo, aliyense apite ku dziko la kwawo!”
37 Alltså blef Konungen död, och vardt förd till Samarien; och de begrofvo honom i Samarien.
Ndipo mfumu ija inafa, nabwera nayo ku Samariya, ndipo anayika mʼmanda kumeneko.
38 Och då de tvådde vagnen vid dammen för Samarien, slekte hundar hans blod; och skökor tvådde honom, efter Herrans ord, det han talat hade.
Anatsuka galeta lija pa dziwe la ku Samariya (pamene ankasamba akazi achiwerewere) ndipo agalu ananyambita magazi a mfumuyo, monga momwe Yehova ananenera.
39 Hvad mer af Achab sägandes är, och hvad allt han gjort hafver, och om det elphenbenshus som han byggde, och om alla de städer som han byggde, si, det är skrifvet i Israels Konungars Chrönico.
Tsono ntchito zina za Ahabu, kuphatikiza zonse anazichita, nyumba yaufumu imene anamanga yokutidwa ndi minyanga ya njovu, mizinda yotetezedwa, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?
40 Alltså afsomnade Achab med sina fäder; och hans son Ahasia vardt Konung i hans stad.
Ahabu anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Ahaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
41 Och Josaphat, Asa son, vardt Konung öfver Juda, i fjerde årena Achabs, Israels Konungs;
Yehosafati, mwana wa Asa anakhala mfumu ya ku Yuda chaka chachinayi cha Ahabu mfumu ya ku Israeli.
42 Och var fem och tretio år gammal, då han vardt Konung, och regerade fem och tjugu år i Jerusalem; hans moder het Asuba, Silhi dotter;
Yehosafati anali wa zaka 35 pamene analowa ufumu, ndipo analamulira ku Yerusalemu zaka 25. Amayi ake anali Azuba mwana wa Silihi.
43 Och vandrade uti allom sins faders Asa väg, och gick icke derifrå, och gjorde det Herranom behagade. Dock kastade han icke bort de höjder; och folket offrade och rökte ännu på höjderna.
Pa zinthu zonse, Yehosafati anayenda mʼnjira za Asa abambo ake ndipo sanachite zotsutsana ndi machitidwe a abambo ake. Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova. Komabe, malo azipembedzo sanawawononge, ndipo anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
44 Och han hade frid med Israels Konung.
Yehosafati anakhala mwamtendere ndi mfumu ya ku Israeli.
45 Hvad nu mer af Josaphat sägandes är, och hans magt, hvad han gjort, och huru han stridt hafver, si, det är skrifvet i Juda Konungars Chrönico.
Ntchito zake zina za Yehosafati, zinthu zimene anachita ndi zamphamvu zimene anaonetsa, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Yuda?
46 Och fördref han desslikes utu landena hvad ännu qvart var af de roffare, som i hans faders Asa tid igenblefne voro.
Iye anachotsa mʼdzikomo amuna onse ochita zachiwerewere mwa chipembedzo amene anatsalira pa nthawi ya ulamuliro wa Asa, abambo ake.
47 Och ingen Konung var i Edom; men en höfvitsman var regent.
Nthawi imeneyo kunalibe mfumu ku Edomu, amene ankalamulira anali munthu woyikidwa ndi mfumu ya ku Yuda.
48 Och Josaphat hade låtit göra skepp i hafvet, som skulle till Ophir att hemta guld; men de foro intet åstad; förty de vordo sönderslagne i EzionGeber.
Yehosafati anapanga sitima zapamadzi zopita ku Ofiri kukatenga golide, koma sitimazo sizinayende chifukwa zinawonongeka ku Ezioni Geberi.
49 På den tiden sade Ahasia, Achabs son, till Josaphat: Låt mina tjenare fara med dina tjenare i skeppen; men Josaphat ville icke.
Nthawi imeneyo Ahaziya mwana wa Ahabu anawuza Yehosafati kuti, “Anthu anga ayende pa madzi pamodzi ndi anthu anu,” koma Yehosafati anakana.
50 Och Josaphat afsomnade med sina fäder, och vardt begrafven med sina fäder uti Davids hans faders stad; och Joram hans son vardt Konung i hans stad.
Ndipo Yehosafati anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide. Ndipo Yoramu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
51 Ahasia, Achabs son, vardt Konung öfver Israel i Samarien, i sjuttonde årena i Josaphats, Juda Konungs, och regerade öfver Israel i tu år;
Ahaziya mwana wa Ahabu anakhala mfumu ya ku Israeli ku Samariya mʼchaka cha 17 cha Yehosafati mfumu ya ku Yuda, ndipo analamulira Israeli zaka ziwiri.
52 Och gjorde det ondt var för Herranom, och vandrade i sins faders och sine moders väg, och i Jerobeams, Nebats sons, väg, hvilken Israel kom till att synda.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, chifukwa anayenda mʼnjira za abambo ndi amayi ake komanso mʼnjira za Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa Israeli.
53 Och han tjente Baal, och tillbad honom, och förtörnade Herran Israels Gud, såsom hans fader gjorde.
Potumikira ndi kupembedza Baala, iye anakwiyitsa Yehova Mulungu wa Israeli, monga momwe anachitira abambo ake.

< 1 Kungaboken 22 >