< 1 Kungaboken 2 >

1 Som nu tiden led, att David skulle dö, böd han sinom son Salomo, och sade:
Davide ali pafupi kumwalira, analangiza mwana wake Solomoni kuti:
2 Jag går alla verldenes väg; så var nu tröst, och var en man.
“Ndatsala pangʼono kupita kumene munthu wina aliyense amayenera kupitako. Tsono khala wamphamvu, uvale zilimbe,
3 Och akta på Herrans dins Guds vakt, så att du vandrar i hans vägar, och håller hans seder, bud, rätter, vittnesbörd, såsom skrifvet är i Mose lag; på det du skall vara klok i allt det du gör, och ehvart du dig vänder;
ndipo uzichita zimene Yehova Mulungu wako amafuna, uziyenda mʼnjira zake, uzisunga malangizo ndi malamulo ake monga momwe zinalembedwera mʼMalamulo a Mose, kuti zonse zimene udzachite zidzakuyendere bwino kulikonse kumene udzapite.
4 På det Herren skall uppväcka sitt ord, som han öfver mig talat hafver och sagt: Om din barn bevara sina vägar, så att de vandra troliga, och af allt hjerta och af allo själ, för mig, så skall aldrig fattas af dig en man på Israels stol.
Ndipo Yehova akwaniritse zimene anandilonjeza kuti, ‘Ngati zidzukulu zako zidzakhala mosamala, niziyenda mokhulupirika pamaso panga ndi mtima wawo wonse ndi moyo wawo wonse, sudzasowa munthu wokhala pa mpando waufumu wa Israeli.’
5 Och vetst du väl hvad Joab, ZeruJa son, hafver gjort mig, hvad han gjorde de två härhöfvitsmän i Israel, Abner, Ners son, och Amasa, Jethers son, hvilka han drap, och utgöt krigsblod i fridenom, och lät komma krigsblod uppå sitt bälte, det omkring hans länder var, och uppå sina skor, som på hans fötter voro.
“Tsono iwe ukudziwanso zoyipa zimene Yowabu mwana wa Zeruya anandichitira pakupha atsogoleri awiri a ankhondo a Israeli, Abineri mwana wa Neri ndi Amasa mwana wa Yeteri. Iye anawapha ndi kukhetsa magazi nthawi ya mtendere ngati nthawi ya nkhondo, ndipo anapaka magazi amenewo pa lamba wa mʼchiwuno mwake ndi pa nsapato za ku mapazi ake.
6 Gör efter dina vishet, så att du icke förer hans grå hår med frid ned till helvete. (Sheol h7585)
Iwe uchite kwa iye molingana ndi nzeru zako, koma usalole kuti afe ndi ukalamba ndi kupita ku manda mwamtendere. (Sheol h7585)
7 Och Barsillai barnom, den Gileaditens, skall du bevisa barmhertighet, så att de äta vid ditt bord; förty de gåfvo sig till mig, då jag flydde för dinom broder Absalom.
“Koma ana a Barizilai wa ku Giliyadi uwakomere mtima ndipo uwalole kuti akhale mʼgulu la anthu amene azidya pamodzi nawe. Pakuti anandisamalira pamene ndinkathawa mʼbale wako Abisalomu.
8 Och si, du hafver Simei när dig, Gora son, Jemini sons af Bahurim, den mig skamliga bannade, på den tid jag gick till Mahanaim; men han kom neder emot mig vid Jordan; då svor jag honom vid Herran, och sade: Jag vill icke dräpa dig med svärd.
“Ndipo kumbukira kuti uli ndi Simei mwana wa Gera, wa fuko la Benjamini wochokera ku Bahurimu, amene ananditemberera koopsa tsiku limene ndimapita ku Mahanaimu. Atabwera kudzakumana nane ku Yorodani, ine ndinalumbira mʼdzina la Yehova kuti, ‘Sindidzakupha iwe ndi lupanga.’
9 Men låt icke du blifva honom oskyldig; ty du äst en vis man, och vetst väl hvad du honom göra skall, att du låter hans grå hår med blod komma neder till helvete. (Sheol h7585)
Koma tsopano usamuyese ngati munthu wosalakwa. Iwe ndiwe munthu wanzeru. Udzadziwa choti uchite naye. Ngakhale ndi wokalamba, aphedwe ndithu.” (Sheol h7585)
10 Så afsomnade då David med sina fäder, och vardt begrafven uti Davids stad.
Tsono Davide anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu Mzinda wa Davide.
11 Men tiden, som David hade varit Konung öfver Israel, var fyratio år. I sju år var han Konung i Hebron, och tre och tretio år i Jerusalem.
Iyeyo nʼkuti atalamulira Israeli kwa zaka makumi anayi. Ku Hebroni analamulira zaka zisanu ndi ziwiri ndipo ku Yerusalemu analamulira zaka 33.
12 Och Salomo satt på sins faders Davids stol, och hans rike vardt storliga befäst.
Choncho Solomoni anakhala pa mpando waufumu wa abambo ake Davide, ndipo ufumu wake unakhazikika kwambiri.
13 Men Adonia, Haggiths son, kom in till BathSeba, Salomos moder; och hon sade: Kommer du ock med frid? Han sade: Ja.
Tsono Adoniya, mwana wa Hagiti, anapita kwa Batiseba, amayi ake a Solomoni. Batiseba anamufunsa kuti, “Kodi wabwera mwamtendere?” Iye anayakha kuti, “Eya, ndi zamtendere.”
14 Och han sade: Jag hafver något tala med dig. Hon sade: Säg.
Ndipo iye anawonjezera kunena kuti, “Ndili ndi mawu oti ndiyankhule nanu.” Batiseba anayankha kuti, “Yankhula.”
15 Han sade: Du vetst, att riket var mitt; och hela Israel hade vändt sitt ansigte till mig, att jag skulle vordit Konung; men nu är riket förvändt, och vordet mins broders; af Herranom är det hans vordet.
Tsono Adoniya anati, “Monga inu mukudziwa, ufumu unali wanga. Aisraeli onse ankayembekezera kuti ine ndidzakhala mfumu yawo. Koma zinthu zinasintha ndipo ufumu wapita kwa mʼbale wanga; pakuti wapatsa iye ufumuwu ndi Yehova.
16 Nu beder jag en bön af dig låt icke mitt ansigte komma till blygd. Hon sade till honom: Säg.
Tsono ndili ndi pempho limodzi kwa inu. Musandikanize ayi.” Batiseba anati, “Nena.”
17 Han sade: Tala med Konungen Salomo, ty han låter icke ditt ansigte komma till blygd, att han gifver mig Abisag af Sunem till hustru.
Adoniya anapitiriza kunena kuti, “Chonde, inu mupemphe mfumu Solomoni kuti andipatse Abisagi wa ku Sunemu kuti akhale mkazi wanga pakuti mukapempha inu sadzakukanizani.”
18 BathSeba sade: Väl; jag vill på dina vägnar tala till Konungen.
Batiseba anayankha kuti, “Chabwino. Ndidzakuyankhulira kwa mfumu.”
19 Och BathSeba kom in till Konung Salomo, till att tala med honom, på Adonia vägnar. Och Konungen stod upp, och gick emot henne, och tillbad henne, och satte sig på sin stol; och för Konungens moder vardt ock satt en stol, så att hon satte sig på hans högra sido.
Batiseba atapita kwa Mfumu Solomoni kukayankhula naye mʼmalo mwa Adoniya, mfumu inanyamuka kukumana naye, ndipo inaweramira amayi akewo, kenaka inakhala pa mpando wake waufumu. Iye anayitanitsa mpando wina kuti amayi ake akhalepo ndipo anakhala pansi ku dzanja lake lamanja.
20 Och hon sade: Jag beder en liten bön af dig; låt icke mitt ansigte komma till blygd. Konungen sade till henne: Bed, min moder; jag vill icke låta ditt ansigte komma till blygd.
Amayi akewo anati, “Ndikufuna ndikupempheni kanthu kakangʼono. Chonde musandikanize.” Mfumu inayankha kuti, “Pemphani amayi, ine sindikukanizani.”
21 Hon sade: Låt gifva Abisag af Sunem dinom broder Adonia till hustru.
Ndipo amayiwo anati, “Mulole kuti Abisagi wa ku Sunemu akhale mkazi wa mʼbale wanu Adoniya.”
22 Då svarade Konung Salomo, och sade till sina moder: Hvi beder du om Abisag af Sunem till Adonia? Bed honom ock riket med; förty han är min äldste broder, och han hafver Presten AbJathar och Joab, ZeruJa son.
Koma Mfumu Solomoni inayankha amayi ake aja kuti, “Chifukwa chiyani mukupemphera Adoniya Abisagi wa ku Sunemu? Mungathenso kumupemphera ufumu pakuti iyeyu ndi mkulu wanga ndipo mupemphereninso wansembe Abiatara ndi Yowabu mwana wa Zeruya!”
23 Och Konung Salomo svor vid Herran och sade: Gud göre mig det och det, Adonia skall detta hafva talat emot sitt lif.
Pamenepo Mfumu Solomoni inalumbira mʼdzina la Yehova kuti, “Mulungu andilange ine koopsa ngati Adoniya saphedwa chifukwa cha pempho lakeli!
24 Och nu, så visst som Herren lefver, den mig stadfäst hafver, och låtit sitta på mins faders Davids stol och den mig ett hus gjort hafver, såsom han sagt hafver; i dag skall Adonia dö.
Tsono pali Yehova wamoyo, amene anandikhazikitsa ine pa mpando waufumu wa abambo anga Davide ndi kundipatsa ufumu monga analonjezera, Adoniya aphedwa lero lomwe lino!”
25 Och Konung Salomo sände bort Benaja, Jojada son; han slog honom, så att han blef död.
Choncho Mfumu Solomoni inalamula Benaya mwana wa Yehoyada ndipo anakantha Adoniyayo, nafa.
26 Och till Presten AbJathar sade Konungen: Gack bort till Anathoth till din åker, ty du hörer döden till; men jag vill icke dräpa dig i dag; förty du hafver burit Herrans Herrans ark för minom fader David, och hafver med lidit, hvad som helst min fader lidit hafver.
Ndipo mfumu inati kwa Abiatara wansembe, “Pita ku Anatoti ku minda yako chifukwa ndiwe woyenera kufa, koma sindikupha tsopano, chifukwa unkanyamula Bokosi la Chipangano la Ambuye Yehova pamaso pa abambo anga Davide ndipo unazunzika limodzi ndi abambo angawo.”
27 Alltså fördref Salomo AbJathar, att han icke måtte blifva Herrans Prest; på det Herrans ord fullbordas skulle, som han öfver Eli hus talat hade i Silo.
Kotero Solomoni anachotsa Abiatara pa udindo wokhala wansembe wa Yehova, kukwaniritsa mawu a Yehova amene anayankhula za nyumba ya Eli ku Silo.
28 Och detta ryktet kom för Joab; ty Joab höll sig intill Adonia, ehuruväl han icke hade hållit sig till Absalom. Då flydde Joab in uti Herrans tabernakel, och fattade hornen af altaret.
Yowabu atamva zimenezi anathawira ku tenti ya Yehova ndipo anakagwira msonga za guwa lansembe, popeza Yowabu ndiye anathandiza Adoniya kuwukira koma sanathandize Abisalomu.
29 Och det vardt bådadt Konung Salomo, att Joab var flydd uti Herrans tabernakel, och si, han står vid altaret. Då sände Salomo Benaja, Jojada son, och sade: Gack, och slå honom.
Mfumu Solomoni inawuzidwa kuti Yowabu wathawira ku tenti ya Yehova ndipo ali pambali pa guwa lansembe. Tsono Solomoni analamula Benaya mwana wa Yehoyada kuti, “Pita, kamukanthe!”
30 Och då Benaja kom till Herrans tabernakel, sade han till honom: Så säger Konungen: Gack härut. Han sade: Nej, här vill jag dö. Och Benaja sade detta Konungenom igen, och sade: Så hafver Joab sagt, och så hafver han svarat mig.
Choncho Benaya analowa mʼtenti ya Yehova ndipo anati kwa Yowabu, “Mfumu ikuti ‘Tuluka!’” Koma iye anayankha kuti, “Ayi, ine ndifera muno.” Benaya anakafotokozera mfumu kuti, “Umu ndi mmene Yowabu wandiyankhira.”
31 Konungen sade till honom: Gör såsom han sagt hafver, och slå honom, och begraf honom, att du ifrå mig och mins faders hus tager det blod, som Joab oförskyldt utgjutit hafver.
Pamenepo mfumu inalamula Benaya kuti, “Kachite monga iye wanenera. Ukamukanthe ndi kumuyika mʼmanda. Ukatero udzandichotsera ine pamodzi ndi nyumba ya abambo anga mlandu wa anthu osalakwa amene Yowabu anawapha.
32 Och Herren betale honom hans blod uppå hans hufvud, att han hafver slagit två män, de der redeligare och bättre voro än han; och hafver dräpit dem med svärd, så att min fader David deraf intet visste, nämliga Abner, Ners son, den härhöfvitsmannen öfver Israel, och Amasa, Jethers son, härhöfvitsman öfver Juda;
Yehova adzamubwezera zomwe anachita pokhetsa magazi, chifukwa iye anakantha ndi lupanga anthu awiri abwino ndi olungama kuposa iye, nawapha, abambo anga Davide osadziwa. Anthu awiriwo ndi Abineri mwana wa Neri, wolamulira gulu lankhondo la Israeli ndi Amasa mwana wa Yeteri, wolamulira gulu lankhondo la Yuda.
33 Så att deras blod må betaldt varda på Joabs hufvud, och hans säds, i evig tid. Men David och hans säd, hans hus och hans stol, hafve frid af Herranom i evig tid.
Magazi amene Yowabu anakhetsa akhale pamutu pake ndi pa zidzukulu zake kwamuyaya. Koma pa Davide ndi zidzukulu zake, nyumba yake ndi mpando wake waufumu pakhale mtendere wochokera kwa Yehova kwamuyaya.”
34 Och Benaja, Jojada son, gick upp, och slog honom, och drap honom; och han vardt begrafven i sitt hus i öknene.
Choncho Benaya mwana wa Yehoyada anapita kukakantha Yowabu nʼkumupha ndipo anayikidwa mʼmanda mʼnyumba yakeyake ya ku chipululu.
35 Och Konungen satte Benaja, Jojada son, i hans stad öfver hären; och Zadok Presten satte Konungen i AbJathars stad.
Mfumu inayika Benaya mwana wa Yehoyada kuti akhale woyangʼanira gulu lankhondo mʼmalo mwa Yowabu ndipo inayika Zadoki kuti akhale wansembe mʼmalo mwa Abiatara.
36 Och Konungen sände bort, och lät kalla Simei, och sade till honom: Bygg dig ett hus i Jerusalem, och bo der, och gack intet ut dädan, antingen hit eller dit.
Kenaka mfumu inatuma anthu kukayitana Simei ndipo inamuwuza kuti, “Udzimangire nyumba mu Yerusalemu ndipo uzikhala kumeneko, koma usatuluke mu mzinda kupita kwina kulikonse.
37 På hvilken dag du der utgår, och går öfver den bäcken Kidron, så vet att du skall döden dö; ditt blod vare på ditt hufvud.
Tsiku lomwe udzatulukemo ndi kuwoloka Chigwa cha Kidroni, udziwiretu kuti udzafa ndipo magazi ako adzakhala pamutu pako.”
38 Simei sade till Konungen: Det är en god mening; såsom min herre Konungen sagt hafver, så skall din tjenare göra. Så bodde Simei i Jerusalem i långan tid.
Simei anayankha mfumu kuti, “Zimene mwanenazi nʼzabwino. Kapolo wanu adzachita monga mbuye wanga mfumu mwanenera.” Choncho Simei anakhala mu Yerusalemu nthawi yayitali.
39 Men det begaf sig efter tre år, att två tjenare lupo ifrå Simei till Achis, Maacha son, Konungen i Gath. Och Simei vardt sagdt: Si, dine tjenare äro i Gath.
Koma patatha zaka zitatu, akapolo awiri a Simei anathawira kwa Akisi mwana wa Maaka, mfumu ya ku Gati, ndipo Simei anawuzidwa kuti, “Akapolo anu ali ku Gati.”
40 Då stod Simei upp, och sadlade sin åsna, och drog åstad till Gath till Achis, att han skulle söka sina tjenare; och då han ditkom, förde han sina tjenare ifrå Gath.
Atamva zimenezi, anakwera bulu wake ndipo anapita kwa Akisi ku Gati kukafunafuna akapolo ake. Choncho Simei anapita ndi kukatenga akapolo ake ku Gati ndipo anabwera nawo.
41 Och det vardt sagdt Salomo, att Simei var faren af Jerusalem till Gath, och igen kommen.
Solomoni atawuzidwa kuti Simei anatuluka mu Yerusalemu ndi kupita ku Gati ndipo kuti wabwerako,
42 Då sände Konungen bort, och lät kalla Simei, och sade till honom: Hafver jag icke svorit dig vid Herran, och betygat dig, och sagt: På hvilken dag du fore ut, antingen hit eller dit, att du då veta skulle att du skulle döden dö? Och du sade till mig: Jag: hafver hört en god mening.
mfumu inamuyitanitsa Simei ndipo inamufunsa kuti, “Kodi sindinakulumbiritse mʼdzina la Yehova ndi kukuchenjeza kuti, ‘Tsiku limene udzatuluka kupita kwina kulikonse, udziwe kuti udzafa’? Nthawi imeneyo iwe unandiwuza kuti, ‘Zimene mwanena nʼzabwino. Ine ndidzamvera.’
43 Hvi hafver du då icke hållit dig efter Herrans ed, och det bud som jag dig budit hafver?
Chifukwa chiyani tsono sunasunge lumbiro lako kwa Yehova? Bwanji nanga sunamvere lamulo limene ndinakuwuza?”
44 Och Konungen sade till Simei: Du vetst allt det onda, som ditt hjerta med sig vet, som du minom fader David gjort hafver; Herren hafver betalat dina ondsko på ditt hufvud;
Mfumuyo inawuzanso Simei kuti, “Ukudziwa mu mtima mwakomo zoyipa zonse zimene unachitira abambo anga Davide. Tsopano Yehova akubwezera zoyipa zakozo.
45 Och Konung Salomo är välsignad, och Davids stol varder befäst för Herranom i evig tid.
Koma Mfumu Solomoni idzadalitsidwa ndipo mpando waufumu wa Davide udzakhazikika pamaso pa Yehova kwamuyaya.”
46 Och Konungen böd Benaja, Jojada son. Han gick ut, och slog honom, att han blef död. Och riket vardt befäst i Salomos hand.
Pamenepo mfumu inalamula Benaya mwana wa Yehoyada ndipo iye anapita kukakantha Simei ndi kumupha. Tsono ufumu unakhazikika mʼdzanja la Solomoni.

< 1 Kungaboken 2 >