< 1 Kungaboken 16 >
1 Så kom Herrans ord till Jehu, Hanani son, emot Baesa, och sade:
Ndipo Yehova anayankhula kudzera mwa Yehu mwana wa Hanani, mawu odzudzula Baasa kuti,
2 Derföre, att jag dig utu stoftet upphäfvit hafver, och gjort dig till en Första öfver mitt folk Israel, och du vandrar i Jerobeams väg, och kommer mitt folk Israel till att synda, så att du mig förtörnar genom deras synder;
“Ine ndinakukuza kuchokera pa fumbi ndipo ndinakupanga kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli, koma iwe wakhala ukuyenda mʼnjira za Yeroboamu ndi kuchimwitsa anthu anga Aisraeli naputa mkwiyo wanga chifukwa cha machimo awo.
3 Si, så vill jag borttaga Baesa efterkommande, och hans hus efterkommande, och vill sätta ditt hus såsom Jerobeams hus, Nebats sons.
Taonani, Ine ndatsala pangʼono kuwononga Baasa pamodzi ndi nyumba yake, ndipo ndidzachitira nyumba yake zimene ndinachita pa nyumba ya Yeroboamu mwana wa Nebati.
4 Den af Baesa dör i staden, honom skola hundar uppäta; och den af honom dör på markene, honom skola himmelens foglar uppäta.
Agalu adzadya aliyense wa banja la Baasa amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame za mu mlengalenga zidzadya iwo amene adzafere kuthengo.”
5 Hvad nu mer om Baesa sägandes är, och hvad han gjort hafver, och hans magt, si, det är skrifvet uti Israels Konungars Chrönico.
Tsono ntchito zina za Baasa ndi zamphamvu zake zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
6 Och Baesa afsomnade med sina fäder, och vardt begrafven i Thirza; och hans son Ela vardt Konung i hans stad.
Baasa anamwalira nayikidwa mʼmanda amene anayikidwa makolo ake ku Tiriza. Ndipo Ela mwana wake anakhala mfumu mʼmalo mwake.
7 Och Herrans ord kom genom Propheten Jehu, Hanani son, öfver Baesa, och öfver hans hus, och emot allt det onda, som han för Herranom gjort hade, till att förtörna honom genom sina händers verk, att det skulle varda såsom Jerobeams hus, och derföre, att han denna slagit hade.
Komatu Yehova anayankhula kwa Baasa pamodzi ndi banja lake lonse kudzera mwa mneneri Yehu mwana wa Hanani, chifukwa cha zoyipa zonse zimene iye anachita pamaso pa Yehova, kukwiyitsa Yehovayo nakhala ngati nyumba ya Yeroboamu ndiponso chifukwa anawonongeratu banja la Yeroboamu.
8 Uti sjette och tjugonde årena Asa, Juda Konungs, vardt Ela, Baesa son, Konung öfver Israel i Thirza, i tu år.
Mʼchaka cha 26 cha ufumu wa Asa mfumu ya Yuda, Ela mwana wa Baasa anakhala mfumu ya Israeli, ndipo analamulira ku Tiriza zaka ziwiri.
9 Men hans tjenare Simri, en öfverste öfver hälften af vagnarna, gjorde ett förbund emot honom; men han var i Thirza, drack och var drucken i Arza hus, fogdans i Thirza.
Zimuri, mmodzi mwa akuluakulu ake, amene ankalamulira theka la magaleta ake, anamuchitira chiwembu. Nthawi imeneyi Ela anali ku Tiriza, akumwa koledzera nako mʼnyumba ya Ariza, munthu amene ankayangʼanira nyumba yaufumu ku Tiriza.
10 Och Simri kom derin, och slog honom ihjäl, uti sjunde och tjugonde årena Asa, Juda Konungs; och blef Konung i hans stad.
Zimuri anadzalowa, namukantha ndi kumupha mʼchaka cha 27 cha Asa mfumu ya Yuda. Ndipo Zimuriyo anakhala mfumu mʼmalo mwake.
11 Och då han var Konung, och satt på sin stol, slog han hela Baesa hus, och lät intet qvart blifva, icke den som på väggena pissar; dertill hans fränder och vänner.
Zimuri atangoyamba kulamulira, anapha banja lonse la Baasa. Sanasiyepo munthu wamwamuna ndi mmodzi yemwe, wachibale kapena bwenzi lake.
12 Alltså förgjorde Simri hela Baesa hus, efter Herrans ord, som han om Baesa talat hade, genom den Propheten Jehu;
Choncho Zimuri anawononga banja lonse la Baasa, molingana ndi mawu amene Yehova anayankhula motsutsa Baasa kudzera mwa mneneri Yehu,
13 För alla Baesa och hans sons Ela synders skull, som de gjort hade, och kommo Israel till att synda, och förtörnade Herran Israels Gud i deras afguderi.
chifukwa cha machimo onse amene Baasa ndi mwana wake Ela anachita nachimwitsa Israeli, anakwiyitsa Yehova, Mulungu wa Israeli ndi mafano awo osapindulitsa.
14 Hvad nu mer af Ela sägandes är, och allt det han gjorde, si, det är skrifvet uti Israels Konungars Chrönico.
Tsono ntchito zina za Ela ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
15 Uti sjunde och tjugonde årena Asa, Juda Konungs, vardt Simri Konung i sju dagar i Thirza; ty folket låg för Gibbethon de Philisteers.
Mʼchaka cha 27 cha Asa mfumu ya Yuda, Zimuri analamulira ku Tiriza masiku asanu ndi awiri. Gulu la ankhondo linali litamanga misasa pafupi ndi Gibetoni, mzinda wa Afilisti.
16 Då nu folket i lägret hörde sägas, att Simri hade gjort ett förbund, och slagit Konungen ihjäl, gjorde hele Israel på samma dagen Amri, härhöfvitsmannen, till Konung öfver Israel i lägrena.
Ankhondo amene anali ku misasa atamva kuti Zimuri wachita chiwembu ndi kupha mfumu, tsiku lomwelo ku misasako anasankha Omuri, mkulu wa ankhondo kukhala mfumu ya Israeli.
17 Och Amri drog upp, och hele Israel med honom, ifrå Gibbethon, och belade Thirza.
Tsono Omuri ndi Aisraeli onse amene anali naye anachoka ku Gibetoni ndi kukazinga Mzinda wa Tiriza.
18 Då nu Simri såg, att staden skulle varda vunnen, gick han uti palatset i Konungshusena, och brände sig upp med Konungshusena, och blef död;
Zimuri ataona kuti mzinda walandidwa, anathawira ku nsanja ya nyumba ya mfumu ndipo anatentha nyumbayo iye ali momwemo. Kotero iyeyo anafa,
19 För sina synders skull, som han gjort hade, så att han hade gjort det ondt var för Herranom, och vandrade uti Jerobeams väg, och i hans synd, som han gjorde, och kom Israel till att synda.
chifukwa cha machimo amene iye anachita, kuchita zoyipa pamaso pa Yehova ndi kuyenda mʼnjira za Yeroboamu, nachimwitsa nazo Aisraeli.
20 Hvad nu mer af Simri sägandes är, och huru han gjorde ett förbund, si, det är skrifvet i Israels Konungars Chrönico.
Tsono ntchito zina za Zimuri ndi chiwembu chake chimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
21 På den tiden söndrade sig folket Israel i två delar: en hälften höll sig intill Thibni, Ginaths son, och gjorde honom till Konung; den andra hälften höll sig intill Amri.
Pambuyo pake Aisraeli anagawikana pakati: theka linatsatira Tibini mwana wa Ginati kuti limulonge ufumu, ndipo theka lina linatsatira Omuri.
22 Men det folk, som höll sig intill Amri, vardt starkare än det folk, som höll sig intill Thibni, Ginaths son. Och Thibni blef död, och så blef Amri Konung.
Koma anthu otsatira Omuri anali amphamvu kupambana amene ankatsatira Tibini mwana wa Ginati. Choncho Tibini anafa ndipo Omuri anakhala mfumu.
23 Uti första och tretionde årena Asa, Juda Konungs, vardt Amri Konung öfver Israel i tolf år; och regerade i Thirza i sex år.
Mʼchaka cha 31 cha Asa mfumu ya Yuda, Omuri anakhala mfumu ya Israeli, ndipo analamulira zaka 12 ndi miyezi isanu ndi umodzi ku Tiriza.
24 Han köpte Samarie berg af Semer, för två centener silfver; och byggde uppå bergena, och kallade staden, som han byggde, efter Semers namn, som herre var på Samarie berg.
Iye anagula phiri la Samariya kwa Semeri pa mtengo wa ndalama 6,000 za siliva ndipo pa phiripo anamangapo mzinda, nawutcha Samariya, potsata dzina la Semeri, dzina la mwini wakale wa phirilo.
25 Och Amri gjorde det ondt var för Herranom, och var argare än alla de för honom varit hade;
Koma Omuri anachita zoyipa pamaso pa Yehova ndipo anachimwa kuposa mafumu ena onse amene analipo iye asanakhale mfumu.
26 Och vandrade i alla Jerobeams vägar, Nebats sons, och i hans synder, dermed han kom Israel till att synda, så att de förtörnade Herran Israels Gud uti deras afguderi.
Pakuti iye anayenda mʼnjira zonse za Yeroboamu mwana wa Nebati, ndipo tchimo lake anachimwitsa nalo Aisraeli, nakwiyitsa Yehova Mulungu wa Israeli ndi mafano awo opandapake.
27 Hvad nu mer af Amri sägandes är, och allt det han gjort hafver, och om hans magt som han bedref, si, det är skrifvet uti Israels Konungars Chrönico.
Tsono ntchito zina za Omuri ndi zamphamvu zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
28 Och Amri afsomnade med sina fäder, och vardt begrafven i Samarien; och Achab hans son vardt Konung i hans stad.
Choncho Omuri anamwalira nayikidwa mʼmanda amene anayikidwa makolo ake ku Samariya. Ndipo Ahabu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
29 Uti åttonde och tretionde årena Asa, Juda Konungs, vardt Achab, Amri son, Konung öfver Israel; och regerade öfver Israel i Samarien tu och tjugu år;
Mʼchaka cha 38 cha ufumu wa Asa, mfumu ya Yuda, Ahabu mwana wa Omuri anakhala mfumu ya Israeli nalamulira Israeli ku Samariya zaka 22.
30 Och gjorde det ondt var för Herranom, öfver alla dem som för honom varit hade.
Ahabu mwana wa Omuri anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova kupambana mafumu onse akale.
31 Och var honom icke nog, att han vandrade i Jerobeams, Nebats sons, synder; utan tog dertill Isebel, EthBaals dotter, Konungens i Zidon, till hustru, och gick bort, och tjente Baal, och tillbad honom;
Iye sanachiyese ngati chinthu chochepa chabe kuchita machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, koma anakwatiranso Yezebeli, mwana wa Etibaala mfumu ya Asidoni, nayamba kutumikira Baala ndi kumupembedza.
32 Och uppsatte Baal ett altare uti Baals hus, det han honom byggde i Samarien;
Iye anapangira Baala guwa lansembe mʼnyumba ya Baala imene anamanga ku Samariya.
33 Och gjorde en lund; så att Achab mer gjorde till att förtörna Herran Israels Gud, än alle Israels Konungar, som för honom varit hade.
Ahabu anapanganso fano la Asera ndi kukwiyitsa kwambiri Yehova Mulungu wa Israeli, kupambana mafumu onse a Israeli amene analipo iye asanakhale mfumu.
34 På samma tid byggde Hiel af BethEl Jericho. Det kostade honom hans första son Abiram, då han grundvalen lade; och hans yngsta son Segub, då han satte portarna derföre, efter Herrans ord, som han sagt hade genom Josua, Nuns son.
Pa nthawi ya Ahabu, Hiyeli wa ku Beteli anamanganso mzinda wa Yeriko. Pa nthawi yomanga maziko ake, mwana wake woyamba wa mwamuna, Abiramu anamwalira, ndipo pa nthawi yomanga zipata zake, mwana wa mngʼono wa mwamuna Segubu, anamwaliranso. Izi zinachitika monga momwe Yehova ananenera kudzera mwa Yoswa mwana wa Nuni.