< 1 Kungaboken 1 >

1 Och då Konung David var gammal, och väl till ålders kommen, kunde han icke varda varm, ändå man höljde honom med kläder.
Mfumu Davide atakalamba sankamva kufunda ngakhale akamufunditsa mabulangeti.
2 Då sade hans tjenare till honom: Låt dem söka minom herra Konungenom en pigo, en jungfru som står för Konungenom, och sköter honom, och sofver i hans famn, och värmer min herra Konungen.
Choncho nduna zake zinamuwuza kuti, “Tiloleni tifune namwali woti azikhala nanu ndi kumakusamalirani. Namwaliyo azigona pafupi nanu kuti mbuye wathu mfumu muzimva kufundira.”
3 Och de sökte upp en dägelig pigo i alla Israels gränsor, och funno Abisag af Sunem, och hade henne till Konungen.
Kotero anafunafuna mʼdziko lonse la Israeli mtsikana wokongola ndipo anapeza Abisagi wa ku Sunemu, nabwera naye kwa mfumu.
4 Och hon var en ganska dägelig piga, och hon skötte Konungen, och tjente honom; men Konungen kände henne intet.
Mtsikanayo anali wokongola kwambiri ndipo ankasamalira mfumu ndi kumayitumikira, koma mfumuyo sinakhale naye malo amodzi.
5 Men Adonia, Haggiths son, hof sig upp, och sade: Jag vill vara Konung; och gjorde sig vagnar och resenärar, och femtio män till drabanter för sig.
Nthawi imeneyi Adoniya, mwana wa Hagiti, anayamba kudzitukumula ndipo anati, “Ndidzakhala mfumu ndine.” Choncho anadzikonzera galeta ndi akavalo, pamodzi ndi anthu 50 woti azithamanga patsogolo pake.
6 Och hans fader bekymrade honom intet i sinom tid, så att han sade: Hvi gör du så? Och han var ock en dägelig man; och han hade födt honom näst efter Absalom.
(Abambo ake sanalowererepo nʼkamodzi komwe ndipo sanafunsepo kuti, “Nʼchifukwa chiyani ukuchita zimenezi?” Adoniyayo anali wokongola kwambiri ndipo anali wopondana ndi Abisalomu).
7 Och han hade sitt råd med Joab, ZeruJa son, och med AbJathar Presten; de hulpo Adonia.
Adoniya anagwirizana ndi Yowabu mwana wa Zeruya ndiponso Abiatara wansembe, ndipo iwowa anamuthandiza.
8 Men Presten Zadok, och Benaja, Jojada son, och Nathan Propheten, och Simei, och Rei, och de Davids hjeltar, voro icke med Adonia.
Koma Zadoki wansembe, Benaya mwana wa Yehoyada, mneneri Natani, Simei ndi Rei ndiponso asilikali amphamvu a Davide sanamutsate Adoniya uja.
9 Och då Adonia offrade får, och oxar, och gödd boskap, vid den stenen Soheleth, som låg vid den brunnen Rogel, böd han alla sina bröder Konungens söner, och alla Juda män Konungens tjenare;
Kenaka Adoniya anapereka nsembe za nkhosa ndi ngʼombe ndiponso ana angʼombe onenepa ku Mwala wa Zohereti kufupi ndi Eni Rogeli. Iye anayitana abale ake onse, ana aamuna a mfumu ndiponso akuluakulu onse a ku Yuda,
10 Men den Propheten Nathan, och Benaja, och de hjeltar, och Salomo, sin broder, böd han intet.
koma sanayitane mneneri Natani kapena Benaya kapenanso asilikali amphamvu a Davide ngakhalenso mʼbale wake Solomoni.
11 Då sade Nathan till BathSeba, Salomos moder: Hafver du icke hört, att Adonia, Haggiths son, är Konung vorden, och vår herre David vet intet deraf?
Pamenepo Natani anafunsa Batiseba, amayi ake a Solomoni, kuti, “Kodi simunamve kuti Adoniya, mwana wa Hagiti, walowa ufumu popanda Davide mbuye wathu kudziwa?
12 Så kom nu, jag vill gifva dig ett råd, att du må undsätta dina och dins sons Salomos själ.
Tsopano ine ndikulangizeni inu mmene mungapulumutsire moyo wanu ndi moyo wa mwana wanu Solomoni.
13 Bort, och gack in till Konungen David, och säg till honom: Hafver du icke, min herre Konung, svorit, och sagt dina tjenarinno: Din son Salomo skall vara Konung efter mig, och han skall sitta på minom stol; hvi är då Adonia Konung vorden?
Pitani msanga kwa Mfumu Davide ndipo mukanene kuti, ‘Mbuye wanga mfumu, kodi simunalumbire kwa ine mdzakazi wanu kuti, ‘Ndithu mwana wako Solomoni ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwanga, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu?’ Nanga nʼchifukwa chiyani Adoniya walowa ufumu?’
14 Si, medan du ännu der är, och talar med Konungenom, vill jag komma in efter dig, och fullkomna ditt tal.
Pamene inu muzikayankhula ndi mfumu, ine ndidzalowa ndi kuchitira umboni mawu anuwo.”
15 Och BathSeba gick in till Konungen i kammaren; och Konungen var ganska gammal; och Abisag af Sunem tjente Konungenom.
Choncho Batiseba anapita nakalowa ku chipinda kukaonana ndi mfumu imene inali itakalamba kwambiri, kumene Abisagi wa ku Sunemu uja ankayisamalira.
16 Och BathSeba böjde sig, och tillbad Konungen. Konungen sade: Hvad vill du?
Batiseba anagwada nalambira mfumu. Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi nʼchiyani chimene ukufuna?”
17 Hon sade till honom: Min Herre, du hafver svorit dine tjenarinno vid Herran din Gud: Din son Salomo skall vara Konung efter mig, och sitta på minom stol.
Iye anayankha kuti, “Mbuye wanga, inu mwini munalumbira kwa ine mdzakazi wanu mʼdzina la Yehova Mulungu wanu kuti, ‘Solomoni mwana wako ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwa ine, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.’
18 Men nu, si, Adonia är Konung vorden; och min herre Konungen vet intet deraf.
Koma tsopano Adoniya ndiye walowa ufumu, ndipo inu mbuye wanga mfumu, simukuzidziwa zimenezi.
19 Han hafver offrat oxar, och gödd boskap, och mång får, och hafver budit alla Konungens söner; dertill AbJathar Presten, och Joab härhöfvitsmannen; men din tjenare Salomo hafver han intet budit.
Ndipo wapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndi nkhosa ndi mbuzi ndipo wayitana ana anu onse, wansembe Abiatara ndiponso Yowabu mkulu wa ankhondo, koma sanayitane kapolo wanu Solomoni.
20 Men du äst min herre Konung; hela Israels ögon se på dig, att du skall gifva dem före, ho som skall sitta på mins herras Konungens stol efter honom.
Mbuye wanga mfumu, maso a Aisraeli onse ali pa inu, kuti adziwe kuchokera kwa inu amene adzakhala pa mpando waufumu wa mbuye wanga mʼmalo mwanu.
21 När nu min herre Konungen med sina fader afsomnad är, så måste jag och min son Salomo syndare vara.
Mukapanda kutero, mbuye wanga, mukadzangotisiya nʼkulondola kumene kunapita makolo anu, ine pamodzi ndi mwana wangayu Solomoni adzatiyesa owukira.”
22 Medan hon ännu talade med Konungenom, kom Propheten Nathan.
Pamene Batiseba amayankhula ndi mfumu, mneneri Natani analowa.
23 Och de sade Konungenom till: Si, Propheten Nathan är der. Och som han kom in för Konungen, tillbad han Konungen på sitt ansigte neder till jordena;
Ndipo anthu anawuza mfumu kuti, “Kwabwera mneneri Natani.” Kotero iye anafika pamaso pa mfumu ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi.
24 Och sade: Min herre Konung, hafver du sagt: Adonia skall vara Konung efter mig, och sitta på minom stol?
Natani anafunsa kuti, “Mbuye wanga mfumu, kodi mwalengeza kuti Adoniya adzakhala mfumu mʼmalo mwanu, ndi kuti adzakhala pa mpando wanu waufumu?
25 Ty han är i dag nedergången, och hafver offrat oxar, och gödd boskap, och mång får, och hafver budit alla Konungens söner, och höfvitsmännerna, dertill Presten AbJathar; och si, de äta och dricka för honom, och säga: Lycka ske Konungenom Adonia!
Lero lomwe lino wakapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndiponso nkhosa ndi mbuzi. Iye wayitana ana anu onse, atsogoleri a nkhondo, ndiponso wansembe Abiatara. Panopa onsewa akudya ndi kumwa naye ndipo akunena kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Adoniya!’
26 Men mig din tjenare, och Zadok Presten, och Benaja, Jojada son, och din tjenare Salomo, hafver han intet budit.
Koma ine kapolo wanu, wansembe Zadoki ndi Benaya mwana wa Yehoyada, ndiponso kapolo wanu Solomoni sanatiyitane.
27 Är det så af minom herra Konungenom befaldt, och du hafver det din tjenare icke veta låtit, hvilken uppå mins herras Konungens stol efter honom sitta skall?
Kodi zimenezi mbuye wanga mfumu mwazichita ndinu, osawawuza atumiki anu kuti adziwe amene adzakhale pa mpando waufumu mʼmalo mwanu?”
28 Konung David svarade, och sade: Kaller mig BathSeba. Och hon kom in för Konungen; och då hon stod för Konungenom,
Pamenepo mfumu Davide anati, “Muyitaneni Batiseba.” Kotero Batiseba analowa ndipo anayimirira pamaso pa mfumu.
29 Svor Konungen, och sade: Så sant som Herren lefver, som min själ förlossat hafver utur alla nöd;
Tsono mfumu inalumbira kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene anandipulumutsa ine ku mavuto onse,
30 Jag vill i dag göra, såsom jag dig vid Herran Israels Gud svorit hafver, och sagt: Salomo din son skall vara Konung efter mig, och han skall sitta på minom stol för mig.
ndithu ine lero ndichita zonse zimene ndinalumbira kwa Yehova Mulungu wa Israeli kuti, mwana wako Solomoni adzakhala mfumu mʼmalo mwanga ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.”
31 Då böjde sig BathSeba med sitt anlete neder till jordena, och tillbad Konungen, och sade: Lycka minom herra Konung David i evig tid.
Pamenepo Batiseba anawerama, nagunditsa mutu wake pansi nalambira mfumu, ndipo anati, “Mbuye wanga Mfumu Davide mukhale ndi moyo wautali!”
32 Och Konung David sade: Kaller mig Presten Zadok, och Propheten Nathan, och Benaja, Jojada son. Och då de kommo in för Konungen,
Mfumu Davide anati, “Ndiyitanireni wansembe Zadoki, mneneri Natani ndi Benaya mwana wa Yehoyada.” Atafika pamaso pa mfumu,
33 Sade Konungen till dem: Tager med eder edars herras tjenare, och sätter min son Salomo uppå mina mulo, och förer honom ned till Gihon;
mfumuyo inati kwa iwo, “Tengani atumiki anga ndipo mukweze mwana wanga Solomoni pa bulu wanga ndipo mupite naye ku Gihoni. Mukalize lipenga ndi kufuwula kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Solomoni!’
34 Och Presten Zadok, samt med Propheten Nathan, smörje honom der till Konung öfver Israel; och blåser med basuner, och säger: Lycka ske Konung Salomo!
Kumeneko Zadoki wansembe ndi mneneri Natani akamudzoze kuti akhale mfumu ya Israeli. Kenaka mukalize lipenga ndi kumanena kuti ‘Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni.’
35 Och drager med honom upp, och kommer, så skall han sitta på minom stol, och vara Konung för mig; och jag vill bjuda honom, att han skall vara en Förste öfver Israel och Juda.
Ndipo pobwera muzikamutsata pambuyo. Iyeyo akabwere kuno ndi kudzakhala pa mpando wanga waufumu ndi kudzalamulira mʼmalo mwanga. Ndamusankha kukhala wolamulira Israeli ndi Yuda.”
36 Då svarade Benaja, Jojada son, Konungenom, och sade: Amen; det säge också Herren, mins herras Konungens Gud.
Benaya mwana wa Yehoyada anayankha mfumu kuti, “Ameni! Yehova Mulungu wa mbuye wanga mfumu akhazikitse kuti zichitike motero.
37 Såsom Herren hafver varit med min herra Konungenom, så vare han ock med Salomo, att hans stol må större varda än mins herras Konung Davids stol.
Monga momwe Yehova wakhalira ndi inu mbuye wanga mfumu, momwemonso akhale ndi Solomoni ndi kukhazikitsa ufumu wake kuti ukhale waukulu kuposa ufumu wa mbuye wanga Mfumu Davide!”
38 Då gingo Presten Zadok och Propheten Nathan, och Benaja, Jojada son, och Crethi och Plethi, neder, och satte Salomo på Konung Davids mulo, och förde honom till Gihon.
Kotero Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndiponso Apeleti, anthu oteteza mfumu, anapita kukamukweza Solomoni pa bulu wa Mfumu Davide ndi kupita naye ku Gihoni.
39 Och Presten Zadok tog oljohornet utu tabernaklet, och smorde Salomo; och de blåste med basuner, och allt folket sade: Lycka ske Konung Salomo!
Wansembe Zadoki anatenga nyanga ya mafuta yochokera ku malo opatulika ndi kumudzoza Solomoni. Kenaka analiza lipenga ndipo anthu onse anafuwula kuti, “Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni!”
40 Och allt folket drog upp efter honom, och folket pipade med pipor, och var ganska gladt, så att det skall i markene utaf deras skri.
Ndipo anthu onsewo anapita namutsatira pambuyo akuyimba zitoliro ndi kukondwerera kwambiri, kotero nthaka inagwedezeka chifukwa cha phokoso lawo.
41 Och Adonia hörde det, och alle de budne som med honom voro, och de hade allaredo ätit; och då Joab hörde basunens ljud, sade han: Hvart vill det skriet och bullret i stadenom?
Adoniya pamodzi ndi anthu onse oyitanidwa amene anali naye anamva zimenezi pamene ankamaliza madyerero awo. Atamva kulira kwa malipenga, Yowabu anafunsa kuti, “Kodi phokoso lonselo mu mzindamo likutanthauza chiyani?”
42 Som han ännu talade, si, då kom Jonathan, AbJathars Prestens son; och Adonia sade: Kom härin; ty du äst en dugelig man, och bär god tidende.
Iye akuyankhula, Yonatani mwana wa wansembe Abiatara anafika. Adoniya anati, “Lowa. Munthu wabwino ngati iwe ayenera kubweretsa nkhani yabwino.”
43 Jonathan svarade, och sade till Adonia: Ja, vår herre Konung David hafver gjort Salomo till Konung;
Yonatani anayankha Adoniya kuti, “Ayi ndithu, zinthu sizili bwino! Mbuye wathu Mfumu Davide walonga Solomoni ufumu.
44 Och hafver sändt med honom Presten Zadok, och Propheten Nathan, och Benaja, Jojada son, och Crethi och Plethi; och de hafva satt honom på Konungens mulo.
Mfumu yatuma Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndi Apeleti ku Gihoni ndipo iwo amukweza pa bulu wa mfumu,
45 Och Presten Zadok, med Propheten Nathan hafver smort honom till Konung i Gihon; och de äro uppdragne dädan med fröjd, så att staden sorlar; det är det skri, som I hört hafven.
ndipo Zadoki wansembe ndi mneneri Natani adzoza Solomoni ku Gihoni kuti akhale mfumu. Ndipo kuchokera kumeneko akhala akululutira, kotero kuti mu mzinda monse muli phokoso lokhalokha. Ndiyetu phokoso limene mukulimvalo.
46 Dertill sitter Salomo på Konungastolen.
Ndipo Solomoni wakhala kale pa mpando wake waufumu.
47 Och Konungens tjenare hafva ingångit till att välsigna vår herra Konung David, och hafva sagt: Din Gud göre Salomo ett bättre namn än ditt namn är, och göre hans stol större än din stol; och Konungen hafver tillbedit, der han låg på sängene.
Kuwonjezera pamenepo, nduna za mfumu zabwera kale kudzayamika mbuye wathu Mfumu Davide, pomanena kuti, ‘Mulungu wanu atchukitse dzina la Solomoni kuposa dzina lanu ndipo ufumu wake ukule kupambana ufumu wanu!’ Ndipo mfumu inawerama niyamba kupembedza pa bedi lake,
48 Och Konungen hafver så sagt: Lofvad vare Herren Israels Gud, som i dag hafver låtit en sitta på minom stol, så att min ögon det sett hafva.
inati, ‘Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, amene wasankha wolowa mʼmalo mwanga ine ndikanali ndi moyo lero lino.’”
49 Då vordo förskräckte och stodo upp alle de som när Adonia budne vore, och gingo bort, hvar och en sin väg.
Anthu onse amene Adoniya anawayitana ananjenjemera ndi mantha, ndipo anayimirira, kenaka anamwazikana.
50 Men Adonia fruktade sig för Salomo, och stod upp, och gick bort, och fattade hornen af altaret.
Koma Adoniya, poopa Solomoni, anapita ku Nyumba ya Mulungu nakagwira msonga za guwa lansembe.
51 Och Salomo vardt sagdt: Si, Adonia fruktar för Konung Salomo; och si, han fattar altarets horn, och säger: Konung Salomo svärje mig i dag, att han icke dräper sin tjenare med svärd.
Tsono Solomoni anawuzidwa kuti, “Adoniya akukuopani inu Mfumu Solomoni ndipo wagwira msonga za guwa lansembe. Iye akuti, ‘Mfumu Solomoni alumbire kuti sadzapha kapolo wake ndi lupanga.’”
52 Salomo sade: Vill han vara redelig, så skall icke ett hår af honom falla på jordena; men varder något ondt befunnet med honom, så skall han dö.
Solomoni anayankha kuti, “Ngati iyeyo aonetse kuti ndi munthu wakhalidwe labwino, ngakhale tsitsi la mʼmutu mwake silidzathothoka ndi kugwera pansi, koma akapezeka kuti ali ndi khalidwe loyipa, adzafa ndithu.”
53 Och Konung Salomo sände bort, och lät hemta honom neder ifrån altaret; och då han kom, tillbad han Konung Salomo; men Salomo sade till honom: Gack i ditt hus.
Pamenepo Mfumu Solomoni inatuma anthu ndipo anakamutenga paguwa paja. Adoniya anabwera ndi kudzalambira Mfumu Solomoni, ndipo Solomoni anati, “Pita ku nyumba yako.”

< 1 Kungaboken 1 >