< 1 Krönikeboken 5 >

1 Rubens barn, första Israels sons, ty han var förste sonen; men derföre, att han sins fäders säng besmittade, vardt hans förstfödslorätt gifven Josephs barnom, Israels sons; och han vardt icke räknad till förstfödslona.
Ana a Rubeni mwana woyamba wa Israeli (iye anali woyamba kubadwa, koma atagona ndi mkazi wamngʼono wa abambo ake, ulemu wake wokhala mwana woyamba unaperekedwa kwa ana a Yosefe. Kotero iye sanalembedwe pa mndandanda wa mayina ngati mwana woyamba kubadwa,
2 Ty Juda, som mägtig var ibland sina bröder, honom vardt Förstadömet för honom gifvet, och Joseph förstfödslorätten.
ndipo ngakhalenso Yuda anali wamphamvu kwambiri pakati pa abale ake, ndi kuti wolamulira anachokera mwa iye, ulemu wa mwana woyamba kubadwa unaperekedwa kwa Yosefe)
3 Så äro nu Rubens, första Israels sons, barn: Hanoch, Pallu, Hezron och Charmi.
ana a Rubeni mwana woyamba wa Israeli ndi awa: Hanoki, Palu, Hezironi, ndi Karimi.
4 Joels barn voro: Semaja. Hans son var Gog. Hans son var Simei.
Ana a Yoweli anali awa: Semaya, Gogi, Simei,
5 Hans son var Micha. Hans son var Reaja. Hans son var Baal.
Mika, Reaya, Baala,
6 Hans son var Beera, hvilken ThiglathPilneser, Konungen i Assyrien, bortförde fången; han är en Förste ibland de Rubeniter.
ndiponso Beeri, amene Tigilati-Pileseri mfumu ya Asuri anamugwira ukapolo. Mtsogoleri wa fuko la Rubeni anali Beeri.
7 Men hans bröder i deras ätter, då de i deras börd räknade vordo, hade Jegiel och Zacharia för höfvitsmän.
Abale awo mwa mabanja awo, potsata mndandanda wa mʼbado wawo, ndi awa: Yeiyeli, mtsogoleri, Zekariya,
8 Och Bela, Asas son, Serna sons, Joels sons, han bodde i Aroer, och intill Nebo och BaalMeon;
ndiponso Bela mwana wa Azazi, mwana wa Sema, mwana wa Yoweli. Iwo ankakhala ku Aroeri mpaka ku Nebo ndi Baala-Meoni.
9 Och bodde emot öster intill man kommer till öknena vid den älfvena Phrath; förty deras boskap var mycken i Gileads land.
Iwo anakhala cha kummawa mpaka kukafika polowera mʼchipululu cha mbali ina ya Mtsinje wa Yufurate, chifukwa ziweto zawo zinaswana kwambiri mʼdziko la Giliyadi.
10 Och i Sauls tid förde de örlig emot de Hagariter, så att de föllo genom desses hand, och bodde i deras hyddor, in mot alla den östra ängden Gilead.
Pa nthawi ya Sauli anachita nkhondo ndi Ahagiri ndi kuwagonjetsa. Tsono iwo anakhala mʼmatenti a Ahagiri ku dera lonse la kummawa kwa Giliyadi.
11 Gads barn bodde tvärtöfver ifrå dem, uti de landena Basan, allt intill Salcha:
Anthu a fuko la Gadi anakhala moyandikana ndi fuko la Rubeni ku Basani mpaka ku Saleka:
12 Joel den främste, Sapham den andre, Jaenai och Saphat i Basan.
Mtsogoleri wawo ku Basani anali Yoweli, wachiwiri anali Safamu, kenaka Yanayi ndi Safati.
13 Och deras bröder i deras fäders hus voro: Michael, Mesullam, Seba, Jorai, Jaecan, Sia och Eber, de sju.
Abale awo mwa mabanja awo anali awa: Mikayeli, Mesulamu, Seba, Yorayi, Yakani, Ziya ndi Eberi, onse ali asanu ndi awiri.
14 Desse äro Abihails barn, Huri sons, Jaroahs sons, Gileads sons, Michaels sons, Jesisai sons, Jahdo sons, Bus sons.
Amenewa ndiwo anali ana a Abihaili, mwana wa Huri, mwana wa Yarowa, mwana wa Giliyadi, mwana wa Mikayeli, mwana wa Yesisayi, mwana wa Yahido, mwana wa Buzi.
15 Ahi, Abdiels son, Guni sons, var en öfverste uti deras fäders hus;
Ahi mwana wa Abdieli, mwana wa Guni, anali mtsogoleri wa banja la makolo awo.
16 Och bodde uti Gilead i Basan, och i dess döttrar, och i alla Sarons förstäder, allt intill dess ändar.
Fuko la Gadi linakhala ku Giliyadi, ku Basani ndi midzi yozugulira, madera onse a msipu a ku Saroni mpaka kumene amalekezera.
17 Desse vordo alle räknade i Jothams, Juda Konungs, och Jerobeams, Israels Konungs tid.
Mayina onsewa analembedwa potsata mndandanda wa mibado yawo pa nthawi ya ulamuliro wa Yotamu mfumu ya Yuda ndi Yeroboamu mfumu ya Israeli.
18 Rubens barn, de Gaditers, och de halfva slägtenes Manasse, voro stridsamme män, som sköld och svärd föra och båga spänna kunde, och förfarne till att strida; de voro fyra och fyratio tusend, och sjuhundrad och sextio, som i här drogo.
Mafuko a Rubeni, Gadi ndi theka la Manase, anali ndi anthu 44, 760 okonzeka kulowa usilikali; anthu amatupi amphamvu, amene amatha kugwiritsa ntchito chishango ndi lupanga, amene amatha kugwiritsa ntchito uta, amene anaphunzitsidwa kumenya nkhondo.
19 Och då de stridde med de Hagariter, hulpo dem Jetur, Naphis och Nodab;
Iwo anachita nkhondo ndi Ahagiri, Yeturi, Nafisi ndi Nodabu.
20 Och gåfvo de Hagariter i deras händer, och allt det som med dem var; förty de ropade till Gud i stridene, och han bönhörde dem; ty de trodde till honom.
Iwowo anathandizidwa polimbana nawo ndipo Mulungu anapereka Ahagiri mʼmanja mwawo; popeza iwo anafuwulira kwa Mulungu pa nkhondopo. Iye anayankha mapemphero awo chifukwa anamudalira.
21 Och de förde bort deras boskap, femtiotusend camelar, tuhundrad och femtio tusend får, tutusend åsnar, och hundradtusend menniskors själar.
Choncho iwo analanda ziweto za Ahagiri: ngamira 50,000, nkhosa ndi mbuzi 250,000 ndi abulu 2,000. Ndiponso anagwira akapolo 100,000,
22 Och der föllo månge såre; ty striden var af Gudi. Och de bodde i deras stad allt intill den tiden de fångne vordo.
enanso ambiri anaphedwa, chifukwa nkhondoyo inali ya Mulungu. Ndipo iwo anakhala mʼdzikomo mpaka pa nthawi ya ukapolo.
23 De halfva slägtenes Manasse barn bodde i de landena, ifrå Basan allt intill BaalHermon och Senir, och det berget Hermon, och de voro månge.
Theka la fuko la Manase linkakhala ku dziko la kummawa kuyambira ku Basani mpaka ku Baala-Herimoni, kumene ndi ku Seniri (Phiri la Herimoni) ndipo anthuwo anali ochuluka kwambiri.
24 Och desse voro höfvitsmän till deras fäders hus: Epher, Jisei, Eliel, Asriel, Jeremia, Hodavia, Jahdiel; väldige, mägtige män, och namnkunnige höfvitsmän uti deras fäders husom.
Atsogoleri a mabanja awo anali awa: Eferi, Isi, Elieli, Azirieli, Yeremiya, Hodaviya ndi Yahidieli. Iwo anali asilikali olimba mtima, anthu otchuka, ndiponso atsogoleri a mabanja awo.
25 Och då de förtogo sig emot deras fäders Gud, och i horeri gingo efter de folks gudar der i landena, som Gud för dem förgjort hade,
Koma iwo anali osakhulupirika kwa Mulungu wa makolo awo ndipo anadzipereka okha kwa milungu ya anthu okhala mʼdzikomo amene Mulungu anawawononga pamene iwowo ankafika.
26 Uppväckte Israels Gud Phuls anda, Konungens i Assyrien, och ThiglathPilnesers anda, Konungens i Assyrien, och förde bort de Rubeniter, Gaditer och den halfva slägtena Manasse, och lät komma dem till Halah och Hober och Hara, och till den älfvena Gosan, allt intill denna dag.
Kotero Mulungu wa Israeli anayika mkwiyo mwa Puli mfumu ya Asuri (ameneyu ndi Tigilati-Pileseri mfumu ya Asuri) amene anatenga fuko la Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase kupita nawo ku ukapolo. Iye anapita nawo ku Hala, Habori, Hara ndi ku mtsinje wa Gozani, kumene ali mpaka lero lino.

< 1 Krönikeboken 5 >