< 1 Krönikeboken 17 >

1 Det begaf sig, då David bodde i sitt hus, sade han till Propheten Nathan: Si, jag bor uti cedrehus; och Herrans förbunds ark under tapeter.
Davide atakhazikika mʼnyumba yake yaufumu, anawuza mneneri Natani kuti, “Ine pano ndikukhala mʼnyumba yaufumu yomanga ndi mitengo ya mkungudza, pomwe Bokosi la Chipangano la Yehova lili mu tenti.”
2 Nathan sade till David: Allt det i ditt hjerta är, det gör; ty Gud är med dig.
Natani anayankha Davide kuti, “Chitani chilichonse chimene chili mu mtima mwanu, chifukwa Mulungu ali nanu.”
3 Men i samma natt ene kom Guds ord till Nathan, och sade:
Usiku umenewo mawu a Mulungu anafika kwa Natani, ndipo anati,
4 Gack och säg minom tjenare David: Detta säger Herren: Du skall icke bygga mig ett hus till boning.
“Pita kamuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova akunena kuti, sudzandimangira ndiwe nyumba yokhalamo.’
5 Förty jag hafver icke bott uti något hus, ifrå den dag, då jag Israels barn utförde, allt intill denna dagen; utan jag hafver varit der tabernaklet varit hafver, och boningen.
Ine sindinakhalepo mʼnyumba kuyambira tsiku limene ndinatulutsa Israeli mʼdziko la Igupto mpaka lero lino. Ndakhala ndikuyenda kuchoka mʼtenti ina kupita mʼtenti ina, kuchoka malo ena kupita malo ena.
6 Ehvar jag vandrade i hela Israel, hafver jag ock någor tid talat till någon domare i Israel, den jag budit hafver, att föda mitt folk, och sagt: Hvi byggen I icke mig ett cedrehus?
Konse ndakhala ndikuyenda ndi Aisraeli onse, kodi ndinanenapo kwa wina aliyense wa atsogoleri awo amene ndinamulamula kuweta anthu anga kuti, ‘Kodi nʼchifukwa chiyani simunandimangire nyumba ya mitengo ya mkungudza?’”
7 Så säg nu alltså till min tjenare David: Detta säger Herren Zebaoth: Jag hafver tagit dig utaf markene, der du följde fåren, att du skulle vara en Förste öfver mitt folk Israel;
Ndipo tsopano umuwuze mtumiki wanga Davide kuti, “Yehova Wamphamvuzonse akuti, Ine ndinakutenga ku busa ukuweta nkhosa, kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga, Aisraeli.
8 Och hafver varit med dig, ehvart du for, och hafver utrotat dina fiendar för dig; och hafver gjort dig ett namn, såsom de store på jordene namn hafva.
Ineyo ndinali nawe kulikonse kumene unkapita, ndipo ndachotsa adani ako onse pamaso pako. Tsopano ndidzakuza dzina lako kuti likhale mʼgulu la mayina a anthu otchuka kwambiri pa dziko lapansi.
9 Men jag skall sätta mino folke Israel ett rum, och skall plantera det, så att det skall der bo, och icke mer rördt varda; och arghetens barn skola icke mer qvälja det, såsom tillförene,
Ndipo ndidzawapatsa malo anthu anga, Aisraeli ndipo ndidzawadzala pamalo awoawo kuti asadzavutitsidwenso. Anthu oyipa sadzawazunzanso monga ankachitira poyamba paja;
10 Och på den tiden, då jag böd domarena öfver mitt folk Israel. Och jag skall undertrycka alla dina fiendar; och förkunnar dig, att Herren vill bygga dig ett hus.
monga akhala akuchitira kuchokera nthawi imene ndinasankha atsogoleri a anthu anga Aisraeli. Ine ndidzagonjetsanso adani anu onse. “‘Ine ndikulengeza kwa iwe kuti Yehova adzakhazikitsa banja lako.
11 När nu dine dagar ute äro, att du går till dina fäder, så skall jag uppväcka dina säd efter dig, den en af dina söner vara skall, honom vill jag bereda ett rike.
Masiku ako akadzatha ndipo ukadzatsatira makolo ako, Ine ndidzawutsa mphukira yako imene idzalowa mʼmalo mwako, mmodzi mwa ana ako, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake.
12 Han skall bygga mig ett hus, och jag vill stadfästa hans stol till evig tid.
Iye ndiye amene adzandimangira nyumba, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya.
13 Jag skall vara hans fader, och han skall vara min son; och jag skall icke vända mina barmhertighet ifrå honom, såsom jag vände henne ifrå honom, som för dig var;
Ine ndidzakhala abambo ake, ndipo iye adzakhala mwana wanga. Ine sindidzasiya kumukonda monga ndinachitira ndi amene unalowa mʼmalo mwawo.
14 Utan jag skall sätta honom i mitt hus, och uti mitt rike evinnerliga, så att hans stol skall blifva beständig i evig tid.
Ndidzamuyika kukhala wolamulira nyumba yanga ndi ufumu wanga kwamuyaya. Mpando wake waufumu udzakhazikika kwamuyaya.’”
15 Och då Nathan efter all desso ord och syn talat hade med David,
Natani anafotokozera Davide mawu onse avumbulutso limene analandira.
16 Kom Konung David, och blef inför Herranom, och sade: Ho är jag, Herre Gud? Och hvad är mitt hus, att du hafver låtit mig komma härtill?
Choncho Mfumu Davide analowa mu tenti nakhala pamaso pa Yehova, ndipo anati, “Ine ndine yani, Inu Yehova Mulungu, ndipo banja langa nʼchiyani kuti mundifikitse pamene ndafikapa?
17 Och dig hafver ändå icke tyckt det nog vara, Gud; utan du hafver ock öfver dins tjenares hus ännu talat om tillkommande ting i framtiden, och hafver sett till mig, Herre Gud, ofvanefter, såsom en menniska den andra.
Inu Mulungu, kukhala ngati izi ndi zosakwanira pamaso panu, Inuyo mwayankhula zatsogolo la banja la mtumiki wanu. Mwandiyangʼana ndipo mwandiyesa ngati munthu wolemekezeka kwambiri pakati pa anthu, Inu Yehova Mulungu.”
18 Hvad skall David mer säga till dig, att du skulle ära din tjenare? Du känner din tjenare.
“Kodi Davide anenenso chiyani kwa Inu, pakuti mwachitira ulemu wotere mtumiki wanu? Pakuti Inu mukumudziwa mtumiki wanu.
19 Herre, för din tjenares skull, efter ditt hjerta hafver du all sådana stor ting gjort, att du skulle all storhet kunnoga göra.
Inu Yehova, chifukwa cha mtumiki wanu komanso mwa chifuniro chanu, mwachita chinthu chachikulu ichi ndipo mwawulula malonjezo anu aakulu onse.
20 Herre, ingen är din like, och ingen Gud är utan du, af hvilkom vi med vår öron hört hafve.
“Palibe wina wofanana nanu, Inu Yehova, ndipo palibe Mulungu wina koma Inu nokha monga tamvera ndi makutu athu.
21 Och hvar är något folk på jordene, såsom ditt folk Israel, dit en Gud gången är, till att förlossa sig ett folk, och göra sig sjelfvom ett Namn af stor och förskräckelig ting, till att utdrifva Hedningar för dino folke, som du utur Egypten förlossat hafver?
Ndipo ndi ndani wofanana ndi anthu anu Aisraeli, mtundu wokhawo pa dziko lapansi umene Mulungu wake anapita kukawuwombola, monga anthu akeake ndi kukadzitchukitsa yekha pochita zinthu zodabwitsa zazikulu, pothamangitsa mitundu ina pamaso pa anthu ake, amene Inu munawawombola ku Igupto?
22 Och hafver gjort ditt folk Israel dig till folk evinnerliga, och du, Herre, äst deras Gud vorden.
Inu munawapanga anthu anu Aisraeli kukhala anuanu kwamuyaya, ndipo Inu, Inu Yehova ndinu Mulungu wawo.
23 Nu, Herre, det ord, som du talat hafver öfver din tjenare, och öfver hans hus, varde sant i evig tid, och gör såsom du sagt hafver.
“Ndipo tsopano Yehova, sungani kwamuyaya lonjezo limene mwachita ndi mtumiki wanu ndi banja lake, likhazikitseni kwamuyaya. Chitani monga mwalonjezera,
24 Och ditt Namn varde sant och stort i evig tid, att man säga må: Herren Zebaoth Israels Gud är Gud i Israel; och dins tjenares Davids hus vare beständigt för dig.
kotero dzina lanu likhazikike ndi kukhala lotchuka mpaka muyaya. Ndipo anthu adzanena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa woyangʼanira Israeli, ndi Mulungu wa Israeli!’ Ndipo banja la mtumiki wanu Davide lidzakhazikika pamaso panu.
25 Ty du, min Gud, hafver öppnat din tjenares öra, att du vill bygga honom ett hus; derföre hafver din tjenare funnit, att han inför dig beder.
“Inu Mulungu wanga, mwaululira mtumiki wanu kuti mudzamumangira nyumba. Nʼchifukwa chake ine mtumiki wanu ndalimba mtima kupemphera motere.
26 Nu, Herre, du äst Gud, och du hafver sådana god ting sagt till din tjenare.
Inu Yehova, ndinu Mulungu! Mwalonjeza zinthu zabwinozi kwa mtumiki wanu.
27 Tag nu till att välsigna dins tjenares hus, att det blifver evinnerliga för dig; ty hvad du, Herre, välsignar, det är välsignadt evinnerliga.
Ndipo chakukomerani kudalitsa banja la mtumiki wanu kuti likhale pamaso panu mpaka muyaya. Pakuti Inu Yehova mwalidalitsa, lidzakhala lodalitsika mpaka muyaya.”

< 1 Krönikeboken 17 >