< 1 Krönikeboken 10 >

1 De Philisteer stridde emot Israel, och de af Israel flydde för de Philisteer, och de slagne föllo på Gilboa berg.
Tsono Afilisti anachitanso nkhondo ndi Aisraeli ndipo Aisraeli anathawa Afilistiwo, kotero kuti ambiri anaphedwa pa phiri la Gilibowa.
2 Och de Philisteer gåfvo sig hardt in på Saul och hans söner, och slogo Jonathan, AbiNadab och MalchiSua, Sauls söner.
Afilisti anapanikiza kwambiri Sauli ndi ana ake, ndipo anapha Yonatani, Abinadabu ndi Maliki-Suwa.
3 Och striden vardt skarp emot Saul; och de bågaskyttar kommo inpå honom, så att han blef sår af skyttorna.
Nkhondo inakula kwambiri mozungulira Sauli ndipo pamene anthu amauta anamupeza, anamuvulaza.
4 Då sade Saul till sin vapnedragare: Drag ditt svärd ut, och stick mig igenom dermed, att desse oomskorne icke komma och fara skamliga med mig. Men hans vapnedragare ville icke; ty han fruktade sig svårliga. Då tog Saul sitt svärd, och föll deruppå.
Tsono Sauli anawuza mnyamata wake wonyamula zida zake kuti, “Solola lupanga lako undiphe, kuopa kuti anthu osachita mdulidwewa angabwere ndi kudzandizunza ine.” Koma mnyamata wonyamula zida uja anachita mantha kwambiri ndipo sanathe kutero. Choncho Sauli anatenga lupanga lake lomwe nagwerapo.
5 Som nu hans vapnedragare såg, att Saul var död, föll han ock på svärdet, och blef död.
Mnyamata wonyamula zida zake uja ataona kuti Sauli wafa, nayenso anadzigwetsera pa lupanga lake nafa.
6 Alltså blef Saul död, och hans tre söner, och hans hela hus tillika.
Motero Sauli ndi ana ake atatu anafa, pamodzi ndi banja lake lonse anafera limodzi.
7 Då nu de män af Israel, som i dalenom voro, sågo att de voro flydde, och att Saul och hans söner voro döde, öfvergåfvo de sina städer, och flydde; och de Philisteer kommo, och bodde deruti.
Pamene Aisraeli onse amene anali mʼchigwa anaona kuti gulu lankhondo lathawa komanso kuti Sauli ndi ana ake aphedwa, nawonso anathawa kusiya mizinda yawo. Ndipo Afilisti anabwera kudzakhalamo.
8 Den andra morgonen kommo de Philisteer till att afkläda de slagna, och funno Saul och hans söner liggande på Gilboa berg;
Mmawa mwake, Afilisti atabwera kudzatenga zinthu za anthu ophedwa, anapeza Sauli ndi ana ake atafa pa phiri la Gilibowa.
9 Och klädde honom af, och togo hans hufvud och hans vapen, och sände uti de Philisteers land allt omkring, och läto förkunnat för deras afgudar och folkena;
Iwo anamuvula zovala zake, natenga mutu wake ndi zida zake zankhondo. Ndipo anatumiza amithenga mʼdziko lonse la Afilisti kukafalitsa nkhani yabwinoyi kwa mafano awo ndi kwa anthu awo.
10 Och lade hans vapen i deras guds hus; och hans hufvud slogo de på Dagons hus.
Iwo anayika zida zake zankhondo mʼnyumba zopembedzera milungu yawo ndipo anapachika mutu wake mʼnyumba ya Dagoni.
11 Då nu alle de i Jabes i Gilead hörde allt det de Philisteer Saul gjort hade,
Pamene anthu onse okhala ku Yabesi Giliyadi anamva zimene Afilisti anachitira Sauli,
12 Reste de upp alle stridsamme män, och togo Sauls lekamen, och hans söners, och förde dem till Jabes, och begrofvo deras ben under den eken i Jabes; och fastade i sju dagar.
anthu awo onse olimba mtima anapita kukatenga mitembo ya Sauli ndi ana ake ndipo anabwera nayo ku Yabesi. Anakwirira mafupa awo pansi pa mtengo wabwemba ku Yabesi, ndipo anasala kudya masiku asanu ndi awiri.
13 Alltså blef Saul död i sine missgerning, som han emot Herran gjort hade, emot Herrans ord, det han icke höll; också derföre, att han frågade spåqvinnona,
Sauli anafa chifukwa anali wosakhulupirika pamaso pa Yehova. Iye sanasunge mawu a Yehova, pakuti anakafunsira nzeru kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa,
14 Och icke frågade Herran; derföre drap han honom, och vände riket till David, Isai son.
sanafunsire nzeruzo kwa Yehova. Choncho Yehova anamupha ndi kupereka ufumu kwa Davide mwana wa Yese.

< 1 Krönikeboken 10 >