< Zaburi 83 >

1 Ee Mungu, usikae kimya! usitupuuze na kustarehe, Ee Mungu.
Nyimbo. Salimo la Asafu. Inu Mulungu musakhale chete; musangoti phee, Mulungu musangoti duu.
2 Tazama, adui zako wanafanya vurugu, na wale wakuchukiao wameinua vichwa vyao.
Onani adani anu akuchita chiwawa, amene amadana nanu autsa mitu yawo.
3 Wanafanya hila juu ya watu wako na kwa pamoja kupanga njama dhidi ya wale uwalindao. Wamesema,
Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu; Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.
4 “Njoni na tuwaangamize wao kama taifa. Kisha jina la Israeli halitakumbukwa.”
Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”
5 Wamepanga njama pamoja wakiwa na mkakati mmoja; wamefanya muungano dhidi yako.
Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu; Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:
6 Hii inajumuisha hema za Edomu na Waishmaeli, na watu wa Moabu na Wahagari, ambao wamepanga njama pamoja nao
Matenti a Edomu ndi Aismaeli, Mowabu ndi Ahagiri,
7 Gebal, Amoni, Amaleki; pia inajumuisha Filisti na wenyeji wa Tiro.
Agebala, Aamoni ndi Aamaleki, Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.
8 Ashuri pia ameshirikina nao; wanawasaidia wana wa Lutu. Serah
Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo kupereka mphamvu kwa ana a Loti. (Sela)
9 Ufanye kwao kama ulivyofanya kwa Midiani, kama ulivyofanya kwa Sisera na kwa Yabini kwenye Mto Kishoni.
Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani, monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.
10 Waliangamizwa kule Endori na wakawa kama mbolea juu ya chi.
Amene anawonongedwa ku Endori ndi kukhala ngati zinyalala.
11 Uvifanye vyeo vyao kama Oreb na Zeeb, na wakuu wao wote kama Zeba na Zalmuna.
Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,
12 Wao walisema, natujimilikishe malisho ya Mungu.”
amene anati, “Tiyeni tilande dziko la msipu la Mulungu.”
13 Ee Mungu wangu, uwafanye kama mavumbi ya kisulisuli, kama makapi mbele ya upepo,
Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga, ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.
14 Kama moto uteketezao msitu, na kama miali ya moto iwakayo milimani.
Monga moto umatentha nkhalango, kapena malawi a moto kuyatsa phiri,
15 Uwafuatie kwa tufani yako, na kuwafadhaisha kwa dhoruba yako.
kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho, ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.
16 Uwajaze nyuso zao kwa aibu ili kwamba waweze kulitafuta jina lako, Yahwe.
Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.
17 Nao waaibishwe na kufadhaishwa milele; waangamizwe katika aibu.
Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse; awonongeke mwa manyazi.
18 Kisha watajua kwamba ni wewe pekee, Yahwe, Uliye Juu ya nchi yote.
Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova, ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.

< Zaburi 83 >