< Zaburi 119 >
1 Wamebarikiwa wale ambao njia zao hazina lawama, waenendao katika sheria ya Yahwe.
Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
2 Wamebarikiwa wale wazishikao amri zake thabiti, wamtafutao kwa moyo wao wote.
Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
3 Hawatendi makosa; wanaenenda katika njia zake.
Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
4 Wewe umetuamuru kuyashika maagizo yako ili tuyachunguze kwa umakini.
Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
5 Oh, ningependa njia zangu ziwe thabiti nizitii amri zako!
Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
6 Ndipo sitaaibika nizifikiripo amri zako zote.
Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
7 Nitakushukuru wewe kwa unyofu wangu wa moyo nijifunzapo amri za haki yako.
Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
8 Nitazitii amri zako; usiniache peke yangu. BETH.
Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
9 Ni jinsi gani kijana aweza kuendelea kuishi katika njia yake ya utakatifu? Ni kwa kulitii neno lako.
Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
10 Kwa moyo wangu wote ninakutafuta wewe; Usiniache nipotee mbali na maagizo yako.
Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
11 Moyoni mwangu nimeliweka neno lako ili nisije nikakutenda dhambi.
Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
12 Umetukuka, Yahwe; unifundishe amri zako.
Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
13 Kwa kinywa changu nimetangaza amri ya haki yako yote ambayo umeifunua.
Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
14 Ninafurahi katika njia ya amri za agano lako zaidi kuliko katika utajiri.
Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
15 Nitayatafakari maagizo yako na kuzitilia maanani njia zako.
Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
16 Ninafurahia katika amri zako; sitalisahau neno lako. GIMEL.
Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
17 Uwe mwema kwa mtumishi wako ili niweze kuishi na kulishika neno lako.
Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
18 Ufungue macho yangu ili niweze kuona mambo ya ajabu katika sheria yako.
Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
19 Mimi ni mgeni katika nchi; usizifiche amri zako mbali nami.
Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
20 Moyo wangu unauma kwa kutamani sana kuzijua amri zako za haki wakati wote.
Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
21 Wewe huwakemea wenye kiburi, waliolaaniwa, wanao tanga-tanga mbali na amri zako.
Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
22 Uniokoe dhidi ya aibu na udhalilishaji, maana nimezitii amri za agano lako.
Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
23 Ingawa watawala wanapanga njama na kunikashfu, mtumishi wako huzitafakali amri zako.
Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
24 Amri za agano lako ni furaha yangu, na washauri wangu. DALETH.
Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
25 Uhai wangu unashikamana na mavumbi! nipe uhai kwa neno lako.
Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
26 Nilikuambia mapito yangu, na ulinijibu; nifundishe sheria zako.
Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
27 Unifahamishe njia ya maagizo yako, ili niweze kutafakari juu ya mafundisho yako ya ajabu.
Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
28 Nimelemewa na huzuni! Nitie nguvu kwa neno lako.
Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
29 Uiondoe kwangu njia ya udanganyifu; kwa wema wako unifundishe sheria yako.
Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
30 Nimechagua njia ya uaminifu; siku zote nimeweka amri za haki yako mbele yangu.
Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
31 Ninashikamana na amri za agano lako; Yahwe, usiniache niaibike.
Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
32 Nitakimbia katika njia ya amri zako, kwa sababu wausukuma moyo wangu kufanya hivyo. HE
Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
33 Unifundishe, Yahwe, njia za sheria yako, nami nitazishika hadi mwisho.
Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
34 Unipe uelewa, nami nitazishika sheria zako; nitazitii kwa moyo wangu wote.
Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
35 Uniongoze katika njia ya amri zako, maana ninafurahi kuenenda katika hizo.
Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
36 Uelekeze moyo wangu kuzielekea amari za agano lako na uniweke mbali na matendo yasiyo haki tena.
Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
37 Uyageuze macho yangu dhidi ya kutazama mambo yasiyofaa; unihuishe katika njia zako.
Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
38 Umtendee mtumishi wako ahadi ambayo uliifanya kwa wale wanaokuheshimu wewe.
Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
39 Uniondolee shutumu niiogopayo, maana hukumu zako za haki ni njema.
Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
40 Tazama, nimeyatamani maagizo yako; unihuishe katika haki yako. VAV.
Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
41 Ee Yahwe, unipe upendo wako usiokwisha na wokovu wako kulingana na ahadi yako;
Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
42 ndipo nitakuwa na jibu kwa ajili ya yule anayenidhihaki.
ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
43 Usiliondoe neno la kweli mdomoni mwangu, maana nimesubiri kwa ajili ya amri zako za haki.
Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
44 Nitazitii sheria zako siku zote, milele na milele.
Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
45 Nitaenenda salama, maana ninayatafuta maagizo yako.
Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
46 Nitazinena amri zako thabiti mbele ya wafalme nami sitaaibika.
Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
47 Ninafurahia katika amri zako, nizipendazo sana.
popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
48 Nitaziinulia mikono yangu amri zako, nizipendazo; nitazitafakari sheria zako. ZAYIN.
Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
49 Kumbuka ahadi yako kwa mtumishi wako kwa sababu umenipa tumaini.
Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
50 Hii ni faraja yangu katika mateso: kuwa ahadi yako imeniweka hai.
Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
51 Wenye kiburi wamenicheka, lakini sijaiacha sheria yako.
Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
52 Nimezitafakari amri zako za haki tangu zamani, Yahwe, nami ninajifariji mwenyewe.
Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
53 Hasira kali imenishikilia kwa sababu ya waovu wanaoikataa sheria yako.
Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
54 Sheria zako zimekuwa nyimbo zangu katika nyumba ninayoishi kwa muda.
Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
55 Ninalifikiria jina lako wakati wa usiku, Yahwe, na kuzishika sheria zako.
Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
56 Hili limekuwa zoezi langu kwa sababu nimeyatii maagizo yako. HETH.
Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
57 Yahwe ni sehemu yangu; nimeamua kuyatii maneno yake.
Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
58 Kwa bidii ninaomba neema yako kwa moyo wangu wote; unihurumie, kama neno lako lilivyo ahidi.
Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
59 Nilizichunguza njia zangu na kugeuzia miguu yangu kwenye amri za agano lako.
Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
60 Naharakisha na sichelewi kuzishika amri zako.
Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
61 Kamba za waovu zimenifunga; nami sijaisahau sheria yako.
Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
62 Katikati ya usiku ninaamka kukushukuru wewe kwa sababu ya amri za haki yako.
Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
63 Ninaurafiki na wale wanao kuabudu wewe, wale wote watiio maagizo yako.
Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
64 Yahwe, nchi, imejaa uaminifu wa agano lako; unifundishe sheria zako. TETH.
Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
65 Wewe umemtendea mema mtumishi wako, Yahwe, sawasawa na neno lako.
Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
66 Unifundishe utambuzi sahihi na uelewa, kwa kuwa nimeamini katika amri zako.
Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
67 Kabla sijateswa nilipotea, lakini sasa nimelitii neno lako.
Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
68 Wewe ni mwema, na ndiye yule utendaye mema; unifundishe sheria zako.
Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
69 Wenye kiburi wamenichafua kwa uongo, lakini niliyashika maagizo yako kwa moyo wangu wote.
Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
70 Mioyo yao ni migumu, lakini ninafurahia katika sheria yako.
Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
71 Ni vizuri kwangu kuwa nimeteseka ili niweze kujifunza sheria zako.
Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
72 Maagizo yatokayo kinywani mwako ni ya thamani zaidi kwangu kuliko maelfu ya vipande vya dhahabu na fedha. YOD.
Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
73 Mikono yako imeniumba na kunitengeneza; unipe uelewa ili niweze kujifunza amri zako.
Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
74 Wale wanao kucha wewe watafurahi wanionapo kwa sababu ninapata tumaini katika neno lako.
Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
75 Ninajua, Yahwe, kuwa amri zako ni za haki, na kuwa katika uaminifu ulinitesa.
Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
76 Agano lako aminifu na linifariji, kama ulivyomwahidi mtumishi wako.
Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
77 Unihurumie ili niweze kuishi, kwa maana sheria yako ni furaha yangu.
Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
78 Wenye kiburi na waaibishwe, maana wamenitukana; bali mimi nitayatafakari maagizo yako.
Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
79 Wale wote wanao kucha wewe na wanigeukie, wale wazijuao amri za agano lako.
Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
80 Moyo wangu uwe mkamilifu pamoja na heshima kwa sheria zako ili nisiaibike. KAPH.
Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
81 Ninazimia kwa kutamani sana kuwa wewe unaweza kuniokoa! Ninamatumaini katika neno lako.
Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
82 Macho yangu yanatamani sana kuiona ahadi yako; ni lini utanifariji mimi?
Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
83 Kwa maana nimekuwa kama kiriba katika moshi; sisahau sheria zako.
Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
84 Ni kwa muda gani gani mtumishi wako atalazimika kuyavumilia haya; ni lini utawahukumu wale wanaonitesa?
Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
85 Wenye kiburi wamenichimbia shimo, wasiotii sheria yako.
Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
86 Amri zako zote ni za kuaminika; wale watu walinitesa bila ya haki; unisaidie.
Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
87 karibu kunifanya nifikie mwisho juu ya nchi hii, lakini siyakatai maagizo yako.
Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
88 Kwa upendo wako thabiti, uniweke hai, ili niweze kuzitii amri zako. LAMEDH.
Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
89 Yahwe, neno lako linasimama milele; neno lako limefanywa imara mbinguni.
Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
90 Uaminifu wako wadumu kwa ajili ya vizazi vyote; umeiimarisha nchi, nayo inadumu.
Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
91 Vitu yote yaliendelea mpaka leo hii, kama vile ulivyosema katika amri zako za haki, maana vitu vyote ni watumishi wako.
Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
92 Kama sheria yako isingekuwa furaha yangu, ningeangamia katika mateso yangu.
Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
93 Sitayasahau kamwe maagizo yako, maana kupitia hayo umeniweka hai.
Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
94 Mimi ni wako, kwa maana ninayatafuta maagizo yao.
Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
95 Waovu hujiandaa kuniangamiza, lakini nitatafuta kuzielewa amri za agano lako.
Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
96 Nimeona kuwa kila kitu kina mipaka, lakini amri zako ni pana, zaidi ya mipaka. MEM.
Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
97 Oh ni jinsi gani naipenda sheria yako! Ni tafakari yangu mchana kutwa.
Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
98 Amri zako hunifanya mwenye hekima kuliko adui zangu, maana amri zako siku zote ziko pamoja nami.
Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
99 Ninauelewa zaidi kuliko walimu wangu wote, kwa maana ninazitafakari amri za agano lako.
Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
100 Ninaelewa kuliko wale wanaonizidi umri; hii ni kwa sababu nimeyashika maagizo yako.
Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
101 Nimeiepusha miguu yangu na kila njia ya uovu ili niweze kulitii neno lako.
Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
102 Sijaenda kinyume na amri zako za haki, kwa maana wewe umenifundisha.
Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
103 Ni jinsi gani maneno yako ni matamu kwenye majaribu yangu, naam, matamu kuliko asali kinywani mwangu!
Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
104 Kupitia maagizo yako ninapata utambuzi; kwa hiyo kila njia isiyo ya kweli.
Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
105 Neno lako ni taa ya mguu miguu yangu na mwanga wa njia yangu.
Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
106 Nimeapa na nimethibitisha, kuwa nitazitii amri za haki yako.
Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
107 Nimeteswa sana; uniweke hai, Yahwe, kama ulivyoahidi katika neno lako.
Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
108 Yahwe, tafadhali pokea dhabihu yangu ya hiari ya kinywa changu, na unifundishe amri zako za haki.
Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
109 Uhai wangu ziku zote uko mkononi mwangu, lakini bado sisahau sheria yako.
Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
110 Waovu wamenitegea mtego, lakini sijapotea mbali na maagizo yako.
Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
111 Nimezifanya amri za agano lako kama urithi wangu milele, maana hizo ni furaha ya moyo wangu.
Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
112 Moyo wangu umewekwa kuzitii sheria zako milele mpaka mwisho kabisa. SAMEKH.
Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
113 Ninawachukia watu wa kusita-sita, lakini naipenda sheria yako.
Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
114 Wewe ni ficho langu na ngao yangu; nalingoja neno lako.
Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
115 Ondokeni kwangu, ninyi mtendao uovu, ili niweze kuzitii amri za Mungu wangu.
Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
116 Uniwezeshe kwa neno lako ili niweze kuishi na nisiaibike na matumaini yangu.
Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
117 Unisaidie, nami nitakuwa salama; siki zote nitazitafakari sheria zako.
Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
118 Wewe huwakataa wale wote wapoteao mbali na sheria zako, maana watu hao ni wadanganyifu na si wakuaminika.
Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
119 Wewe huwaondoa waovu wa nchi kama takataka; kwa hiyo ninazipenda amri zako thabiti.
Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
120 Mwili wangu hutetemeka kwa hofu yako, na ninaziogopa amri za haki yako. AYIN.
Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
121 Ninafanya kilicho sahihi na haki; usiniache kwa watesi wangu.
Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
122 Uwe mdhamini wa ustawi wa mtumishi wako; usiwaache wenye kiburi wanionee.
Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
123 Macho yangu yanachoka kwa kuusubiri wokovu wako na neno lako la haki.
Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
124 Mwoneshe mtumishi wako uaminifu wa agano lako, na unifundishe sheria zako.
Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
125 Mimi ni mtumishi wako; unipe uelewa ili niweze kuzijua amri za agano lako.
Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
126 Ni wakati wa Yahwe kutenda, kwa maana watu wamevunja sheria yako.
Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
127 Hakika ninazipenda amri zako kuliko dhahabu, naam, kuliko dhahabu safi.
Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
128 Hivyo ninayafuata maagizo yako yote kwa makini, na ninachukia kila njia ya uongo. PE.
ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
129 Sheria zako ni za ajabu, ndiyo sababu ninazitii.
Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
130 Ufafanuzi wa maneno yako huleta nuru; na kumpa ufahamu mjinga.
Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
131 Ninafungua kinywa changu na kutweta, maana ninazitamani amri zako.
Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
132 Unigeukie na unihurumie, kama ufanyavyo siku zote kwa wale walipendao jina lako.
Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
133 Uziongoze hatua zangu kwa neno lako; usiruhusu dhambi yeyote initawale.
Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
134 Unikomboe dhidi ya wanadamu waonevu ili niyatii maagizo yako.
Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
135 Uso wako umwangazie mtumishi wako, na unifundishe sheria zako.
Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
136 Mito ya machozi yatiririka kutoka machoni pangu kwa sababu watu hawaitii sheria yako. TSADHE.
Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
137 Wewe ni mwenye haki, Yahwe, na amri zako ni haki.
Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
138 Umezipa amri za agano lako haki na uaminifu.
Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
139 Hasira imeniangamiza kwa sababu adui zangu husahau maneno yako.
Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
140 Neno lako limepimwa sana, naye mtumishi wako analipenda.
Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
141 Sina umuhimu na ninadharauliwa, lakini bado siyasahau maagizo yako.
Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
142 Hukumu yako ni ya haki milele, na sheria yako ni ya kuaminika.
Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
143 Japo dhiki na taabu vimenipata, amri zako bado ni furaha yangu.
Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
144 Amri za agano lako ni za haki milele; unipe uelewa ili niweze kuishi. QOPH.
Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
145 Nililia kwa moyo wangu wote, “Unijibu, Yahwe, nitazishika sheria zako.
Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
146 Ninakuita wewe; uniokoe, nami nitazitii amri za agano lako.”
Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
147 NInaamka asubuhi kabla jua halijachomoza na kulia kwa ajili ya msaada.
Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
148 Ninatumaini katika maneno yako. Macho yangu yako wazi usiku kucha ili niweze kutafakari juu ya neno lako.
Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
149 Sikia sauti yangu katika uaminifu wa agano lako; uniweke hai, Yahwe, kama ulivyoahidi katika amri zako za haki.
Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
150 Wale wanaonitesa wananikaribia, lakini wako mbali na sheria yako.
Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
151 Wewe uko karibu, Yahwe, na amri zako ni za kuaminika.
Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
152 Muda mrefu uliopita nilijifunza kutoka katika amri za agano lako ulizoziweka katika mahali pa milele. RESH.
Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
153 Uyatazame mateso yangu na unisaidie, maana siisahau sheria yako.
Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
154 Unitetee na kunikomboa; unihifadhi, kama ulivyo ahidi katika neno lako.
Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
155 Wokovu uko mbali na waovu, maana hawazipendi amri zako.
Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
156 Matendo yako ya huruma ni makuu, Yahwe; uniweke hai; kama ufanyavyo siku zote.
Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
157 Watesi wangu na adui zangu ni wengi, lakini bado sijaenda mbali na amri za agano lako.
Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
158 Nimewaona wasaliti wakitia kinyaa kwa sababu hawalishiki neno lako.
Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
159 Tazama jinsi niyapendavyo maagizo yako; uniweke hai, Yahwe, kama ulivyoahidi katika uaminifu wa agano lako.
Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
160 Kiini cha neno lako ni kweli; kila mmoja mwenye amri za haki hudumu milele. SHIN.
Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
161 Wakuu hunitesa bila sababu; moyo wangu hutetemeka, ukiogopa kutolitii neno lako.
Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
162 Ninalifurahia neno lako kama apataye nyara nyingi.
Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
163 Ninachukia na kudharau uongo, lakini naipenda sheria yako.
Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
164 Mara saba kwa siku ninakusifu wewe kwa sababu ya amri zako za haki.
Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
165 Wana amani nyingi, waipendao sheria yako; hakuna cha kuwatia mashakani.
Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
166 Naungoja wokovu wako, Yahwe, na ninatii amri zako.
Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
167 Ninazishika amri zako thabiti, na ninazipenda sana.
Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
168 Ninayashika maagizo yako na amri zako thabiti, kwa maana unajua kila kitu nifanyacho. TAV.
Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
169 Sikia kilio changu, Yahwe; unipe uelewa wa neno lako.
Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
170 Maombi yangu yaje mbele zako; unisaidie, kama ulivyoahidi katika neno lako.
Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
171 Midomo yangu na imwage sifa, maana wewe unanifundisha sheria zako.
Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
172 Ulimi wangu na uimbe kuhusu neno lako, maana amri zako zote ni za haki.
Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
173 Mkono wako unisaidie, maana nimechagua maagizo yako.
Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
174 Ninautamani wokovu wako, Yahwe, na sheria yako ni furaha yangu.
Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
175 Naomba niishi na nikusifu wewe, na amri zako za haki zinisaidie.
Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
176 Nimetanga-tanga kama kondoo aliyepotea; mtafute mtumishi wako, kwa maana sijazisahau amri zako.
Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.