< Zaburi 116 >
1 Nampenda Yahwe kwa kuwa anasikia sauti yangu na kuomba kwangu kwa ajili ya huruma.
Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
2 Kwa sababu alinisikiliza, nitamuita yeye ningali ninaishi.
Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
3 Kamba za mauti zilinizunguka, na mitego ya kuzimu ilinikabili; niliona dhiki na huzuni. (Sheol )
Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol )
4 Kisha niliita kwa jina la Yahwe: “Tafadhali Yahwe, uiokoe nafsi yangu.”
Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
5 Yahwe ni mwenye neema na haki; Mungu wetu ni mwenye huruma.
Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
6 Yahwe huwalinda wasio na hila; nilishushwa chini akaniokoa.
Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
7 Nafsi yangu inaweza kurudi mahali pake pa kupumzika, kwa kuwa Yahwe amekuwa mwema kwangu.
Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
8 Kwa maana uliokoa uhai wangu dhidi ya kifo, mcho yangu dhidi ya machozi, na miguu yangu dhidi ya kujikwaa.
Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
9 Nitamtumikia Yahwe katika nchi ya walio hai.
kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
10 Nilimwamini yeye, hata niliposema, “nimeteswa sana.”
Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
11 Kwa haraka nilisema, “Watu wote ni waongo.”
Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
12 Nimlipeje Yahwe kwa wema wake wote kwangu?
Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
13 Nitakiinua kikombe cha wokovu, na kuliitia jina la Yahwe.
Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
14 Nitatimiza viapo vyangu kwa Yahwe katika uwepo wa watu wake wote.
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
15 Mauti ya wacha Mungu ina thamani machoni pa Mungu.
Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
16 Ee Yahwe, hakika, mimi ni mtumishi wako; mimi ni mtumishi wako, mwana wa mjakazi wako; umefungua vifungo vyangu.
Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
17 Nitakutolea dhabihu ya shukrani na nitaliitia jina la Yahwe.
Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
18 Nitatimiza viapo vyangu kwa Yahwe katika uwepo wa watu wake wote,
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
19 katika nyua za nyumba ya Yahwe, katikati yako, Yerusalemu. Msifuni Yahwe.
mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.