< Zaburi 109 >

1 Zaburi ya Daudi. Mungu ninaye msifu, usinyamaze kimya.
Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Salimo la Davide. Mulungu amene ndimakutamandani, musakhale chete,
2 Kwa maana waovu na wadanganyifu wananishambulia; wanazungumza uongo dhidi yangu.
pakuti anthu oyipa ndi achinyengo atsekula pakamwa pawo kutsutsana nane; iwo ayankhula motsutsana nane ndi malilime abodza.
3 Wananizunguka na kusema mambo ya chuki, na wananishambulia bila sababu.
Andizungulira ndi mawu audani, amandinena popanda chifukwa.
4 Wananilipa kashfa badala ya upendo, lakini mimi ninawaombea.
Mʼmalo mwa chikondi changa amandineneza, koma ine ndine munthu wapemphero.
5 Wananilipa uovu badala ya mema, na wanachukia upendo wangu.
Iwo amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino, ndi udani mʼmalo mwa chikondi changa.
6 Teua mtu mwovu aliye adui zaidi kama watu hawa; teua mshitaki asimame mkono wake wa kuume.
Sankhani munthu woyipa kuti amutsutse iye; lolani wotsutsa ayime ku dzanja lake lamanja.
7 Na atakapohukumiwa, aonekane na hatia; maombi yake yachukuliwe kuwa ni dhambi.
Pamene aweruzidwa, apezeke kuti ndi wolakwa, ndipo mapemphero ake amutsutse.
8 Siku zake na ziwe chahe; mamlaka yake na yachukuliwe na mtu mwingine.
Masiku ake akhale owerengeka; munthu wina atenge malo ake a utsogoleri.
9 Watoto wake wawe yatima, na mke wake awe mjane.
Ana ake akhale amasiye ndipo mkazi wake akhale wopanda mwamuna.
10 Watoto wake wenye kutanga tanga na kuombaomba, wakiondoka katika nyumba zao zilizo haribika na kuomba chakula au pesa kwa wapita njia.
Ana ake akhale oyendayenda ndi opemphapempha; apirikitsidwe kuchoka pa mabwinja a nyumba zawo.
11 Mdai na achukue vitu vyake vyote amilikivyo; wageni wateke mapato ya kazi yake.
Wokongoza alande zonse zimene ali nazo; alendo afunkhe ntchito za manja ake.
12 Asiwepo mtu yeyote wa kumfanyia wema; mtu yeyote asiwahurumie yatima wake.
Pasapezeke ndi mmodzi yemwe womukomera mtima kapena kumvera chisoni ana ake amasiye.
13 Watoto wake waangamizwe; majina yao na yafutwe katika kizazi kijacho.
Zidzukulu zake zithe nʼkufa, mayina awo afafanizidwe mu mʼbado wotsatirawo.
14 Uovu wa baba zake utajwe kwa Yahwe; na dhambi ya mama yake isisahaulike.
Mphulupulu za makolo ake zikumbukiridwe pamaso pa Yehova; tchimo la amayi ake lisadzafafanizidwe.
15 Hatia zao na ziwe mbele ya Yahwe siku zote; Yahwe na aiondoe kumbukumbu yao duniani.
Machimo awo akhale pamaso pa Yehova nthawi zonse, kuti Iye achotse chikumbutso chawo pa dziko lapansi.
16 Yahwe na afanye hivi kwa sababu mtu huyu kamwe hakusumbuka kuonesha uaminifu wa agano wowote, lakini badala yake aliwasumbua wanyonge, wahitaji, na kuwaua walio vunjika moyo.
Pakuti iye sanaganizirepo zochita chifundo, koma anazunza mpaka kuwapha anthu osauka ndi osweka mtima.
17 Alipenda kulaani; na imrudie juu yake. Alichukia kubariki; baraka zozote na zisije kwake.
Anakonda kutemberera, matembererowo abwerere kwa iye; sanakondwe nʼkudalitsa anthu ena, choncho madalitso akhale kutali naye.
18 Alijivika kulaani kana kwamba ni vazi lake, na laana yake iliingia ndani yake kama maji, na kama mafuta mifupani mwake.
Anavala kutemberera ngati chovala; kutemberera kunalowa mʼthupi lake ngati madzi, kulowa mʼmafupa ake ngati mafuta.
19 Laana zake na ziwe kwake kama vazi avaalo kujifunika mwenyewe, na kama mkanda avaao kila siku.
Matemberero akhale ngati chofunda chodzikutira nacho, ngati lamba wovala tsiku ndi tsiku.
20 Na haya yawe malipo ya mshitaki wangu kutoka kwa Yahwe, ya wale wasemao mambo maovu juu yangu.
Awa akhale malipiro ochokera kwa Yehova pa onditsutsa anga, kwa iwo amene amayankhula zoyipa za ine.
21 Yahwe Bwana wangu, unishughulikie kwa wema kwa ajili ya jina lako. Kwa sababu uaminifu wa agano lako ni mwema, uniokoe.
Koma Inu Ambuye Wamphamvuzonse, muchite nane molingana ndi dzina lanu, chifukwa cha ubwino wa chikondi chanu, pulumutseni.
22 Kwa maana ni mnyonge na muhitaji, na moyo wangu umejeruhiwa ndani yangu.
Pakuti ndine wosauka ndi wosowa, ndipo mtima wanga ukuwawa mʼkati mwanga.
23 Ninatoweka kama kivuli cha jioni; ninapeperushwa kama nzige.
Ndikuzimirira ngati mthunzi wa kumadzulo, ndapirikitsidwa ngati dzombe.
24 Magoti yangu ni dhaifu kutokana na kufunga; ninakuwa mwembamba na mifupa.
Mawondo anga afowoka chifukwa cha kusala zakudya, thupi langa lawonda ndi mutu wanga womwe.
25 Nimedharauliwa na washitaki wangu; wanionapo; hutikisa vichwa vyao.
Ndine chinthu chotonzedwa kwa otsutsana nane; akandiona, amapukusa mitu yawo.
26 Nisaidie, Yahwe Mungu wangu; uniokoe kwa uaminifu wa agano lako.
Thandizeni Inu Yehova Mulungu wanga; pulumutseni molingana ndi chikondi chanu.
27 Nao wajue kuwa wewe umefanya haya, kwamba wewe, Yahwe, umetenda haya.
Adaniwo adziwe kuti limeneli ndi dzanja lanu, kuti Inu Yehova mwachita zimenezi.
28 Ingawa wananilaani, tafadhali unibariki; wanishambuliapo, waaibishwe, lakini mtumishi wako afurahi.
Angathe kutemberera, koma Inu mudzadalitsa; pamene iwo andiputa adzachititsidwa manyazi, koma mtumiki wanu adzasangalala.
29 Washitaki wangu na wavishwe kwa aibu; wavae aibu yao kama vazi.
Onditsutsa adzavekedwa mnyozo, ndipo adzadzifunditsa manyazi ngati chovala.
30 Kwa kinywa changu ninatoa shukrani kuu kwa Yahwe; nitamsifu yeye katikati ya kusanyiko.
Ndi pakamwa panga ndidzathokoza Yehova kwambiri; ndidzamutamanda mʼgulu lalikulu la anthu.
31 Maana nitasimama mkono wa kuume wa mhitaji, ili nimuokoe dhidi ya wale wanao muhukumu.
Popeza Iye amayima ku dzanja lamanja la munthu wosowayo, kupulumutsa moyo wake kwa iwo amene agamula molakwa.

< Zaburi 109 >