< Mithali 9 >

1 Hekima amejenga nyumba yake; amechonga nguzo saba kutoka katika miamba.
Nzeru inamanga nyumba yake; inayimika nsanamira zake zisanu ndi ziwiri.
2 Ameandaa wanyama wake kwa chakula cha usiku; ameichanganya divai yake; na kuandaa meza yake.
Inapha ziweto zake ndipo yasakaniza vinyo wake; inasakaniza vinyo wake ndi kuyala tebulo lake.
3 Amewatuma watumishi wake kupeleka mialiko na kutoka mahali pa juu sana kwenye mji anaita:
Nzeruyo inatuma adzakazi ake, kuti akakhale pamwamba penipeni pa mzinda ndi kukalengeza kuti,
4 “Wale wasiofunzwa waje hapa!” anawaambia wale wasionaufahamu.
“Aliyense amene ali munthu wamba, abwere kuno!” Kwa onse opanda nzeru inkanena kuti,
5 Njoo, ule chakula, na unywe divai nimeshaichanganya.
“Bwerani, dzadyeni chakudya changa ndipo dzamweni vinyo amene ndakonza.
6 Acheni njia zenu za kijinga, na mkaishi; tembeeni katika njia ya ufahamu.
Lekani zopusa zanu kuti mukhale ndi moyo; yendani njira ya nzeru yomvetsa zinthu.”
7 Yeyote amrekebishaye mwenye dhihaka hukaribisha matusi na yeyote anayemshutumu mtu mbaya atapata madhara.
Aliyense amene amayesa kukonza munthu wonyoza amadziputira minyozo; aliyense amene amadzudzula munthu woyipa amadetsa mbiri yake.
8 Usimshutumu mwenye dhihaka, ama atakuchukia; mshutumu mtu mwenye busara, naye atakupenda.
Usadzudzule munthu wonyoza kuti angadzadane nawe; dzudzula munthu wanzeru ndipo adzakukonda.
9 Mpe mafundisho mtu mwenye busara, naye atakuwa na busara zaidi; mfundishe mtu mwenye haki, naye ataongeza elimu.
Ukalangiza munthu wanzeru ndiye adzapitirira kukhala wanzeru; ukaphunzitsa munthu wolungama ndiye adzawonjezera kuphunzira kwake.
10 Hofu ya Mungu ni chanzo cha hekima na maarifa ya Mtakatifu ni ufahamu.
Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru; kudziwa Woyerayo ndiko kukhala womvetsa bwino zinthu.
11 Maana kwa njia yangu siku zako zitazidishwa na uzima wako utaongezewa miaka.
Chifukwa cha ine nzeru, masiku ako adzachuluka, ndipo zaka za moyo wako zidzawonjezeredwa.
12 Kama unahekima, unahekima kwako mwenyewe, lakini ukidharau, utaibeba peke yako.
Ngati ndiwe wanzeru, nzeru yakoyo idzakupindulitsa; ngati ndiwe wonyoza ena, udzavutika wekha.
13 Mwanamke mpumbavu anakelele nyingi- hajafunzwa wala haelewi chochote.
Uchitsiru ndi mkazi waphokoso, wopulikira ndiponso wosadziwa zinthu.
14 Anakaa kwenye mlango wa nyumba yake, kwenye kiti cha sehemu ya juu sana ya mji.
Iye amakhala pa mpando, pa khomo la nyumba yake, pamalo aatali a mu mzinda,
15 Anawaita kwa sauti wanaopita karibu, watu wale wanaotembea wima katika njia zao.
kuti aziyitana anthu ongodutsa, amene akunka nayenda njira zawo.
16 Wale ambao hamjafunzwa njoni hapa ndani!” anawaambia wale wasio na akili. “
Amati, “Onse amene ndi anthu wamba abwere kuno,” ndipo kwa wopanda nzeru amati,
17 Maji ya kuiba ni matamu na mkate unaoliwa kwa siri unapendeza.”
“Madzi akuba ndiye amatsekemera; chakudya chodya mobisa ndi chokoma!”
18 Lakini hajui kwamba wafu wapo pale, wageni wake wapo kwenye vina vya kuzimu. (Sheol h7585)
Koma amunawo sadziwa kuti akufa ali kale komweko, ndi kuti alendo ake alowa kale mʼmanda akuya. (Sheol h7585)

< Mithali 9 >