< Mithali 2 >

1 Mwanangu, kama ukiyapokea maneno yangu na kuzitunza amri zangu,
Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,
2 usikilize hekima na utaelekeza moyo wako katika ufahamu.
ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;
3 kama utalilia ufahamu na kupaza sauti yako kwa ajili ya ufahamu,
ngati upempha kuti uzindikire zinthu inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,
4 kama utautafuta kama fedha na kupekua ufahamu kama unatafuta hazina iliyojificha,
ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,
5 ndipo utakapofahamu hofu ya Yehova na utapata maarifa ya Mungu.
ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova; ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.
6 Kwa kuwa Yohova hutoa hekima, katika kinywa chake hutoka maarifa na ufahamu.
Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru, ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.
7 Yeye huhifadhi sauti ya hekima kwa wale wampendezao, yeye ni ngao kwa wale waendao katika uadilifu,
Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo. Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,
8 huongoza katika njia za haki na atalinda njia ya waaminifu kwake.
pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama. Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.
9 Ndipo utakapoelewa wema, haki, usawa na kila njia njema.
Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo, kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.
10 Maana hekima itaingia moyoni mwako na maarifa yataipendeza nafsi yako.
Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako, kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.
11 Busara itakulinda, ufahamu utakuongoza.
Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga; kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.
12 Vitakuokoa kutoka katika njia ya uovu, kutoka kwa wale waongeao mambo potovu.
Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa, kwa anthu amabodza,
13 Ambao huziacha njia za wema na kutembea katika njia za giza.
amene amasiya njira zolungama namayenda mʼnjira zamdima,
14 Hufurahia wanapotenda maovu na hupendezwa katika upotovu.
amene amakondwera pochita zoyipa namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.
15 Hufuata njia za udanganyifu na kwa kutumia ghilba huficha mapito yao.
Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota, ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.
16 Busara na hekima zitakuokoa kutoka kwa mwanamke malaya, kutoka kwa mwanamke anayetafuta visa na mwenye maneno ya kubembeleza.
Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo; kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,
17 Yeye humwacha mwenzi wa ujana wake na kusahau agano la Mungu wake.
amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.
18 Maana nyumba yake huinama na kufa na mapito yake yatakupeleka kwa wale walioko kaburini.
Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa; njira zake zimamufikitsa ku manda.
19 Wote waiendeao njia yake hawatarudi tena na wala hawataziona njia za uzima.
Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera kapena kupezanso njira zamoyo.
20 kwa hiyo utatembea katika njia ya watu wema na kufuata njia za wale watendao mema.
Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino, uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.
21 Kwa wale watendao mema watafanya makazi yao katika nchi, na wale wenye uadilifu watadumu katika nchi.
Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;
22 Lakini waovu wataondolewa katika nchi na wale wasioamini wataondolewa katika nchi.
Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo, ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.

< Mithali 2 >