< Nehemia 13 >

1 Siku hiyo walisoma Kitabu cha Musa katika masikio ya watu. Ilionekana imeandikwa ndani yake kwamba hakuna Mwamoni au Mmoabu anapaswa kuja katika kusanyiko la Mungu, milele.
Pa tsiku limenelo anawerenga buku la Mose anthu akumva. Ndipo anapeza mawu akuti, Mwamoni kapena Mmowabu asalowe konse mu msonkhano wa Mulungu.
2 Hii ilikuwa kwa sababu hawakuja kwa watu wa Israeli na mkate na maji, bali walikuwa wamemwajiri Balaamu kulaani Israeli. Hata hivyo, Mungu wetu aligeuza laana kuwa baraka.
Paja iwowa sanawachingamire Aisraeli kukawapatsa chakudya ndi madzi. Mʼmalo mwake analemba ganyu Baalamu kuti adzawatemberere. Komabe Mulungu wathu anasandutsa tembererolo kukhala mdalitso.
3 Mara tu waliposikia sheria, waliwatenga Israeli toka kwa kila mgeni.
Anthu atamva lamuloli, anachotsa pakati pawo onse amene anali achilendo.
4 Sasa kabla ya hapo Eliashibu kuhani akawekwa juu ya vyumba vya nyumba ya Mungu wetu. Alikuwa na uhusiano na Tobia.
Izi zisanachitike, wansembe Eliyasibu anali atasankhidwa kukhala woyangʼanira zipinda zosungiramo katundu za Nyumba ya Mulungu. Iyeyu ankagwirizana kwambiri ndi Tobiya.
5 Eliashibu alimuandalia Tobia chumba kikubwa, ambako hapo awali waliweka sadaka ya nafaka, uvumba, makala, na sehemu ya kumi ya nafaka, divai, na mafuta, ambazo ziliwekwa kwa ajili ya Walawi, waimbaji, walinzi wa mlango, na michango kwa makuhani.
Choncho anamupatsa chipinda chachikulu chimene kale ankasungamo zopereka zakudya, lubani, ziwiya, zopereka za chakhumi za tirigu, vinyo ndi mafuta zoyenera kuperekedwa kwa Alevi, oyimba nyimbo ndi alonda a ku Nyumba ya Mulungu, komanso mphatso zoyenera kupereka kwa ansembe.
6 Lakini wakati huu wote sikuwepo Yerusalemu. Kwa mwaka wa thelathini na mbili wa Artashasta mfalme wa Babeli, nilikwenda kwa mfalme. Baada ya muda nikamwomba mfalme ruhusa ya kuondoka,
Koma pamene izi zonse zinkachitika mu Yerusalemu, ine kunalibe popeza mʼchaka cha 32 cha Aritasasita mfumu ya Babuloni ine ndinabwerera kwa mfumu. Patapitanso nthawi ndinapempha chilolezo kwa mfumuyo
7 na nikarudi Yerusalemu. Nikafahamu mabaya ambayo Eliashibu alikuwa amefanya kwa kumpa Tobia chumba cha kuhifadhi katika mahakama ya nyumba ya Mungu.
ndipo ndinabwerera ku Yerusalemu. Kumeneko ndinamva za chinthu choyipa chimene Eliyasibu anachita pomupatsa Tobiya chipinda mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu.
8 Nilikuwa na hasira sana na nikatupa vitabu vya nyumba ya Tobia nje ya chumba cha kuhifadhi.
Ndinapsa mtima kwambiri ndipo ndinataya kunja katundu yense wa Tobiya amene anali mʼchipindamo.
9 Niliamuru kwamba watakase vituo vya kuhifadhi, nami nikarudisha ndani yao makala ya nyumba ya Mungu, sadaka ya nafaka, na uvumba.
Ndinalamulira kuti ayeretse zipinda, ndipo kenaka ndinabwezeramo zida za mʼNyumba ya Mulungu, pamodzi ndi chopereka cha zakudya ndi lubani.
10 Niligundua kwamba sehemu zilizotolewa kwa ajili ya kuwapa Walawi hazikutolewa kwao, ili waweze kuondoka haraka hekaluni, kila mmoja kwenda shambani kwake, kama waimbaji waliofanya walivyoondoka.
Ndinapezanso kuti Alevi sankalandira magawo awo amene amayera kulandira. Chotsatira chake Alevi onse pamodzi ndi oyimba nyimbo amene ankagwira ku Nyumba ya Mulungu anathawa, aliyense kupita ku munda wake.
11 Kwa hiyo nikawasiliana na maafisa na kusema, 'Kwa nini nyumba ya Mungu imeachwa?' Niliwakusanya pamoja na kuwaweka kwenye nafasi zao.
Choncho ndinadzudzula akuluakulu aja ndipo ndinawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani Nyumba ya Mulungu yasiyidwa?” Ndipo ine ndinawayitanitsa pamodzi ndi kuwayika mʼmalo awo.
12 Kisha Yuda wote wakaleta zaka ya nafaka, divai mpya, na mafuta kwenye vituo vya kuhifadhi.
Pambuyo pake Ayuda anayambanso kubwera ndi zopereka zawo za chakhumi cha tirigu, vinyo ndi mafuta kuti ziperekedwe ku nyumba yosungiramo chuma.
13 Nikawaweka kama watunza hazina juu ya hazina, Shelemia kuhani, na Sadoki mwandishi, na Walawi, Pedaya. Hanani, mwana wa Zakuri, mwana wa Matania, alikuwa na wafuasi wao, kwa sababu walihesabiwa kuwa waaminifu. Kazi yao ilikuwa kusambaza vifaa kwa washirika wao.
Ndipo ndinasankha wansembe Selemiya, mlembi Zadoki, ndi Mlevi wotchedwa Pedaya kukhala oyangʼanira zipinda zosungiramo. Ndinasankhanso Hanani mwana wa Zakuri mwana wa Mataniya kukhala wowathandizira chifukwa ndinaona kuti anthu awa anali odalirika. Ntchito yawo inali yogawira abale awo zinthu zofunika.
14 Nikumbuke, Ee Mungu wangu, juu ya hili, wala usiondoe matendo mema niliyoyatenda kwa ajili ya nyumba ya Mungu wangu na huduma zake.
Inu Mulungu wanga, mundikumbukire pa zimenezi, ndipo musafafanize ntchito zanga zimene ndachita mokhulupirika pa Nyumba yanu pofuna kukutumikirani.
15 Siku hizo nikaona watu wa Yuda waliokanyaga mvinyo siku ya Sabato, na kuleta makundi ya nafaka, na kuwapakia punda, na divai, na zabibu, na tini, na kila aina ya mizigo nzito, waliyoleta Yerusalemu siku ya Sabato. Nikashuhudia kuwa walikuwa wakiuza chakula siku hiyo.
Nthawi imeneyo ndinaona anthu a mu Yuda akuponda ndi kufinya mphesa pa tsiku la Sabata. Ena ankawunjika tirigu milumilu ndi kumasenzetsa abulu. Enanso ankabwera ndi vinyo, mphesa, mkuyu ndi katundu wa mitundumitundu ku Yerusalemu pa tsiku la Sabata. Choncho ndinawachenjeza za kugulitsa zakudya pa tsiku la Sabata.
16 Watu kutoka Tiro waliokaa Yerusalemu walileta samaki na kila aina ya bidhaa, na wakawauza siku ya Sabato kwa watu wa Yuda na katika mji!
Nawonso anthu a ku Turo amene ankakhala mu Yerusalemu ankabweretsa nsomba ndi akatundu ena onse amalonda kudzagulitsa pa Sabata kwa anthu a mʼdziko la Yuda ndi a mu Yerusalemu.
17 Kisha nikawaambia viongozi wa Yuda, “Je! ni ubaya gani huu mnafanya, kuinajisi siku ya Sabato?
Ndipo ndinadzudzula anthu olemekezeka a dziko la Yuda. Ndinawafunsa kuti, “Nʼchoyipa chanji mukuchitachi, kumayipitsa tsiku la Sabata chotere?
18 Je! Baba zenu hawakufanya hivyo? Je, Mungu wetu hakuleta mabaya haya juu yetu na juu ya mji huu? Sasa unaleta ghadhabu zaidi juu ya Israeli kwa kudharau Sabato.”
Makolo anu anachita zomwezi ndipo Mulungu wathu anadzetsa mavuto pa ife ndi pa mzinda uwu. Kodi inu mukufuna kuwutsanso mkwiyo wa Mulungu pa Israeli pamene mukudetsa tsiku la Sabata?”
19 Mara ilipokuwa giza kwenye milango ya Yerusalemu kabla ya Sabato, niliamuru milango ifungwe na kwamba haifai kufunguliwa hadi baada ya Sabato. Niliwaweka baadhi ya watumishi wangu kwenye malango ili mzigo wowote usiweze kuletwa siku ya Sabato.
Nʼchifukwa chake ndikulamula kuti pamene kuyamba kuda, tsiku la Sabata lisanayambe, azitseka zipata zonse za Yerusalemu ndipo asazitsekule mpaka sabata litatha. Ndinayika ena mwa antchito anga oyangʼanira pa zipata kuti katundu aliyense asalowe mu Yerusalemu pa tsiku la Sabata.
20 Wafanyabiashara na wauzaji wa kila aina ya bidhaa walikimbia nje ya Yerusalemu mara moja au mbili.
Choncho kamodzi kapena kawiri anthu amalonda ndi anthu ogulitsa katundu osiyanasiyana ankagona usiku wonse kunja kwa Yerusalemu.
21 Lakini niliwaonya, “Mbona mnakaa nje ya ukuta? Ikiwa mtafanya hivyo tena, nitakuweka mikononi!” Kutoka wakati huo hawakuja siku ya sabato.
Koma ndinawachenjeza ndi kuwafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukugona pafupi ndi khoma? Ngati muchitanso zimenezi, ine ndidzakugwirani.” Kuyambira nthawi imeneyo, sanabwerenso pa tsiku la Sabata.
22 Nikawaamuru Walawi kujitakasa, na kuja kulinda milango, ili kutakasa siku ya Sabato. Nikumbuke kwa hili pia, Mungu wangu, na kunipatia huruma kwa sababu ya uaminifu wa agano ulilonalo kwangu.
Ndipo ndinalamulira Alevi kuti adziyeretse okha ndi kubwera kudzalonda pa zipata ndi cholinga choti tsiku la Sabata likhale tsiku loyera. Inu Mulungu wanga, kumbukireninso ine pa zimenezi ndipo mundisunge malingana ndi chikondi chanu chachikulu chosasinthika.
23 Katika siku hizo niliona Wayahudi waliokuwa wameoa wanawake wa Ashdodi, Amoni na Moabu.
Masiku amenewo ndinaonanso anthu a ku Yuda amene anakwatira akazi ochokera ku Asidodi, Amoni ndi Mowabu.
24 Nusu ya watoto wao walizungumza lugha ya Ashdodi, lakini hawakuweza kuzungumza lugha ya Yuda, lakini lugha ya mmoja wa watu wengine.
Theka la ana awo linkayankhula chiyankhulo cha Asidodi kapena chiyankhulo chimodzi cha anthu ena, ndipo sankathanso kuyankhula chiyankhulo cha Ayuda.
25 Nami nikawasiliana nao, na mimi niliwaadhibu, na nikawapiga baadhi yao na kuvuta nywele zao. Naliwaapisha kwa Mungu, nikisema, Msiwape wana wao binti zenu, wala msiwachukue binti zao kwa ajili ya wana wenu, wala ninyi wenyewe.
Tsono ndinakangana nawo ndi kuwatemberera. Ndinamenya ena mwa anthuwo ndi kuzula tsitsi lawo. Ine ndinawalumbiritsa mʼdzina la Mulungu kuti, “Inu musapereke ana anu aakazi kuti akwatiwe ndi ana awo aamuna kapena inuyo ngakhale ana anu aamuna kukwatira ana awo aakazi.
26 Je, Sulemani mfalme wa Israeli hakufanya dhambi kwa sababu ya wanawake hawa? Miongoni mwa mataifa mengi hapakuwa na mfalme kama yeye, na alipendwa na Mungu wake. Mungu akamfanya awe mfalme juu ya Israeli wote. Hata hivyo, wake zake wa kigeni walimfanya atende dhambi.
Kodi Solomoni mfumu ya Israeli suja anachimwa chifukwa cha ukwati ngati umenewu. Pakati pa mitundu yambiri panalibe mfumu ngati iyi. Iye anakondedwa ndi Mulungu wake, ndipo Mulungu anamuyika kukhala mfumu ya Israeli yense, koma iyeyo anachimwa chifukwa cha akazi achilendo.
27 Je, tunapaswa kukusikiliza na kufanya uovu huu hata kumhalifu Mungu wetu na kuwaoa wanawake wageni?
Kodi tsopano ife tizimva inu kuti mukuchita choyipa chachikulu chimenechi, kupandukira Yehova Mulungu wathu pomakwatira akazi achilendo?”
28 Mmoja wa wana wa Yoyada, mwana wa Eliashibu, kuhani mkuu, alikuwa mkwewe na Sanbalati Mhoroni. Kwa hiyo nilimondoa kutoka mbele yangu.
Mmodzi mwa ana aamuna a Yehoyada mwana Eliyasibu mkulu wa ansembe nʼkuti nthawi imeneyi ali mpongozi wa Sanibalati wa ku Horoni. Choncho ndinamuthamangitsa pamaso panga.
29 Wakukumbushe, Mungu wangu, kwa sababu wameunajisi ukuhani, na agano la ukuhani na Walawi.
Inu Mulungu wanga, mukumbukire mmene iwo anayipitsira unsembe, pangano la unsembe komanso la Alevi.
30 Kwa hiyo nimewatakasa kutoka kila kitu kigeni, na kuimarisha kazi za makuhani na Walawi, kila mmoja kwa kazi yake mwenyewe.
Motero ndinayeretsa ansembe ndi Alevi powachotsera kalikonse kachilendo. Ndipo ndinakhazikitsa ntchito zawo, kuti aliyense akhale pa ntchito yake.
31 Nilitoa sadaka za kuni wakati uliowekwa na matunda ya kwanza. Nikumbuke, Mungu wangu, kwa mema.
Ndiponso kupereka nkhuni ndi zipatso zoyamba kucha pa nthawi yake. Ndikumbukireni pondikomera mtima, Inu Mulungu wanga.

< Nehemia 13 >