< Yoshua 12 >
1 Basi hawa ndio wafalme wa nchi, ambao watu wa Israeli walishindwa. Waisraeli walichukua miliki ya nchi katika upande wa mashariki mwa Yordani sehemu ambako jua huchomoza, kutoka bonde la Mto Arnoni hadi Mlima Hermoni, na nchi yote ya Araba kuelekea kusini.
Aisraeli anagonjetsa dziko lonse la kummawa kwa Yorodani, kuyambira ku chigwa cha Arinoni mpaka ku phiri la Herimoni pamodzi ndi dera lonse la kummawa kwa Araba. Iwo anatenga dzikoli kukhala lawo, ndipo mafumu a dzikoli anali awa:
2 Sihoni, mfalme wa Waamori, aliishi katika Heshiboni. Alitawala kutoka Aroeri, ambayo iko juu ya bonde la Arnoni kutoka katikati ya bonde, na nusu ya Geleadi kushuka mpaka Mto Yaboki katika mpaka wa Waamori.
Sihoni mfumu ya Aamori, amene ankakhala mu Hesiboni. Iye analamulira kuyambira ku Aroeri mzinda umene uli mʼmphepete mwa mtsinje wa Arinoni, mpaka ku mtsinje wa Yaboki, umene uli mʼmalire mwa Aamori, kuphatikizanso theka la dziko la Giliyadi.
3 Sihoni pia alitawala juu ya Araba mpaka Bahari ya Kinerethi, kwenda mashariki, kuelekea Bahari ya Araba (Bahari ya Chumvi) upande wa mashariki, hadi huko Bethi Yeshimothi na upande wa kusini, kuelekea chini ya miteremko wa Mlima Pisiga.
Iye ankalamuliranso dera la chigwa cha Yorodani kuyambira ku Nyanja ya Kinereti, kummawa ndi kumatsika mpaka ku Beti-Yesimoti, mzinda umene unali kummawa kwa Nyanja ya Mchere ndi kutsikabe kummwera mpaka pa tsinde pa phiri la Pisiga.
4 Ogu, mfalme wa Bashani, mmoja kati ya mabaki ya Rephaimu, aliyeishi huko Shatarothi na Edrei.
Ogi mfumu ya mzinda wa Basani, amene anali mmodzi mwa otsala mwa Arefaimu. Iye ankakhala ku Asiteroti ndi Ederi.
5 Alitawala juu ya Mlima Hermoni, Saleka, na Bahani yote, hadi mpaka wa watu wa Geshuri na Wamakathi, na nusu ya Gleadi, hadi kufika mpaka wa Sihohi, mfalme wa Heshboni.
Dera la ufumu wake linafika ku phiri la Herimoni, ku Saleka ndi dziko lonse la Basani mpaka ku malire ndi anthu a ku Gesuri Makati. Ufumu wake unaphatikizanso theka la Giliyadi mpaka ku malire a mfumu Sihoni ya ku Hesiboni.
6 Musa mtumishi wa Yahweh, na watu wa Israeli walikuwa wamewashinda, na Musa mtumishi wa Yahweh aliwapa nchi kama mali ya Wareubeni, Wagadi na nusu ya kabila la Manase.
Mose mtumiki wa Yehova ndi Aisraeli anawagonjetsa ndipo anapereka dziko lawo kwa anthu a fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase kuti chikhale cholowa chawo.
7 Hawa ndio wafalme wa nchi ambayo Yoshua na watu wa Israeli waliwashinda katika upande wa magharibi mwa mto Yordani, kutoka Baali Gadi katika bonde karibu na Lebanoni hadi Mlima Halaki karibu na Edom. Yoshua aliyapa nchi makabila ya Israeli ili yaimiliki.
Yoswa ndi Aisraeli onse anagonjetsa mafumu onse okhala kumadzulo kwa mtsinje wa Yorodani kuyambira ku Baala-Gadi, ku chigwa cha Lebanoni mpaka ku phiri la Halaki, kumapita cha ku Seiri. Yoswa anagawira dzikolo mafuko a Israeli kuti likhale cholowa chawo.
8 Aliwapa nchi ya milima, tambarare, Araba, sehemu za milima, nyika na Negevu, nchi ya Wahiti, Waamori, Wakanaani, Waperizi, Wahivi, na Wayebusi.
Dziko limeneli linali dera la ku mapiri, chigwa cha kumadzulo, chigwa cha Yorodani, ku matsitso a kummawa, ndi dziko la chipululu la kummwera. Amene ankakhala mʼdzikoli anali Ahiti, Aamori, Akanaani, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi. Mafumu ake anali awa:
9 Wafalme hawa walikuwa ni mfalme wa Yeriko, mfalme wa Ai iliyo karibu na Betheli,
mfumu ya Yeriko imodzi mfumu ya Ai (kufupi ndi Beteli imodzi
10 mfalme wa Yerusalemu, mfalme wa Enaimu,
mfumu ya Yerusalemu imodzi mfumu ya Hebroni imodzi
11 mfalme wa Yarmuthi, mfalme wa Lakishi,
mfumu ya Yarimuti imodzi mfumu ya Lakisi imodzi
12 mfalme wa Egloni, mfalme wa Gezeri,
mfumu ya Egiloni imodzi mfumu ya Gezeri imodzi
13 mfalme wa Debiri, mfalme wa Gederi,
mfumu ya Debri imodzi mfumu ya Gederi imodzi
14 mfalme wa Horima, mfalme wa Aradi,
mfumu ya Horima imodzi mfumu ya Aradi imodzi
15 mfalme wa Libna, mfalme wa Adula,
mfumu ya Libina imodzi mfumu ya Adulamu imodzi
16 mfalme wa Makeda, mfalme wa Betheli,
mfumu ya Makeda imodzi mfumu ya Beteli imodzi
17 mfalme wa Tapua, mfalme wa Heferi,
mfumu ya Tapuwa imodzi mfumu ya Heferi imodzi
18 mfalme wa Afeki, mfalme wa Lasharoni,
mfumu ya Afeki imodzi mfumu ya Lasaroni imodzi
19 mfalme wa Madoni, mfalme wa Hazori,
mfumu ya Madoni imodzi mfumu ya Hazori imodzi
20 mfalme wa Shimroni - Meroni, mfalme wa Akshafu.
mfumu ya Simuroni Meroni imodzi mfumu ya Akisafu imodzi
21 mfalme wa Taanaki, mfalme wa Megido,
mfumu ya Taanaki imodzi mfumu ya Megido imodzi
22 mfalme wa Kedeshi, mfalme wa Jokineamu katika Karmeli,
mfumu ya Kadesi imodzi mfumu ya Yokineamu ku Karimeli imodzi
23 mfalme wa Dori katika Nafutali Dori, mfalme Goyimu katika Giligali, na
mfumu ya Dori ku Nafoti Dori imodzi mfumu ya Goyini ku Giligala imodzi
24 mfalme Tiriza. Hesabu ya wafalme ilikuwa ni thelathini na moja kwa ujumla wake.
mfumu ya Tiriza imodzi mafumu onse pamodzi analipo 31.