< Ezekieli 26 >
1 Hivyo ilikuwa katika mwaka wa kumi na moja, siku ya kwanza ya mwezi, lile neno la Yahwe likanijia, kusema,
Pa chaka cha khumi ndi chimodzi, tsiku loyamba la mwezi, Yehova anandiyankhula kuti:
2 “Mwanadamu, kwa sababu Tiro amesema juu ya Yerusalemuu, 'Aha! Malango ya watu waliovunjika! Amenigeukia; Nitajazwa kwa sababu ameharibika.'
“Iwe mwana wa munthu, anthu a ku Turo ananyogodola Yerusalemu kuti ‘Hii! Uja amene anali chipata choloweramo anthu a mitundu ina wawonongeka. Zitseko zake zatsekukira ife. Tidzalemera popeza wasanduka bwinja.’
3 Kwa hiyo Bwana Yahwe asema hivi, 'Tazama! Niko juu yako, Tiro, na nitayainua mataifa mengi juu yako kama bahari iiunuavyo mawimbi yake.
Nʼchifukwa chake, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakulangani, inu anthu a ku Turo. Ndidzakuyitanirani anthu a mitundu ina kuti adzakulangeni monga momwe mafunde amawombera pa Nyanja.
4 Wataziharibu kuta za Tiro na kuiangusha chini minara yao. Nitafagia mavumbi yake mbali na kumfanya kama jiwe tupu.
Anthuwo adzawononga makoma a Turo ndi kugwetsa nsanja zake. Ndidzapala dothi lake ndipo ndidzamusandutsa thanthwe losalala.
5 Atakuwa sehemu ya kuwekea nyavu kati ya bahari, kwa kuwa nimesema hilo-hivi ndivyo Bwana Yahwe asemavyo-na atakuwa mateka kwa ajili ya mataifa.
Udzakhala poyanikapo makoka pakati pa nyanja. Ine Ambuye Yehova ndayankhula zimenezo. Udzasanduka chofunkha cha anthu a mitundu ina.
6 Binti zake walioko mashambani watachinjwa kwa panga, na watajua kwamba mimi ni Yahwe.'
Anthu okhala ku mtunda adzasakazidwa ndi lupanga. Pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
7 Kwa kuwa hivi ndivyo Bwana Yahwe asemavyo: Tazama, kutoka kaskazini namleta Nebukadreza mfalme wa Babeli, mfalme wa wafalme, dhidi ya Tiro, pamoja na farasi na magari ya farasi, na pamoja na waendesha farasi na watu wengi.
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Iwe Turo, ndidzakubweretsera Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni mfumu ya mafumu, kuchokera kumpoto pamodzi ndi akavalo ndiponso magaleta, anthu okwera pa akavalo ndi gulu lalikulu la ankhondo.
8 Atawaua binti zako katika shamba. Ataweka kazi ya boma na kujenga ulaghai dhidi ya kuta zako na kuziinua ngao dhidi yao.
Anthu okhala ku mtunda adzawapha ndi lupanga. Adzapanga mitumbira yankhondo ndi kukukwezera zishango kuti alimbane nawe.
9 Ataweka vyombo vya kubomolea dhidi ya kuta zako, na vyombo vyake vitaanguka chini ya minara yako.
Adzagwetsa makoma ako ndi zida zogumulira khoma ndi kugwetsa nsanja zako ndi nkhwangwa zake.
10 Farasi zake zitakuwa nyingi kwamba mavumbi yao yatawafunika. Kuta zako zitatikisika kwa mlio wa waendesha farasi, magurudumu, na magari ya farasi. Wakati atakapoingia malango yako, ataingia kama watu waingiavyo kwenye mji ambao kuta zimebomolewa.
Akavalo ake adzakhala ochuluka kwambiri kotero kuti adzakukwirira ndi fumbi lawo. Makoma ako adzagwedezeka ndi mdidi wa akavalo, ngolo ndi magaleta pamene iye adzalowa pa zipata monga mmene amalowera mu mzinda umene makoma ake agwetsedwa.
11 Kwato za farasi zake zitaikanyaga mitaa yako yote. Atawaua watu wako kwa upanga na nguzo za uweza wako zitaanguka chini.
Akavalo ake adzapondaponda mʼmisewu yako yonse ndi ziboda zawo. Adzapha anthu ako ndi lupanga. Mizati yako yolimba idzagwetsedwa.
12 Watauteka nyara utajiri wako na bidhaa iliyoporwa. Watabomoa kuta zako na kuziharibu nyumba zako za kifahari. Mawe yako, mbao zako, na kokoto watazitupa kwenye maji.
Iwo adzafunkha chuma chako ndipo adzalanda zinthu zako za malonda. Adzagwetsa makoma ako ndi kuwononga nyumba zako zabwino. Adzaponya miyala yako, matabwa ako ndi dothi lako mʼnyanja.
13 Nitaikomesha sauti ya nyimbo zako. Sauti ya vinubi haitasikika tena.
Choncho ndidzathetsa phokoso la nyimbo zanu, ndipo kulira kwa apangwe ako sikudzamvekanso.
14 Nitakufanya jiwe tupu, utakuwa mahali ambapo nyavu zitasambazwa kuzikausha. Hutajengwa tena, kwa kuwa mimi, Bwana Yahwe nimesema-hivi ndivyo Bwana Yahwe asemavyo.
Ndidzakusandutsa thanthwe losalala, ndipo udzakhala malo woyanikapo makoka a nsomba. Sudzamangidwanso, pakuti Ine Yehova ndayankhula, akutero Ambuye Yehova.
15 Bwana Yahwe amwambia hivi Tiro, 'Je visiwa havitatetemeka kwa mlio wa kuanguka kwako, na pamoja na watakaogumia kwa jeraha wakati machinjio mabaya yatakapokuwa kati yako?
“Ine Ambuye Yehova ndikukuwuza, iwe mzinda wa Turo, kuti zilumba zidzagwedezeka pakumva za kugwa kwako ndiponso poona anthu opweteka akubuwula ndipo anthu akuphedwa pakati pako.
16 Kisha wakuu wote wa bahari watakaposhuka kutoka kwenye viti vyao vya enzi na kuvua mavazi yao rasmi na kutupa mavazi yaliyonakshiwa. Watavaa wenyewe kwa kutetemeka, wataketi chini na kutetemeka kila wakati, na wataogopa kwa sababu yako.
Pamenepo mafumu a mʼmbali mwa nyanja adzatsika pa mipando yawo yaufumu. Adzayika pambali mikanjo yawo ndi kuvala zovala zawo zamakaka. Adzachita mantha ndipo adzakhala pansi akunjenjemera kosalekeza. Adzathedwa nzeru poona zimene zakugwera.
17 Watainua maombolezo juu yako na kukwambia, umekuwaje, uliyekuwa umekaliwa na manahodha wa meli, umeharibika. Mji mashuhuri ulikuwa imara sana-sasa umetoka kwenye bahari. Wale wanaoishi ndani yake wanaotia hofu kuhusu wenyewe juu ya kila mmoja aliyeishi karibu nao.
Pamenepo adzayimba nyimbo yokudandaula ndipo adzati kwa iwe: “‘Nʼkuchita kuwonongeka chotere, iwe mzinda wotchuka, wodzaza ndi anthu a ku nyanja! Unali wamphamvu pa nyanja, iwe ndi nzika zako; unkaopseza anthu onse amene ankakhala kumeneko.
18 Sasa fukwe zitatetemeka katika siku ya kuanguka kwako. Visiwa katika bahari vimeogofya, kwa sababu umekufa.'
Tsopano mayiko a mʼmbali mwa nyanja akunjenjemera chifukwa cha kugwa kwako; okhala pa zilumba nawonso agwidwa ndi mantha aakulu chifukwa cha kugwa kwako.’
19 Kwa kuwa Bwana Yahwe asema hivi: wakati nitakapokufanya wewe mji kuwa ukiwa, kama miji mingine ambayo haikaliwi, wakati nitakapoviinua vilindi dhidi yako, na wakati maji makuu yatakapokufunika,
“Mawu a Ine Ambuye Yehova ndi awa: Ndidzakusandutsa bwinja, ngati mizinda imene anthu sangathe kukhalamo. Ndidzakuphimba ndi madzi ozama a mʼnyanja, madzi amphamvu woti akumize.
20 kisha nitakushusha chini kwenda kwa watu wa nyakati za zamani, kama wengingine walioenda chini kwenye shimo; kwa kuwa nitakufanya uishi katika falme za chini za dunia kama uharibifu wa nyakati za zamani. Kwa sababu hii hutarudi na kusimama katika nchi ya walio hai.
Ndidzakugwetsa pansi kuti ukhale pamodzi ndi anthu amvulazakale amene akutsikira ku manda. Ine ndidzakusunga ku dzenjeko ngati ku bwinja losiyidwa kalekale, pamodzi ndi anthu amene anafa kale motero sudzabwererako kukhala pakati pa anthu amoyo.
21 Nitaweka janga juu yako, na hutakuwepo tena milele. Kisha utatafutwa, lakini hutapatikana milele tena-hivi ndivyo Bwana Yahwe asemavyo.”
Ine ndidzakuthetsa mochititsa mantha, ndipo sudzakhalaponso. Anthu adzakufunafuna, koma sudzapezekanso, akutero Ambuye Yehova.”