< Zaburi 89 >

1 Utenzi wa Ethani Mwezrahi. Nitaimba juu ya upendo mkuu wa Bwana milele; kwa kinywa changu nitajulisha uaminifu wako ujulikane kwa vizazi vyote.
Ndakatulo ya Etani, wa banja la Ezara. Ndidzayimba za chikondi chachikulu cha Yehova kwamuyaya; ndi pakamwa panga ndidzachititsa kuti kukhulupirika kwanu kudziwike ku mibado yonse.
2 Nitatangaza kuwa upendo wako unasimama imara milele na uaminifu wako umeuthibitisha mbinguni.
Ndidzalalikira kuti chikondi chanu chidzakhazikika mpaka muyaya, kuti Inu munakhazikitsa kukhulupirika kwanu kumwamba kwenikweniko.
3 Ulisema, “Nimefanya agano na mteule wangu, nimemwapia mtumishi wangu Daudi,
Inu munati, “Ndachita pangano ndi wosankhidwa wanga, ndalumbira kwa Davide mtumiki wanga kuti,
4 ‘Nitaimarisha uzao wako milele na kudumisha ufalme wako kwa vizazi vyote.’”
‘Ndidzakhazikitsa zidzukulu zako mpaka muyaya. Ndidzachititsa kuti mpando wako waufumu ukhazikike ku mibado yonse,’” (Sela)
5 Ee Bwana, mbingu zinayasifu maajabu yako, uaminifu wako pia katika kusanyiko la watakatifu.
Mayiko akumwamba amatamanda zozizwitsa zanu Yehova, kukhulupirika kwanunso, mu msonkhano wa oyera mtima anu.
6 Kwa kuwa ni nani katika mbingu anayeweza kulinganishwa na Bwana? Ni nani miongoni mwa viumbe vya mbinguni aliye kama Bwana?
Pakuti ndani mu mlengalenga angalingane ndi Yehova? Ndani wofanana ndi Yehova pakati pa zolengedwa zakumwamba?
7 Katika kusanyiko la watakatifu, Mungu huogopwa sana, anahofiwa kuliko wote wanaomzunguka.
Mu msonkhano wa oyera mtima Mulungu amaopedwa kwambiri; Iye ndiye wochititsa mantha kupambana onse amene amuzungulira.
8 Ee Bwana Mwenye Nguvu Zote, ni nani aliye kama wewe? Ee Bwana, wewe ni mwenye nguvu, na uaminifu wako unakuzunguka.
Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, ndani wofanana nanu? Yehova ndinu wamphamvu ndipo kukhulupirika kwanu kwakuzungulirani.
9 Wewe unatawala bahari yenye msukosuko; wakati mawimbi yake yanapoinuka, wewe unayatuliza.
Mumalamula nyanja ya mafunde awukali; pamene mafunde ake awundana Inu mumawakhalitsa bata.
10 Wewe ulimponda Rahabu kama mmojawapo wa waliochinjwa; kwa mkono wako wenye nguvu, uliwatawanya adui zako.
Munaphwanya Rahabe monga munthu wophedwa; ndi dzanja lanu lamphamvu munabalalitsa adani anu.
11 Mbingu ni zako, nayo nchi pia ni yako, uliuwekea ulimwengu msingi pamoja na vyote vilivyomo.
Mayiko akumwamba ndi anu ndiponso dziko lapansi ndi lanu; munapanga dziko lonse ndi zonse zili mʼmenemo.
12 Uliumba kaskazini na kusini; Tabori na Hermoni wanaliimbia jina lako kwa furaha.
Munalenga Kumpoto ndi Kummwera; Tabori ndi Herimoni akuyimba ndi chimwemwe pa dzina lanu.
13 Mkono wako umejaa uwezo; mkono wako una nguvu, mkono wako wa kuume umetukuzwa.
Mkono wanu ndi wamphamvu; dzanja lanu ndi lamphamvu, dzanja lanu lamanja ndi lopambana.
14 Haki na hukumu ndio msingi wa kiti chako cha enzi; upendo na uaminifu vinakutangulia.
Chilungamo ndi chiweruzo cholungama ndiye maziko a mpando wanu waufumu; chikondi ndi kukhulupirika zimayenda patsogolo panu.
15 Heri ni wale ambao wamejifunza kukusifu kwa shangwe, wanaotembea katika mwanga wa uwepo wako, Ee Bwana.
Ndi odala amene aphunzira kuyamika Inu, amene amayenda mʼkuwunika kwa nkhope yanu Yehova.
16 Wanashangilia katika jina lako mchana kutwa, wanafurahi katika haki yako.
Amakondwera mʼdzina lanu tsiku lonse lathunthu; amasangalala koposa mʼchilungamo chanu.
17 Kwa kuwa wewe ni utukufu na nguvu yao, kwa wema wako unatukuza pembe yetu.
Pakuti Inu ndiye ulemerero wawo ndi mphamvu yawo ndipo mwa kukoma mtima kwanu Inu mumakweza nyanga yathu.
18 Naam, ngao yetu ni mali ya Bwana, na mfalme wetu mali ya Aliye Mtakatifu wa Israeli.
Ndithudi, chishango chathu ndi cha Yehova, Mfumu yathu kwa Woyerayo wa Israeli.
19 Ulizungumza wakati fulani katika maono, kwa watu wako waaminifu, ukasema: “Nimeweka nguvu kwa shujaa, nimemwinua kijana miongoni mwa watu.
Kale munayankhula mʼmasomphenya, kwa anthu anu okhulupirika munati, “Ndapatsa mphamvu wankhondo; ndakweza mnyamata wochokera pakati pa anthu.
20 Nimemwona Daudi, mtumishi wangu, na nimemtia mafuta yangu matakatifu.
Ndamupeza mtumiki wanga Davide; ndamudzoza ndi mafuta opatulika.
21 Kitanga changu kitamtegemeza, hakika mkono wangu utamtia nguvu.
Dzanja langa lidzamuchirikiza; zoonadi, mkono wanga udzamupatsa mphamvu.
22 Hakuna adui atakayemtoza ushuru, hakuna mtu mwovu atakayemwonea.
Adani sadzamulamula kuti apereke msonkho; anthu oyipa sadzamusautsa.
23 Nitawaponda adui zake mbele zake na kuwaangamiza watesi wake.
Ndidzaphwanya adani ake pamaso pake ndi kukantha otsutsana naye.
24 Upendo wangu mkamilifu utakuwa pamoja naye, kwa Jina langu pembe yake itatukuzwa.
Chikondi changa chokhulupirika chidzakhala naye, ndipo kudzera mʼdzina langa nyanga yake idzakwezedwa.
25 Nitauweka mkono wake juu ya bahari, mkono wake wa kuume juu ya mito.
Ndidzayika dzanja lake pa nyanja, dzanja lake lamanja pa mitsinje.
26 Naye ataniita kwa sauti, ‘Wewe ni Baba yangu, Mungu wangu, Mwamba na Mwokozi wangu.’
Iyeyo adzafuwula kwa Ine kuti, ‘Ndinu Atate anga, Mulungu wanga, Thanthwe ndi Chipulumutso changa.’
27 Nitamteua pia awe mzaliwa wangu wa kwanza, aliyetukuka kuliko wafalme wote wa dunia.
Ndidzamuyika kuti akhale mwana wanga woyamba kubadwa; wokwezedwa kwambiri pakati pa mafumu a dziko lapansi.
28 Nitadumisha upendo wangu kwake milele, na agano langu naye litakuwa imara.
Ndidzamusungira chifundo changa kwamuyaya, ndipo pangano langa ndi iye silidzatha.
29 Nitaudumisha uzao wake milele, kiti chake cha enzi kama mbingu zinavyodumu.
Ine ndidzakhazikitsa zidzukulu zake mpaka muyaya, mpando wake waufumu ngati masiku a miyamba.
30 “Kama wanae wataacha amri yangu na wasifuate sheria zangu,
“Ngati ana ake adzataya lamulo langa ndi kusatsatira malangizo anga,
31 kama wakihalifu maagizo yangu na kutoshika amri zangu,
ngati adzaswa malamulo anga ndi kulephera kusunga ziphunzitso zanga,
32 nitaadhibu dhambi yao kwa fimbo, uovu wao kwa kuwapiga,
Ine ndidzalanga tchimo lawo ndi ndodo, mphulupulu zawo powakwapula.
33 lakini sitauondoa upendo wangu kwake, wala sitausaliti uaminifu wangu kamwe.
Koma sindidzachotsa chikondi changa pa iye, kapena kukhala wosakhulupirika kwa iyeyo.
34 Mimi sitavunja agano langu wala sitabadili lile ambalo midomo yangu imelitamka.
Sindidzaswa pangano langa kapena kusintha zimene milomo yanga yayankhula.
35 Mara moja na kwa milele, nimeapa kwa utakatifu wangu, nami sitamdanganya Daudi:
Ndinalumbira kamodzi mwa kuyera kwanga ndipo sindidzanama kwa Davide,
36 kwamba uzao wake utaendelea milele, na kiti chake cha enzi kitadumu mbele zangu kama jua;
kuti zidzukulu zake zidzakhale kwamuyaya ndipo mpando wake waufumu udzakhazikika pamaso panga ngati dzuwa;
37 kitaimarishwa milele kama mwezi, shahidi mwaminifu angani.”
udzakhazikika kwamuyaya monga mwezi, mboni yokhulupirika mʼmitambo. (Sela)
38 Lakini wewe umemkataa, umemdharau, umemkasirikia sana mpakwa mafuta wako.
“Koma tsopano Inu mwamukana, mwamutaya, mwamukwiyira kwambiri wodzozedwa wanu.
39 Umelikana agano lako na mtumishi wako, na umeinajisi taji yake mavumbini.
Mwakana pangano ndi mtumiki wanu ndipo mwadetsa mʼfumbi chipewa chake chaufumu.
40 Umebomoa kuta zake zote, na ngome zake zote umezifanya kuwa magofu.
Inu mwagumula makoma ake onse ndipo mwasandutsa bwinja malinga ake.
41 Wote wapitao karibu wamemnyangʼanya mali zake; amekuwa dharau kwa jirani zake.
Onse amene amadutsa amalanda zinthu zake; iye wakhala chotonzedwa cha anansi ake.
42 Umeutukuza mkono wa kuume wa adui zake, umewafanya watesi wake wote washangilie.
Mwakweza dzanja lamanja la adani ake; mwachititsa kuti adani ake akondwere.
43 Umegeuza makali ya upanga wake, na hukumpa msaada katika vita.
Mwabunthitsa lupanga lake, simunamuthandize pa nkhondo.
44 Umeikomesha fahari yake, na kukiangusha kiti chake cha enzi.
Inu mwathetsa kukongola kwa ulemerero wake ndipo mwagwetsa pansi mpando wake waufumu.
45 Umezifupisha siku za ujana wake, umemfunika kwa vazi la aibu.
Mwachepetsa masiku a unyamata wake; mwamuphimba ndi chofunda chochititsa manyazi. (Sela)
46 Hata lini, Ee Bwana? Utajificha milele? Ghadhabu yako itawaka kama moto hata lini?
“Mpaka liti Yehova? Kodi mudzadzibisa mpaka kalekale? Mpaka liti ukali wanu udzayaka ngati moto?
47 Kumbuka jinsi maisha yangu yanavyopita haraka. Ni kwa ubatili kiasi gani umemuumba mwanadamu!
Kumbukirani kuti masiku a moyo wanga ndi ochepa pakuti munalenga kwachabe anthu onse!
48 Ni mtu gani awezaye kuishi na asione kifo, au kujiokoa mwenyewe kutoka nguvu za kaburi? (Sheol h7585)
Kodi ndi munthu uti angakhale ndi moyo ndi kusaona imfa? Kapena kudzipulumutsa yekha ku mphamvu ya manda? (Sela) (Sheol h7585)
49 Ee Bwana, uko wapi upendo wako mkuu wa mwanzoni, ambao katika uaminifu wako ulimwapia Daudi?
Inu Ambuye kodi chili kuti chikondi chanu chachikulu choyamba chija, chimene mwa kukhulupirika kwanu munalumbira kwa Davide?
50 Bwana kumbuka jinsi mtumishi wako amesimangwa, jinsi ninavyovumilia moyoni mwangu dhihaka za mataifa yote,
Kumbukirani, Ambuye momwe mtumiki wanu wanyozedwera, momwe ndakhalira ndi kusunga mu mtima mwanga mawu a pangano a anthu a mitundu yonse,
51 dhihaka ambazo kwazo adui zako wamenisimanga, Ee Bwana, ambazo kwazo wamesimanga kila hatua ya mpakwa mafuta wako.
mawu achipongwe amene adani anu akhala akunyoza, Inu Yehova, ndi mawu amene akhala akunyoza mayendedwe onse a wodzozedwa wanu.
52 Msifuni Bwana milele!
“Matamando akhale kwa Yehova mpaka muyaya!”

< Zaburi 89 >