< Zaburi 83 >
1 Wimbo. Zaburi ya Asafu. Ee Mungu, usinyamaze kimya, usinyamaze, Ee Mungu, usitulie.
Nyimbo. Salimo la Asafu. Inu Mulungu musakhale chete; musangoti phee, Mulungu musangoti duu.
2 Tazama watesi wako wanafanya fujo, jinsi adui zako wanavyoinua vichwa vyao.
Onani adani anu akuchita chiwawa, amene amadana nanu autsa mitu yawo.
3 Kwa hila, wanafanya shauri dhidi ya watu wako, wanafanya shauri baya dhidi ya wale unaowapenda.
Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu; Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.
4 Wanasema, “Njooni, tuwaangamize kama taifa, ili jina la Israeli lisikumbukwe tena.”
Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”
5 Kwa nia moja wanapanga mashauri mabaya pamoja, wanafanya muungano dhidi yako,
Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu; Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:
6 mahema ya Edomu na Waishmaeli, ya Wamoabu na Wahagari,
Matenti a Edomu ndi Aismaeli, Mowabu ndi Ahagiri,
7 Gebali, Amoni na Amaleki, Ufilisti, pamoja na watu wa Tiro.
Agebala, Aamoni ndi Aamaleki, Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.
8 Hata Ashuru wameungana nao kuwapa nguvu wazao wa Loti.
Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo kupereka mphamvu kwa ana a Loti. (Sela)
9 Uwatendee kama vile ulivyowatendea Midiani, na kama vile ulivyowatendea Sisera na Yabini hapo kijito cha Kishoni,
Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani, monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.
10 ambao waliangamia huko Endori na wakawa kama takataka juu ya nchi.
Amene anawonongedwa ku Endori ndi kukhala ngati zinyalala.
11 Wafanye wakuu wao kama Orebu na Zeebu, watawala wao kama Zeba na Salmuna,
Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,
12 ambao walisema, “Na tumiliki nchi ya malisho ya Mungu.”
amene anati, “Tiyeni tilande dziko la msipu la Mulungu.”
13 Ee Mungu wangu, wapeperushe kama mavumbi ya kisulisuli, kama makapi yapeperushwayo na upepo.
Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga, ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.
14 Kama vile moto uteketezavyo msitu au mwali wa moto unavyounguza milima,
Monga moto umatentha nkhalango, kapena malawi a moto kuyatsa phiri,
15 wafuatilie kwa tufani yako na kuwafadhaisha kwa dhoruba yako.
kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho, ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.
16 Funika nyuso zao kwa aibu ili watu walitafute jina lako, Ee Bwana.
Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.
17 Wao na waaibishwe na kufadhaishwa milele, na waangamie kwa aibu.
Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse; awonongeke mwa manyazi.
18 Hebu wajue kwamba wewe, ambaye jina lako ni Bwana, kwamba wewe peke yako ndiwe Uliye Juu Sana ya dunia yote.
Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova, ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.