< Zaburi 63 >

1 Zaburi ya Daudi. Wakati alipokuwa katika Jangwa la Yuda. Ee Mungu, wewe ni Mungu wangu, nakutafuta kwa moyo wote; nafsi yangu inakuonea kiu, mwili wangu unakuonea wewe shauku, katika nchi kame na iliyochoka mahali ambapo hapana maji.
Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda. Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga, moona mtima ine ndimakufunafunani; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu, thupi langa likulakalaka inu, mʼdziko lowuma ndi lotopetsa kumene kulibe madzi.
2 Nimekuona katika mahali patakatifu na kuuona uwezo wako na utukufu wako.
Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.
3 Kwa sababu upendo wako ni bora kuliko uhai, midomo yangu itakuadhimisha.
Chifukwa chikondi chanu ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.
4 Nitakusifu siku zote za maisha yangu, na kwa jina lako nitainua mikono yangu.
Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga, ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.
5 Nafsi yangu itatoshelezwa kama kwa wingi wa vyakula; kwa midomo iimbayo kinywa changu kitakusifu wewe.
Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona. Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.
6 Kitandani mwangu ninakukumbuka wewe, ninawaza juu yako makesha yote ya usiku.
Pa bedi panga ndimakumbukira inu; ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.
7 Kwa sababu wewe ndiwe msaada wangu, chini ya uvuli wa mbawa zako naimba.
Chifukwa ndinu thandizo langa, ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.
8 Nafsi yangu inaambatana nawe, mkono wako wa kuume hunishika.
Moyo wanga umakangamira Inu; dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.
9 Wale wanaotafuta uhai wangu wataharibiwa, watakwenda chini kwenye vilindi vya dunia.
Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa; adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.
10 Watatolewa wafe kwa upanga, nao watakuwa chakula cha mbweha.
Iwo adzaperekedwa ku lupanga ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.
11 Bali mfalme atafurahi katika Mungu, wale wote waapao kwa jina la Mungu watamsifu, bali vinywa vya waongo vitanyamazishwa.
Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu; onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo, koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.

< Zaburi 63 >