< Zaburi 37 >
1 Zaburi ya Daudi. Usisumbuke kwa ajili ya watendao maovu, wala usiwaonee wivu watendao mabaya,
Salimo la Davide. Usamavutike chifukwa cha anthu oyipa kapena kuchitira nsanje amene akuchita cholakwa;
2 kwa maana kama majani watanyauka mara, kama mimea ya kijani watakufa mara.
pakuti monga udzu iwo adzafota msanga, ngati mbewu zobiriwira adzanyala msanga.
3 Mtumaini Bwana na utende yaliyo mema; Kaa katika nchi ukafurahie malisho salama.
Khulupirira Yehova ndipo uzichita zabwino; khazikika mʼdziko ndi kutsata zokhulupirika.
4 Jifurahishe katika Bwana naye atakupa haja za moyo wako.
Udzikondweretse wekha mwa Yehova ndipo Iye adzakupatsa zokhumba za mtima wako.
5 Mkabidhi Bwana njia yako, mtumaini yeye, naye atatenda hili:
Pereka njira yako kwa Yehova; dalira Iye ndipo Iyeyo adzachita izi:
6 Yeye atafanya haki yako ingʼae kama mapambazuko, na hukumu ya shauri lako kama jua la adhuhuri.
Iye adzachititsa chilungamo chako kuwala ngati mʼbandakucha, chiweruzo chako ngati dzuwa la masana.
7 Tulia mbele za Bwana na umngojee kwa uvumilivu; usisumbuke watu wanapofanikiwa katika njia zao, wanapotekeleza mipango yao miovu.
Khala chete pamaso pa Yehova ndipo umudikire mofatsa; usavutike pamene anthu apambana mʼnjira zawo, pamene iwo achita zinthu zawo zoyipa.
8 Epuka hasira na uache ghadhabu, usihangaike: itakuongoza tu kutenda uovu.
Pewa kupsa mtima ndipo tembenuka kuchoka ku ukali, usavutike chifukwa zimenezi zimatsogolera ku zoyipa.
9 Kwa maana waovu watakatiliwa mbali, bali wale wanaomtumaini Bwana watairithi nchi.
Pakuti anthu oyipa adzachotsedwa, koma iwo amene amayembekeza mwa Yehova adzalandira dziko.
10 Bado kitambo kidogo, nao waovu hawataonekana, ingawa utawatafuta, hawataonekana.
Kwa kanthawi oyipa sadzapezekanso; ngakhale muwafunefune, sadzapezekanso.
11 Bali wanyenyekevu watairithi nchi na wafurahie amani tele.
Koma ofatsa adzalandira dziko ndipo adzasangalala ndi mtendere waukulu.
12 Waovu hula njama dhidi ya wenye haki na kuwasagia meno,
Oyipa amakonza chiwembu kutsutsana ndi olungama ndipo amawakukutira mano;
13 bali Bwana huwacheka waovu, kwa sababu anajua siku yao inakuja.
koma Ambuye amaseka oyipa pakuti Iye amadziwa kuti tsiku lawo likubwera.
14 Waovu huchomoa upanga na kupinda upinde, ili wawaangushe maskini na wahitaji, kuwachinja wale ambao njia zao ni nyofu.
Oyipa amasolola lupanga ndi kupinda uta kugwetsa osauka ndi osowa, kupha iwo amene njira zawo ndi zolungama.
15 Lakini panga zao zitachoma mioyo yao wenyewe, na pinde zao zitavunjwa.
Koma malupanga awo analasa mitima yawo yomwe, ndipo mauta awo anathyoka.
16 Bora kidogo walicho nacho wenye haki kuliko wingi wa mali wa waovu wengi;
Zabwino zochepa zimene olungama ali nazo ziposa chuma cha anthu oyipa ambiri;
17 kwa maana nguvu za waovu zitavunjwa, lakini Bwana humtegemeza mwenye haki.
pakuti mphamvu ya oyipa idzasweka, koma Yehova amasunga olungama.
18 Bwana anazifahamu siku za wanyofu, na urithi wao utadumu milele.
Masiku a anthu osalakwa amadziwika ndi Yehova, ndipo cholowa chawo chidzakhala mpaka muyaya.
19 Siku za maafa hawatanyauka, siku za njaa watafurahia wingi wa vitu.
Pa nthawi ya mavuto iwo sadzafota; mʼmasiku a njala adzakhala ndi zinthu zambiri.
20 Lakini waovu wataangamia: Adui za Bwana watakuwa kama uzuri wa mashamba, watatoweka, watatoweka kama moshi.
Koma oyipa adzawonongeka; adani a Yehova adzakhala ngati kukongola kwa kuthengo, iwo adzazimirira ngati utsi.
21 Waovu hukopa na hawalipi, bali wenye haki hutoa kwa ukarimu.
Oyipa amabwereka ndipo sabweza koma olungama amapereka mowolowamanja.
22 Wale wanaobarikiwa na Bwana watairithi nchi, bali wale anaowalaani watakatiliwa mbali.
Iwo amene Yehova amawadalitsa adzalandira dziko, koma amene Iye amawatemberera adzachotsedwa.
23 Kama Bwana akipendezwa na njia ya mtu, yeye huimarisha hatua zake,
Ngati Yehova akondwera ndi njira ya munthu, amakhazikitsa mayendedwe ake;
24 ajapojikwaa, hataanguka, kwa maana Bwana humtegemeza kwa mkono wake.
ngakhale atapunthwa sadzagwa, pakuti Yehova amamutchinjiriza ndi dzanja lake.
25 Nilikuwa kijana na sasa ni mzee, lakini sijaona kamwe wenye haki wameachwa au watoto wao wakiombaomba chakula.
Ine ndinali wamngʼono ndipo tsopano ndakalamba koma sindinaonepo olungama akusiyidwa kapena ana awo akupempha chakudya.
26 Wakati wote ni wakarimu na hukopesha bila masharti. Watoto wao watabarikiwa.
Iwo ndi owolowamanja nthawi zonse ndipo amabwereketsa mwaufulu; ana awo adzadalitsika.
27 Acha ubaya na utende wema, nawe utaishi katika nchi milele.
Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; pamenepo udzakhazikika mʼdziko kwamuyaya.
28 Kwa kuwa Bwana huwapenda wenye haki naye hatawaacha waaminifu wake. Watalindwa milele, lakini uzao wa waovu utakatiliwa mbali.
Pakuti Yehova amakonda wolungama ndipo sadzasiya okhulupirika ake. Iwo adzatetezedwa kwamuyaya, koma zidzukulu za oyipa zidzachotsedwa;
29 Wenye haki watairithi nchi, na kuishi humo milele.
olungama adzalandira dziko ndipo adzakhazikikamo kwamuyaya.
30 Kinywa cha mwenye haki hutamka hekima, nao ulimi wake huzungumza lililo haki.
Pakamwa pa munthu wolungama pamayankhula za nzeru, ndipo lilime lake limayankhula zolungama.
31 Sheria ya Mungu wake imo moyoni mwake; nyayo zake hazitelezi.
Lamulo la Mulungu wake lili mu mtima mwake; mapazi ake saterereka.
32 Watu waovu huvizia wenye haki, wakitafuta kuwaua;
Oyipa amabisala kudikira olungama; kufunafuna miyoyo yawoyo;
33 lakini Bwana hatawaacha mikononi mwao wala hatawaacha wahukumiwe kuwa wakosa wanaposhtakiwa.
koma Yehova sadzawasiya pansi pa mphamvu yawo kapena kuti atsutsidwe pamene abweretsedwa pa milandu.
34 Mngojee Bwana, na uishike njia yake. Naye atakutukuza uirithi nchi, waovu watakapokatiliwa mbali, utaliona hilo.
Khulupirira Yehova, ndipo sunga njira yake; Iye adzakukweza ndipo udzalandira dziko kuti likhale lako; udzaona anthu oyipa akuwonongeka.
35 Nimemwona mtu mwovu na mkatili akistawi kama mwerezi wa Lebanoni,
Ine ndinaona munthu woyipa ndi munthu wopanda chifundo akupeza bwino ngati mtengo wobiriwira pa nthaka ya makolo ake.
36 lakini alitoweka mara na hakuonekana, ingawa nilimtafuta, hakupatikana.
Koma sanachedwe kumwalira ndipo sanaonekenso; ngakhale ndinamuyangʼanayangʼana, sanapezekenso.
37 Watafakari watu wasio na hatia, wachunguze watu wakamilifu, kuna mafanikio kwa mtu apendaye amani.
Ganizira za munthu wosalakwa, yangʼanitsitsa munthu wolungama; udzaona kuti ali ndi tsogolo labwino ndipo ali ndi zidzukulu zambiri.
38 Lakini watenda dhambi wote wataangamizwa, mafanikio yao yatakatiliwa mbali.
Koma anthu ochimwa adzawonongeka; iwowo pamodzi ndi zidzukulu zawo zomwe.
39 Wokovu wa wenye haki hutoka kwa Bwana, yeye ni ngome yao wakati wa shida.
Chipulumutso cha olungama chimachokera kwa Yehova; Iye ndiye linga lawo pa nthawi ya masautso.
40 Bwana huwasaidia na kuwaokoa, huwaokoa kutoka kwa waovu na kuwahifadhi, kwa maana wanamkimbilia.
Yehova amawathandiza ndi kuwalanditsa; Iye amawalanditsa kwa oyipa ndi kuwapulumutsa, pakuti amathawira kwa Iye.