< Zaburi 130 >

1 Wimbo wa kwenda juu. Kutoka vilindini ninakulilia, Ee Bwana.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndikulirira kwa Inu Yehova ndili mʼdzenje lozama;
2 Ee Bwana, sikia sauti yangu. Masikio yako na yawe masikivu kwa kilio changu unihurumie.
Ambuye imvani mawu anga. Makutu anu akhale tcheru kumva kupempha chifundo kwanga.
3 Kama wewe, Ee Bwana, ungeweka kumbukumbu ya dhambi, Ee Bwana, ni nani angeliweza kusimama?
Inu Yehova, mukanamawerengera machimo, Inu Yehova, akanayima chilili ndani wopanda mlandu?
4 Lakini kwako kuna msamaha, kwa hiyo wewe unaogopwa.
Koma kwa Inu kuli chikhululukiro; nʼchifukwa chake mumaopedwa.
5 Namngojea Bwana, nafsi yangu inangojea, katika neno lake naweka tumaini langu.
Ndimayembekezera Yehova, moyo wanga umayembekezera, ndipo ndimakhulupirira mawu ake.
6 Nafsi yangu inamngojea Bwana kuliko walinzi waingojeavyo asubuhi, naam, kuliko walinzi waingojeavyo asubuhi.
Moyo wanga umayembekezera Ambuye, kupambana momwe alonda amayembekezera mmawa, inde, kupambana momwe alonda amayembekezera mmawa,
7 Ee Israeli, mtumaini Bwana, maana kwa Bwana kuna upendo usiokoma, na kwake kuna ukombozi kamili.
Yembekeza Yehova, iwe Israeli, pakuti Yehova ali ndi chikondi chosasinthika ndipo alinso ndi chipulumutso chochuluka.
8 Yeye mwenyewe ataikomboa Israeli kutoka dhambi zao zote.
Iye mwini adzawombola Israeli ku machimo ake onse.

< Zaburi 130 >