< Zaburi 121 >

1 Wimbo wa kwenda juu. Nayainua macho yangu nitazame vilima, msaada wangu utatoka wapi?
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndikweza maso anga ku mapiri; kodi thandizo langa limachokera kuti?
2 Msaada wangu hutoka kwa Bwana, Muumba wa mbingu na dunia.
Thandizo langa limachokera kwa Yehova, wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
3 Hatauacha mguu wako uteleze, yeye akulindaye hatasinzia,
Sadzalola kuti phazi lako literereke; Iye amene amakusunga sadzawodzera.
4 hakika, yeye alindaye Israeli hatasinzia wala hatalala usingizi.
Taonani, Iye amene amasunga Israeli sadzawodzera kapena kugona.
5 Bwana anakulinda, Bwana ni uvuli wako mkono wako wa kuume,
Yehova ndiye amene amakusunga; Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.
6 jua halitakudhuru mchana, wala mwezi wakati wa usiku.
Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana, kapena mwezi nthawi ya usiku.
7 Bwana atakukinga na madhara yote, atayalinda maisha yako,
Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse; adzasunga moyo wako.
8 Bwana atakulinda unapoingia na unapotoka, tangu sasa na hata milele.
Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako; kuyambira tsopano mpaka muyaya.

< Zaburi 121 >