< Zaburi 115 >

1 Sio kwetu sisi, Ee Bwana, sio kwetu sisi, bali utukufu ni kwa jina lako, kwa sababu ya upendo na uaminifu wako.
Kwa ife ayi Yehova, kwa ife ayi koma ulemerero ukhale pa dzina lanu, chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika ndiponso chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
2 Kwa nini mataifa waseme, “Yuko wapi Mungu wao?”
Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akunena kuti, “Mulungu wawo ali kuti?”
3 Mungu wetu yuko mbinguni, naye hufanya lolote limpendezalo.
Mulungu wathu ali kumwamba; Iye amachita chilichonse chimene chimamukondweretsa.
4 Lakini sanamu zao ni za fedha na dhahabu, zilizotengenezwa kwa mikono ya wanadamu.
Koma mafano awo ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
5 Zina vinywa, lakini haziwezi kusema, zina macho, lakini haziwezi kuona;
Pakamwa ali napo koma sayankhula, maso ali nawo koma sapenya;
6 zina masikio, lakini haziwezi kusikia, zina pua, lakini haziwezi kunusa;
makutu ali nawo koma samva, mphuno ali nazo koma sanunkhiza;
7 zina mikono, lakini haziwezi kupapasa, zina miguu, lakini haziwezi kutembea; wala koo zao haziwezi kutoa sauti.
manja ali nawo koma akakhudza samva kanthu; mapazi ali nawo koma sayenda; kapena pakhosi pawo kutulutsa mawu.
8 Wale wanaozitengeneza watafanana nazo, vivyo hivyo wale wote wanaozitumainia.
Anthu amene amapanga mafanowo adzafanana nawo, chimodzimodzinso onse amene amadalira mafanowo.
9 Ee nyumba ya Israeli, mtumainini Bwana, yeye ni msaada na ngao yao.
Inu Aisraeli, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
10 Ee nyumba ya Aroni, mtumainini Bwana, yeye ni msaada na ngao yao.
Iwe nyumba ya Aaroni, dalira Yehova; Iye ndiye thandizo lako ndi chishango chako.
11 Ninyi mnaomcha, mtumainini Bwana, yeye ni msaada na ngao yao.
Inu amene mumaopa Iye, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
12 Bwana anatukumbuka na atatubariki: ataibariki nyumba ya Israeli, ataibariki nyumba ya Aroni,
Yehova watikumbukira ndipo adzatidalitsa: adzadalitsa nyumba ya Israeli, adzadalitsa nyumba ya Aaroni,
13 atawabariki wale wanaomcha Bwana, wadogo kwa wakubwa.
adzadalitsa iwo amene amaopa Yehova; aangʼono ndi aakulu omwe.
14 Bwana na awawezeshe kuongezeka, ninyi na watoto wenu.
Yehova akuwonjezereni madalitso; inuyo pamodzi ndi ana anu.
15 Mbarikiwe na Bwana Muumba wa mbingu na dunia.
Mudalitsidwe ndi Yehova, Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
16 Mbingu zilizo juu sana ni mali ya Bwana, lakini dunia amempa mwanadamu.
Kumwamba ndi kwa Yehova, koma dziko lapansi Iye walipereka kwa anthu.
17 Sio wafu wanaomsifu Bwana, wale washukao mahali pa kimya,
Si anthu akufa amene amatamanda Yehova, amene amatsikira kuli chete;
18 bali ni sisi tunaomtukuza Bwana, sasa na hata milele. Msifuni Bwana.
ndi ife amene timatamanda Yehova, kuyambira tsopano mpaka muyaya. Tamandani Yehova.

< Zaburi 115 >