< Mithali 6 >
1 Mwanangu, kama umekuwa mdhamini wa jirani yako, ikiwa umeshika mikono kwa kuweka ahadi kwa ajili ya mwingine,
Mwana wanga, ngati wamuperekera mnansi wako chikole, ngati walonjeza kumulipirira mlendo,
2 kama umetegwa na ulichosema, umenaswa kwa maneno ya kinywa chako,
ngati wagwidwa ndi zimene iwe unanena, wakodwa ndi mawu a mʼkamwa mwako.
3 basi fanya hivi mwanangu, ili ujiweke huru, kwa kuwa umeanguka mikononi mwa jirani yako: Nenda ukajinyenyekeshe kwake; msihi jirani yako!
Tsono popeza iwe mwana wanga wadziponya mʼmanja mwa mnansi wako, chita izi kuti udzipulumutse: pita msanga ukamupemphe mnansi wako; kuti akumasule!
4 Usiruhusu usingizi machoni pako, usiruhusu kope zako zisinzie.
Usagone tulo, usawodzere.
5 Jiweke huru, kama swala mkononi mwa mwindaji, kama ndege kutoka kwenye mtego wa mwindaji.
Dzipulumutse monga imachitira mphoyo mʼdzanja la mlenje, ndi monga imachitira mbalame mu msampha wa munthu wosaka.
6 Ewe mvivu, mwendee mchwa; zitafakari njia zake ukapate hekima!
Pita kwa nyerere, mlesi iwe; kaonetsetse njira zake kuti uphunzirepo kanthu!
7 Kwa maana yeye hana msimamizi, wala mwangalizi, au mtawala,
Zilibe mfumu, zilibe woyangʼanira kapena wolamulira,
8 lakini hujiwekea akiba wakati wa kiangazi na hukusanya chakula chake wakati wa mavuno.
komabe zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe ndipo zimatuta chakudyacho nthawi yokolola.
9 Ewe mvivu, utalala hata lini? Utaamka lini kutoka usingizi wako?
Kodi uzingogonabe pamenepo mpaka liti mlesi iwe? Kodi tulo tako tidzatha liti?
10 Bado kulala kidogo, kusinzia kidogo, bado kukunja mikono kidogo upate kupumzika:
Ukati ndingogona pangʼono, ndingowodzera pangʼono ndingopinda manjawa pangʼono kuti ndipumule,
11 hivyo umaskini utakuja juu yako kama mnyangʼanyi, na kupungukiwa kutakujia kama mtu mwenye silaha.
umphawi udzakugwira ngati mbala ndipo usiwa udzafika ngati munthu wachifwamba.
12 Mtu mbaya sana na mlaghai, ambaye huzungukazunguka na maneno ya upotovu,
Munthu wachabechabe, munthu woyipa, amangoyendayenda ndi kumayankhula zoyipa,
13 ambaye anakonyeza kwa jicho lake, anayetoa ishara kwa miguu yake na kuashiria kwa vidole vyake,
amatsinzinira maso ake, namakwakwaza mapazi ake ndi kulozaloza ndi zala zake,
14 ambaye hupanga ubaya kwa udanganyifu moyoni mwake: daima huchochea fitina.
amalingalira zoyipa ndi mtima wake wachinyengo ndipo nthawi zonse amangokhalira kuyambitsa mikangano pakati pa anthu.
15 Kwa hiyo maafa yatamkumba ghafula; ataangamizwa mara, pasipo msaada.
Nʼchifukwa chake tsoka lidzamugwera modzidzimutsa; adzawonongeka msangamsanga popanda chomupulumutsa.
16 Kuna vitu sita anavyovichukia Bwana, naam, viko saba vilivyo chukizo kwake:
Pali zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Yehova amadana nazo, zinthu zisanu ndi ziwiri zimene zimamunyansa:
17 macho ya kiburi, ulimi udanganyao, mikono imwagayo damu isiyo na hatia,
maso onyada, pakamwa pabodza, manja akupha munthu wosalakwa,
18 moyo uwazao mipango miovu, miguu iliyo myepesi kukimbilia uovu,
mtima wokonzekera kuchita zoyipa, mapazi othamangira msanga ku zoyipa,
19 shahidi wa uongo ambaye humwaga uongo, na mtu ambaye huchochea fitina kati ya ndugu.
mboni yonama yoyankhula mabodza komanso munthu amene amayambitsa mikangano pakati pa abale.
20 Mwanangu, zishike amri za baba yako, wala usiyaache mafundisho ya mama yako.
Mwana wanga, usunge malamulo a abambo ako; ndipo usataye zimene anakuphunzitsa amayi ako.
21 Yafunge katika moyo wako daima, yakaze kuizunguka shingo yako.
Zimenezi uzimatirire pa mtima pako masiku onse, uzimangirire mʼkhosi mwako.
22 Wakati utembeapo, yatakuongoza; wakati ulalapo, yatakulinda; wakati uamkapo, yatazungumza nawe.
Ukamayenda, zidzakulozera njira; ukugona, zidzakulondera; ukudzuka, zidzakuyankhula.
23 Kwa maana amri hizi ni taa, mafundisho haya ni mwanga na maonyo ya maadili ni njia ya uzima,
Paja malamulo awa ali ngati nyale, malangizowa ali ngati kuwunika, ndipo chidzudzulo cha mwambo ndiwo moyo weniweni,
24 yakikulinda na mwanamke aliyepotoka, kutokana na maneno laini ya mwanamke aliyepotoka.
kukupulumutsa kwa mkazi wadama, zimenezi zidzakutchinjiriza kwa mkazi wadama, ndi kukuthandiza kuti usamvere mawu oshashalika a mkazi wachiwerewere.
25 Moyo wako usitamani uzuri wake wala macho yake yasikuteke,
Mu mtima wako usakhumbire kukongola kwake, asakukope ndi zikope zake,
26 kwa maana kahaba atakufanya uwe maskini, hata ukose kipande cha mkate, naye mwanamke mzinzi huwinda maisha yako hasa.
paja mkazi wadama amakusandutsa kukhala ngati nyenyeswa za buledi ndipo mkazi wa mwini wake amasokonezeratu moyo wako wonse.
27 Je, mtu aweza kuchotea moto kwenye paja lake bila nguo zake kuungua?
Kodi munthu angathe kutenga moto zovala zake osapsa?
28 Je, mtu aweza kutembea juu ya makaa ya moto yanayowaka bila miguu yake kuungua?
Kodi munthu angathe kuyenda pa makala amoto mapazi ake osapserera?
29 Ndivyo alivyo mtu alalaye na mke wa mwanaume mwingine; hakuna yeyote amgusaye huyo mwanamke ambaye hataadhibiwa.
Ndizo zimachitikira munthu amene amagonana ndi mkazi wa munthu wina. Aliyense wokhudza mkazi wotere adzalangidwa.
30 Watu hawamdharau mwizi kama akiiba kukidhi njaa yake wakati ana njaa.
Paja anthu sayinyoza mbala ikaba chifukwa chakuti ili ndi njala.
31 Pamoja na hayo, kama akikamatwa, lazima alipe mara saba, ingawa inamgharimu utajiri wote wa nyumba yake.
Komabe ngati mbalayo igwidwa iyenera kulipira kasanu nʼkawiri, ngakhale kulandidwa katundu wa mʼnyumba mwake.
32 Lakini mwanaume aziniye na mwanamke hana akili kabisa; yeyote afanyaye hivyo hujiangamiza mwenyewe.
Munthu wochita chigololo ndi wopanda nzeru. Wochita zimenezi amangodziwononga yekha.
33 Mapigo na aibu ni fungu lake na aibu yake haitafutika kamwe;
Adzalandira mabala ndi mʼnyozo, ndipo manyazi ake sadzamuchokera.
34 kwa maana wivu huamsha ghadhabu ya mume, naye hataonyesha huruma alipizapo kisasi.
Paja nsanje imachititsa mwini mkaziyo kukalipa, ndipo sadzachita chifundo pobwezera.
35 Hatakubali fidia yoyote; atakataa malipo, hata yakiwa makubwa kiasi gani.
Iye savomera dipo lililonse; sangapepeseke ngakhale umupatse mphatso zochuluka motani.