< Mithali 4 >

1 Sikilizeni wanangu, mafundisho ya baba yenu; sikilizeni kwa makini na mpate ufahamu.
Ananu, mverani malangizo a abambo anu; tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
2 Ninawapa mafundisho ya maana, kwa hiyo msiyaache mafundisho yangu.
Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino. Choncho musasiye malangizo anga.
3 Nilipokuwa mvulana mdogo katika nyumba ya baba yangu, ningali mchanga na mtoto pekee kwa mama yangu,
Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga; mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
4 baba alinifundisha akisema, “Yashike maneno yangu yote kwa moyo wako wote; yashike maagizo yangu na wewe utaishi.
Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti, “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako, usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
5 Pata hekima, pata ufahamu; usiyasahau maneno yangu wala usiyaache.
Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu; usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
6 Usimwache hekima naye atakuweka salama; mpende, naye atakulinda.
Usasiye nzeru ndipo idzakusunga. Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
7 Hekima ni bora kuliko vitu vyote; kwa hiyo jipe hekima. Hata ikikugharimu vyote ulivyo navyo, pata ufahamu.
Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru. Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
8 Mstahi, naye atakukweza; mkumbatie, naye atakuheshimu.
Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza; ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
9 Atakuvika shada la neema kichwani mwako na kukupa taji ya utukufu.”
Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako; idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”
10 Sikiliza mwanangu, kubali ninachokuambia, nayo miaka ya maisha yako itakuwa mingi.
Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena, ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
11 Ninakuongoza katika njia ya hekima na kukuongoza katika mapito yaliyonyooka.
Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
12 Utembeapo, hatua zako hazitazuiliwa; ukimbiapo, hutajikwaa.
Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana; ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
13 Mkamate sana elimu, usimwache aende zake; mshike, maana yeye ni uzima wako.
Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi. Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
14 Usiuweke mguu wako katika njia ya waovu wala usitembee katika njia ya watu wabaya.
Usayende mʼnjira za anthu oyipa kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
15 Epukana nayo, usisafiri katika njia hiyo; achana nayo, na uelekee njia yako.
Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo; uzilambalala nʼkumangopita.
16 Kwa kuwa hawawezi kulala mpaka watende uovu; wanashindwa hata kusinzia mpaka wamwangushe mtu.
Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa; tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
17 Wanakula mkate wa uovu, na kunywa mvinyo wa jeuri.
Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
18 Njia ya wenye haki ni kama nuru ya kwanza ya mapambazuko, ambayo hungʼaa zaidi na zaidi mpaka mchana mkamilifu.
Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
19 Lakini njia ya waovu ni kama giza nene; hawajui kinachowafanya wajikwae.
Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani; iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
20 Mwanangu, yasikilize kwa makini yale ninayokuambia; sikiliza kwa makini maneno yangu.
Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena; tchera khutu ku mawu anga.
21 Usiruhusu yaondoke machoni pako, yahifadhi ndani ya moyo wako;
Usayiwale malangizo angawa, koma uwasunge mu mtima mwako.
22 kwa sababu ni uzima kwa wale wanaoyapata na afya kwa mwili wote wa mwanadamu.
Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
23 Zaidi ya yote, linda moyo wako, kuliko yote uyalindayo, maana ndiko zitokako chemchemi za uzima.
Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu pakuti ndiwo magwero a moyo.
24 Epusha kinywa chako na ukaidi; weka mazungumzo machafu mbali na midomo yako.
Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota; ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
25 Macho yako na yatazame mbele, kaza macho yako moja kwa moja mbele yako.
Maso ako ayangʼane patsogolo; uziyangʼana kutsogolo molunjika.
26 Sawazisha mapito ya miguu yako na njia zako zote ziwe zimethibitika.
Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
27 Usigeuke kulia wala kushoto; epusha mguu wako na ubaya.
Usapatukire kumanja kapena kumanzere; usapite kumene kuli zoyipa.

< Mithali 4 >