< Mithali 23 >

1 Uketipo kula chakula na mtawala, angalia vyema kile kilicho mbele yako,
Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira, uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,
2 na utie kisu kooni mwako kama ukiwa mlafi.
ngati ndiwe munthu wadyera udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.
3 Usitamani vyakula vyake vitamu kwa kuwa chakula hicho ni cha hila.
Usasirire zakudya zake, pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.
4 Usijitaabishe ili kuupata utajiri, uwe na hekima kuonyesha kujizuia.
Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma, ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.
5 Kufumba na kufumbua utajiri hutoweka, huwa kama umepata mabawa ghafula, ukaruka na kutoweka angani kama tai.
Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo. Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.
6 Usile chakula cha mtu mchoyo, usitamani vyakula vyake vitamu,
Usadye chakudya cha munthu waumbombo, usalakalake zakudya zake zokoma;
7 kwa maana yeye ni aina ya mtu ambaye kila mara anafikiri juu ya gharama. Anakuambia, “Kula na kunywa,” lakini moyo wake hauko pamoja nawe.
paja iye ndi munthu amene nthawi zonse amaganizira za mtengo wake ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,” koma sakondweretsedwa nawe.
8 Utatapika kile kidogo ulichokula, nawe utakuwa umepoteza bure maneno yako ya kumsifu.
Udzasanza zimene wadyazo ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.
9 Usizungumze na mpumbavu, kwa maana atadhihaki hekima ya maneno yako.
Usayankhule munthu wopusa akumva, pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.
10 Usisogeze jiwe la mpaka wa zamani wala kunyemelea kwenye mashamba ya yatima,
Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,
11 kwa kuwa Mtetezi wao ni mwenye nguvu, atalichukua shauri lao dhidi yako.
paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.
12 Elekeza moyo wako kwenye mafundisho na masikio yako kwenye maneno ya maarifa.
Mtima wako uzikhala pa malangizo ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.
13 Usimnyime mtoto adhabu, ukimwadhibu kwa fimbo, hatakufa.
Usaleke kumulangiza mwana; ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.
14 Mwadhibu kwa fimbo na kuiokoa nafsi yake kutoka mautini. (Sheol h7585)
Ukamukwapula ndi tsatsa udzapulumutsa moyo wake. (Sheol h7585)
15 Mwanangu, kama moyo wako una hekima, basi moyo wangu utafurahi,
Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru, inenso mtima wanga udzakondwera.
16 utu wangu wa ndani utafurahi, wakati midomo yako itakapozungumza lililo sawa.
Mtima wanga udzakondwera pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.
17 Usiuruhusu moyo wako kuwaonea wivu wenye dhambi, bali kila mara uwe na bidii katika kumcha Bwana.
Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa, koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.
18 Hakika kuna tumaini la baadaye kwa ajili yako, nalo tarajio lako halitakatiliwa mbali.
Ndithu za mʼtsogolo zilipo ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.
19 Sikiliza, mwanangu na uwe na hekima, weka moyo wako kwenye njia iliyo sawa.
Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru, mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.
20 Usiwe miongoni mwa wanywao mvinyo, au wale walao nyama kwa pupa,
Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.
21 kwa maana walevi na walafi huwa maskini, nako kusinzia huwavika matambara.
Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi ndipo aulesi adzavala sanza.
22 Msikilize baba yako, aliyekuzaa, wala usimdharau mama yako atakapokuwa mzee.
Mvera abambo ako amene anakubala, usanyoze amayi ako pamene akalamba.
23 Nunua kweli wala usiiuze, pata hekima, adabu na ufahamu.
Gula choonadi ndipo usachigulitse; ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.
24 Baba wa mwenye haki ana furaha kubwa, naye aliye na mwana mwenye hekima humfurahia.
Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu; Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
25 Baba yako na mama yako na wafurahi, mama aliyekuzaa na ashangilie!
Abambo ndi amayi ako asangalale; amene anakubereka akondwere!
26 Mwanangu, nipe moyo wako, macho yako na yafuate njia zangu,
Mwana wanga, undikhulupirire ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.
27 kwa maana kahaba ni shimo refu na mwanamke mpotovu ni kisima chembamba.
Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama; ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.
28 Kama mnyangʼanyi, hungojea akivizia, naye huzidisha wasio waaminifu miongoni mwa wanaume.
Amabisala ngati mbala yachifwamba, ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.
29 Ni nani mwenye ole? Ni nani mwenye huzuni? Ni nani mwenye ugomvi? Ni nani mwenye malalamiko? Ni nani aliye na majeraha yasiyo na sababu? Ni nani mwenye macho mekundu?
Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni? Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo? Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?
30 Ni hao wakaao sana kwenye mvinyo, hao waendao kuonja mabakuli ya mvinyo uliochanganywa.
Ndi amene amakhalitsa pa mowa, amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.
31 Usiukodolee macho mvinyo wakati ukiwa mwekundu, wakati unapometameta kwenye bilauri, wakati ushukapo taratibu!
Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo, pamene akuwira mʼchikho pamene akumweka bwino!
32 Mwishowe huuma kama nyoka na kutia sumu yake kama nyoka mwenye sumu.
Potsiriza pake amaluma ngati njoka, ndipo amajompha ngati mphiri.
33 Macho yako yataona mambo mageni na moyo wako kuwazia mambo yaliyopotoka.
Maso ako adzaona zinthu zachilendo ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.
34 Utakuwa kama alalaye katikati ya bahari, alalaye juu ya kamba ya merikebu.
Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja, kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.
35 Utasema, “Wamenipiga lakini sikuumia! Wamenichapa, lakini sisikii! Nitaamka lini ili nikanywe tena?”
Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe! Andimenya koma sindinamve kanthu! Kodi ndidzuka nthawi yanji? Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”

< Mithali 23 >