< Ayubu 4 >

1 Ndipo Elifazi Mtemani akajibu:
Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
2 “Kama mtu akithubutu kuzungumza nawe, kutakukasirisha? Lakini ni nani awezaye kujizuia asiseme?
“Ngati wina atakuyankha, kodi ungakhumudwe? Koma ndani angakhale chete wosayankhula?
3 Fikiri jinsi ambavyo umewafundisha watu wengi, jinsi ambavyo umeitia nguvu mikono iliyokuwa dhaifu.
Taganiza momwe iwe walangizira anthu ambiri, momwe walimbitsira anthu ofowoka.
4 Maneno yako yamewategemeza wale waliojikwaa; umeyatia nguvu magoti yaliyokuwa dhaifu.
Mawu ako analimbitsa anthu ofuna kugwa; unachirikiza anthu wotha mphamvu.
5 Lakini sasa hii taabu imekujia wewe, nawe unashuka moyo; imekupiga wewe, nawe unafadhaika.
Koma tsopano mavuto akufikira ndipo wataya mtima, zakukhudza ndipo uli ndi mantha.
6 Je, kumcha Mungu kwako hakupaswi kuwa ndiyo matumaini yako na njia zako kutokuwa na lawama ndilo taraja lako?
Kodi kuopa Mulungu kwako sindiko kulimbika mtima kwako? Ndipo moyo wako wosalakwa ndiye chiyembekezo chako?
7 “Fikiri sasa: Ni mtu yupi asiye na hatia ambaye aliwahi kuangamia? Ni wapi wanyofu waliwahi kuangamizwa?
“Ganiza bwino tsopano: Kodi munthu wosalakwa anawonongekapo nʼkale lonse? Nʼkuti kumene munthu wolungama mtima anaphedwa?
8 Kwa jinsi ambavyo mimi nimechunguza, wale walimao ubaya na wale hupanda uovu, huvuna hayo hayo hayo.
Monga ndaonera ine, anthu amene amatipula zoyipa, ndi iwo amene amadzala mavuto, amakolola zomwezo.
9 Kwa pumzi ya Mungu huangamizwa; kwa mshindo wa hasira zake huangamia.
Iwo amaphedwa ndi mpweya wa Mulungu; amawonongeka ndi mpweya waukali wa mkwiyo wake.
10 Simba anaweza kunguruma na kukoroma, lakini bado meno ya simba mkubwa huvunjika.
Mikango imabangula ndi kulira, komabe mano a mikango yamphamvu amathyoledwa.
11 Simba anaweza kuangamia kwa kukosa mawindo, nao wana wa simba jike hutawanyika.
Mkango umafa chifukwa chosowa nyama, ndipo ana amkango amamwazikana.
12 “Neno lililetwa kwangu kwa siri, masikio yangu yakasikia mnongʼono wake.
“Mawu anabwera kwa ine mwamseri, makutu anga anamva kunongʼona kwake.
13 Katikati ya ndoto za kutia wasiwasi wakati wa usiku, hapo usingizi mzito uwapatapo wanadamu,
Mʼkati mwa maloto ochititsa mantha usiku, nthawi imene anthu amagona tulo tofa nato,
14 hofu na kutetemeka kulinishika na kufanya mifupa yangu yote itetemeke.
ndinagwidwa ndi mantha, ndi kuyamba kunjenjemera ndipo mafupa anga onse anaweyeseka.
15 Kuna roho aliyepita mbele ya uso wangu, nazo nywele za mwili wangu zikasimama.
Pamenepo mzimu unadutsa pamaso panga, ndipo ubweya wa pa thupi langa unayima kuti njoo.
16 Yule roho akasimama, lakini sikuweza kutambua kilikuwa kitu gani. Umbo fulani lilisimama mbele ya macho yangu, kukawa na ukimya kisha nikasikia sauti:
Chinthucho chinayimirira koma sindinathe kuzindikira kuti chinali chiyani. Chinthu chinayima patsogolo panga, kunali zii ndipo ndinamva mawu akuti,
17 ‘Je, binadamu aweza kuwa mwadilifu kuliko Mungu? Je, mtu aweza kuwa safi kuliko Muumba wake?
‘Kodi munthu angathe kukhala wolungama kupambana Mulungu? Kodi munthu angathe kukhala wangwiro kupambana Mlengi wake?
18 Kama Mungu hawaamini watumishi wake, kama yeye huwalaumu malaika zake kwa kukosea,
Ngati Mulungu sakhulupirira atumiki ake omwe, ngati Iye amawapeza angelo ake ndi cholakwa,
19 ni mara ngapi zaidi wale waishio katika nyumba za udongo wa mfinyanzi, ambazo misingi yake ipo mavumbini, ambao wamepondwa kama nondo!
nanga kuli bwanji ndi iwo amene amakhala mʼnyumba zadothi, amene maziko awo ndi fumbi, amene amathudzuka mosavuta ngati kadziwotche!
20 Kati ya mawio na machweo huvunjwa vipande vipande; bila yeyote kutambua, huangamia milele.
Mmawa ali moyo, pofika madzulo afa; mwakachetechete, amawonongeka kwamuyaya.
21 Je, kamba za hema yao hazikungʼolewa, hivyo hufa bila hekima?’
Kodi zonse zimene ali nazo sizimatheratu, kotero kuti amafa osadziwa nʼkanthu komwe?’

< Ayubu 4 >