< Salmos 97 >
1 El Señor es Rey, que la tierra tenga gozo; alégrense todas las costas e islas.
Yehova akulamulira, dziko lapansi lisangalale; magombe akutali akondwere.
2 Nubes oscuras lo rodean; su reino se basa en la justicia y el juicio correcto.
Mitambo ndi mdima waukulu zamuzungulira; chilungamo ndi kuweruza molungama ndiwo maziko a mpando wake waufumu.
3 Fuego va delante de él, quemando a todos los que están contra él, a su alrededor alrededor.
Moto umapita patsogolo pake ndi kunyeketsa amaliwongo kumbali zonse.
4 Sus relámpagos iluminan el mundo; la tierra lo vio con miedo.
Zingʼaningʼani zake zimawalitsa dziko lonse; dziko lapansi limaona ndipo limanjenjemera.
5 Los montes se volvieron como cera delante del Señor, ante él Señor de toda la tierra.
Mapiri amasungunuka ngati phula pamaso pa Yehova, pamaso pa Ambuye a dziko lonse lapansi.
6 Los cielos dieron la noticia de su justicia, y todo el pueblo vio su gloria.
Mayiko akumwamba amalengeza za chilungamo chake, ndipo mitundu yonse ya anthu imaona ulemerero wake.
7 Avergonzados todos los que adoran las imágenes y se enorgullecen de los dioses falsos; Dale culto, todos ustedes dioses.
Onse amene amalambira mafano osema amachititsidwa manyazi, iwo amene amanyadira mafano; mulambireni, inu milungu yonse!
8 Sión escuchó y se alegró; y las hijas de Judá estaban llenas de alegría, por tus decisiones, oh Señor.
Ziyoni akumva ndipo akukondwera, midzi ya Yuda ikusangalala chifukwa cha maweruzo anu Yehova.
9 Porque tú, Señor altísimo, estás sobre toda la tierra; eres levantado sobre todos los demás dioses.
Pakuti Inu Yehova ndi Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi; ndinu wokwezeka kupambana milungu yonse.
10 Ustedes amantes de Jehová, aborrezcan el mal; él guarda las almas de sus santos; él los quita de la mano de los pecadores.
Iwo amene amakonda Yehova adane ndi zoyipa pakuti Iye amayangʼanira miyoyo ya amene amamukhulupirira ndipo amawapulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa
11 La luz brilla sobre los amantes de la justicia, y para los rectos de corazón hay alegría.
Kuwala kumafika pa anthu olungama, ndi chimwemwe kwa olungama mtima.
12 Alégrense en el Señor, hombres rectos; alabando el recuerdo de su santo nombre.
Kondwerani mwa Yehova Inu olungama ndipo tamandani dzina lake loyera.